< Yoswa 10 >

1 Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
Now when Adoni-zedek King of Ierusalem had heard how Ioshua had taken Ai and had destroyed it, (for as he had done to Iericho and to the King thereof, so he had done to Ai and to the King thereof) and howe the inhabitants of Gibeon had made peace with Israel, and were among them,
2 Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
Then they feared exceedingly: for Gibeon was a great citie, as one of the royall cities: for it was greater then Ai, and all the men thereof were mightie.
3 Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
Wherefore Adoni-zedek King of Ierusalem sent vnto Hoham King of Hebron, and vnto Piram King of Iarmuth, and vnto Iapia King of Lachish, and vnto Debir King of Eglon, saying,
4 Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
Come vp vnto me, and helpe me, that we may smite Gibeon: for they haue made peace with Ioshua and with the children of Israel.
5 Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
Therefore the fiue Kings of the Amorites, the King of Ierusalem, the King of Hebron, the King of Iarmuth, the King of Lachish, and the King of Eglon gathered themselues together, and went vp, they with all their hostes, and besieged Gibeon, and made warre against it.
6 Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
And the men of Gibeon sent vnto Ioshua, euen to the hoste to Gilgal, saying, Withdrawe not thine hand from thy seruants: come vp to vs quickly, and saue vs, and helpe vs: for all the Kings of the Amorites which dwell in the mountaines, are gathered together against vs.
7 Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
So Ioshua ascended from Gilgal, he, and all the people of warre with him, and all the men of might.
8 Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
And the Lord sayd vnto Ioshua, Feare them not: for I haue giuen them into thine hand: none of them shall stand against thee.
9 Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
Ioshua therefore came vnto them suddenly: for he went vp from Gilgal all the night.
10 Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
And the Lord discomfited them before Israel, and slew them with a great slaughter at Gibeon, and chased them along the way that goeth vp to Beth-horon, and smote them to Azekah and to Makkedah.
11 Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
And as they fled from before Israel, and were in the going downe to Beth-horon, the Lord cast downe great stones from heauen vpon them, vntill Azekah, and they dyed: they were more that dyed with the hailestones, then they whom the children of Israel slewe with the sword.
12 Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
Then spake Ioshua to the Lord, in the day when the Lord gaue the Amorites before the children of Israel, and he sayd in the sight of Israel, Sunne, stay thou in Gibeon, and thou moone, in the valley of Aialon.
13 Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
And the Sunne abode, and the moone stood still, vntill the people auenged themselues vpon their enemies: (Is not this written in the booke of Iasher?) so the Sunne abode in the middes of the heauen, and hasted not to goe downe for a whole day.
14 Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
And there was no day like that before it, nor after it, that the Lord heard the voyce of a man: for the Lord fought for Israel.
15 Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
After, Ioshua returned, and all Israel with him vnto the campe to Gilgal:
16 Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
But the fiue Kings fled and were hid in a caue at Makkedah.
17 Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
And it was tolde Ioshua, saying, The fiue Kings are found hid in a caue at Makkedah.
18 Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
Then Ioshua said, Roule great stones vpon the mouth of the caue, and set men by it for to keepe them.
19 Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
But stand ye not still: follow after your enemies, and smite all the hindmost, suffer them not to enter into their cities: for the Lord your God hath giuen them into your hand.
20 Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
And when Ioshua and the children of Israel had made an ende of slaying them with an exceeding great slaughter till they were consumed, and the rest that remained of them were entred into walled cities,
21 Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
Then all the people returned to the campe, to Ioshua at Makkedah in peace: no man mooued his tongue against the children of Israel.
22 Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
After, Ioshua sayd, Open the mouth of the caue, and bring out these fiue Kings vnto me forth of the caue.
23 Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
And they did so, and brought out those fiue Kings vnto him forth of the caue, euen the King of Ierusalem, the King of Hebron, ye King of Iarmuth, the King of Lachish, and the King of Eglon.
24 Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
And when they had brought out those Kings vnto Ioshua, Ioshua called for all the men of Israel, and sayd vnto the chiefe of the men of warre, which went with him, Come neere, set your feete vpon the necks of these Kings: and they came neere and set their feete vpon their necks.
25 Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
And Ioshua sayd vnto them, Feare not, nor be faint hearted, but be strong and of a good courage: for thus will the Lord doe to all your enemies, against whome ye fight.
26 Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
So then Ioshua smote them, and slewe them, and hanged them on fiue trees, and they hanged still vpon the trees vntill the euening.
27 Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
And at the going downe of the sunne, Ioshua gaue commandement, that they should take them downe off the trees, and cast them into the caue (wherein they had bene hid) and they layde great stones vpon the caues mouth, which remaine vntill this day.
28 Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
And that same day Ioshua tooke Makkedah and smote it with the edge of the sword, and the King thereof destroyed he with them, and all the soules that were therein, he let none remaine: for hee did to the King of Makkedah as he had done vnto the King of Iericho.
29 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
Then Ioshua went from Makkedah, and all Israel with him vnto Libnah, and fought against Libnah.
30 Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
And the Lord gaue it also and the King thereof into the hand of Israel: and he smote it with the edge of the sword, and all the soules that were therein: he let none remaine in it: for he did vnto the King thereof, as he had done vnto the King of Iericho.
31 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
And Ioshua departed from Libnah, and all Israel with him vnto Lachish, and besieged it, and assaulted it.
32 Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
And the Lord gaue Lachish into the hand of Israel, which tooke it the second day, and smote it with the edge of the sword, and all the soules that were therein, according to all as he had done to Libnah.
33 Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
Then Horam King of Gezer came vp to helpe Lachish: but Ioshua smote him and his people, vntill none of his remained.
34 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
And from Lachish Ioshua departed vnto Eglon, and all Israel with him, and they besieged it, and assaulted it,
35 Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
And they tooke it the same day, and smote it with the edge of the sword, and all the soules that were therein he vtterly destroyed the same day, according to all that he had done to Lachish.
36 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
Then Ioshua went vp from Eglon, and all Israel with him vnto Hebron, and they fought against it.
37 Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
And when they had taken it, they smote it with the edge of the sword, and the King thereof, and all the cities thereof, and all the soules that were therein: he left none remaining, according to all as he had done to Eglon: for he destroyed it vtterly, and all the soules that were therein.
38 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
So Ioshua returned, and all Israel with him to Debir, and fought against it.
39 Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
And when he had taken it, and the King thereof, and all the citie thereof, they smote them with the edge of the sword, and vtterly destroyed all the soules that were therein, he let none remaine: as he did to Hebron, so he did to Debir, and to the King thereof, as he had also done to Libnah, and to the King thereof.
40 Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
So Ioshua smote all the hill countreys, and the South countreys, and the valleys, and the hill sides, and all their Kings, and let none remaine, but vtterly destroyed euery soule, as the Lord God of Israel had commanded.
41 Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
And Ioshua smote them from Kadesh-barnea euen vnto Azzah, and all the countrey of Goshen, euen vnto Gibeon.
42 Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
And all these Kings, and their land did Ioshua take at one time, because the Lord God of Israel fought for Israel.
43 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.
Afterward, Ioshua and all Israel with him returned vnto the campe in Gilgal.

< Yoswa 10 >