< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
І сталося по смерті Мойсея, раба Божого, і сказав Господь до Ісуса, сина Нави́нового, Мойсеєвого слуги, говорячи:
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
„Мойсей, раб Мій, помер. А тепер уставай, перейди цей Йорда́н ти та ввесь народ цей до того кра́ю, що Я даю їм, Ізраїлевим синам.
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
Кожне місце, що стопа́ ноги вашої сту́пить на ньому, Я дав вам, як Я говорив був Мойсеєві.
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
Від пустині й цього Лива́ну й аж до Великої Річки, річки Ефра́ту, увесь край хітте́ян, і аж до Великого моря на за́хід буде ваша границя.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
Не встоїть ніхто перед тобою по всі дні життя твого. Як був Я з Мойсеєм, так буду з тобою, — не залишу́ тебе й не покину тебе.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Будь сильний та відва́жний, бо ти зробиш, що народ цей посяде той край, що Я присягнув був їхнім батька́м дати їм.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Тільки будь дуже сильний та відважний, щоб доде́ржувати чинити за всім тим Зако́ном, що наказав був тобі Мойсей, Мій раб, — не відхи́лишся від нього ні право́руч, ні ліво́руч, щоб щастило тобі в усьому, де ти будеш ходити.
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
Нехай книга цього Зако́ну не відійде від твоїх уст, але будеш розду́мувати про неї вдень та вночі, щоб доде́ржувати чинити все, що написано в ній, бо тоді зробиш щасливими доро́ги свої, і тоді буде щастити тобі.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
Чи ж не наказав Я тобі: будь сильний та відва́жний? Не бійся й не лякайся, бо з тобою Госпо́дь, Бог твій, у всьому, де́ ти будеш ходити“.
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
І наказав Ісус урядникам наро́ду, говорячи:
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
„Перейдіть посеред табо́ру, і накажіть наро́дові, говорячи: Приготуйте собі пожи́ву на дорогу, бо по трьох днях ви перехо́дите цей Йорда́н, щоб увійти посісти той край, що Господь, Бог ваш, дає вам його на спадщину“.
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
А Руви́мовому й Ґадовому та половині пле́мени Манасіїного Ісус сказав, говорячи:
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
„Пам'ятайте те слово, що вам наказав був Мойсей, раб Господній, говорячи: Господь, Бог ваш, що відпочи́нок дає вам, дав вам цей край.
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
Ваші жінки́, діти ваші та ваша худоба зоста́нуться в кра́ї, що дав вам Мойсей по той бік Йорда́ну, а ви пере́йдете озбро́єні перед вашими братами, усі сильні військо́ві, і допоможете їм,
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
аж поки Господь не дасть відпочи́нку вашим братам, як вам, і посядуть і вони той край, що Господь, Вог ваш, дає їм. І ви ве́рнетеся до краю вашого спа́дку, і посядете його, що дав вам Мойсей, раб Господній, по той бік Йорда́ну на схід сонця“.
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
А вони відповіли́ Ісусові, говорячи: „Усе, що накажеш нам, ми зро́бимо, і до всього, куди пошлеш нас, пі́демо.
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
Усе так, як слухалися ми Мойсея, так будемо слу́хатися тебе́, тільки нехай буде Господь, Бог твій, з тобою, як був Він із Мойсеєм.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Кожен, хто буде неслухня́ний нака́зам твоїм, і не буде слухатися слів твоїх щодо всього, що накажеш йому, нехай буде вбитий. Тільки будь сильний та відважний!“

< Yoswa 1 >