< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
Or, il arriva après la mort de Moïse, serviteur du Seigneur, que le Seigneur parla à Josué, fils de Nun, serviteur de Moïse, et qu’il lui dit:
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
Moïse, mon serviteur est mort, lève-toi, passe le Jourdain, toi et tout le peuple avec toi, et va dans la terre que je donnerai moi-même aux enfants d’Israël.
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
Tout lieu que la plante de votre pied aura foulé, je vous le livrerai, comme j’ai dit à Moïse.
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
Depuis le désert et le Liban jusqu’au grand fleuve d’Euphrate, toute la terre des Héthéens, jusqu’à la grande mer contre le couchant du soleil, sera votre limite.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
Nul ne pourra vous résister pendant tous les jours de ta vie: comme j’ai été avec Moïse, ainsi je serai avec toi, je ne te laisserai, ni ne t’abandonnerai.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Prends courage et sois fort, car c’est toi qui partageras à ce peuple par le sort la terre, au sujet de laquelle j’ai juré à leurs pères que je la leur livrerais.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Prends donc courage, et sois très fort, afin que tu gardes et que tu pratiques toute la loi que t’a prescrite Moïse, mon serviteur: ne t’en détourne ni à droite ni à gauche, afin que tu comprennes tout ce que tu fais.
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
Que le livre de cette loi ne s’éloigne point de ta bouche; tu le méditeras les jours et les nuits, afin que tu gardes et pratiques tout ce qui y est écrit: alors tu dirigeras ta voie et tu la comprendras.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
Voici que je te l’ordonne, prends courage et sois fort. Ne crains point, et ne t’épouvante point, parce que le Seigneur ton Dieu est avec toi en quelque lieu que tu ailles.
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
Et Josué ordonna aux princes du peuple, disant: Passez par le milieu du camp, et commandez au peuple, et dites:
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
Préparez-vous des vivres, parce qu’après trois jours vous passerez le Jourdain, et vous entrerez entrerez pour la posséder, dans la terre que le Seigneur votre Dieu va vous donner.
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
Aux Rubénites aussi et aux Gadites et à la demi-tribu de Manassé, il dit:
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
Souvenez-vous de ce que vous ordonna Moïse, serviteur du Seigneur, disant: Le Seigneur votre Dieu vous a donné le repos et toute cette terre.
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
Vos femmes, vos enfants et vos bestiaux demeureront dans la terre que vous a livrée Moïse en deçà du Jourdain; mais vous, passez armés devant vos frères, vous tous forts de la main, et combattez pour eux,
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
Jusqu’à ce que le Seigneur donne le repos à vos frères, comme il vous l’a donné à vous-mêmes; et qu’ils possèdent eux aussi la terre que le Seigneur votre Dieu va leur donner: et c’est ainsi que vous retournerez dans la terre de votre possession, et que vous habiterez dans cette terre que vous a donnée Moïse, serviteur de Dieu en deçà du Jourdain contre le levant.
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
Et ils répondirent à Josué et dirent: Nous ferons tout ce que tu nous as ordonné; et nous irons partout où tu nous enverras.
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
Comme nous avons obéi en toutes choses à Moïse, ainsi nous t’obéirons à toi-même. Seulement que le Seigneur ton Dieu soit avec toi, comme il a été avec Moïse.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Que celui qui contredira ta parole, et qui n’obéira pas à tous les discours que tu lui prescriras, meure; seulement, toi, fortifie-toi, et agis courageusement.

< Yoswa 1 >