< Yoswa 1 >
1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
and to be after death Moses servant/slave LORD and to say LORD to(wards) Joshua son: child Nun to minister Moses to/for to say
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
Moses servant/slave my to die and now to arise: rise to pass [obj] [the] Jordan [the] this you(m. s.) and all [the] people [the] this to(wards) [the] land: country/planet which I to give: give to/for them to/for son: descendant/people Israel
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
all place which to tread palm: sole foot your in/on/with him to/for you to give: give him like/as as which to speak: promise to(wards) Moses
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
from [the] wilderness and [the] Lebanon [the] this and till [the] river [the] Great (Sea) river Euphrates all land: country/planet [the] Hittite and till [the] sea [the] Great (Sea) entrance [the] sun to be border: area your
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
not to stand man: anyone to/for face: before your all day life your like/as as which to be with Moses to be with you not to slacken you and not to leave: forsake you
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
to strengthen: strengthen and to strengthen for you(m. s.) to inherit [obj] [the] people [the] this [obj] [the] land: country/planet which to swear to/for father their to/for to give: give to/for them
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
except to strengthen: strengthen and to strengthen much to/for to keep: careful to/for to make: do like/as all [the] instruction which to command you Moses servant/slave my not to turn aside: turn aside from him right and left because be prudent in/on/with all which to go: went
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
not to remove scroll: book [the] instruction [the] this from lip your and to mutter in/on/with him by day and night because to keep: careful to/for to make: do like/as all [the] to write in/on/with him for then to prosper [obj] way: journey your and then be prudent
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
not to command you to strengthen: strengthen and to strengthen not to tremble and not to to be dismayed for with you LORD God your in/on/with all which to go: went
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
and to command Joshua [obj] official [the] people to/for to say
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
to pass in/on/with entrails: among [the] camp and to command [obj] [the] people to/for to say to establish: prepare to/for you provision for in/on/with still three day you(m. p.) to pass [obj] [the] Jordan [the] this to/for to come (in): come to/for to possess: take [obj] [the] land: country/planet which LORD God your to give: give to/for you to/for to possess: take her
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
and to/for Reubenite and to/for Gad and to/for half tribe [the] Manasseh to say Joshua to/for to say
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
to remember [obj] [the] word which to command [obj] you Moses servant/slave LORD to/for to say LORD God your to rest to/for you and to give: give to/for you [obj] [the] land: country/planet [the] this
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
woman: wife your child your and livestock your to dwell in/on/with land: country/planet which to give: give to/for you Moses in/on/with side: beyond [the] Jordan and you(m. p.) to pass armed to/for face: before brother: compatriot your all mighty man [the] strength and to help [obj] them
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
till which to rest LORD to/for brother: compatriot your like/as you and to possess: take also they(masc.) [obj] [the] land: country/planet which LORD God your to give: give to/for them and to return: return to/for land: country/planet possession your and to possess: take [obj] her which to give: give to/for you Moses servant/slave LORD in/on/with side: beyond [the] Jordan east [the] sun
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
and to answer [obj] Joshua to/for to say all which to command us to make: do and to(wards) all which to send: depart us to go: went
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
like/as all which to hear: obey to(wards) Moses so to hear: obey to(wards) you except to be LORD God your with you like/as as which to be with Moses
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
all man which to rebel [obj] lip: word your and not to hear: obey [obj] word your to/for all which to command him to die except to strengthen: strengthen and to strengthen