< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
And it was after [the] death of Moses [the] servant of Yahweh and he said Yahweh to Joshua [the] son of Nun [the] servant of Moses saying.
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
Moses servant my he has died and therefore arise pass over the Jordan this you and all the people this into the land which I [am] about to give to them to [the] people of Israel.
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
Every place which it will tread [the] sole of foot your on it to you I have given it just as I spoke to Moses.
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
From the wilderness and Lebanon this and to the river great [the] river of Euphrates all [the] land of the Hittites and to the sea great [the] setting of the sun it will be territory your.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
Not he will stand anyone before you all [the] days of life your just as I was with Moses I will be with you not I will abandon you and not I will leave you.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Be strong and be bold for you you will cause to inherit the people this the land which I swore to fathers their to give to them.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Only be strong and be bold exceedingly to take care to do according to all the law which he commanded you Moses servant my may not you turn aside from it right and left so that you may prosper in every where you will go.
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
Not it will depart [the] book of the law this from mouth your and you will meditate on it by day and night so that you may take care to do according to every [thing] written in it for then you will make successful ways your and then you will be successful.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
¿ Not have I commanded you be strong and be bold may not you be terrified and may not you be dismayed for [is] with you Yahweh God your in every where you will go.
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
And he commanded Joshua [the] officers of the people saying.
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
Pass - in [the] midst of the camp and command the people saying prepare for yourselves food for in yet - three days you [are] about to pass over the Jordan this to go to take possession of the land which Yahweh God your [is] about to give to you to take possession of it.
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
And to the Reubenite[s] and to the Gadite[s] and to [the] half of [the] tribe of Manasseh he said Joshua saying.
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
Remember the word which he commanded you Moses [the] servant of Yahweh saying Yahweh God your [is] giving rest to you and he will give to you the land this.
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
Wives your little one[s] your and livestock your they will remain in the land which he gave to you Moses on [the] other side of the Jordan and you you will pass over arrayed for battle before brothers your all [the] mighty [men] of strength and you will help them.
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
Until that he will give rest Yahweh - to brothers your like you and they will take possession of also they the land which Yahweh God your [is] about to give to them and you will return to [the] land of possession your and you will take possession of it which - he gave to you Moses [the] servant of Yahweh on [the] other side of the Jordan [the] rising of the sun.
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
And they answered Joshua saying all that you have commanded us we will do and to every where you will send us we will go.
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
According to all that we listened to Moses so we will listen to you only may he be Yahweh God your with you just as he was with Moses.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Every person who he will rebel toward mouth your and not he will obey words your to all that you will command him he will be put to death only be strong and be bold.

< Yoswa 1 >