< Yona 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti,
Or la parole de Yahvé fut adressée à Jonas, fils d'Amittaï, en ces termes:
2 “Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”
« Lève-toi, va à Ninive, la grande ville, et prêche contre elle, car leur méchanceté est montée devant moi. »
3 Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.
Mais Jonas se leva pour fuir vers Tarsis, loin de la présence de Yahvé. Il descendit à Joppé, et trouva un navire qui allait à Tarsis; il paya le prix du navire, et y descendit, pour aller avec eux à Tarsis, loin de la présence de Yahvé.
4 Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.
Mais Yahvé fit souffler un grand vent sur la mer, et il y eut une grande tempête sur la mer, de sorte que le navire risquait de se briser.
5 Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato.
Alors les marins eurent peur, et chacun cria à son dieu. Ils jetèrent à la mer la cargaison qui se trouvait dans le navire pour alléger le navire. Mais Jonas était descendu dans les profondeurs du navire, il était couché et dormait profondément.
6 Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”
Alors le capitaine du navire s'approcha de lui et lui dit: « Que veux-tu dire, dormeur? Lève-toi, invoque ton Dieu! Peut-être ton Dieu nous remarquera-t-il, afin que nous ne périssions pas. »
7 Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.
Ils se dirent tous les uns aux autres: « Venez! Tirons au sort, afin de savoir qui est responsable de ce mal qui nous frappe. » Ils tirèrent donc au sort, et le sort tomba sur Jonas.
8 Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”
Ils lui demandèrent alors: « Dis-nous, je t'en prie, à cause de qui ce malheur est sur nous. Quelle est ta profession? D'où viens-tu? Quel est ton pays? De quel peuple es-tu? »
9 Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”
Il leur dit: « Je suis hébreu et je crains Yahvé, le Dieu des cieux, qui a fait la mer et la terre sèche. »
10 Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).
Alors les hommes eurent une grande peur et lui dirent: « Qu'as-tu fait? » Car les hommes savaient qu'il fuyait la présence de Yahvé, parce qu'il le leur avait dit.
11 Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”
Et ils lui dirent: « Que te ferons-nous, pour que la mer se calme à nos yeux? » Car la mer devenait de plus en plus houleuse.
12 Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”
Il leur dit: « Prenez-moi, et jetez-moi dans la mer. Alors la mer se calmera pour vous, car je sais que c'est à cause de moi que cette grande tempête est sur vous. »
13 Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja
Les hommes ramaient avec force pour les ramener à terre, mais ils ne pouvaient pas, car la mer devenait de plus en plus agitée contre eux.
14 Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.”
Alors ils crièrent à Yahvé et dirent: « Nous te supplions, Yahvé, nous te supplions de ne pas nous laisser mourir pour la vie de cet homme, et de ne pas faire retomber sur nous le sang innocent; car toi, Yahvé, tu as fait ce qui t'a plu. »
15 Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata.
Ils prirent donc Jonas et le jetèrent dans la mer, et la mer cessa de se déchaîner.
16 Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.
Les hommes eurent une grande crainte de l'Éternel, et ils offrirent un sacrifice à l'Éternel et firent des vœux.
17 Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.
Yahvé prépara un énorme poisson pour engloutir Jonas, et Jonas resta dans le ventre du poisson trois jours et trois nuits.

< Yona 1 >