< Yona 3 >

1 Ndipo Yehova anayankhula ndi Yona kachiwiri kuti,
Ilizwi leNkosi laselifika kuJona ngokwesibili, lisithi:
2 “Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire uthenga umene ndikupatsa.”
Sukuma, uye eNineve, lowana umuzi omkhulu, utshumayele kuwo intshumayelo engikutshela yona.
3 Yona anamvera mawu a Yehova ndipo anapita ku Ninive. Tsono Ninive unali mzinda waukulu kwambiri; wofunika masiku atatu kuwudutsa.
UJona wasesukuma, waya eNineve, njengokwelizwi leNkosi. Phela iNineve yayingumuzi omkhulu kakhulu, uhambo lwezinsuku ezintathu.
4 Yona analowa mu mzindawo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi. Iye ankalalikira kuti, “Atsala masiku makumi anayi kuti Ninive awonongedwe.”
UJona waseqala ukungena emzini, uhambo losuku olulodwa. Wamemeza, wathi: Kusesezinsuku ezingamatshumi amane, khona iNineve izagenqulwa.
5 Anthu a ku Ninive anakhulupirira Mulungu. Analengeza kuti aliyense, wamkulu ndi wamngʼono yemwe asale zakudya ndipo avale chiguduli.
Abantu beNineve basebekholwa kuNkulunkulu, bamemezela ukuzila ukudla, bagqoka amasaka, kusukela komkhulu wabo kwaze kwaba komncinyane wabo.
6 Mfumu ya ku Ninive itamva nkhaniyi, inatsika pa mpando wake waufumu, nivula mkanjo wake waufumu ndipo inavala chiguduli ndi kukhala pansi pa fumbi.
Ngoba ilizwi lafinyelela enkosini yeNineve; yasisukuma esihlalweni sayo sobukhosi, yakhulula isembatho sayo kuyo, yazimbomboza ngesaka, yahlala emlotheni.
7 Tsono mfumuyo inalengeza mu Ninive kuti, “Mwa lamulo lochokera kwa mfumu ndi akalonga ake: “Munthu aliyense kapenanso nyama, ngʼombe kapena nkhosa, zisadye kanthu kalikonse; musazilole kuti zidye kapena kumwa.
Yasimemezela yathi kuyo iNineve ngomthetho wenkosi labakhulu bayo, isithi: Kakungabi lomuntu, kumbe inyamazana, inkomo kumbe imvu, okuzanambitha loba yini; kakungadli, kakunganathi amanzi.
8 Koma anthu avale ziguduli, ndipo nyamanso aziveke ziguduli. Munthu aliyense azifuwula kwa Mulungu ndi mphamvu zake zonse. Anthuwo asiye makhalidwe awo oyipa ndi machitidwe achiwawa.
Kodwa kakuthi umuntu lenyamazana kwembeswe amasaka, bakhale kuNkulunkulu ngamandla, yebo, baphenduke, ngulowo lalowo endleleni yakhe embi, lodlakeleni olusezandleni zabo.
9 Angadziwe ndani? Mwina Mulungu nʼkutikhululukira ndipo mwa chifundo chake nʼkuleka kutikwiyira, ifeyo osawonongedwa.”
Ngubani owaziyo, uNkulunkulu angaphenduka azisole, aphenduke asuke kukuvutha kolaka lwakhe, ukuze singabhubhi.
10 Mulungu ataona zimene anthuwo anachita, ndi mmene anasiyira makhalidwe awo oyipa, anawachitira chifundo ndipo sanabweretse chiwonongeko chimene anawaopseza nacho.
UNkulunkulu wasebona imisebenzi yabo, ukuthi baphendukile endleleni yabo embi; uNkulunkulu wazisola ngobubi ayethe uzabenza kubo, akaze abenza.

< Yona 3 >