< Yona 3 >

1 Ndipo Yehova anayankhula ndi Yona kachiwiri kuti,
Ilizwi likaThixo laselifika kuJona ngokwesibili lathi:
2 “Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire uthenga umene ndikupatsa.”
“Hamba uye edolobheni elikhulu laseNiniva uyotshumayela kulo ilizwi engikunika lona.”
3 Yona anamvera mawu a Yehova ndipo anapita ku Ninive. Tsono Ninive unali mzinda waukulu kwambiri; wofunika masiku atatu kuwudutsa.
UJona walilalela ilizwi likaThixo, waya eNineve. Phela iNiniva yayilidolobho elikhulu kakhulu, ukulethekela lonke kwakuthatha insuku ezintathu.
4 Yona analowa mu mzindawo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi. Iye ankalalikira kuti, “Atsala masiku makumi anayi kuti Ninive awonongedwe.”
Ngelanga lokuqala, uJona wangena phakathi komuzi. Wamemezela wathi, “Kusele insuku ezingamatshumi amane kuphela ukuba iNiniva ichithwe.”
5 Anthu a ku Ninive anakhulupirira Mulungu. Analengeza kuti aliyense, wamkulu ndi wamngʼono yemwe asale zakudya ndipo avale chiguduli.
Abantu beNiniva babekholwa kuNkulunkulu. Bamemezela ukuthi kuzilwe ukudla, njalo bonke kusukela komkhulu kusiya komncinyane bavunula amasaka.
6 Mfumu ya ku Ninive itamva nkhaniyi, inatsika pa mpando wake waufumu, nivula mkanjo wake waufumu ndipo inavala chiguduli ndi kukhala pansi pa fumbi.
Ilizwi selifikile enkosini yaseNiniva, yasukuma esihlalweni sayo sobukhosi, yakhumula izembatho zayo zobukhosi, yazembathisa isaka yahlala phansi ebhuqwini.
7 Tsono mfumuyo inalengeza mu Ninive kuti, “Mwa lamulo lochokera kwa mfumu ndi akalonga ake: “Munthu aliyense kapenanso nyama, ngʼombe kapena nkhosa, zisadye kanthu kalikonse; musazilole kuti zidye kapena kumwa.
Yase ikhupha isimemezelo eNiniva esithi: “Ngomthetho wenkosi lezikhulu zayo: Akungavunyelwa muntu kumbe inyamazana, imihlambi yenkomo loba eyezimvu ukuthi ithinte ulutho oludliwayo; makungavunyelwa kudle kumbe kunathe.
8 Koma anthu avale ziguduli, ndipo nyamanso aziveke ziguduli. Munthu aliyense azifuwula kwa Mulungu ndi mphamvu zake zonse. Anthuwo asiye makhalidwe awo oyipa ndi machitidwe achiwawa.
Kodwa akuthi umuntu loba yinyamazana kwembathe amasaka. Wonke umuntu kamemeze ngokukhawuleza kuNkulunkulu. Kabadele izindlela zabo zobubi lobudlwangudlwangu babo.
9 Angadziwe ndani? Mwina Mulungu nʼkutikhululukira ndipo mwa chifundo chake nʼkuleka kutikwiyira, ifeyo osawonongedwa.”
Ngubani okwaziyo na? Mhlawumbe uNkulunkulu angadeda kuthi ngesihawu sakhe aphenduke elakeni lwakhe olwesabekayo ukuze singabhubhi.”
10 Mulungu ataona zimene anthuwo anachita, ndi mmene anasiyira makhalidwe awo oyipa, anawachitira chifundo ndipo sanabweretse chiwonongeko chimene anawaopseza nacho.
Kwathi uNkulunkulu esebonile abakwenzayo ukuthi baguquka ezindleleni zabo zobubi, wabazwela isihawu kazabe esabehlisela incithakalo ayesonge ngayo.

< Yona 3 >