< Yona 2 >
1 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
Desde las entrañas del pez oró Jonás a Yahvé, y dijo:
2 Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol )
“Clamé a Yahvé en mi angustia, y Él me oyó; desde el vientre del scheol pedí auxilio, y Tú has atendido a mi voz. (Sheol )
3 Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
Me arrojaste a lo más profundo, al seno de los mares; me circundaron aguas torrenciales, todas tus olas y ondas pasaron sobre mí.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
Entonces dije: «Desterrado he sido de delante de tus ojos, pero volveré a contemplar tu santo Templo».
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
Las aguas me han encerrado hasta el alma, me rodea el abismo y los juncos han enredado mi cabeza.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
He descendido hasta las raíces de las montañas; los cerrojos de la tierra me encerraron para siempre; pero Tú sacaste mi vida desde la fosa, Yahvé, Dios mío.
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
Cuando mi alma desfallecía dentro de mí, me acordé de Yahvé; y llegó mi plegaria a tu presencia en el templo santo tuyo.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
Los que van tras las mentirosas vanidades abandonan su misericordia.
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
Mas yo te ofreceré sacrificios con cánticos de alabanza; cumpliré los votos que he hecho, pues de Yahvé viene la salvación.”
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
Entonces Yahvé dio orden al pez, y este vomitó a Jonás en tierra.