< Yona 2 >

1 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
И замоли се Јона Господу Богу свом из трбуха рибљег,
2 Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
И рече: Завапих у невољи својој ка Господу, и услиши ме; из утробе гробне повиках, и Ти чу глас мој. (Sheol h7585)
3 Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
Јер си ме бацио у дубине, у срце мору, и вода ме оптече; све поплаве Твоје и вали Твоји прелазише преко мене.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
И рекох: Одбачен сам испред очију Твојих; али ћу још гледати свету цркву Твоју.
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
Оптекоше ме воде до душе, бездана ме опколи, сита омота ми се око главе.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
Сиђох до крајева горских, преворнице земаљске нада мном су довека; али Ти извади живот мој из јаме, Господе Боже мој.
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
Кад нестајаше душа моја у мени, поменух Господа, и молитва моја дође к Теби, у свету цркву Твоју.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
Који држе лажне таштине, остављају своју милост.
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
А ја ћу Ти гласом захвалним принети жртву, испунити што сам заветовао; спасење је у Господа.
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
И Господ заповеди риби, те избљува Јону на земљу.

< Yona 2 >