< Yona 2 >
1 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
Or, Jonas fit sa prière à l'Éternel son Dieu, dans le ventre du poisson.
2 Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol )
Et il dit: Dans ma détresse j'ai invoqué l'Éternel, et il m'a répondu; du sein du Sépulcre j'ai crié, et tu as entendu ma voix. (Sheol )
3 Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
Tu m'as jeté dans l'abîme, au cœur de la mer, et le courant m'a environné. Toutes tes vagues et tous tes flots ont passé sur moi.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
Et moi je disais: Je suis rejeté de devant tes yeux! Cependant je verrai encore le temple de ta sainteté!
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
Les eaux m'ont environné jusqu'à l'âme; l'abîme m'a enveloppé; les roseaux ont entouré ma tête.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
J'étais descendu jusqu'aux racines des montagnes; la terre avait fermé sur moi ses barres pour toujours. Mais tu as fait remonter ma vie de la fosse, Éternel, mon Dieu!
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
Quand mon âme défaillait en moi, je me suis souvenu de l'Éternel, et ma prière est parvenue jusqu'à toi, dans le temple de ta sainteté.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
Ceux qui s'attachent à des vanités trompeuses abandonnent celui qui leur fait miséricorde;
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
Mais moi, je t'offrirai des sacrifices avec chant de louange, j'accomplirai les vœux que j'ai faits. Le salut est de l'Éternel!
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
Alors l'Éternel commanda au poisson, et le poisson vomit Jonas sur la terre.