< Yona 2 >

1 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
Ja Joona rukoili Herraa, Jumalaansa, kalan sisässä
2 Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
ja sanoi: "Minä huusin ahdistuksessani Herraa, ja hän vastasi minulle. Tuonelan kohdussa minä huusin apua, ja sinä kuulit minun ääneni. (Sheol h7585)
3 Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
Sinä syöksit minut syvyyteen, merten sydämeen, ja virta ympäröitsi minut, kaikki sinun kuohusi ja aaltosi vyöryivät minun ylitseni.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
Minä ajattelin: Olen karkoitettu pois sinun silmiesi edestä. Kuitenkin minä saan vielä katsella sinun pyhää temppeliäsi.
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
Vedet piirittivät minut aina sieluun asti, syvyys ympäröitsi minut, kaisla kietoutui päähäni.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
Minä vajosin alas vuorten perustuksiin asti, maan salvat sulkeutuivat minun ylitseni iankaikkisesti. Mutta sinä nostit minun henkeni ylös haudasta, Herra, minun Jumalani.
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
Kun sieluni nääntyi minussa, minä muistin Herraa, ja minun rukoukseni tuli sinun tykösi, sinun pyhään temppeliisi.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
Ne, jotka kunnioittavat vääriä jumalia, hylkäävät armonantajansa.
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
Mutta minä tahdon uhrata sinulle kiitoksen kaikuessa. Mitä olen luvannut, sen minä täytän. Herrassa on pelastus."
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
Sitten Herra käski kalaa, ja se oksensi Joonan kuivalle maalle.

< Yona 2 >