< Yona 2 >

1 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
And Jonah prayed to the Lord, his God, from the belly of the fish.
2 Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
And he said: “I cried out to the Lord from my tribulation, and he heeded me. From the belly of hell, I cried out, and you heeded my voice. (Sheol h7585)
3 Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
And you have thrown me into the deep, in the heart of the sea, and a flood has encircled me. All your whirlpools and your waves have passed over me.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
And I said: I am expelled from the sight of your eyes. Yet, truly, I will see your holy temple again.
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
The waters surrounded me, even to the soul. The abyss has walled me in. The ocean has covered my head.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
I descended to the base of the mountains. The bars of the earth have enclosed me forever. And you will raise up my life from corruption, Lord, my God.
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
When my soul was in anguish within me, I called to mind the Lord, so that my prayer might come to you, to your holy temple.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
Those who in vain observe vanities, abandon their own mercy.
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
But I, with a voice of praise, will sacrifice to you. I will repay whatever I have vowed to the Lord, because of my salvation.”
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
And the Lord spoke to the fish, and it vomited Jonah onto dry land.

< Yona 2 >