< Yona 2 >

1 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
I modlil se Jonáš Hospodinu Bohu svému v střevách té ryby,
2 Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
A řekl: Z ssoužení svého volal jsem k Hospodinu, a ozval se mi; z břicha hrobu křičel jsem, a vyslyšel jsi hlas můj. (Sheol h7585)
3 Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
Nebo jsi mne uvrhl do hlubiny, do prostřed moře, a řeka obklíčila mne; všecka vlnobití tvá i rozvodnění tvá na mne se svalila.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
Bylť jsem již řekl: Vyhnán jsem od očí tvých, ale ještěť pohledím na tvůj svatý chrám.
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
Obklíčily mne vody až k duši, propast obklíčila mne, lekno otočilo se okolo hlavy mé.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
Až k spodkům hor dostal jsem se, země závorami svými zalehla mi na věčnost, ty jsi však vysvobodil od porušení život můj, ó Hospodine Bože můj.
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
Když se svírala ve mně duše má, na Hospodina jsem se rozpomínal, i přišla k tobě modlitba má do chrámu svatého tvého.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
Kteříž ostříhají marností pouhých, dobroty Boží se zbavují.
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
Já pak s hlasem díkčinění obětovati budu tobě; což jsem slíbil, splním. Hojné vysvobození jest u Hospodina.
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
Rozkázal pak byl Hospodin rybě té, i vyvrátila Jonáše na břeh.

< Yona 2 >