< Yohane 1 >
1 Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
Kumatangilo kuvali kwina linzwi, mi linzwi lyivena kwa Ireeza, mi linzwi ivali Ireeza.
2 Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
Ichi chiva kwina ku matangilo ni Ireeza.
3 Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
Zintu zonse ziva pangwa kwali, mi nikusena iye kakwina nanga chintu chonke chisena chapangwa chiva pangwa
4 Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
Mwali kuva kwina vuhalo, mi vuhalo vu vwina mwiseli lya vantu vonse.
5 Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
Iseli lyi munika mukwelima, mi mukwelima kena uvakomi iseli.
6 Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
Kuva kwina mukwame yava ku tumitwe kwa Ireeza, uzo izina lyakwe ivali Johani.
7 Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
Avakezi cho kuva Impaki kwiza ku paka ze seli, njokuti vonse njete va zumine kakwe.
8 Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
Johani kena vali iseli, kono avakezi kuti za pake ze seli.
9 Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
Ivali iseli lyeniti, lyiha iseli ku vantu vonse, lyikeza mwi fasi.
10 Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
Avena mwi fasi, mi fasi lyiva pangwa kwali, mi fasi kena lyiva kumwizi.
11 Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
Avakezi kuzakwe, mi zakwe kena ziva mutambuli.
12 Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
Kono kwavo vangi vava mutambuli, vava zumini mwi zina lyakwe, Avahi inswanelo yo kuva vana ve Ireeza.
13 ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
Ava kena vava zalwa cha malaha, kapa kentato ye nyama, kapa ke ntato yo muntu, kono ye Ireeza.
14 Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
Mi linzwi chilyeza kuva inyama niku hala mukati ketu. Tuva voni inkanya yakwe, inkanya sina yozo mi iye vulyo yava kuka zwilila kwe Shetu, ye zwile chisemo ni niti.
15 Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
Jahani avapaki kuamana iye niku lilila kwakwe, na wamba, uzu njiyena wa kwavo vani va wambi, 'uzo yo keza mumasule angu u i hitilila, kakuli kwavali kwina ni niseni kuva kwateni ime.'”
16 Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
Kuzwa ku kwizula kwakwe tuva tambili chisemo kuzwa chisemo.
17 Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
Kaho mulao uvahewa kwa Mushe. Chisemo ne niti ziva kezi ka Jesu Kreste.
18 Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
Kakwina yava voni Ireeza ke nako ni nako. Ireeza yenkefela, yena hembali ni chizuva che Shetu, ava mwizivahazi.
19 Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
Mi uvu nji vupaki bwa Johani aho majuda hava tumina ma Prisita ni naLivite kwali kuzwa kwa Jerusalema kuka muvuza, “njewe ni?”
20 Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
Chentukuluho chawamba, mi kena va sampuli, kono che tava, “kena njime Kreste.”
21 Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
Cwale chiva muvuza, “Uchinzi cwale? Njewe Eliya?” Cha cho, “kena ime,” Chiva cho, “Umuporofita?” Chetava,” Ne.”
22 Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
Cwale chiva wamba kwakwe, “njewe ni, njokuti tuwole kukaha inkalavo kwavo vakatutuma? Uwambanzi kuama iwe umwine?”
23 Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
Chacho, “ni mulumo, ulila mwihalaupa: 'Mupange inzila ya Simwine iwoloke; sina muporofita Isaya mwava teli.”
24 Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
Mi avo vavatumwa vavali ma Pharisi.
25 anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
Chiva, muvuza niku muwambila, “Chinzi hokoloveza cwale heva kena njewe Kreste kapa Eliya kapa muporofita?”
26 Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
Mi Johani cha vetava, kuwamba, “nikoloveza cha menzi. Kono mukati kenu kuzimene muntu imusezi;
27 Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
iye yani chilila, uzo tukwele twe nsangu kani swaneli kusumununa.”
28 Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
Izi zintu ziva pangwini Bethani kwi neku lyimwi lya Jordani, uko Johani kwava ka kolovelezwa.
29 Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
Izuva lyi chilila Johani cha vona Jesu na keza kwali, “Lole, kwina imbelele ya Ireeza izwisa zivi mwi fasi!
30 Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
Uzu njiyena kuni va wambi, 'iye yokeza ku masule angu uni hitilila, kakuli kwavali kwina nini seni kuva kwateni.'
31 Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
Kena niva kumwizi, kono ivapangali kuti e zivahazwe ku isilaele kuti niva ku koloveza ni menzi.”
32 Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
Johani avapaki, kuwamba, “na vona Luho nilushetumuka sina inkuva kwi wulu, mi lyeza kwi kala hewulu lyakwe.
33 Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
kena niva mwi zivi, kono iye yava ni tumi kwiza kukoloveza ni menzi wawamba kwangu, 'Kozo yete uvone Luhuho ni lushemukela hali ni kwikala hali, njeye yo koloveza mu Luhuho lu Jolola.'
34 Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
Niva voni vonse niku paka kuti uzu nji mwana wa Ireeza.”
35 Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
Hape, izuva lyi chilila, sina Johani hava kuzimene ni Varutwana vo vele,
36 Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
vava voni Jesu na yenda hembali, mi Johani chawamba, “Lole, Imbela ye Ireeza!”
37 Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
Mi varutwana vakwe vava muzuwi na wamba izi, mi chive chilila Jesu.
38 Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
Cwale Jesu chava vona niva mwichilile mi chava wambila, “Musakanzi?” Chivetava, “Rabbi (Itoloka muruti), Wikala kwi?”
39 Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
Cha wamba kuvali, “mwize ze muvone.” Cwale chiva keza kwiza kuvona kwekala; vave kali naye ilyo izuva, hakuli chivali inako ikwana ikumu.
40 Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
Zumwi kuvali ava zuwi Johani na wamba mi nikwi chilila Jesu ivali nji Andrew, mukulwa Simone Pitolosi.
41 Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
Avatangi kuwana mukulwe Simone mi chawamba kwali, “Twawana Messiah” (italusa Kreste).
42 Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
Ava muleti kwa Jesu. Mi Jesu cha mulola niku wamba, “Njewe Simoni mwana Johani, Kosupwe Cephas” (itoloka Pitolosi).
43 Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
Izuva lyi chilila, Jesu hava kusaka kuyenda kwa Galilee, cha wana Filipi niku muwambila, “Nichilile.”
44 Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
Hanu Filipi ava kukazwililekwa Bethsaida, intoropo ya Andrew ni Pitolosi.
45 Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
Filipi chawana Natheniel niku wamba kwali, “Iye uzo Mushe ava ñoli mumulao, ni maporofita, chitwa muwana: Jesu mwana a Josefa, kwa Nazereta.”
46 Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
Nathaniel chamu wambila, “kwina chintu chilotu chiwola kuzwa kwa Narazeta?” Fiipi chamu wambila, “wize zo vone.”
47 Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
Jesu chavona Natheniel nakeza kwali niku wamba zali, “vone, mu isilaele we niti, yasena kuchenga!”
48 Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
Nathaniel cha mu wambila, “unizini vule?” Jesu chetava niku mu wambila, “Filipi naseni kukusumpa, ni wina munsi ye chikuni cha feige, niva kuvoni.”
49 Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
Nathaniel che tava, “Rabbi, umwana we Ireeza! umurena wa Isilaele!”
50 Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
Jesu che tava niku mu wambila, “kakuli na wamba kwako, 'naku vona munsi ye chikuni cha feige; uzumina? Movone zintu zikando kuhita izi.”
51 Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”
mi chawamba, “Zeniti, zeniti, ni wamba kwako, Kovone ma wulu ne yalukite, ni ma ñiloyi e Ireeza azwa hansi nikuya kwi wulu hewulu lya Mwana a Muntu.”