< Yohane 1 >
1 Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
In the beginning was the Word, and the Word was with God, and the Word was God.
2 Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
He was in the beginning with God.
3 Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
Everything was made through Him, and without Him nothing was made that was made.
4 Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
In Him was life, and that life was the light of mankind.
5 Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
The light shines in the darkness, but the darkness hasn’t overcome it.
6 Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
There was a man sent from God, whose name was John.
7 Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
This man came as a witness, to testify about the light, that all through him might believe.
8 Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
He wasn’t that light, but was sent as a witness of that light.
9 Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
The true light that enlightens everyone was coming into the world.
10 Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
The Word was in the world, and though the world was made through Him, the world didn’t recognize Him.
11 Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
He came to His own, and those who were His own didn’t receive Him.
12 Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
But as many as received Him, to them He gave the right to become God’s children, to those who believe in His name:
13 ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
who were born, not of blood, nor of the will of the flesh, nor of the will of man, but of God.
14 Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
The Word became flesh and lived among us, and we saw His glory, the glory as of the only Son of the Father, full of grace and truth.
15 Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
John testified about Him. He cried out, saying, “This was He who I told you about when I said, ‘He who comes after me has surpassed me because He was before me.’”
16 Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
From His fullness we have all received grace upon grace.
17 Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
The Law was given through Moses, but grace and truth came through Jesus Christ.
18 Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
No one has ever seen God, but God’s only born Son, who is near to the heart of His Father, has made Him known.
19 Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
Now this is the testimony of John, when the Jews sent priests and Levites from Jerusalem to ask him, “Who are you?”
20 Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
He confessed, and didn’t deny, but confessed, “I’m not the Christ.”
21 Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
They asked him, “Then who are you? Are you Elijah?” He said, “I am not.” “Are you the Prophet?” He answered, “No.”
22 Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
Then they asked him, “Who are you? Give us an answer to take back to those who sent us. What do you say about yourself?”
23 Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
John replied in the words of Isaiah the prophet, “I am the voice of one calling in the desert, ‘Make straight the way for the Lord.’”
24 Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
Now those who were sent were Pharisees.
25 anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
They asked him, saying, “Why then do you baptize if you aren’t the Christ, nor Elijah, nor the Prophet?”
26 Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
John answered them, saying, “I baptize with water, but One stands among you that you don’t know.
27 Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
It is He who, coming after me, is preferred before me, whose sandal strap I’m not worthy to untie.”
28 Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
This all happened at Bethany on the other side of the Jordan, where John was baptizing.
29 Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
The next day, John saw Jesus coming toward him, and said, “Look! God’s Lamb who takes away the sin of the world!
30 Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
This is the One I meant when I said, ‘A man who comes after me is preferred before me because He existed before me.’
31 Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
I didn’t know Him, but the reason I came baptizing with water was that He might be revealed to Israel.”
32 Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
John testified, saying, “I saw the Spirit descending from Heaven like a dove, and He remained upon Him.
33 Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
I wouldn’t have known Him, but He who sent me to baptize with water told me, ‘Whoever you see the Spirit descending upon, and remaining on Him, this is He who baptizes with the Holy Spirit.’
34 Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
I have seen and I testify that this is God’s Son.”
35 Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
The next day, John again stood with two of His disciples.
36 Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
When he saw Jesus passing by, he said, “Look, God’s Lamb!”
37 Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
The two disciples heard him say this, and they followed Jesus.
38 Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
Jesus turned, and seeing them following, asked them, “What are you looking for?” They said to Him, “Rabbi” (which, when translated, means Teacher), “Where are You staying?”
39 Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
He told them, “Come and see.” They came and saw where He was staying, and spent that day with Him. It was about the tenth hour.
40 Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
Andrew, Simon Peter’s brother, was one of the two who heard what John had said and who had followed Jesus.
41 Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
The first thing Andrew did was to find his brother, Simon, and tell him, “We have found the Messiah” (that is, translated, the Christ).
42 Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
Andrew brought Simon to Jesus. Jesus looked at him, and said, “You are Simon the son of Jonah. You will be called Cephas” (which is translated Peter).
43 Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
The next day Jesus decided to leave for Galilee. Finding Philip, he told him, “Follow me.”
44 Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
Philip was from Bethsaida, the city of Andrew and Peter.
45 Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
Philip found Nathanael and told him, “We have found Him who Moses in the Law, and also the prophets, wrote about — Jesus of Nazareth, the son of Joseph.”
46 Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
Nathanael asked Philip, “Can anything good come out of Nazareth?” Philip told Nathanael, “Come and see.”
47 Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
Jesus saw Nathanael coming toward Him, and said of Nathanael, “Look! An Israelite indeed, who has no deceit in him!”
48 Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
Nathanael asked Him, “How do You know me?” Jesus answered, “Before Philip called you, when you were under the fig tree, I saw you.”
49 Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
Nathanael answered, “Rabbi, You are God’s Son. You are the King of Israel.”
50 Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
Jesus said to him, “Because I told you that I saw you under the fig tree, do you believe? You will see greater things than these.”
51 Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”
And He told him, “Most assuredly, I tell you, you will see Heaven opened, and God’s angels ascending and descending on the Son of Man.”