< Yohane 8 >

1 Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi.
ปฺรตฺยูเษ ยีศุ: ปนรฺมนฺทิรมฺ อาคจฺฉตฺ
2 Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa.
ตต: สรฺเวฺวษุ โลเกษุ ตสฺย สมีป อาคเตษุ ส อุปวิศฺย ตานฺ อุปเทษฺฏุมฺ อารภตฯ
3 Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo
ตทา อธฺยาปกา: ผิรูศินญฺจ วฺยภิจารกรฺมฺมณิ ธฺฤตํ สฺตฺริยเมกามฺ อานิย สรฺเวฺวษำ มเธฺย สฺถาปยิตฺวา วฺยาหรนฺ
4 anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo.
เห คุโร โยษิตมฺ อิมำ วฺยภิจารกรฺมฺม กุรฺวฺวาณำ โลกา ธฺฤตวนฺต: ฯ
5 Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?”
เอตาทฺฤศโลกา: ปาษาณาฆาเตน หนฺตวฺยา อิติ วิธิรฺมูสาวฺยวสฺถาคฺรนฺเถ ลิขิโตสฺติ กินฺตุ ภวานฺ กิมาทิศติ?
6 Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye. Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake.
เต ตมปวทิตุํ ปรีกฺษาภิปฺราเยณ วากฺยมิทมฺ อปฺฤจฺฉนฺ กินฺตุ ส ปฺรหฺวีภูย ภูมาวงฺคลฺยา เลขิตุมฺ อารภตฯ
7 Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.”
ตตไสฺต: ปุน: ปุน: ปฺฤษฺฏ อุตฺถาย กถิตวานฺ ยุษฺมากํ มเธฺย โย ชโน นิรปราธี เสอว ปฺรถมมฺ เอนำ ปาษาเณนาหนฺตุฯ
8 Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.
ปศฺจาตฺ ส ปุนศฺจ ปฺรหฺวีภูย ภูเมา เลขิตุมฺ อารภตฯ
9 Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo.
ตำ กถํ ศฺรุตฺวา เต สฺวสฺวมนสิ ปฺรโพธํ ปฺราปฺย เชฺยษฺฐานุกฺรมํ เอไกกศ: สรฺเวฺว พหิรคจฺฉนฺ ตโต ยีศุเรกากี ตยกฺตฺโตภวตฺ มธฺยสฺถาเน ทณฺฑายมานา สา โยษา จ สฺถิตาฯ
10 Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”
ตตฺปศฺจาทฺ ยีศุรุตฺถาย ตำ วนิตำ วินา กมปฺยปรํ น วิโลกฺย ปฺฤษฺฏวานฺ เห วาเม ตวาปวาทกา: กุตฺร? โกปิ ตฺวำ กึ น ทณฺฑยติ?
11 Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.” “Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”
สาวทตฺ เห มเหจฺฉ โกปิ น ตทา ยีศุรโวจตฺ นาหมปิ ทณฺฑยามิ ยาหิ ปุน: ปาปํ มาการฺษี: ฯ
12 Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”
ตโต ยีศุ: ปุนรปิ โลเกภฺย อิตฺถํ กถยิตุมฺ อารภต ชคโตหํ โชฺยติ: สฺวรูโป ย: กศฺจินฺ มตฺปศฺจาท คจฺฉติ ส ติมิเร น ภฺรมิตฺวา ชีวนรูปำ ทีปฺตึ ปฺราปฺสฺยติฯ
13 Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”
ตต: ผิรูศิโน'วาทิษุสฺตฺวํ สฺวารฺเถ สฺวยํ สากฺษฺยํ ททาสิ ตสฺมาตฺ ตว สากฺษฺยํ คฺราหฺยํ น ภวติฯ
14 Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita.
ตทา ยีศุ: ปฺรตฺยุทิตวานฺ ยทฺยปิ สฺวารฺเถ'หํ สฺวยํ สากฺษฺยํ ททามิ ตถาปิ มตฺ สากฺษฺยํ คฺราหฺยํ ยสฺมาทฺ อหํ กุต อาคโตสฺมิ กฺว ยามิ จ ตทหํ ชานามิ กินฺตุ กุต อาคโตสฺมิ กุตฺร คจฺฉามิ จ ตทฺ ยูยํ น ชานีถฯ
15 Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense.
ยูยํ เลากิกํ วิจารยถ นาหํ กิมปิ วิจารยามิฯ
16 Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma.
กินฺตุ ยทิ วิจารยามิ ตรฺหิ มม วิจาโร คฺรหีตโวฺย ยโตหมฺ เอกากี นาสฺมิ เปฺรรยิตา ปิตา มยา สห วิทฺยเตฯ
17 Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka.
ทฺวโย รฺชนโย: สากฺษฺยํ คฺรหณียํ ภวตีติ ยุษฺมากํ วฺยวสฺถาคฺรนฺเถ ลิขิตมสฺติฯ
18 Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”
อหํ สฺวารฺเถ สฺวยํ สากฺษิตฺวํ ททามิ ยศฺจ มม ตาโต มำ เปฺรริตวานฺ โสปิ มทรฺเถ สากฺษฺยํ ททาติฯ
19 Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?” Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.”
ตทา เต'ปฺฤจฺฉนฺ ตว ตาต: กุตฺร? ตโต ยีศุ: ปฺรตฺยวาทีทฺ ยูยํ มำ น ชานีถ มตฺปิตรญฺจ น ชานีถ ยทิ มามฺ อกฺษาสฺยต ตรฺหิ มม ตาตมปฺยกฺษาสฺยตฯ
20 Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.
ยีศุ รฺมนฺทิร อุปทิศฺย ภณฺฑาคาเร กถา เอตา อกถยตฺ ตถาปิ ตํ ปฺรติ โกปิ กรํ โนทโตลยตฺฯ
21 Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”
ตต: ปรํ ยีศุ: ปุนรุทิตวานฺ อธุนาหํ คจฺฉามิ ยูยํ มำ คเวษยิษฺยถ กินฺตุ นิไช: ปาไป รฺมริษฺยถ ยตฺ สฺถานมฺ อหํ ยาสฺยามิ ตตฺ สฺถานมฺ ยูยํ ยาตุํ น ศกฺษฺยถฯ
22 Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’”
ตทา ยิหูทียา: ปฺราโวจนฺ กิมยมฺ อาตฺมฆาตํ กริษฺยติ? ยโต ยตฺ สฺถานมฺ อหํ ยาสฺยามิ ตตฺ สฺถานมฺ ยูยํ ยาตุํ น ศกฺษฺยถ อิติ วากฺยํ พฺรวีติฯ
23 Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino.
ตโต ยีศุเสฺตภฺย: กถิตวานฺ ยูยมฺ อธ: สฺถานียา โลกา อหมฺ อูรฺทฺวฺวสฺถานีย: ยูยมฺ เอตชฺชคตฺสมฺพนฺธียา อหมฺ เอตชฺชคตฺสมฺพนฺธีโย นฯ
24 Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”
ตสฺมาตฺ กถิตวานฺ ยูยํ นิไช: ปาไป รฺมริษฺยถ ยโตหํ ส ปุมานฺ อิติ ยทิ น วิศฺวสิถ ตรฺหิ นิไช: ปาไป รฺมริษฺยถฯ
25 Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?” Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi,
ตทา เต 'ปฺฤจฺฉนฺ กสฺตฺวํ? ตโต ยีศุ: กถิตวานฺ ยุษฺมากํ สนฺนิเธา ยสฺย ปฺรสฺตาวมฺ อา ปฺรถมาตฺ กโรมิ เสอว ปุรุโษหํฯ
26 ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”
ยุษฺมาสุ มยา พหุวากฺยํ วกฺตฺตวฺยํ วิจารยิตวฺยญฺจ กินฺตุ มตฺเปฺรรยิตา สตฺยวาที ตสฺย สมีเป ยทหํ ศฺรุตวานฺ ตเทว ชคเต กถยามิฯ
27 Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake.
กินฺตุ ส ชนเก วากฺยมิทํ โปฺรกฺตฺตวานฺ อิติ เต นาพุธฺยนฺตฯ
28 Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa.
ตโต ยีศุรกถยทฺ ยทา มนุษฺยปุตฺรมฺ อูรฺทฺวฺว อุตฺถาปยิษฺยถ ตทาหํ ส ปุมานฺ เกวล: สฺวยํ กิมปิ กรฺมฺม น กโรมิ กินฺตุ ตาโต ยถา ศิกฺษยติ ตทนุสาเรณ วากฺยมิทํ วทามีติ จ ยูยํ ชฺญาตุํ ศกฺษฺยถฯ
29 Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.”
มตฺเปฺรรยิตา ปิตา มามฺ เอกากินํ น ตฺยชติ ส มยา สารฺทฺธํ ติษฺฐติ ยโตหํ ตทภิมตํ กรฺมฺม สทา กโรมิฯ
30 Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.
ตทา ตไสฺยตานิ วากฺยานิ ศฺรุตฺวา พหุวสฺตาสฺมินฺ วฺยศฺวสนฺฯ
31 Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga.
เย ยิหูทียา วฺยศฺวสนฺ ยีศุเสฺตโภฺย'กถยตฺ
32 Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”
มม วาเกฺย ยทิ ยูยมฺ อาสฺถำ กุรุถ ตรฺหิ มม ศิษฺยา ภูตฺวา สตฺยตฺวํ ชฺญาสฺยถ ตต: สตฺยตยา ยุษฺมากํ โมกฺโษ ภวิษฺยติฯ
33 Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’”
ตทา เต ปฺรตฺยวาทิษุ: วยมฺ อิพฺราหีโม วํศ: กทาปิ กสฺยาปิ ทาสา น ชาตาสฺตรฺหิ ยุษฺมากํ มุกฺตฺติ รฺภวิษฺยตีติ วากฺยํ กถํ พฺรวีษิ?
34 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo.
ตทา ยีศุ: ปฺรตฺยวททฺ ยุษฺมานหํ ยถารฺถตรํ วทามิ ย: ปาปํ กโรติ ส ปาปสฺย ทาส: ฯ
35 Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. (aiōn g165)
ทาสศฺจ นิรนฺตรํ นิเวศเน น ติษฺฐติ กินฺตุ ปุโตฺร นิรนฺตรํ ติษฺฐติฯ (aiōn g165)
36 Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu.
อต: ปุโตฺร ยทิ ยุษฺมานฺ โมจยติ ตรฺหิ นิตานฺตเมว มุกฺตฺตา ภวิษฺยถฯ
37 Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu.
ยุยมฺ อิพฺราหีโม วํศ อิตฺยหํ ชานามิ กินฺตุ มม กถา ยุษฺมากมฺ อนฺต: กรเณษุ สฺถานํ น ปฺราปฺนุวนฺติ ตสฺมาทฺเธโต รฺมำ หนฺตุมฺ อีหเธฺวฯ
38 Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”
อหํ สฺวปิตุ: สมีเป ยทปศฺยํ ตเทว กถยามิ ตถา ยูยมปิ สฺวปิตุ: สมีเป ยทปศฺยต ตเทว กุรุเธฺวฯ
39 Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.” Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita.
ตทา เต ปฺรตฺยโวจนฺ อิพฺราหีมฺ อสฺมากํ ปิตา ตโต ยีศุรกถยทฺ ยทิ ยูยมฺ อิพฺราหีม: สนฺตานา อภวิษฺยต ตรฺหิ อิพฺราหีม อาจารณวทฺ อาจริษฺยตฯ
40 Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi.
อีศฺวรสฺย มุขาตฺ สตฺยํ วากฺยํ ศฺรุตฺวา ยุษฺมานฺ ชฺญาปยามิ โยหํ ตํ มำ หนฺตุํ เจษฺฏเธฺว อิพฺราหีมฺ เอตาทฺฤศํ กรฺมฺม น จการฯ
41 Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.” Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”
ยูยํ สฺวสฺวปิตุ: กรฺมฺมาณิ กุรุถ ตทา ไตรุกฺตฺตํ น วยํ ชารชาตา อสฺมากมฺ เอเกอว ปิตาสฺติ ส เอเวศฺวร:
42 Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha.
ตโต ยีศุนา กถิตมฺ อีศฺวโร ยทิ ยุษฺมากํ ตาโตภวิษฺยตฺ ตรฺหิ ยูยํ มยิ เปฺรมากริษฺยต ยโตหมฺ อีศฺวรานฺนิรฺคตฺยาคโตสฺมิ สฺวโต นาคโตหํ ส มำ ปฺราหิโณตฺฯ
43 Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga.
ยูยํ มม วากฺยมิทํ น พุธฺยเธฺว กุต: ? ยโต ยูยํ มโมปเทศํ โสฒุํ น ศกฺนุถฯ
44 Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza.
ยูยํ ไศตานฺ ปิตุ: สนฺตานา เอตสฺมาทฺ ยุษฺมากํ ปิตุรภิลาษํ ปูรยถ ส อา ปฺรถมาตฺ นรฆาตี ตทนฺต: สตฺยตฺวสฺย เลโศปิ นาสฺติ การณาทต: ส สตฺยตายำ นาติษฺฐตฺ ส ยทา มฺฤษา กถยติ ตทา นิชสฺวภาวานุสาเรไณว กถยติ ยโต ส มฺฤษาภาษี มฺฤโษตฺปาทกศฺจฯ
45 Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine!
อหํ ตถฺยวากฺยํ วทามิ การณาทสฺมาทฺ ยูยํ มำ น ปฺรตีถฯ
46 Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira?
มยิ ปาปมสฺตีติ ปฺรมาณํ ยุษฺมากํ โก ทาตุํ ศกฺโนติ? ยทฺยหํ ตถฺยวากฺยํ วทามิ ตรฺหิ กุโต มำ น ปฺรติถ?
47 Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”
ย: กศฺจน อีศฺวรีโย โลก: ส อีศฺวรียกถายำ มโน นิธตฺเต ยูยมฺ อีศฺวรียโลกา น ภวถ ตนฺนิทานาตฺ ตตฺร น มนำสิ นิธเทฺวฯ
48 Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”
ตทา ยิหูทียา: ปฺรตฺยวาทิษุ: ตฺวเมก: โศมิโรณีโย ภูตคฺรสฺตศฺจ วยํ กิมิทํ ภทฺรํ นาวาทิษฺม?
49 Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza.
ตโต ยีศุ: ปฺรตฺยวาทีตฺ นาหํ ภูตคฺรสฺต: กินฺตุ นิชตาตํ สมฺมเนฺย ตสฺมาทฺ ยูยํ มามฺ อปมนฺยเธฺวฯ
50 Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza.
อหํ สฺวสุขฺยาตึ น เจษฺเฏ กินฺตุ เจษฺฏิตา วิจารยิตา จาปร เอก อาเสฺตฯ
51 Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.” (aiōn g165)
อหํ ยุษฺมภฺยมฺ อตีว ยถารฺถํ กถยามิ โย นโร มทียํ วาจํ มนฺยเต ส กทาจน นิธนํ น ทฺรกฺษฺยติฯ (aiōn g165)
52 Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ (aiōn g165)
ยิหูทียาสฺตมวทนฺ ตฺวํ ภูตคฺรสฺต อิตีทานีมฺ อไวษฺมฯ อิพฺราหีมฺ ภวิษฺยทฺวาทินญฺจ สรฺเวฺว มฺฤตา: กินฺตุ ตฺวํ ภาษเส โย นโร มม ภารตีํ คฺฤหฺลาติ ส ชาตุ นิธานาสฺวาทํ น ลปฺสฺยเตฯ (aiōn g165)
53 Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”
ตรฺหิ ตฺวํ กิมฺ อสฺมากํ ปูรฺวฺวปุรุษาทฺ อิพฺราหีโมปิ มหานฺ? ยสฺมาตฺ โสปิ มฺฤต: ภวิษฺยทฺวาทิโนปิ มฺฤตา: ตฺวํ สฺวํ กํ ปุมำสํ มนุเษ?
54 Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine.
ยีศุ: ปฺรตฺยโวจทฺ ยทฺยหํ สฺวํ สฺวยํ สมฺมเนฺย ตรฺหิ มม ตตฺ สมฺมนนํ กิมปิ น กินฺตุ มม ตาโต ยํ ยูยํ สฺวียมฺ อีศฺวรํ ภาษเธฺว เสอว มำ สมฺมนุเตฯ
55 Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake.
ยูยํ ตํ นาวคจฺฉถ กินฺตฺวหํ ตมวคจฺฉามิ ตํ นาวคจฺฉามีติ วากฺยํ ยทิ วทามิ ตรฺหิ ยูยมิว มฺฤษาภาษี ภวามิ กินฺตฺวหํ ตมวคจฺฉามิ ตทากฺษามปิ คฺฤหฺลามิฯ
56 Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”
ยุษฺมากํ ปูรฺวฺวปุรุษ อิพฺราหีมฺ มม สมยํ ทฺรษฺฏุมฺ อตีวาวาญฺฉตฺ ตนฺนิรีกฺษฺยานนฺทจฺจฯ
57 Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”
ตทา ยิหูทียา อปฺฤจฺฉนฺ ตว วย: ปญฺจาศทฺวตฺสรา น ตฺวํ กิมฺ อิพฺราหีมมฺ อทฺรากฺษี: ?
58 Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!”
ยีศุ: ปฺรตฺยวาทีทฺ ยุษฺมานหํ ยถารฺถตรํ วทามิ อิพฺราหีโม ชนฺมน: ปูรฺวฺวกาลมารภฺยาหํ วิเทฺยฯ
59 Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.
ตทา เต ปาษาณานฺ อุตฺโตลฺย ตมาหนฺตุมฺ อุทยจฺฉนฺ กินฺตุ ยีศุ รฺคุปฺโต มนฺติราทฺ พหิรฺคตฺย เตษำ มเธฺยน ปฺรสฺถิตวานฺฯ

< Yohane 8 >