< Yohane 8 >
1 Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi.
but Jesus went to the Mount of Olives.
2 Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa.
Now very early in the morning, he came again into the temple, and all the people came to him, and he sat down and taught them.
3 Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo
Then the scribes and the Pharisees brought a woman taken in adultery, and having set her in the midst,
4 anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo.
they said to him, "Teacher, we found this woman in adultery, in the very act.
5 Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?”
Now in the Law, Moses commanded us to stone such. So what do you say?"
6 Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye. Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake.
Now they said this to test him, that they might have something to accuse him of. But Jesus stooped down, and wrote on the ground with his finger.
7 Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.”
But when they continued asking him, he looked up and said to them, "He who is without sin among you, let him throw the first stone at her."
8 Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.
Again he stooped down, and with his finger wrote on the ground.
9 Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo.
But when they heard it, they went out one by one, beginning from the oldest, even to the last, and he was left alone with the woman where she was, in the middle.
10 Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”
Then Jesus, standing up, said to her, "Woman, where are they? Did no one condemn you?"
11 Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.” “Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”
And she said, "No one, Lord." And Jesus said, "Neither do I condemn you. Go, and sin no more."
12 Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”
Again, therefore, Jesus spoke to them, saying, "I am the light of the world. He who follows me will not walk in the darkness, but will have the light of life."
13 Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”
The Pharisees therefore said to him, "You testify about yourself. Your testimony is not valid."
14 Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita.
Jesus answered them, "Even if I testify about myself, my testimony is true, for I know where I came from, and where I am going; but you do not know where I came from, or where I am going.
15 Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense.
You judge according to the flesh. I judge no one.
16 Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma.
Even if I do judge, my judgment is true, for I am not alone, but I am with the Father who sent me.
17 Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka.
It's also written in your Law that the testimony of two people is valid.
18 Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”
I am one who testifies about myself, and the Father who sent me testifies about me."
19 Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?” Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.”
They said therefore to him, "Where is your Father?" Jesus answered, "You know neither me, nor my Father. If you knew me, you would know my Father also."
20 Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.
Jesus spoke these words in the treasury, as he taught in the temple. Yet no one arrested him, because his hour had not yet come.
21 Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”
Jesus said therefore again to them, "I am going away, and you will seek me, and you will die in your sins. Where I go, you cannot come."
22 Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’”
The Jewish leaders therefore said, "Will he kill himself, that he says, 'Where I am going, you cannot come?'"
23 Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino.
He said to them, "You are from beneath. I am from above. You are of this world. I am not of this world.
24 Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”
I said therefore to you that you will die in your sins; for unless you believe that I am he, you will die in your sins."
25 Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?” Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi,
They said therefore to him, "Who are you?" Jesus said to them, "Just what I have been saying to you from the beginning.
26 ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”
I have many things to speak and to judge concerning you. However he who sent me is true; and the things which I heard from him, these I say to the world."
27 Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake.
They did not understand that he spoke to them about the Father.
28 Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa.
Jesus therefore said to them, "When you have lifted up the Son of Man, then you will know that I am he, and I do nothing of myself, but as the Father taught me, I say these things.
29 Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.”
He who sent me is with me. The Father hasn't left me alone, for I always do the things that are pleasing to him."
30 Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.
As he spoke these things, many believed in him.
31 Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga.
Jesus therefore said to those Judeans who had believed him, "If you remain in my word, then you are truly my disciples.
32 Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”
You will know the truth, and the truth will make you free."
33 Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’”
They answered him, "We are Abraham's descendants, and have never been in bondage to anyone. How can you say, 'You will be made free?'"
34 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo.
Jesus answered them, "Truly I tell you, everyone who commits sin is the slave of sin.
35 Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. (aiōn )
A slave does not live in the house forever. A son remains forever. (aiōn )
36 Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu.
So if the Son sets you free, you will be free indeed.
37 Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu.
I know that you are Abraham's descendants, yet you seek to kill me, because my word finds no place in you.
38 Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”
I say the things which I have seen with my Father; and you also do the things which you have heard from your father."
39 Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.” Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita.
They answered him, "Our father is Abraham." Jesus said to them, "If you were Abraham's children, you would do the works of Abraham.
40 Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi.
But now you seek to kill me, a man who has told you the truth, which I heard from God. Abraham did not do this.
41 Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.” Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”
You do the works of your father." They said to him, "We were not born of sexual immorality. We have one Father, God."
42 Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha.
Therefore Jesus said to them, "If God were your father, you would love me, for I came out and have come from God. For I have not come of myself, but he sent me.
43 Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga.
Why do you not understand my speech? Because you cannot hear my word.
44 Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza.
You are of your father, the devil, and you want to do the desires of your father. He was a murderer from the beginning, and does not stand in the truth, because there is no truth in him. When he speaks a lie, he speaks on his own; for he is a liar, and its father.
45 Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine!
But because I tell the truth, you do not believe me.
46 Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira?
Which of you convicts me of sin? If I tell the truth, why do you not believe me?
47 Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”
He who is of God hears the words of God. For this cause you do not hear, because you are not of God."
48 Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”
Then the Judeans answered him, "Do not we say well that you are a Samaritan, and have a demon?"
49 Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza.
Jesus answered, "I do not have a demon, but I honor my Father, and you dishonor me.
50 Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza.
But I do not seek my own glory. There is one who seeks and judges.
51 Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.” (aiōn )
Truly, truly, I tell you, if a person keeps my word, he will never see death." (aiōn )
52 Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ (aiōn )
Then the Judeans said to him, "Now we know that you have a demon. Abraham died, and the prophets; and you say, 'If anyone keeps my word, he will never taste of death.' (aiōn )
53 Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”
Are you greater than our father, Abraham, who died? The prophets died. Who do you make yourself out to be?"
54 Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine.
Jesus answered, "If I glorify myself, my glory is nothing. It is my Father who glorifies me, of whom you say 'He is our God.'
55 Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake.
You have not known him, but I know him. If I said, 'I do not know him,' I would be like you, a liar. But I know him, and keep his word.
56 Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”
Your father Abraham rejoiced to see my day. He saw it, and was glad."
57 Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”
The Judeans therefore said to him, "You are not yet fifty years old, and have you seen Abraham?"
58 Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!”
Jesus said to them, "Truly, truly, I tell you, before Abraham came into existence, I AM."
59 Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.
Therefore they took up stones to throw at him, but Jesus was concealed, and went out of the temple.