< Yohane 7 >
1 Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
Mançile qiyğa I'sa Galileyee ı'ğiykar. Yahudeeşine ç'ak'ınbışis I'sa gik'as ıkkanva, Mana Yahudeyayeeqa hayk'an deş.
2 Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
Yahudeeşin K'odiybışin bayram k'ane qıxha ıxha.
3 abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
Çocaaşe I'sayk'le eyhen: – İnyaa ımaxva, Yahudeyayeeqa hoora. Ğu ha'an karbı Yiğne telebabışik'led g'acecen.
4 Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
Vuc qıvaats'as ıkkanne insanee karbı dyugulenda ha'anbı deşxhe. Ğu in karbı ha'axhee, Ğucar Ğu dyunyeys qıvaats'e'e.
5 Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
Mang'une çocaaşed Mang'ulqa inyam ha'a ıxha deş.
6 Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
Manke I'see manbışik'le eyhen: – Yizda gah qabı deş, şosme mısa qadiy ha'as eyxhen.
7 Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
Dyunyeys şu g'umooce qeepxhes deş. Zıme g'ımece qıxha, Zı mançin işbı pisınbı ıxhay aq'val aqqaqqava.
8 Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
Şu bayrameeqa havak'ne, Zıme, Yizda gah qidyabıynçil-alla, maqa ı'qqəs deş.
9 Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
I'see manıd uvhu, Galileyee axva.
10 Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
Mang'un çocar bayrameeqa hapk'ıniyle qiyğa, Manar şavuk'lecar g'ıdecesın xhinne, dyugulenra bayrameeqa hayk'an.
11 Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
Yahudeeşine ç'ak'ınbışe I'sa t'abal ha'a-ha'a, «Mana nyaane vorva?» qidghın ha'a ıxha.
12 Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
I'sa milletne ghalecar ıxha. Sassanbışee «Yugna insan vorva», mansanbışed «De'eş, milletıs horbı ha'ava» eyhe ıxha.
13 Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
Yahudeeşine ç'ak'ınbışile qəvəyq'ənva, Mang'une hək'eena gaf, gırgıng'uk'le g'avxhesın xhinne, neng'ussecab haa'as vəəxə vuxha deş.
14 Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
Bayramın sura ıxhayle qiyğa, I'sa Allahne Xaasqa arı, xət qa'a giyğal.
15 Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
Yahudeeşin ç'ak'ınbı mançile ghalybı aaqı avxu, eyhen: – Mang'vee nyaacad qətqı' deş! Nençene Mang'uk'le manimeen kar ats'a?
16 Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
I'see manbışis alidghıniy qele: – Zı helen ats'al Zaken deş vod, Zı G'axuvuyng'uken vod.
17 Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
Şavusiy Allahee eyhen ha'as ıkkan, Zı helen ats'al Mang'uken, Zaken deş ıxhay ats'axhxhesın.
18 Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
Cukedğana eyheng'us, vuc axtı qa'as ıkkan. Vuc G'axuvuname axtı qa'as ıkkanna qorkuna vor, Mang'uqa horud eyxhen deş.
19 Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
Mısee şos Q'aanun huvu. Vuşde neng'veecad Q'aanunun eyhen ha'a deş. Nya'a şos Zı gik'as ıkkan?
20 Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
Milletın alidghıniy qele: – Yiğne ad cinıd. Şavusiy Ğu gik'as ıkkan?
21 Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
I'see manbışik'le eyhen: – Zı sa iş hav'u, vuşun gırgınbı ghalybı aaqı avxu.
22 Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
Mısee şok'le sunnat ha'as vukkanva uvhu. Yic man ha'a, Mısayle ögilyne dideeşecad gibğıl. Şu Şabbatne yiğılib sunnat haa'a.
23 Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
Mısayne Q'aanunun eyhen ixhecenva, şu insan Şabbatıl sunnat ha'a. Nişil-allane Zı Şabbatıl insan bıkırra yug qı'ıva, şu Zalqa qəl haa'a?
24 Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
Şu aq'vale g'ecen xhinnee muhaakima haa'a. Qopkuvalika ilyaakı, muhaakima hee'e.
25 Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
Manke İyerusalimne milletın eyhen: – Gik'as ıkkanna mana dişde vor?
26 Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
Haane, Mang'vee gırgıng'uk'le g'iyxhe-g'iyxhe gırgın yuşan he'eeyid, Mang'uk'le vuççud eyhe deş. Mıts'an, ç'ak'ınbışik'le Mana hək'erar Masixh ıxhay ats'axhxha ixhes.
27 Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
Yic mana İnsan nençe ıxhay şak'le ats'an. Masixh qöömeeme, Mana nençe ıxhay şavuk'lecad ats'a ixhes deş.
28 Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
Allahne Xaasne xət qa'amee, I'see axtıda eyhen: – Şok'le hək'erar Zı ats'anane, nençe qariyid ats'anne? Zı Zakecar deş arı, Zı G'axuvuna qorkuna vor. Şok'le Mana ats'a deş,
29 koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
Zı Mang'usse qariyl-alla, Zak'le Mana ats'a. Mang'vee Zı g'axuvu.
30 Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
Manbışis I'sa aqqas ıkkiykan. Mang'una gah qidyabıva, şavaacadıd Mang'ulqa xıl g'oyt'al deş.
31 Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
Milletıkene geebınbışe Mang'ulqa inyam hı'ı, eyhen: – Masixh qarımee, əlaamatbı İng'uled geed deş hagvas.
32 Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
Fariseyaaşik'le milletın I'sayne hək'ee eyhen g'iyxhen. Kaahinaaşin ç'ak'ınbışeyiy fariseyaaşe Mana aqqasva g'aravulyçer g'uxoole.
33 Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
I'see eyhen: – Zı şoka geer ixhes deş. Mançile qiyğa Zı G'axuvuyng'une k'anyaqa əlyhəəs.
34 Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
Şu Zı t'abala'asda, aveekes deş. Zı ark'ınne cigeeqar şosse ables vəəxəs deş.
35 Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
Maane Yahudeeşine ç'ak'ınbışe sana-sang'uke qidghın ha'a: – Şak'le ivdeekesde cigeeqa nyaqaniyxan Mana ı'qqəs? Yunanaaşine yı'q'nee vooxhene cühüt'yaaşine k'anyaqa hark'ın, Yunanaaşisniyxan xət qa'as?
36 Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
«Şu Zı t'abala'asda, aveekes deş. Zı ark'ınne cigeeqar şosse ables vəəxəs deş» mane cuvabıka hucooniyxan eyhes ıkkan?
37 Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
Bayramne nekke qiyğiyne yiğıl I'sa oza qıxha, axtıda eyhen: – Şavuniy ghal qeqqu, Zasqa qarı ulyoğecen.
38 Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
Muq'addasne Otk'uniybışee otk'unin xhinnee, Zalqa inyam hı'iyng'une yik'eençe, ı'mı'r hoolene xhinen damabı gyotstses.
39 Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
Mang'vee manva, Cul inyam ha'anbışe alyaat'asde Allahne Rı'hı'ne hək'ee eyhe ıxha. Allahee I'sayna xəbvalla mankilqame hidyag'uynçil-alla, inyam ha'anbışis man Rı'h huvu ıxha deş.
40 Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
Milletıkene sabaranbışik'le man eyhenbı g'ayxhımee, «İna hək'erar qalesda peyğambar ooxhurva» eyhe.
41 Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
Sabaranbışemee «İna Masixhır» eyhe, samebınbışemee eyhen: – Masixh Galileyeençe'e qales deş.
42 Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
Nya'a Muq'addasne Otk'uniybışee otk'un dişde, Masixh Davudne nasılençena, Davud eyxhene Bet-Lexemne xiveençe qales?
43 Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
İnsanar I'sayl-alla cuvabılqa abayle.
44 Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
Sabaranbışis Mana aqqas ıkkiykıneeyir, nenacar Mang'uk set'a deş.
45 Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
G'aravulyçer kaahinaaşine ç'ak'ınbışisqayiy fariseeyaaşine k'anyaqa sapk'ılmee, manbışe g'aravulyçeeşike qiyghanan: – Nya'a şu Mana qidyarı?
46 Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
G'aravulyçeeşe eyhen: – Həşdilyqamee sacar insan məxür yuşan hı'ı deş.
47 Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
Fariseyaaşe manbışik'le eyhen: – Deşxhee Mang'vee şunabne yəqqı'le qığavhu?
48 “Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
Sa xərıng'veexheyid sa fariseyexheyid Mang'ulqa inyam hı'ıye?
49 Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
İne milletık'le Q'aanunne hək'ee hucoona ats'a? Manbı gulyoptulıynbı!
50 Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
Ögilycar I'sayne k'anyaqa arıyne Nikodim donane fariseyee manbışik'le eyhen:
51 “Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
– Yişde Q'aanunus sik'ı, insanıl k'ırı ilydiyxhı, mang'vee hucooyiy ha'ava dyats'axhxha, mana muhaakima hı'iy qotkuda deş.
52 Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
Manbışe Nikodimık'le eyhen: – Deşxhee, ğunar G'alileyeençene vor? Otk'uneeqa ilekke, vak'lecad g'acesın, sacar peyğambar Galileyeençe qöö deş.
53 Kenaka onse anachoka, napita kwawo.
Mançile qiyğa gırgınbı cone xaaqa avayk'an.