< Yohane 6 >
1 Nthawi ina zitatha izi, Yesu anawolokera ku gombe la kutali la nyanja ya Galileya (iyi ndi nyanja ya Tiberiya),
After this Jesus went away across the Lake of Galilee (that is, the Lake of Tiberias).
2 ndipo gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye chifukwa linaona zizindikiro zodabwitsa zimene anazichita pa odwala.
A vast multitude followed Him, because they witnessed the miracles on the sick which He was constantly performing.
3 Kenaka Yesu anakwera pa phiri nakhala pansi ndi ophunzira ake.
Then Jesus went up the hill, and sat there with His disciples.
4 Tsopano phwando la Paska la Ayuda linali pafupi.
The Jewish Festival, the Passover, was at hand.
5 Yesu atakweza maso ndi kuona gulu lalikulu la anthu likubwera kwa Iye, anati kwa Filipo, “Kodi tingagule kuti buledi kuti anthu awa adye?”
And when He looked round and saw an immense crowd coming towards Him, He said to Philip, "Where shall we buy bread for all these people to eat?"
6 Iye anafunsa izi kumuyesa chabe, pakuti Iye ankadziwa chimene ankayenera kuchita.
He said this to put Philip to the test, for He Himself knew what He was going to do.
7 Filipo anamuyankha Iye kuti, “Malipiro a miyezi isanu ndi itatu sangathe kugula buledi okwanira aliyense kuti adye!”
"Seven pounds' worth of bread," replied Philip, "is not enough for them all to get even a scanty meal."
8 Mmodzi wa ophunzira ake, Andreya, mʼbale wa Simoni Petro, anati,
One of His disciples, Andrew, Simon Peter's brother, said to Him,
9 “Pano pali mnyamata amene ali ndi buledi musanu wabarele ndi tinsomba tiwiri, kodi zingakwane onsewa?”
"There is a boy here with five barley loaves and a couple of fish: but what is that among so many?"
10 Yesu anati, “Awuzeni anthuwa akhale pansi.” Pamalo pamenepa panali udzu wambiri ndipo amuna amene anakhala pansi anali osachepera 5,000.
"Make the people sit down," said Jesus. The ground was covered with thick grass; so they sat down, the adult men numbering about 5,000.
11 Kenaka Yesu anatenga bulediyo, atayamika anagawira iwo amene anakhala pansi, chimodzimodzinso nsombazo monga momwe iwo anafunira.
Then Jesus took the loaves, and after giving thanks He distributed them to those who were resting on the ground; and also the fish in like manner--as much as they desired.
12 Ndipo atakhuta, Iye anati kwa ophunzira ake, “Tolani zotsala kuti pasawonongeke kanthu.”
When all were fully satisfied, He said to His disciples, "Gather up the broken portions that remain over, so that nothing be lost."
13 Choncho iwo anasonkhanitsa makombo nadzaza madengu khumi ndi awiri.
Accordingly they gathered them up; and with the fragments of the five barley loaves--the broken portions that remained over after they had done eating--they filled twelve baskets.
14 Pambuyo pake anthu ataona chizindikiro chodabwitsa chimene Yesu anachita, iwo anati, “Zoonadi uyu ndi Mneneri wakudzayo mʼdziko la pansi.”
Thereupon the people, having seen the miracle He had performed, said, "This is indeed the Prophet who was to come into the world."
15 Yesu atadziwa kuti iwo amafuna kubwera kudzamuwumiriza kuti akhale mfumu, anachoka napita ku phiri pa yekha.
Perceiving, however, that they were about to come and carry Him off by force to make Him a king, Jesus withdrew again up the hill alone by Himself.
16 Pofika madzulo, ophunzira ake anatsikira ku nyanja,
When evening came on, His disciples went down to the Lake.
17 kumene iwo analowa mʼbwato ndi kuyamba kuwoloka nyanja kupita ku Kaperenawo. Tsopano kunali kutada ndipo Yesu anali asanabwerere kwa iwo.
There they got on board a boat, and pushed off to cross the Lake to Capernaum. By this time it had become dark, and Jesus had not yet joined them.
18 Mphepo yamphamvu inawomba ndipo nyanja inalusa.
The Lake also was getting rough, because a strong wind was blowing.
19 Iwo atayenda makilomita asanu kapena asanu ndi limodzi, anaona Yesu akuyandikira bwatolo, akuyenda pa madzi; ndipo anachita mantha.
When, however, they had rowed three or four miles, they saw Jesus walking on the water and coming near the boat.
20 Koma Iye anawawuza kuti, “Ndine, musaope.”
They were terrified; but He called to them. "It is I," He said, "do not be afraid."
21 Ndipo iwo analola kumutenga mʼbwatomo, nthawi yomweyo bwatolo linafika ku gombe la nyanja kumene ankapita.
Then they were willing to take Him on board; and in a moment the boat reached the shore at the point to which they were going.
22 Pa tsiku lotsatira gulu la anthu limene linatsala kumbali ina yanyanjayo linaona kuti panali bwato limodzi lokha, ndipo kuti Yesu sanalowe mʼbwatomo pamodzi ndi ophunzira ake, koma kuti ophunzirawo anapita okha.
Next morning the crowd who were still standing about on the other side of the Lake found that there had been but one small boat there, and they had seen that Jesus did not go on board with His disciples, but that His disciples went away without Him.
23 Kenaka mabwato ena ochokera ku Tiberiya anafika pafupi ndi pamalo pamene anthu anadya buledi Ambuye atayamika.
Yet a number of small boats came from Tiberias to the neighbourhood of the place where they had eaten the bread after the Lord had given thanks.
24 Nthawi yomwe gulu la anthu linaona kuti Yesu kapena ophunzira ake sanali pamenepo, ilo linalowanso mʼmabwatowo ndi kupita ku Kaperenawo kukamufunafuna Yesu.
When however the crowd saw that neither Jesus nor His disciples were there, they themselves also took boats and came to Capernaum to look for Jesus.
25 Atamupeza mbali ina ya nyanjayo, iwo anamufunsa Iye kuti, “Rabi, mwafika nthawi yanji kuno?”
So when they had crossed the Lake and had found Him, they asked Him, "Rabbi, when did you come here?"
26 Yesu anawayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mukundifuna, osati chifukwa munaona zizindikiro zodabwitsa koma chifukwa munadya chakudya ndi kukhuta.
"In most solemn truth I tell you," replied Jesus, "that you are searching for me not because you have seen miracles, but because you ate the loaves and had a hearty meal.
27 Gwirani ntchito, osati chifukwa cha chakudya chimene chimawonongeka koma chifukwa cha chakudya chimene sichiwonongeka mpaka ku moyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani. Mulungu Atate anamusindikiza chizindikiro chomuvomereza.” (aiōnios )
Bestow your pains not on the food which perishes, but on the food that remains unto the Life of the Ages--that food which will be the Son of Man's gift to you; for on Him the Father, God, has set His seal." (aiōnios )
28 Kenaka anamufunsa Iye kuti, “Kodi tichite chiyani kuti tigwire ntchito za Mulungu?”
"What are we to do," they asked, "in order to carry out the things that God requires?"
29 Yesu anayankha kuti, “Ntchito ya Mulungu ndi iyi: Kukhulupirira Iye amene anamutuma.”
"This," replied Jesus, "is above all the thing that God requires--that you should be believers in Him whom He has sent."
30 Choncho iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi mudzatipatsa chizindikiro chodabwitsa chotani kuti ife tichione ndi kukhulupirira Inu? Kodi mudzachita chiyani?
"What miracle then," they asked, "do you perform for us to see and become believers in you? What do you do?
31 Makolo athu akale anadya mana mʼchipululu; monga zalembedwa: ‘anawapatsa buledi wochokera kumwamba kuti adye.’”
Our forefathers ate the manna in the Desert, as it is written, 'He gave them bread out of Heaven to eat'."
32 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti si Mose amene ankakupatsani chakudya chochokera kumwamba, koma ndi Atate anga amene ankakupatsani chakudya chenicheni chochokera kumwamba.
"In most solemn truth I tell you," replied Jesus, "that Moses did not give you the bread out of Heaven, but my Father is giving you the bread--the true bread--out of Heaven.
33 Pakuti chakudya cha Mulungu ndi Iye amene wabwera kuchokera kumwamba ndi kupereka moyo ku dziko la pansi.”
For God's bread is that which comes down out of Heaven and gives Life to the world."
34 Iwo anati, “Ambuye, kuyambira tsopano muzitipatsa buledi ameneyu.”
"Sir," they said, "always give us that bread."
35 Kenaka Yesu ananenetsa kuti, “Ine ndine chakudya chamoyo. Iye amene abwera kwa Ine sadzamva njala, ndipo iye amene akhulupirira Ine sadzamva ludzu.
"I am the bread of Life," replied Jesus; "he who comes to me shall never hunger, and he who believes in me shall never, never thirst.
36 Monga ndakuwuzani kale, ngakhale kuti mwandiona simukukhulupirirabe.
But it is as I have said to you: you have seen me and yet you do not believe.
37 Zonse zimene Atate andipatsa zidzabwera kwa Ine, ndipo aliyense amene adzabwera kwa Ine sindidzamutaya kunja.
Every one whom the Father gives me will come to me, and him who comes to me I will never on any account drive away.
38 Pakuti Ine ndinatsika kuchokera kumwamba osati kudzachita chifuniro changa koma cha Iye amene anandituma Ine.
For I have left Heaven and have come down to earth not to seek my own pleasure, but to do the will of Him who sent me.
39 Ndipo chifuniro cha Iye amene anandituma Ine nʼchakuti ndisatayepo ngakhale ndi mmodzi yemwe mwa onse amene Iye wandipatsa, koma kuti ndidzawaukitse kwa akufa pa tsiku lomaliza.
And this is the will of Him who sent me, that of all that He has given me I should lose nothing, but should raise it to life on the last day.
40 Pakuti chifuniro cha Atate anga ndi chakuti aliyense amene aona Mwanayo namukhulupirira akhale ndi moyo wosatha, ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza.” (aiōnios )
For this is my Father's will, that every one who fixes his gaze on the Son of God and believes in Him should have the Life of the Ages, and I will raise him to life on the last day." (aiōnios )
41 Pamenepo Ayuda anayamba kungʼungʼudza chifukwa anati, “Ine ndine chakudya chotsika kuchokera kumwamba.”
Now the Jews began to find fault about Him because of His claiming to be the bread which came down out of Heaven.
42 Iwo anati, “Kodi uyu si Yesu, mwana wa Yosefe, amene abambo ake ndi amayi ake timawadziwa? Nanga Iyeyu akunena bwanji kuti, ‘Ine ndinatsika kuchokera kumwamba?’”
They kept asking, "Is not this man Joseph's son? Is he not Jesus, whose father and mother we know? What does he mean by now saying, 'I have come down out of Heaven'?"
43 Yesu anayankha kuti, “Musangʼungʼudze pakati panu.”
"Do not thus find fault among yourselves," replied Jesus;
44 Palibe munthu amene angabwere kwa Ine, ngati Atate amene anandituma Ine samubweretsa. Ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza.
"no one can come to me unless the Father who sent me draws him; then I will raise him to life on the last day.
45 Aneneri analemba kuti, “Onse adzaphunzitsidwa ndi Mulungu! Aliyense amene amamva Atate ndi kuphunzira kwa Iye amabwera kwa Ine.
It stands written in the Prophets, 'And they shall all of them be taught by God'. Every one who listens to the Father and learns from Him comes to me.
46 Palibe amene anaona Atate koma yekhayo amene achokera kwa Mulungu; yekhayo ndiye anaona Atate.
No one has ever seen the Father--except Him who is from God. He has seen the Father.
47 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Iye amene akhulupirira ali nawo moyo wosatha. (aiōnios )
"In most solemn truth I tell you that he who believes has the Life of the Ages. (aiōnios )
48 Ine ndine chakudya chamoyo.
I am the bread of Life.
49 Makolo anu akale anadya mana mʼchipululu, komabe anafa.
Your forefathers ate the manna in the Desert, and they died.
50 Koma pano pali chakudya chochokera kumwamba, chimene munthu akadya sangafe.
Here is the bread that comes down out of Heaven that a man may eat it and not die.
51 Ine ndine chakudya chamoyo chochokera kumwamba. Ngati munthu adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi zonse. Chakudya chimenechi ndi thupi langa, limene Ine ndidzalipereka kuti anthu pa dziko lapansi akhale ndi moyo.” (aiōn )
I am the living bread come down out of Heaven. If a man eats this bread, he shall live for ever. Moreover the bread which I will give is my flesh given for the life of the world." (aiōn )
52 Kenaka Ayuda anayamba kutsutsana kwambiri pakati pawo kuti, “Kodi munthu uyu angathe kutipatsa bwanji thupi lake kuti tidye?”
This led to an angry debate among the Jews. "How can this man," they argued, "give us his flesh to eat?"
53 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ngati simungadye thupi la Mwana wa Munthu ndi kumwa magazi ake, simungakhale ndi moyo mwa inu.
"In most solemn truth I tell you," said Jesus, "that unless you eat the flesh of the Son of Man and drink His blood, you have no Life in you.
54 Aliyense amene adya thupi langa ndi kumwa magazi anga ali ndi moyo wosatha ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. (aiōnios )
He who eats my flesh and drinks my blood has the Life of the Ages, and I will raise him up on the last day. (aiōnios )
55 Pakuti thupi langa ndi chakudya chenicheni ndipo magazi anga ndi chakumwa chenicheni.
For my flesh is true food, and my blood is true drink.
56 Aliyense amene adya thupi langa ndi kumwa magazi anga amakhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye.
He who eats my flesh and drinks my blood remains in union with me, and I remain in union with him.
57 Monga Atate amoyo anandituma Ine, ndipo ndili ndi moyo chifukwa cha Atatewo, chomwechonso amene adya thupi langa adzakhala ndi moyo chifukwa cha Ine.
As the ever-living Father has sent me, and I live because of the Father, so also he who eats me will live because of me.
58 Ichi ndiye chakudya chimene chinatsika kuchokera kumwamba. Makolo athu akale anadya mana ndi kufa, koma iye amene adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi yonse.” (aiōn )
This is the bread which came down out of Heaven; it is unlike that which your forefathers ate--for they ate and yet died. He who eats this bread shall live for ever." (aiōn )
59 Iye ankanena izi pamene ankaphunzitsa mʼsunagoge mu Kaperenawo.
Jesus said all this in the synagogue while teaching at Capernaum.
60 Pakumva izi ambiri a ophunzira ake anati, “Ichi ndi chiphunzitso chovuta. Angachilandire ndani?”
Many therefore of His disciples, when they heard it, said, "This is hard to accept. Who can listen to such teaching?"
61 Pozindikira kuti ophunzira ake ankangʼungʼudza, Yesu anawafunsa kuti, “Kodi izi zikukukhumudwitsani?
But, knowing in Himself that His disciples were dissatisfied about it, Jesus asked them,
62 Nanga mutaona Mwana wa Munthu akukwera kupita kumene Iye anali poyamba!
"Does this seem incredible to you? What then if you were to see the Son of Man ascending again where He was before?
63 Mzimu Woyera apereka moyo, thupi silipindula kanthu. Mawu amene ndayankhula kwa inu ndiwo mzimu ndipo ndi moyo.
It is the spirit which gives Life. The flesh confers no benefit whatever. The words I have spoken to you are spirit and are Life.
64 Komabe alipo ena mwa inu amene sakukhulupirira.” Pakuti Yesu ankadziwa kuyambira pachiyambi ena mwa iwo amene samakhulupirira ndi amene adzamupereka Iye.
But there are some of you who do not believe." For Jesus knew from the beginning who those were that did not believe, and who it was that would betray Him.
65 Iye anapitiriza kunena kuti, “Ichi ndi chifukwa chake ndinakuwuzani kuti palibe wina angabwere kwa Ine pokhapokha Atate atamuthandiza.”
So He added, "That is why I told you that no one can come to me unless it be granted him by the Father."
66 Kuyambira nthawi imeneyi ophunzira ake ambiri anabwerera ndipo sanamutsatenso Iye.
Thereupon many of His disciples left Him and went away, and no longer associated with Him.
67 Yesu anafunsa khumi ndi awiriwo kuti, “Kodi inu mukufuna kuchokanso?”
Jesus therefore appealed to the Twelve. "Will you go also?" He asked.
68 Simoni Petro anamuyankha Iye kuti, “Ambuye, ife tidzapita kwa yani? Inu muli ndi mawu amoyo wosatha. (aiōnios )
"Master," replied Simon Peter, "to whom shall we go? Your teachings tell us of the Life of the Ages. (aiōnios )
69 Ife tikhulupirira ndi kudziwa kuti Inu ndinu Woyerayo wa Mulungu.”
And we have come to believe and know that you are indeed the Holy One of God."
70 Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi Ine sindinakusankheni inu khumi ndi awiri? Komabe mmodzi wa inu ndi mdierekezi.”
"Did not I choose you--the Twelve?" said Jesus, "and even of you one is a devil."
71 (Iye amanena Yudasi, mwana wa Simoni Isikarioti amene ngakhale anali mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anali woti adzamupereka).
He alluded to Judas, the son of Simon the Iscariot. For he it was who, though one of the Twelve, was afterwards to betray Him.