< Yohane 5 >

1 Patapita nthawi Yesu anakwera kupita ku Yerusalemu ku phwando la Ayuda.
Hessafe guye, Yesuusi Ayhudeti bonchchiya baaliyas Yerusalaame bis.
2 Ndipo ku Yerusalemuko pafupi ndi chipata cha Nkhosa kuli dziwe limene mʼChihebri limatchedwa Betisaida ndipo ndi lozunguliridwa ndi makumbi asanu.
Yerusalaamen Dorssa Penggiya matan Ibraysxe doonan Beetesayda giya teqeti uttida haathay de7ees. He teqeti uttida haathaa matan ichchashu shemppiya bessati de7oosona.
3 Mʼmenemo munkagonamo gulu lalikulu la anthu odwala, osaona, olumala ndi ofa ziwalo.
[Hessan haathay qaaxxanayssa naagiya] daro hargganchchoti, qooqeti, wobbetinne gunddati zin77idosona.
4 Pakuti nthawi zina mngelo wa Ambuye ankatsikira mʼdziwemo nʼkuvundula madziwo. Woyamba kulowamo madzi atavundulidwa, ankachira ngakhale akhale ndi nthenda yanji.
[Ays giikko, issi issi toho Godaa kiitanchchoy teqettida haathan wodhdhidi haathaa qaathees. Haathay qaaxxiya wode koyro gelida uray bana oykkida ay harggefekka paxees.]
5 Mmodzi wa amene anali pamenepo anali atadwala zaka 38.
He bessan hasttamanne hosppun laythi harggettida issi addey de7ees.
6 Yesu atamuona ali chigonere, nadziwa kuti anakhala chotero kwa nthawi yayitali, anamufunsa iye kuti, “Kodi ukufuna kuchira?”
Yesuusi yan zin77ida addiya be7idi, qassi daro wode harggettidayssa eridi addiyako, “Paxanaw koyay?” yaagis.
7 Wodwalayo anayankha kuti, “Ambuye, ndilibe wina aliyense woti angandithandize kulowa mʼdziwe pamene madzi avundulidwa. Pamene ndikuyesera kuti ndilowemo, wina amalowamo ine ndisanalowemo.”
Hargganchoy zaaridi, “Godaw, haathay qaaxxiya wode tana haathan yeggiya asi baawa. Taani gelana haniya wode haray taappe sinthattidi geli kichchees” yaagis.
8 Ndipo Yesu anati kwa iye, “Imirira! Nyamula mphasa yako yamba kuyenda.”
Yesuusi iyaakko, “Dendda eqqa; ne alggaa tookkada ba” yaagis.
9 Nthawi yomweyo munthuyo anachiritsidwa. Iye ananyamula mphasa yake nayamba kuyenda. Tsiku limene izi zinachitika linali la Sabata.
Addey sohuwarakka paxis; ba alggaa tookkidi bis. Hessi Sambbaata gallasan hanis.
10 Ndipo Ayuda anati kwa munthu amene anachiritsidwayo, “Lero ndi la Sabata; lamulo silikulola iwe kunyamula mphasa yako.”
Hessa gisho, Ayhudeti paxida addiyako, “Hachchi sa7ay Sambbaata; neeni ne alggaa tookkeyssi woga gidenna” yaagidosona.
11 Koma iye anayankha kuti, “Munthu amene wandichiritsa anati kwa ine, ‘Nyamula mphasa yako yamba kuyenda.’”
Shin addey, “Tana pathidayssi, ne alggaa tookkada ba gis” yaagidi zaaris.
12 Pamenepo anamufunsa iye kuti, “Kodi munthu ameneyo ndani amene wakuwuza kuti, ‘Nyamula mphasa yako ndipo yenda?’”
Entti iyaakko, “Nena, ne alggaa tookkada ba giday I oonee?” yaagidi oychchidosona.
13 Munthu amene anachiritsidwayo sanadziwe kuti anali ndani, pakuti Yesu anangolowera mʼgulu la anthu ndi kupita.
Shin Yesuusi he bessan daro asaa giddora erisonna kanthidi bida gisho addey bana pathiday ooneekko erenna.
14 Patapita nthawi Yesu anamupeza ku Nyumba ya Mulungu ndipo anati kwa iye, “Taona uli bwino tsopano. Usakachimwenso kuti choyipa choposa ichi chingakugwere.”
Yesuusi guyeppe he addiya Xoossa Keethan demmidi, “Hekko, neeni paxadasa; hayssafe iitabay nena gakkonna mela zaarada nagara oothofa” yaagis.
15 Munthu uja anachoka ndi kukawawuza Ayuda kuti anali Yesu amene anamuchiritsa iye.
Hessafe guye, addey bidi bana pathidayssi Yesuusa gididayssa Ayhudetas odis.
16 Ndipo popeza Yesu amachita zinthu izi tsiku la Sabata, Ayuda anayamba kumulondalonda.
Yesuusi hessa Sambbaata gallas oothida gisho, Ayhudeti Yesuusa gooda oykkidosona.
17 Yesu anawawuza kuti, “Atate anga amagwira ntchito nthawi zonse mpaka lero lino, ndipo Inenso ndili pa ntchito.”
Yesuusi zaaridi, “Ta Aaway ubba wode oothees; takka oothanaw bessees” yaagis.
18 Chifukwa cha ichi Ayuda anawirikiza kufuna kumupha; osati chifukwa chakuswa Sabata kokha komanso chifukwa ankanena kuti Mulungu ndi Atate ake, nadziyesa Iye wofanana ndi Mulungu.
Yesuusi Sambbaata bonchchonna gisho xalaalas gidonnashin Xoossay ba Aawa gidi bana Xoossara giigisida gisho, Ayhudeti iya wodhanaw kaseyssafe minthidi koyidosona.
19 Yesu anawapatsa yankho ili: “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Mwana sangathe kuchita kanthu pa Iye yekha. Iye amachita zokhazo zimene amaona Atate ake akuchita, chifukwa chilichonse chimene Atate amachita Mwana amachitanso.
Yesuusi zaaridi, “Taani hinttew tuma odays; Na7ay barkka aykkoka oothanaw dandda7enna. I ba Aaway oothishin be7oyssa xalaala oothees. Aaway ootheyssa Na7aykka oothees.
20 Pakuti Atate amakonda Mwana, amamuonetsa zonse zimene Iwo amachita. Inde, Atate adzamuonetsa zinthu zazikulu kuposa zimenezi ndipo mudzadabwa.
Aaway ba Na7aa dosiya gisho I oothiya ooso ubbaa ba Na7aa bessees. Hintte malaalettana mela I hayssafe aadhdhiya ooso ba Na7aa bessana.
21 Pakuti monga Atate amaukitsa akufa nawapatsa moyo, momwemonso Mwana amapereka moyo kwa amene Iye akufuna.
Aaway hayqqidayssata hayqoppe denthidi enttaw de7o immeyssada Na7aykka ba koyeyssatas de7o immees.
22 Komanso, Atate saweruza aliyense koma wapereka kwa Mwana ulamuliro woweruzawo,
Aaway Na7aas pirdda maata ubbaa immisppe attin I oonakka pirddenna.
23 kuti aliyense alemekeze Mwanayo monga momwe amalemekezera Atate. Munthu amene salemekeza Mwana salemekezanso Atate amene anamutuma Mwanayo.
Asay ubbay Aawa bonchcheyssada Na7aakka bonchchana. Na7aa bonchchonna oonikka Na7aa kiittida Aawakka bonchchenna.
24 “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene amamva mawu anga ndi kukhulupirira Iye amene ananditumiza Ine, ali ndi moyo wosatha ndipo sadzaweruzidwa. Iye wachoka mu imfa ndipo walowa mʼmoyo. (aiōnios g166)
“Taani hinttew tuma odays; ta qaala si7eyssasinne tana kiittidayssa ammaneyssas merinaa de7oy de7ees. I hayqoppe de7on pinnida gisho pirddettenna. (aiōnios g166)
25 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti nthawi ikubwera ndipo yafika kale tsopano, pamene akufa adzamva mawu a Mwana wa Mulungu ndipo iwo amene amva adzakhala ndi moyo.
Taani hinttew tuma odays; hayqqida asay Xoossaa Na7aa qaala si7iya wodey yaana; hessika ha77i. He qaalay si7ey de7on daana.
26 Pakuti monga Atate ali gwero la moyo, momwemonso anapereka mphamvu zopereka moyo mwa Mwana.
Aaway de7os pultto gididayssada Na7aakka de7os pultto oothis.
27 Ndipo wamupatsa Iye ulamuliro woweruza chifukwa ndi Mwana wa Munthu.
Na7ay Asa Na7a gidiya gisho Aaway Na7aas pirdda maata immis.
28 “Musadabwe ndi zimenezi. Pakuti nthawi ikubwera pamene onse amene ali mʼmanda adzamva mawu ake
“Duufon de7eyssati iya qaala si7idi denddiya wodey yaana gisho hayssan malaalettofite.
29 ndi kutuluka. Iwo amene anachita zabwino adzauka ndi kupita ku moyo wosatha ndipo amene anachita zoyipa adzauka ndi kupita ku chilango chamuyaya.
Lo77o oothidayssati de7on daanaw qassi iita oothidayssati pirdda ekkanaw duufoppe denddana.
30 Pakuti sindingathe kuchita kena kalikonse pa ndekha. Ine ndimaweruza molingana ndi zomwe Mulungu wandiwuza ndipo kuweruza kwanga ndi kolungama. Ine sindifuna kudzikondweretsa ndekha koma Iye amene anandituma.
“Taani ta maatan aybibaakka oothanaw dandda7ikke. Xoossay taw odidayssada pirddays. Taani tana kiittidayssi koyabaa oothaysippe attin ta koyabaa oothonna gisho ta pirdday tuma.
31 “Ngati ndidzichitira umboni ndekha, umboni wanga si woona.
“Taani tabaa markkatiko ta markkatethay tuma gidenna.
32 Alipo wina amene amandichitira umboni wabwino. Ine ndikudziwa kuti umboni wake wonena za Ine ndi woona.
Tabaa markkattiya hari de7ees; I tabaa markkatteyssi tuma gideyssa taani erays.
33 “Inu munatumiza amithenga kwa Yohane ndipo iye anachitira umboni choona.
“Hintte Yohaannisakko ase kiittin I tumaas markkattis.
34 Sikuti Ine ndikudalira umboni wa munthu; koma ndikunena zimenezi kuti mupulumutsidwe.
Taani hessa hinttew odey, hintte attana mela gadappe attin asa markkatethi taw koshshin gidenna.
35 Yohane anali ngati nyale imene imayaka ndi kuwala, ndipo inu kwa kanthawi munasankha kusangalala ndi kuwala kwakeko.
Yohaannisi muqaadada eexishe poo7is. Hintte guutha wode iya poo7uwan ufayttideta.
36 “Koma Ine ndili ndi umboni woposa uja wa Yohane. Pakuti ntchito imene Atate andipatsa kuti ndiyikwaniritse ndi imene ndikugwira, ndipo ikundichitira umboni kuti Atate andituma Ine.
“Shin taw Yohaannisappe aadhdhiya markki de7ees. Taani oothana mela ta Aaway taw immida oosoti tabaa markkattosona; Aaway tana kiittidayssa qonccisoosona.
37 Ndipo Atate amene anandituma Ine, Iye mwini wandichitira umboni. Inu simunamvepo mawu ake kapena kuona maonekedwe ake,
“Qassi tana kiittida Aawaykka ba huu7en tabaa markkattees. Hintte iya qaala ubbarakka si7ibeekketa woykko iya malaa be7ibeekketa.
38 kapena mawu ake kukhala mwa inu, pakuti simukhulupirira Iye amene anamutuma.
I kiittidayssa hintte ammanonna gisho iya qaalay hintte wozanan baawa.
39 Inu mumasanthula malemba chifukwa mumaganiza kuti mʼmalembamo muli moyo wosatha. Awa ndi malemba amene akundichitira umboni. (aiōnios g166)
“Geeshsha Maxaafatappe merinaa de7o demmanabaa hinttew daanin entta pilggeeta; entti tabaa markkattosona. (aiōnios g166)
40 Koma inu mukukana kubwera kwa Ine kuti mukhale ndi moyo.
Shin hintte de7o demmanaw taakko yaanaw koyekketa.
41 “Ine sindilandira ulemu kuchokera kwa anthu
“Asappe taani bonchcho koyikke.
42 koma Ine ndikukudziwani. Ndikudziwa kuti mʼmitima mwanu mulibe chikondi cha Mulungu.
Shin taani hintte wozanan Xoossaa siiqoy baynnayssa erays.
43 Ine ndabwera mʼdzina la Atate anga, ndipo inu simukundirandira Ine; koma wina wake akabwera mʼdzina la iye mwini, inu mudzamulandira.
Taani ta Aawa maatan yas, shin tana mokkibeekketa. Haray ba maatan yaa wode iya mokkeeta.
44 Kodi inu mudzakhulupirira bwanji ngati mumapatsana ulemu wina ndi mnzake, ndipo simufuna kulandira ulemu kuchokera kwa Mulungu yekhayo?
Hintte issoy issuwafe bonchcho koyeyssati, issi Xoossafe yaa galata ekkanaw koyonnayssati, waanidi tana ammananaw dandda7etii?
45 “Koma inu musaganize kuti Ine ndidzakunenezani kwa Atate. Wokunenezani ndi Mose, amene inu mwayikapo chiyembekezo chanu.
“Taani ta Aawa sinthan hinttena mootiyabaa hinttew daanoppo. Hinttena mootanay hintte ufayssan naagiya Muse.
46 Ngati mukanakhulupirira Mose, mukanakhulupiriranso Ine, pakuti iye analemba za Ine.
Hintte Muse ammanidabaa gidiyakko I tabaa xaafida gisho tanakka ammananashin.
47 Koma ngati simukhulupirira zimene iye analemba, mudzakhulupirira bwanji zimene Ine ndikunena?”
Shin hintte I xaafidayssa ammanonna ixxiko ta qaala waattidi ammananee?” yaagis.

< Yohane 5 >