< Yohane 4 >

1 Yesu atazindikira kuti Afarisi amva zoti Iye ankapeza ndi kubatiza ophunzira ambiri kupambana Yohane,
Як же взнав Господь, що прочули Фарисеї, що Ісус більш учеників єднає і хрестить, нїж Йоан,
2 (ngakhale kuti Yesuyo sankabatiza, koma ophunzira ake).
(хоч Ісус сам не хрестив, а ученики Його; )
3 Iye anachoka ku Yudeya ndi kubwereranso ku Galileya.
то покинув Юдею, та й пійшов знов у Галилею.
4 Ndipo Iye anayenera kudutsa mu Samariya.
Треба ж було Йому проходити через Самарию.
5 Iye anafika mʼmudzi wa Asamariya wotchedwa Sukari, pafupi ndi malo amene Yakobo anapatsa mwana wake Yosefe.
Приходить оце в город Самарянський, названий Сихар, поблизу хутора, що дав Яков ИосиФу, синові своєму.
6 Chitsime cha Yakobo chinali pamenepo ndipo Yesu atatopa ndi ulendo anakhala pansi pambali pa chitsimecho. Nthawi inali pafupifupi ora lachisanu ndi chimodzi masana.
Була ж там криниця Яковова. Оце ж Ісус, утомившись у дорозї, сидїв так на криниці; було ж коло шестої години.
7 Mayi wa Chisamariya atabwera kudzatunga madzi, Yesu anati kwa iye, “Kodi ungandipatse madzi akumwa.”
Приходить жінка з Самариї начерпати води. Рече їй Ісус: Дай менї пити.
8 (Ophunzira ake nʼkuti atapita mʼmudzi kukagula chakudya).
Ученики бо Його пійшли в город, щоб купити ті.
9 Mayiyo anati kwa Iye, “Inu ndinu Myuda ndipo ine ndine Msamariya. Bwanji mukundipempha madzi akumwa?” (Popeza Ayuda ndi Asamariya sankayanjana).
Каже ж Йому жінка Самарянка: Як се Ти, Жидовин бувши, пити просиш від мене, жінки Самарянки? Бо Жиди не сходять ся з Самарянами.
10 Yesu anamuyankha kuti, “Koma iwe ukanadziwa mphatso ya Mulungu ndi Iye amene akukupempha madzi akumwa, ukanamupempha ndipo akanakupatsa madzi amoyo.”
Озвавсь Ісус і рече їй: Коли б знала дар Божий і хто се говорить тобі: Дай менї пити, ти просила б Його, й дав би тобі води живої.
11 Mayiyo anati, “Ambuye, Inu mulibe kanthu kotungira madzi ndipo chitsime ndi chakuya. Kodi madzi amoyowo mungawatenge kuti?
Каже Йому жінка: Добродїю, і черпака не маєш, і колодязь глибокий; звідкіля ж маєш воду живу?
12 Kodi Inu ndinu wamkulu kuposa kholo lathu Yakobo, amene anatipatsa chitsimechi ndipo iye ankamwanso monga anachita ana ake ndi ziweto zake?”
Хиба Ти більший єси отця нашого Якова, що дав нам сей колодязь? і він сам з него пив, і сини його, й скот його.
13 Yesu anayankha kuti, “Aliyense amene amamwa madzi awa amamvanso ludzu,
Озвавсь Ісус і рече їй: Всякий, хто пє воду сю забажає знов;
14 koma aliyense amene adzamwa madzi amene Ine ndidzamupatsa sadzamvanso ludzu. Ndithudi, madzi amene ndidzamupatsa adzakhala kasupe wamadzi wotumphukira ku moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
хто ж напєть ся води, що я дам йому, не забажає до віку; а вода, що дам йому, буде в йому жерелом водії, що тече в житте вічне. (aiōn g165, aiōnios g166)
15 Mayiyo anati kwa Iye, “Ambuye, patseni madzi amenewo kuti ndisadzamvenso ludzu ndi kumabwerabe kuno kudzatunga madzi.”
Каже до Него жінка: Добродїю, дай менї сієї води, щоб не жаждувала, анї ходила сюди черпати.
16 Iye anamuwuza kuti, “Pita kayitane mwamuna wako ndipo ubwere naye.”
Рече їй Ісус: Іди поклич чоловічка твого, та й приходь сюди.
17 Iye anayankha kuti, “Ine ndilibe mwamuna.” Yesu anati kwa iye, “Wakhoza ponena kuti ulibe mwamuna.
Озвалась жінка і каже: Не маю чоловіка. Рече їй Ісус: Добре сказала єси, що чоловіка не маєш;
18 Zoona nʼzakuti iwe wakhala pa banja ndi amuna asanu, ndipo mwamuna amene uli naye tsopano si wako. Zimene wanenazi ndi zoona.”
пять бо чоловіків мала, та й тепер которого маєш, не чоловік тобі; у сьому правду сказала єси.
19 Mayiyo anati, “Ambuye, ine ndazindikira kuti Inu ndinu mneneri.
Каже Йому жінка: Добродїю, бачу, що пророк єси Ти.
20 Makolo athu ankapembedza mʼphiri ili koma inu Ayuda mumati malo amene tiyenera kupembedzera ali ku Yerusalemu.”
Батьки наші на сїй горі покланялись; а ви кажете, що в Єрусалимі місце, де треба покланяти ся.
21 Yesu anati, “Mayi inu khulupirira Ine. Nthawi ikubwera pamene inu simudzapembedza Atate mʼphiri ili kapena mu Yerusalemu.
Рече їй Ісус: Жінко, вір менї, що прийде час, коли нї на горі сїй, анї в Єрусалимі покланяти метесь ви Отцеві.
22 Inu Asamariya mumapembedza chimene simukuchidziwa. Ife timapembedza chimene tikuchidziwa, pakuti chipulumutso nʼchochokera kwa Ayuda.
Ви кланяєтесь, а чому - не знаєте; ми кланяємось, і чому - знаємо, бо спасеннє від Жидів.
23 Koma nthawi ikubwera ndipo yafika kale tsopano pamene opembedza woona adzapembedza Atate mu mzimu ndi mʼchoonadi, pakuti opembedza otere ndiwo amene Atate akuwafuna.
Та прийде час, і вже єсть, що правдиві поклонники поклонять ся Отцеві духом і правдою; Отець бо таких шукає покланяючих ся Йому.
24 Mulungu ndi Mzimu, ndipo omupembedza Iye ayenera kumupembedza mu mzimu ndi mʼchoonadi.”
Дух - Бог, і хто покланяєть ся Йому, духом і правдою мусить покланятись.
25 Mayiyo anati, “Ine ndikudziwa kuti Mesiya (wotchedwa Khristu) akubwera. Akabwera, Iye adzafotokoza zonse kwa ife.”
Каже Йому жінка: Знаю, що Месия прийде (званий Христос). Як прийде Він, звістить нам усе.
26 Ndipo Yesu anamuwuza kuti, “Amene ndikukuyankhulane, ndine amene.”
Рече їй Ісус: Се я, що глаголю тобі.
27 Pa nthawi yomweyo ophunzira ake anabwerera ndipo anadabwa kupeza Iye akuyankhula ndi mayi. Koma palibe amene anamufunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” kapena, “Nʼchifukwa chiyani mukuyankhula naye?”
І прийшли на се ученики Його, й дивувались, що Він із жінкою розмовляв; та нїхто не сказав: Чого тобі треба? або: Про що розмовляєш із нею?
28 Kenaka mayiyo anasiya mtsuko wamadzi, nabwerera ku mzinda ndipo anati kwa anthu,
Покинула тодї відро своє жінка, й пійшла в город, і каже людям:
29 “Tiyeni mukaone munthu amene wandiwuza ine zilizonse zimene ndinazichita. Kodi ameneyu sangakhale Khristu?”
Ійдїть подивіть ся на чоловіка, котрий сказав менї все, що я зробила; чи се не Христос?
30 Iwo anatuluka mʼmudziwo ndi kupita kumene kunali Iye.
Вийшли ж з города, й прийшли до Него.
31 Pa nthawi imeneyi ndi kuti ophunzira ake akumukakamiza kuti, “Rabi idyani.”
Тим часом просили Його ученики: Рави, їж.
32 Koma Iye anawawuza kuti, “Ine ndili ndi chakudya choti ndidye chimene inu simukuchidziwa.”
Він же рече їм: Я маю їжу їсти, котрої ви не знаєте.
33 Ndipo ophunzira ake anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi alipo wina amene anamubweretsera Iye chakudya?”
Казали ж ученики один до одного: Хиба хто приніс Йому їсти?
34 Yesu anati, “Chakudya changa ndikuchita chifuniro cha Iye amene anandituma Ine ndi kumaliza ntchito yake.
Рече їм Ісус: Моя їжа, щоб чинити волю Пославшого мене, й скінчити Його діло.
35 Kodi inu simunena kuti, ‘Kwatsala miyezi inayi ndipo kenaka kukolola?’ Ine ndikukuwuzani kuti, tsekulani maso anu ndipo muyangʼane mʼminda! Mbewu zacha kale kuti zikololedwe.
Хиба ви не кажете: Що ще чотирі місяці, та й жнива прийдуть? Ось глаголю вам: Здійміть очі ваші, та погляньте на ниви, що вже пополовіли на жнива.
36 Ngakhale tsopano amene akukolola akulandira malipiro ake, ndipo akututa mbewu ku moyo wosatha kuti wofesa ndi wokolola asangalale pamodzi. (aiōnios g166)
І приймає жнець плату, й збирає овощ у житте вічне, щоб і хто сїє радував ся, і хто жне. (aiōnios g166)
37 Nʼchifukwa chake mawu akuti, ‘Wina amafesa ndipo wina amakolola’ ndi woona.
Бо у сьому слово правдиве: що инший, хто сіє, а инший, хто жне.
38 Ine ndinakutumani kukakolola zimene simunagwirire ntchito. Ena anagwira ntchito yolemetsa ndipo inu mwatuta phindu la ntchito yawo.”
Я післав вас жати, коло чого ви не працювали; инші люде працювали, а ви на працю їх увійшли.
39 Asamariya ambiri ochokera mʼmudziwo anakhulupirira Iye chifukwa cha umboni wa mayiyo wakuti, “Iye anandiwuza ine zonse ndinazichita.”
З города ж того багато увірувало в Него Самарян через слово жінки, сьвідкуючої: Що сказав мені все, що зробила.
40 Choncho Asamariya atabwera kwa Iye, anamuwumiriza Iye kuti akhale nawo, ndipo Iye anakhala nawo masiku awiri.
Як же прийшли до Него Самаряне, просили Його зістатись у них; і зіставсь там два днї.
41 Ndipo chifukwa cha mawu ake, ena ambiri anakhulupirira.
І багато більше увірувало за слово Його.
42 Iwo anati kwa mayiyo, “Ife sitikukhulupirira chifukwa cha mawu ako okha, koma tsopano ife tadzimvera tokha, ndipo tikudziwa kuti munthu uyu ndithu ndi Mpulumutsi wa dziko lapansi.”
А тій жінці казали: Що вже не задля твого оповідання віруємо; самі бо чули, й знаємо, що се справді Спас сьвіту Христос.
43 Patatha masiku awiri Iye anachoka napita ku Galileya.
Через два ж днї вийшов звідтіля та прийшов у Галилею.
44 (Tsopano Yesu mwini ananena kale kuti mneneri salandira ulemu mʼdziko lake).
Сам бо Ісус сьвідкував, що пророк у своїй отчинї чести не має.
45 Iye atafika ku Galileya, Agalileya anamulandira. Iwo anali ataona zonse zimene anazichita mu Yerusalemu pa phwando la Paska, pakuti iwonso anali komweko.
Як же прийшов у Галилею, прийняли Його Галилейцї, бачивши все, що зробив у Єрусалимі на сьвята: бо й вони ходили на сьвята.
46 Iye anakafikanso ku Kana wa ku Galileya, kumene anasanduliza madzi kukhala vinyo. Ndipo kumeneko kunali nduna ina ya mfumu imene mwana wake wamwamuna anali chigonere akudwala ku Kaperenawo.
Прийшов же Ісус ізнов у Кану Галилейську, де зробив воду вином. І був один царський, котрого син нездужав у Капернаумі.
47 Munthu uyu atamva kuti Yesu wafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya, anapita kwa Iye, namupempha kuti apite akachiritse mwana wakeyo, amene anali pafupi kufa.
Сей, почувши, що Ісус прибув із Юдеї в Галилею, прийшов до Него, й благав Його, щоб пійшов та оздоровив сина його, бо мав умерти.
48 Yesu anawawuza iwo kuti, “Anthu inu pokhapokha mutaona zizindikiro zodabwitsa, simudzakhulupirira.”
Рече ж Ісус до него: Коли ознак та див не побачите, не увіруєте.
49 Nduna ya mfumuyo inati, “Ambuye tiyeni mwana wanga asanafe.”
Каже до Него царський: Господи, йди перш, ніж умре дитина моя.
50 Yesu anayankha kuti, “Pita. Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Munthuyo anakhulupirira mawu a Yesu ndipo ananyamuka.
Рече йому Ісус: Іди, син твій живий. І увірував чоловік слову, що промовив йому Ісус, і пійшов.
51 Iye ali pa njira, antchito ake anakumana naye, namuwuza kuti mwana wanu uja wachira.
Вже ж він ішов, зустріли його слуги його й звістили, кажучи: Що хлопчик твій живий.
52 Iye atafunsa kuti ndi nthawi yanji imene mwana wake anapeza bwino, iwo anati kwa iye, “Malungo anamusiya iye dzulo pa ora lachisanu ndi chiwiri.”
Спитав же в них про годину, коли полегшало йому. І кажуть йому: Що вчора семої години покинула його горячка.
53 Ndipo bamboyo anazindikira kuti iyi inali nthawi yomweyo imene Yesu anati kwa iye, “Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Choncho iye ndi onse a pa banja lake anakhulupirira.
Зрозумів же батько, що тієї самої години, котрої сказав йому Ісус: Що син твій живий; і увірував сам і ввесь дім його.
54 Ichi ndiye chinali chizindikiro chodabwitsa chachiwiri chimene Yesu anachita atafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya.
Се знов другу ознаку зробив Ісус, прийшовши з Юдеї в Галилею.

< Yohane 4 >