< Yohane 4 >

1 Yesu atazindikira kuti Afarisi amva zoti Iye ankapeza ndi kubatiza ophunzira ambiri kupambana Yohane,
Therefore when Jesus knew that the Pharisees had heard, "Jesus is making and baptizing more disciples than John"
2 (ngakhale kuti Yesuyo sankabatiza, koma ophunzira ake).
(although Jesus himself did not baptize, but his disciples),
3 Iye anachoka ku Yudeya ndi kubwereranso ku Galileya.
he left Judea, and departed again into Galilee.
4 Ndipo Iye anayenera kudutsa mu Samariya.
He needed to pass through Samaria.
5 Iye anafika mʼmudzi wa Asamariya wotchedwa Sukari, pafupi ndi malo amene Yakobo anapatsa mwana wake Yosefe.
So he came to a city of Samaria, called Sychar, near the parcel of ground that Jacob gave to his son, Joseph.
6 Chitsime cha Yakobo chinali pamenepo ndipo Yesu atatopa ndi ulendo anakhala pansi pambali pa chitsimecho. Nthawi inali pafupifupi ora lachisanu ndi chimodzi masana.
Jacob's well was there. Jesus therefore, being tired from his journey, sat down by the well. It was about the sixth hour.
7 Mayi wa Chisamariya atabwera kudzatunga madzi, Yesu anati kwa iye, “Kodi ungandipatse madzi akumwa.”
A woman of Samaria came to draw water. Jesus said to her, "Give me a drink."
8 (Ophunzira ake nʼkuti atapita mʼmudzi kukagula chakudya).
For his disciples had gone away into the city to buy food.
9 Mayiyo anati kwa Iye, “Inu ndinu Myuda ndipo ine ndine Msamariya. Bwanji mukundipempha madzi akumwa?” (Popeza Ayuda ndi Asamariya sankayanjana).
The Samaritan woman therefore said to him, "How can you, being a Jew, ask for a drink from me, a Samaritan woman?" (For Jews have no dealings with Samaritans.)
10 Yesu anamuyankha kuti, “Koma iwe ukanadziwa mphatso ya Mulungu ndi Iye amene akukupempha madzi akumwa, ukanamupempha ndipo akanakupatsa madzi amoyo.”
Jesus answered her, "If you knew the gift of God, and who it is who says to you, 'Give me a drink,' you would have asked him, and he would have given you living water."
11 Mayiyo anati, “Ambuye, Inu mulibe kanthu kotungira madzi ndipo chitsime ndi chakuya. Kodi madzi amoyowo mungawatenge kuti?
The woman said to him, "Sir, you have nothing to draw with, and the well is deep. From where do you get that living water?
12 Kodi Inu ndinu wamkulu kuposa kholo lathu Yakobo, amene anatipatsa chitsimechi ndipo iye ankamwanso monga anachita ana ake ndi ziweto zake?”
Are you greater than our father, Jacob, who gave us the well, and drank of it himself, as did his children, and his livestock?"
13 Yesu anayankha kuti, “Aliyense amene amamwa madzi awa amamvanso ludzu,
Jesus answered her, "Everyone who drinks of this water will thirst again,
14 koma aliyense amene adzamwa madzi amene Ine ndidzamupatsa sadzamvanso ludzu. Ndithudi, madzi amene ndidzamupatsa adzakhala kasupe wamadzi wotumphukira ku moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
but whoever drinks of the water that I will give him will never thirst again; but the water that I will give him will become in him a well of water springing up to everlasting life." (aiōn g165, aiōnios g166)
15 Mayiyo anati kwa Iye, “Ambuye, patseni madzi amenewo kuti ndisadzamvenso ludzu ndi kumabwerabe kuno kudzatunga madzi.”
The woman said to him, "Sir, give me this water, so that I do not get thirsty, neither come all the way here to draw."
16 Iye anamuwuza kuti, “Pita kayitane mwamuna wako ndipo ubwere naye.”
He said to her, "Go, call your husband, and come here."
17 Iye anayankha kuti, “Ine ndilibe mwamuna.” Yesu anati kwa iye, “Wakhoza ponena kuti ulibe mwamuna.
The woman answered and said to him, "I have no husband." Jesus said to her, "You said well, 'I have no husband,'
18 Zoona nʼzakuti iwe wakhala pa banja ndi amuna asanu, ndipo mwamuna amene uli naye tsopano si wako. Zimene wanenazi ndi zoona.”
for you have had five husbands; and he whom you now have is not your husband. This you have said truly."
19 Mayiyo anati, “Ambuye, ine ndazindikira kuti Inu ndinu mneneri.
The woman said to him, "Sir, I perceive that you are a prophet.
20 Makolo athu ankapembedza mʼphiri ili koma inu Ayuda mumati malo amene tiyenera kupembedzera ali ku Yerusalemu.”
Our fathers worshiped in this mountain, and you say that in Jerusalem is the place where people ought to worship."
21 Yesu anati, “Mayi inu khulupirira Ine. Nthawi ikubwera pamene inu simudzapembedza Atate mʼphiri ili kapena mu Yerusalemu.
Jesus said to her, "Woman, believe me, the hour comes, when neither in this mountain, nor in Jerusalem, will you worship the Father.
22 Inu Asamariya mumapembedza chimene simukuchidziwa. Ife timapembedza chimene tikuchidziwa, pakuti chipulumutso nʼchochokera kwa Ayuda.
You worship that which you do not know. We worship that which we know; for salvation is from the Jews.
23 Koma nthawi ikubwera ndipo yafika kale tsopano pamene opembedza woona adzapembedza Atate mu mzimu ndi mʼchoonadi, pakuti opembedza otere ndiwo amene Atate akuwafuna.
But the hour comes, and now is, when the true worshippers will worship the Father in spirit and truth, for the Father seeks such to be his worshippers.
24 Mulungu ndi Mzimu, ndipo omupembedza Iye ayenera kumupembedza mu mzimu ndi mʼchoonadi.”
God is spirit, and those who worship him must worship in spirit and truth."
25 Mayiyo anati, “Ine ndikudziwa kuti Mesiya (wotchedwa Khristu) akubwera. Akabwera, Iye adzafotokoza zonse kwa ife.”
The woman said to him, "I know that Messiah comes," (he who is called Christ). "When he has come, he will declare to us all things."
26 Ndipo Yesu anamuwuza kuti, “Amene ndikukuyankhulane, ndine amene.”
Jesus said to her, "I am he, the one who speaks to you."
27 Pa nthawi yomweyo ophunzira ake anabwerera ndipo anadabwa kupeza Iye akuyankhula ndi mayi. Koma palibe amene anamufunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” kapena, “Nʼchifukwa chiyani mukuyankhula naye?”
At this, his disciples came. They were surprised that he was speaking with a woman; yet no one said, "What are you looking for?" or, "Why do you speak with her?"
28 Kenaka mayiyo anasiya mtsuko wamadzi, nabwerera ku mzinda ndipo anati kwa anthu,
So the woman left her water pot, and went away into the city, and said to the people,
29 “Tiyeni mukaone munthu amene wandiwuza ine zilizonse zimene ndinazichita. Kodi ameneyu sangakhale Khristu?”
"Come, see a man who told me everything that I did. Can this be the Christ?"
30 Iwo anatuluka mʼmudziwo ndi kupita kumene kunali Iye.
They went out of the city, and were coming to him.
31 Pa nthawi imeneyi ndi kuti ophunzira ake akumukakamiza kuti, “Rabi idyani.”
In the meanwhile, the disciples urged him, saying, "Rabbi, eat."
32 Koma Iye anawawuza kuti, “Ine ndili ndi chakudya choti ndidye chimene inu simukuchidziwa.”
But he said to them, "I have food to eat that you do not know about."
33 Ndipo ophunzira ake anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi alipo wina amene anamubweretsera Iye chakudya?”
The disciples therefore said one to another, "Has anyone brought him something to eat?"
34 Yesu anati, “Chakudya changa ndikuchita chifuniro cha Iye amene anandituma Ine ndi kumaliza ntchito yake.
Jesus said to them, "My food is to do the will of him who sent me, and to accomplish his work.
35 Kodi inu simunena kuti, ‘Kwatsala miyezi inayi ndipo kenaka kukolola?’ Ine ndikukuwuzani kuti, tsekulani maso anu ndipo muyangʼane mʼminda! Mbewu zacha kale kuti zikololedwe.
Do you not say, 'There are yet four months until the harvest?' Look, I tell you, lift up your eyes and see the fields, that they are white for harvest already.
36 Ngakhale tsopano amene akukolola akulandira malipiro ake, ndipo akututa mbewu ku moyo wosatha kuti wofesa ndi wokolola asangalale pamodzi. (aiōnios g166)
He who reaps receives wages, and gathers fruit to everlasting life; that both he who sows and he who reaps may rejoice together. (aiōnios g166)
37 Nʼchifukwa chake mawu akuti, ‘Wina amafesa ndipo wina amakolola’ ndi woona.
For in this the saying is true, 'One sows, and another reaps.'
38 Ine ndinakutumani kukakolola zimene simunagwirire ntchito. Ena anagwira ntchito yolemetsa ndipo inu mwatuta phindu la ntchito yawo.”
I sent you to reap that for which you have not labored. Others have labored, and you have entered into their labor."
39 Asamariya ambiri ochokera mʼmudziwo anakhulupirira Iye chifukwa cha umboni wa mayiyo wakuti, “Iye anandiwuza ine zonse ndinazichita.”
From that city many of the Samaritans believed in him because of the word of the woman, who testified, "He told me everything that I did."
40 Choncho Asamariya atabwera kwa Iye, anamuwumiriza Iye kuti akhale nawo, ndipo Iye anakhala nawo masiku awiri.
So when the Samaritans came to him, they asked him to stay with them. He stayed there two days.
41 Ndipo chifukwa cha mawu ake, ena ambiri anakhulupirira.
Many more believed because of his word.
42 Iwo anati kwa mayiyo, “Ife sitikukhulupirira chifukwa cha mawu ako okha, koma tsopano ife tadzimvera tokha, ndipo tikudziwa kuti munthu uyu ndithu ndi Mpulumutsi wa dziko lapansi.”
They said to the woman, "Now we believe, not because of your speaking; for we have heard for ourselves, and know that this is indeed the Savior of the world."
43 Patatha masiku awiri Iye anachoka napita ku Galileya.
After the two days he departed from there to Galilee.
44 (Tsopano Yesu mwini ananena kale kuti mneneri salandira ulemu mʼdziko lake).
For Jesus himself testified that a prophet has no honor in his own country.
45 Iye atafika ku Galileya, Agalileya anamulandira. Iwo anali ataona zonse zimene anazichita mu Yerusalemu pa phwando la Paska, pakuti iwonso anali komweko.
So when he came into Galilee, the Galileans received him, having seen all the things that he did in Jerusalem at the feast, for they also went to the feast.
46 Iye anakafikanso ku Kana wa ku Galileya, kumene anasanduliza madzi kukhala vinyo. Ndipo kumeneko kunali nduna ina ya mfumu imene mwana wake wamwamuna anali chigonere akudwala ku Kaperenawo.
Jesus came therefore again to Cana of Galilee, where he made the water into wine. There was a certain nobleman whose son was sick at Capernaum.
47 Munthu uyu atamva kuti Yesu wafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya, anapita kwa Iye, namupempha kuti apite akachiritse mwana wakeyo, amene anali pafupi kufa.
When he heard that Jesus had come out of Judea into Galilee, he went to him, and pleaded with him that he would come down and heal his son, for he was close to death.
48 Yesu anawawuza iwo kuti, “Anthu inu pokhapokha mutaona zizindikiro zodabwitsa, simudzakhulupirira.”
Jesus therefore said to him, "Unless you see signs and wonders, you will in no way believe."
49 Nduna ya mfumuyo inati, “Ambuye tiyeni mwana wanga asanafe.”
The nobleman said to him, "Sir, come down before my child dies."
50 Yesu anayankha kuti, “Pita. Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Munthuyo anakhulupirira mawu a Yesu ndipo ananyamuka.
Jesus said to him, "Go your way. Your son lives." The man believed the word that Jesus spoke to him, and he went his way.
51 Iye ali pa njira, antchito ake anakumana naye, namuwuza kuti mwana wanu uja wachira.
As he was now going down, his servants met him, saying that his son was alive.
52 Iye atafunsa kuti ndi nthawi yanji imene mwana wake anapeza bwino, iwo anati kwa iye, “Malungo anamusiya iye dzulo pa ora lachisanu ndi chiwiri.”
So he inquired of them the hour when he began to get better. They said therefore to him, "Yesterday at one in the afternoon, the fever left him."
53 Ndipo bamboyo anazindikira kuti iyi inali nthawi yomweyo imene Yesu anati kwa iye, “Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Choncho iye ndi onse a pa banja lake anakhulupirira.
So the father knew that it was at that hour in which Jesus said to him, "Your son lives." He believed, as did his whole house.
54 Ichi ndiye chinali chizindikiro chodabwitsa chachiwiri chimene Yesu anachita atafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya.
This is again the second sign that Jesus did, having come out of Judea into Galilee.

< Yohane 4 >