< Yohane 3 >

1 Ndipo panali Mfarisi wotchedwa Nekodimo, wa mʼgulu lolamulira la Ayuda.
Був один чоловік із фарисеїв Никоди́м на ім'я́, начальник юдейський.
2 Iye anabwera kwa Yesu usiku ndipo anati, “Rabi, ife tikudziwa kuti ndinu aphunzitsi wochokera kwa Mulungu, pakuti palibe amene angachite zizindikiro zodabwitsa zimene Inu mukuchita ngati Mulungu sali naye.”
Він до Нього прийшов уночі, та й промовив Йому: „Учителю, знаємо ми, що прийшов Ти від Бога, як Учитель, — бо не може ніхто таких чуд учинити, які чиниш Ти, коли Бог із ним не буде“.
3 Poyankha Yesu ananena kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti, ngati munthu sabadwanso mwatsopano sangathe kuona ufumu wa Mulungu.”
Ісус відповів і до нього сказав: „Поправді, поправді кажу́ Я тобі: Коли хто не наро́диться згори́, то не може побачити Божого Царства“.
4 Nekodimo anati, “Kodi munthu angabadwenso bwanji atakalamba? Kodi angalowe kachiwiri mʼmimba ya amayi ake kuti abadwenso?”
Никоди́м Йому каже: „Як може люди́на родитися, бувши старою? Хіба може вона ввійти до утро́би своїй матері зно́ву й родитись?“
5 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu Woyera, sangalowe mu ufumu wa Mulungu.
Ісус відповів: „Поправді, поправді кажу́ Я тобі: Коли хто не ро́диться з води й Духа, той не може ввійти в Царство Боже.
6 Thupi limabereka thupi, koma Mzimu amabereka mzimu.
Що вродилося з тіла — є тіло, що ж уродилося з Духа — є Дух.
7 Iwe usadabwe chifukwa ndakuwuza kuti, ‘Uyenera kubadwanso.’
Не дивуйся тому́, що сказав Я тобі: Вам необхі́дно родитись згори́.
8 Mphepo imawomba kulikonse kumene ikufuna. Ungathe kumva kuwomba kwake, koma sungathe kudziwa kumene ikuchokera kapena kumene ikupita. Nʼchimodzimodzi ndi amene abadwa ndi Mzimu Woyera.”
Вітер віє, де хоче, і його голос ти чуєш, та не відаєш, звідкіля́ він приходить, і куди він іде. Так буває і з кожним, хто від Духа наро́джений“.
9 Nekodimo anafunsa kuti, “Kodi izi zingatheke bwanji?”
Відповів Никоди́м і до Нього сказав: „Як це статися може?“
10 Yesu anati, “Iwe mphunzitsi wa Israeli, kodi sukuzindikira zimenezi?
Ісус відповів і до нього сказав: „Ти — учитель ізра́їльський, — то чи ж цього не знаєш?
11 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ife tiyankhula zimene tikuzidziwa ndi kuchitira umboni zimene taziona, komabe inu simuvomereza umboni wathu.
Поправді, поправді кажу́ Я тобі: Ми говоримо те, що ми знаємо, а сві́дчимо про те, що́ ми бачили, але сві́дчення нашого ви не приймаєте.
12 Ine ndikuyankhula kwa iwe zinthu za dziko lapansi ndipo sukukhulupirira. Nanga kodi udzakhulupirira bwanji ngati nditayankhula zinthu zakumwamba?
Коли Я говорив вам про зе́мне, та не вірите ви, то я́к же повірите ви, коли Я говоритиму вам про небесне?
13 Palibe wina aliyense anapita kumwamba, koma yekhayo amene watsika kuchokera kumwamba, Mwana wa Munthu.
І не схо́див на небо ніхто, тільки Той, Хто з неба зійшов, — Людський Син, що на небі.
14 Tsono monga Mose anapachika njoka mʼchipululu, moteronso Mwana wa Munthu ayenera kupachikidwa,
І, як Мойсей підні́с змі́я в пустині, так мусить піднесений бути й Син Лю́дський,
15 kuti aliyense amene akhulupirira Iye akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
щоб кожен, хто вірує в Нього, мав вічне життя. (aiōnios g166)
16 “Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
Так бо Бог полюбив світ, що дав Сина Свого Одноро́дженого, щоб кожен, хто вірує в Нього, не згинув, але мав життя вічне. (aiōnios g166)
17 Pakuti Mulungu sanatume Mwana wake ku dziko lapansi, kuti akaweruze, koma kuti akapulumutse dziko lapansi.
Бо Бог не послав Свого Сина на світ, щоб Він світ засуди́в, але щоб через Нього світ спасся.
18 Aliyense wokhulupirira Iye saweruzidwa, koma aliyense wosakhulupirira waweruzidwa kale chifukwa sanakhulupirire dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu.
Хто вірує в Нього, не буде засу́джений; хто ж не вірує, — той вже засуджений, що не повірив в Ім'я́ Одноро́дженого Сина Божого.
19 Ndipo chiweruzo ndi ichi: kuwunika kunabwera mʼdziko lapansi, koma anthu anakonda mdima mʼmalo mwa kuwunikako, chifukwa ntchito zawo zinali zoyipa.
Суд же такий, що світло на світ прибуло́, люди ж те́мряву більш полюбили, як світло, — лихі бо були́ їхні вчинки!
20 Aliyense wochita zoyipa amadana ndi kuwunika, ndipo sabwera poyera chifukwa cha mantha kuti ntchito zake zingaonekere.
Бо кожен, хто робить лихе, нена́видить світло, і не приходить до світла, щоб не зганено вчинків його.
21 Koma aliyense wokhala mu choonadi amabwera ku kuwunika, kuti zionekere poyera zimene iye wachita zachitika kudzera mwa Mulungu.”
А хто робить за правдою, той до світла йде, щоб діла його виявились, бо зроблені в Бозі вони“.
22 Zitatha izi, Yesu ndi ophunzira ake anapita mʼmadera a ku midzi ya ku Yudeya, kumene Iye anakhala kanthawi akubatiza.
По цьому прийшов Ісус та учні Його до країни Юдейської, і з ними Він там проживав та христив.
23 Ndipo Yohane amabatizanso ku Ainoni kufupi ndi Salimu, chifukwa kumeneko kunali madzi ambiri ndipo anthu amabwererabwererabe kudzabatizidwa.
А Іван теж христив в Ено́ні побли́зу Сали́му, бо було там багато води; і прихо́дили люди й христились,
24 (Apa nʼkuti Yohane asanatsekeredwe mʼndende).
бо Іван до в'язниці не був ще поса́джений.
25 Mkangano unabuka pakati pa ophunzira ena a Yohane ndi Ayuda ena pa zamwambo wodziyeretsa wa Ayuda.
І зчинилось змага́ння Іванових учнів з юдеями — про очи́щення.
26 Iwo anabwera kwa Yohane anati, “Rabi, munthu uja munali naye mbali inayo ya mu mtsinje wa Yorodani, amene munamuchitira umboni, taonani naye akubatizanso, ndipo aliyense akupita kwa Iye.”
І прийшли до Івана вони та й сказали йому: „Учителю, Той, Хто був із тобою по то́й бік Йорда́ну, про Якого ти свідчив, — ото христить і Він, і до Нього всі йдуть“.
27 Atamva zimenezi, Yohane anayankha kuti, “Munthu amalandira chokhacho chapatsidwa kwa iye kuchokera kumwamba.
Іван відповів і сказав: „Люди́на нічого приймати не може, як їй з неба не дасться.
28 Inuyo ndinu mboni zanga kuti ine ndinati, ‘Ine sindine Khristu koma ndatumidwa patsogolo pa Iye.’
Ви самі мені свідчите, що я говорив: я — не Христос, але по́сланий я перед Ним.
29 Mwini wake wa mkwatibwi ndi mkwati. Ndipo bwenzi lamkwati limadikira ndi kumvetsera iye, ndipo amakondwa akamva mawu a mkwatiyo. Ine changa ndi chimwemwe ndipo ndine wosangalala kwambiri.
Хто має заручену, той молодий. А дружко́ молодого, що стоїть і його слухає, дуже тішиться з голосу молодого. Така радість моя оце здійснилась!
30 Nʼkoyenera kuti Iyeyo akule, ine ndichepe.
Він має рости, я ж — малі́ти.
31 “Iye wochokera kumwamba ndi wapamwamba pa onse: iye wochokera mʼdziko lapansi ndi wa dziko lapansi, ndipo amayankhula monga mmodzi wa adziko lapansi. Iye wochokera kumwamba ndi wopambana onse.
Хто зве́рху приходить, — Той над усіма́. Хто походить із землі, то той зе́мний, і говорить по-зе́мному. Хто приходить із неба, Той над усіма́,
32 Iye achita umboni pa zimene waziona ndi kuzimva, koma palibe avomereza umboni wake.
і що бачив і чув, те Він свідчить, — та свідо́цтва Його не приймає ніхто.
33 Munthu amene amawulandira akutsimikizira kuti Mulungu ndi woona.
Хто ж прийняв свідо́цтво Його, той стверди́в тим, що Бог правдивий.
34 Pakuti amene Mulungu wamutuma amayankhula mawu a Mulungu; Mulungu wamupatsa Mzimu Woyera mopanda malire.
Бо Кого Бог послав, Той Божі слова́ промовляє, — бо Духа дає Бог без міри.
35 Atate amakonda Mwana ndipo apereka zonse mʼmanja mwake.
Отець любить Сина, і дав усе в Його руку.
36 Aliyense wokhulupirira Mwanayo ali ndi moyo wosatha, koma iye amene samvera Mwanayo sadzawuona moyo, pakuti mkwiyo wa Mulungu umakhala pa iye.” (aiōnios g166)
Хто вірує в Сина, той має вічне життя; а хто в Сина не вірує, той життя не побачить — а гнів Божий на нім перебува́є“. (aiōnios g166)

< Yohane 3 >