< Yohane 3 >
1 Ndipo panali Mfarisi wotchedwa Nekodimo, wa mʼgulu lolamulira la Ayuda.
nikadimanAmA yihUdIyAnAm adhipatiH phirUshI kShaNadAyAM
2 Iye anabwera kwa Yesu usiku ndipo anati, “Rabi, ife tikudziwa kuti ndinu aphunzitsi wochokera kwa Mulungu, pakuti palibe amene angachite zizindikiro zodabwitsa zimene Inu mukuchita ngati Mulungu sali naye.”
yIshaurabhyarNam Avrajya vyAhArShIt, he guro bhavAn IshvarAd Agat eka upadeShTA, etad asmAbhirj nAyate; yato bhavatA yAnyAshcharyyakarmmANi kriyante parameshvarasya sAhAyyaM vinA kenApi tattatkarmmANi karttuM na shakyante|
3 Poyankha Yesu ananena kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti, ngati munthu sabadwanso mwatsopano sangathe kuona ufumu wa Mulungu.”
tadA yIshuruttaraM dattavAn tavAhaM yathArthataraM vyAharAmi punarjanmani na sati kopi mAnava Ishvarasya rAjyaM draShTuM na shaknoti|
4 Nekodimo anati, “Kodi munthu angabadwenso bwanji atakalamba? Kodi angalowe kachiwiri mʼmimba ya amayi ake kuti abadwenso?”
tato nikadImaH pratyavochat manujo vR^iddho bhUtvA kathaM janiShyate? sa kiM puna rmAtR^irjaTharaM pravishya janituM shaknoti?
5 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu Woyera, sangalowe mu ufumu wa Mulungu.
yIshuravAdId yathArthataram ahaM kathayAmi manuje toyAtmabhyAM puna rna jAte sa Ishvarasya rAjyaM praveShTuM na shaknoti|
6 Thupi limabereka thupi, koma Mzimu amabereka mzimu.
mAMsAd yat jAyate tan mAMsameva tathAtmano yo jAyate sa Atmaiva|
7 Iwe usadabwe chifukwa ndakuwuza kuti, ‘Uyenera kubadwanso.’
yuShmAbhiH puna rjanitavyaM mamaitasyAM kathAyAm AshcharyaM mA maMsthAH|
8 Mphepo imawomba kulikonse kumene ikufuna. Ungathe kumva kuwomba kwake, koma sungathe kudziwa kumene ikuchokera kapena kumene ikupita. Nʼchimodzimodzi ndi amene abadwa ndi Mzimu Woyera.”
sadAgatiryAM dishamichChati tasyAmeva dishi vAti, tvaM tasya svanaM shuNoShi kintu sa kuta AyAti kutra yAti vA kimapi na jAnAsi tadvAd AtmanaH sakAshAt sarvveShAM manujAnAM janma bhavati|
9 Nekodimo anafunsa kuti, “Kodi izi zingatheke bwanji?”
tadA nikadImaH pR^iShTavAn etat kathaM bhavituM shaknoti?
10 Yesu anati, “Iwe mphunzitsi wa Israeli, kodi sukuzindikira zimenezi?
yIshuH pratyaktavAn tvamisrAyelo gururbhUtvApi kimetAM kathAM na vetsi?
11 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ife tiyankhula zimene tikuzidziwa ndi kuchitira umboni zimene taziona, komabe inu simuvomereza umboni wathu.
tubhyaM yathArthaM kathayAmi, vayaM yad vidmastad vachmaH yaMchcha pashyAmastasyaiva sAkShyaM dadmaH kintu yuShmAbhirasmAkaM sAkShitvaM na gR^ihyate|
12 Ine ndikuyankhula kwa iwe zinthu za dziko lapansi ndipo sukukhulupirira. Nanga kodi udzakhulupirira bwanji ngati nditayankhula zinthu zakumwamba?
etasya saMsArasya kathAyAM kathitAyAM yadi yUyaM na vishvasitha tarhi svargIyAyAM kathAyAM kathaM vishvasiShyatha?
13 Palibe wina aliyense anapita kumwamba, koma yekhayo amene watsika kuchokera kumwamba, Mwana wa Munthu.
yaH svarge. asti yaM cha svargAd avArohat taM mAnavatanayaM vinA kopi svargaM nArohat|
14 Tsono monga Mose anapachika njoka mʼchipululu, moteronso Mwana wa Munthu ayenera kupachikidwa,
apara ncha mUsA yathA prAntare sarpaM protthApitavAn manuShyaputro. api tathaivotthApitavyaH;
15 kuti aliyense amene akhulupirira Iye akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios )
tasmAd yaH kashchit tasmin vishvasiShyati so. avinAshyaH san anantAyuH prApsyati| (aiōnios )
16 “Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios )
Ishvara itthaM jagadadayata yat svamadvitIyaM tanayaM prAdadAt tato yaH kashchit tasmin vishvasiShyati so. avinAshyaH san anantAyuH prApsyati| (aiōnios )
17 Pakuti Mulungu sanatume Mwana wake ku dziko lapansi, kuti akaweruze, koma kuti akapulumutse dziko lapansi.
Ishvaro jagato lokAn daNDayituM svaputraM na preShya tAn paritrAtuM preShitavAn|
18 Aliyense wokhulupirira Iye saweruzidwa, koma aliyense wosakhulupirira waweruzidwa kale chifukwa sanakhulupirire dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu.
ataeva yaH kashchit tasmin vishvasiti sa daNDArho na bhavati kintu yaH kashchit tasmin na vishvasiti sa idAnImeva daNDArho bhavati, yataH sa IshvarasyAdvitIyaputrasya nAmani pratyayaM na karoti|
19 Ndipo chiweruzo ndi ichi: kuwunika kunabwera mʼdziko lapansi, koma anthu anakonda mdima mʼmalo mwa kuwunikako, chifukwa ntchito zawo zinali zoyipa.
jagato madhye jyotiH prAkAshata kintu manuShyANAM karmmaNAM dR^iShTatvAt te jyotiShopi timire prIyante etadeva daNDasya kAraNAM bhavati|
20 Aliyense wochita zoyipa amadana ndi kuwunika, ndipo sabwera poyera chifukwa cha mantha kuti ntchito zake zingaonekere.
yaH kukarmma karoti tasyAchArasya dR^iShTatvAt sa jyotirR^ItIyitvA tannikaTaM nAyAti;
21 Koma aliyense wokhala mu choonadi amabwera ku kuwunika, kuti zionekere poyera zimene iye wachita zachitika kudzera mwa Mulungu.”
kintu yaH satkarmma karoti tasya sarvvANi karmmANIshvareNa kR^itAnIti sathA prakAshate tadabhiprAyeNa sa jyotiShaH sannidhim AyAti|
22 Zitatha izi, Yesu ndi ophunzira ake anapita mʼmadera a ku midzi ya ku Yudeya, kumene Iye anakhala kanthawi akubatiza.
tataH param yIshuH shiShyaiH sArddhaM yihUdIyadeshaM gatvA tatra sthitvA majjayitum Arabhata|
23 Ndipo Yohane amabatizanso ku Ainoni kufupi ndi Salimu, chifukwa kumeneko kunali madzi ambiri ndipo anthu amabwererabwererabe kudzabatizidwa.
tadA shAlam nagarasya samIpasthAyini ainan grAme bahutaratoyasthitestatra yohan amajjayat tathA cha lokA Agatya tena majjitA abhavan|
24 (Apa nʼkuti Yohane asanatsekeredwe mʼndende).
tadA yohan kArAyAM na baddhaH|
25 Mkangano unabuka pakati pa ophunzira ena a Yohane ndi Ayuda ena pa zamwambo wodziyeretsa wa Ayuda.
apara ncha shAchakarmmaNi yohAnaH shiShyaiH saha yihUdIyalokAnAM vivAde jAte, te yohanaH saMnnidhiM gatvAkathayan,
26 Iwo anabwera kwa Yohane anati, “Rabi, munthu uja munali naye mbali inayo ya mu mtsinje wa Yorodani, amene munamuchitira umboni, taonani naye akubatizanso, ndipo aliyense akupita kwa Iye.”
he guro yarddananadyAH pAre bhavatA sArddhaM ya AsIt yasmiMshcha bhavAn sAkShyaM pradadAt pashyatu sopi majjayati sarvve tasya samIpaM yAnti cha|
27 Atamva zimenezi, Yohane anayankha kuti, “Munthu amalandira chokhacho chapatsidwa kwa iye kuchokera kumwamba.
tadA yohan pratyavochad IshvareNa na datte kopi manujaH kimapi prAptuM na shaknoti|
28 Inuyo ndinu mboni zanga kuti ine ndinati, ‘Ine sindine Khristu koma ndatumidwa patsogolo pa Iye.’
ahaM abhiShikto na bhavAmi kintu tadagre preShitosmi yAmimAM kathAM kathitavAnAhaM tatra yUyaM sarvve sAkShiNaH stha|
29 Mwini wake wa mkwatibwi ndi mkwati. Ndipo bwenzi lamkwati limadikira ndi kumvetsera iye, ndipo amakondwa akamva mawu a mkwatiyo. Ine changa ndi chimwemwe ndipo ndine wosangalala kwambiri.
yo janaH kanyAM labhate sa eva varaH kintu varasya sannidhau daNDAyamAnaM tasya yanmitraM tena varasya shabde shrute. atIvAhlAdyate mamApi tadvad AnandasiddhirjAtA|
30 Nʼkoyenera kuti Iyeyo akule, ine ndichepe.
tena kramasho varddhitavyaM kintu mayA hsitavyaM|
31 “Iye wochokera kumwamba ndi wapamwamba pa onse: iye wochokera mʼdziko lapansi ndi wa dziko lapansi, ndipo amayankhula monga mmodzi wa adziko lapansi. Iye wochokera kumwamba ndi wopambana onse.
ya UrdhvAdAgachChat sa sarvveShAM mukhyo yashcha saMsArAd udapadyata sa sAMsArikaH saMsArIyAM kathA ncha kathayati yastu svargAdAgachChat sa sarvveShAM mukhyaH|
32 Iye achita umboni pa zimene waziona ndi kuzimva, koma palibe avomereza umboni wake.
sa yadapashyadashR^iNochcha tasminneva sAkShyaM dadAti tathApi prAyashaH kashchit tasya sAkShyaM na gR^ihlAti;
33 Munthu amene amawulandira akutsimikizira kuti Mulungu ndi woona.
kintu yo gR^ihlAti sa Ishvarasya satyavAditvaM mudrA NgitaM karoti|
34 Pakuti amene Mulungu wamutuma amayankhula mawu a Mulungu; Mulungu wamupatsa Mzimu Woyera mopanda malire.
IshvareNa yaH preritaH saeva IshvarIyakathAM kathayati yata Ishvara AtmAnaM tasmai aparimitam adadAt|
35 Atate amakonda Mwana ndipo apereka zonse mʼmanja mwake.
pitA putre snehaM kR^itvA tasya haste sarvvANi samarpitavAn|
36 Aliyense wokhulupirira Mwanayo ali ndi moyo wosatha, koma iye amene samvera Mwanayo sadzawuona moyo, pakuti mkwiyo wa Mulungu umakhala pa iye.” (aiōnios )
yaH kashchit putre vishvasiti sa evAnantam paramAyuH prApnoti kintu yaH kashchit putre na vishvasiti sa paramAyuSho darshanaM na prApnoti kintvIshvarasya kopabhAjanaM bhUtvA tiShThati| (aiōnios )