< Yohane 3 >

1 Ndipo panali Mfarisi wotchedwa Nekodimo, wa mʼgulu lolamulira la Ayuda.
Il y avait là un homme d'entre les pharisiens, nommé Nicodème, chef des Juifs.
2 Iye anabwera kwa Yesu usiku ndipo anati, “Rabi, ife tikudziwa kuti ndinu aphunzitsi wochokera kwa Mulungu, pakuti palibe amene angachite zizindikiro zodabwitsa zimene Inu mukuchita ngati Mulungu sali naye.”
Il vint de nuit auprès de Jésus et lui dit: « Rabbi, nous savons que tu es un docteur venu de Dieu; car personne ne peut faire ces signes que tu fais, si Dieu n'est pas avec lui. »
3 Poyankha Yesu ananena kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti, ngati munthu sabadwanso mwatsopano sangathe kuona ufumu wa Mulungu.”
Jésus lui répondit: « En vérité, je te le dis, si quelqu'un ne naît pas de nouveau, il ne peut pas voir le Royaume de Dieu. »
4 Nekodimo anati, “Kodi munthu angabadwenso bwanji atakalamba? Kodi angalowe kachiwiri mʼmimba ya amayi ake kuti abadwenso?”
Nicodème lui dit: « Comment un homme peut-il naître quand il est vieux? Peut-il entrer une seconde fois dans le sein de sa mère et naître? »
5 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu Woyera, sangalowe mu ufumu wa Mulungu.
Jésus répondit: Je te le dis en vérité, si quelqu'un ne naît d'eau et d'Esprit, il ne peut entrer dans le royaume de Dieu.
6 Thupi limabereka thupi, koma Mzimu amabereka mzimu.
Ce qui est né de la chair est chair. Celui qui est né de l'Esprit est esprit.
7 Iwe usadabwe chifukwa ndakuwuza kuti, ‘Uyenera kubadwanso.’
Ne t' étonne pas que je t'aie dit: Il faut que tu naisses de nouveau.
8 Mphepo imawomba kulikonse kumene ikufuna. Ungathe kumva kuwomba kwake, koma sungathe kudziwa kumene ikuchokera kapena kumene ikupita. Nʼchimodzimodzi ndi amene abadwa ndi Mzimu Woyera.”
Le vent souffle où il veut, et vous entendez son bruit; mais vous ne savez d'où il vient ni où il va. Il en est ainsi de quiconque est né de l'Esprit. »
9 Nekodimo anafunsa kuti, “Kodi izi zingatheke bwanji?”
Nicodème lui répondit: « Comment ces choses peuvent-elles être? »
10 Yesu anati, “Iwe mphunzitsi wa Israeli, kodi sukuzindikira zimenezi?
Jésus lui répondit: « Es-tu le docteur d'Israël, et ne comprends-tu pas ces choses?
11 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ife tiyankhula zimene tikuzidziwa ndi kuchitira umboni zimene taziona, komabe inu simuvomereza umboni wathu.
Je vous le dis en vérité, nous disons ce que nous savons et nous rendons témoignage de ce que nous avons vu, et vous ne recevez pas notre témoignage.
12 Ine ndikuyankhula kwa iwe zinthu za dziko lapansi ndipo sukukhulupirira. Nanga kodi udzakhulupirira bwanji ngati nditayankhula zinthu zakumwamba?
Si je vous ai dit des choses terrestres et que vous ne croyiez pas, comment croirez-vous si je vous dis des choses célestes?
13 Palibe wina aliyense anapita kumwamba, koma yekhayo amene watsika kuchokera kumwamba, Mwana wa Munthu.
Personne n'est monté au ciel, sinon celui qui est descendu du ciel, le Fils de l'homme, qui est dans le ciel.
14 Tsono monga Mose anapachika njoka mʼchipululu, moteronso Mwana wa Munthu ayenera kupachikidwa,
Comme Moïse éleva le serpent dans le désert, il faut de même que le Fils de l'homme soit élevé,
15 kuti aliyense amene akhulupirira Iye akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
afin que quiconque croit en lui ne périsse pas, mais ait la vie éternelle. (aiōnios g166)
16 “Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
Car Dieu a tant aimé le monde qu'il a donné son Fils unique, afin que quiconque croit en lui ne périsse pas, mais ait la vie éternelle. (aiōnios g166)
17 Pakuti Mulungu sanatume Mwana wake ku dziko lapansi, kuti akaweruze, koma kuti akapulumutse dziko lapansi.
Car Dieu n'a pas envoyé son Fils dans le monde pour juger le monde, mais pour que le monde soit sauvé par lui.
18 Aliyense wokhulupirira Iye saweruzidwa, koma aliyense wosakhulupirira waweruzidwa kale chifukwa sanakhulupirire dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu.
Celui qui croit en lui n'est pas jugé. Celui qui ne croit pas est déjà jugé, parce qu'il n'a pas cru au nom du Fils unique de Dieu.
19 Ndipo chiweruzo ndi ichi: kuwunika kunabwera mʼdziko lapansi, koma anthu anakonda mdima mʼmalo mwa kuwunikako, chifukwa ntchito zawo zinali zoyipa.
Tel est le jugement: la lumière est venue dans le monde, et les hommes ont préféré les ténèbres à la lumière, parce que leurs œuvres étaient mauvaises.
20 Aliyense wochita zoyipa amadana ndi kuwunika, ndipo sabwera poyera chifukwa cha mantha kuti ntchito zake zingaonekere.
Car quiconque fait le mal hait la lumière et ne vient pas à la lumière, de peur que ses œuvres ne soient dévoilées.
21 Koma aliyense wokhala mu choonadi amabwera ku kuwunika, kuti zionekere poyera zimene iye wachita zachitika kudzera mwa Mulungu.”
Mais celui qui pratique la vérité vient à la lumière, afin que ses œuvres soient révélées, et qu'elles soient faites en Dieu. »
22 Zitatha izi, Yesu ndi ophunzira ake anapita mʼmadera a ku midzi ya ku Yudeya, kumene Iye anakhala kanthawi akubatiza.
Après ces choses, Jésus vint avec ses disciples dans le pays de Judée. Il y resta avec eux, et il baptisa.
23 Ndipo Yohane amabatizanso ku Ainoni kufupi ndi Salimu, chifukwa kumeneko kunali madzi ambiri ndipo anthu amabwererabwererabe kudzabatizidwa.
Jean aussi baptisait à Enon, près de Salim, parce qu'il y avait là beaucoup d'eau. Ils vinrent et furent baptisés;
24 (Apa nʼkuti Yohane asanatsekeredwe mʼndende).
car Jean n'avait pas encore été jeté en prison.
25 Mkangano unabuka pakati pa ophunzira ena a Yohane ndi Ayuda ena pa zamwambo wodziyeretsa wa Ayuda.
Les disciples de Jean eurent alors une dispute avec quelques Juifs au sujet de la purification.
26 Iwo anabwera kwa Yohane anati, “Rabi, munthu uja munali naye mbali inayo ya mu mtsinje wa Yorodani, amene munamuchitira umboni, taonani naye akubatizanso, ndipo aliyense akupita kwa Iye.”
Ils s'approchèrent de Jean et lui dirent: « Rabbi, celui qui était avec toi au-delà du Jourdain, et à qui tu as rendu témoignage, voici qu'il baptise, et tout le monde vient à lui. »
27 Atamva zimenezi, Yohane anayankha kuti, “Munthu amalandira chokhacho chapatsidwa kwa iye kuchokera kumwamba.
Jean répondit: Un homme ne peut rien recevoir si cela ne lui a pas été donné du ciel.
28 Inuyo ndinu mboni zanga kuti ine ndinati, ‘Ine sindine Khristu koma ndatumidwa patsogolo pa Iye.’
Vous rendez vous-mêmes témoignage que j'ai dit: « Je ne suis pas le Christ », mais: « J'ai été envoyé avant lui ».
29 Mwini wake wa mkwatibwi ndi mkwati. Ndipo bwenzi lamkwati limadikira ndi kumvetsera iye, ndipo amakondwa akamva mawu a mkwatiyo. Ine changa ndi chimwemwe ndipo ndine wosangalala kwambiri.
Celui qui a l'épouse est l'époux; mais l'ami de l'époux, qui se tient debout et qui l'écoute, se réjouit beaucoup à cause de la voix de l'époux. C'est pourquoi ma joie est complète.
30 Nʼkoyenera kuti Iyeyo akule, ine ndichepe.
Il faut qu'il augmente, mais il faut que je diminue.
31 “Iye wochokera kumwamba ndi wapamwamba pa onse: iye wochokera mʼdziko lapansi ndi wa dziko lapansi, ndipo amayankhula monga mmodzi wa adziko lapansi. Iye wochokera kumwamba ndi wopambana onse.
« Celui qui vient d'en haut est au-dessus de tout. Celui qui vient de la terre appartient à la terre et parle de la terre. Celui qui vient du ciel est au-dessus de tout.
32 Iye achita umboni pa zimene waziona ndi kuzimva, koma palibe avomereza umboni wake.
Ce qu'il a vu et entendu, il en rend témoignage, et personne ne reçoit son témoignage.
33 Munthu amene amawulandira akutsimikizira kuti Mulungu ndi woona.
Celui qui a reçu son témoignage a marqué de son sceau que Dieu est vrai.
34 Pakuti amene Mulungu wamutuma amayankhula mawu a Mulungu; Mulungu wamupatsa Mzimu Woyera mopanda malire.
En effet, celui que Dieu a envoyé prononce les paroles de Dieu, car Dieu donne l'Esprit sans mesure.
35 Atate amakonda Mwana ndipo apereka zonse mʼmanja mwake.
Le Père aime le Fils, et il a remis toutes choses entre ses mains.
36 Aliyense wokhulupirira Mwanayo ali ndi moyo wosatha, koma iye amene samvera Mwanayo sadzawuona moyo, pakuti mkwiyo wa Mulungu umakhala pa iye.” (aiōnios g166)
Celui qui croit au Fils a la vie éternelle, mais celui qui désobéit au Fils ne verra pas la vie, mais la colère de Dieu demeure sur lui. » (aiōnios g166)

< Yohane 3 >