< Yohane 3 >
1 Ndipo panali Mfarisi wotchedwa Nekodimo, wa mʼgulu lolamulira la Ayuda.
There was a man of the Pharisees named Nicodemus, a ruler of the Jews:
2 Iye anabwera kwa Yesu usiku ndipo anati, “Rabi, ife tikudziwa kuti ndinu aphunzitsi wochokera kwa Mulungu, pakuti palibe amene angachite zizindikiro zodabwitsa zimene Inu mukuchita ngati Mulungu sali naye.”
The same came to Jesus by night, and said to him, Rabbi, we know that thou art a teacher come from God: for no man can do these miracles that thou doest, except God be with him.
3 Poyankha Yesu ananena kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti, ngati munthu sabadwanso mwatsopano sangathe kuona ufumu wa Mulungu.”
Jesus answered and said to him, Verily, verily, I say to thee, Except a man be born again, he cannot see the kingdom of God.
4 Nekodimo anati, “Kodi munthu angabadwenso bwanji atakalamba? Kodi angalowe kachiwiri mʼmimba ya amayi ake kuti abadwenso?”
Nicodemus saith to him, How can a man be born when he is old? can he enter the second time into his mother's womb, and be born?
5 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu Woyera, sangalowe mu ufumu wa Mulungu.
Jesus answered, Verily, verily, I say to thee, Except a man be born of water, and [of] the Spirit, he cannot enter into the kingdom of God.
6 Thupi limabereka thupi, koma Mzimu amabereka mzimu.
That which is born of the flesh, is flesh; and that which is born of the Spirit, is spirit.
7 Iwe usadabwe chifukwa ndakuwuza kuti, ‘Uyenera kubadwanso.’
Marvel not that I said to thee, Ye must be born again.
8 Mphepo imawomba kulikonse kumene ikufuna. Ungathe kumva kuwomba kwake, koma sungathe kudziwa kumene ikuchokera kapena kumene ikupita. Nʼchimodzimodzi ndi amene abadwa ndi Mzimu Woyera.”
The wind bloweth where it will, and thou hearest the sound of it, but canst not tell whence it cometh, and whither it goeth: so is every one that is born of the Spirit.
9 Nekodimo anafunsa kuti, “Kodi izi zingatheke bwanji?”
Nicodemus answered and said to him, How can these things be?
10 Yesu anati, “Iwe mphunzitsi wa Israeli, kodi sukuzindikira zimenezi?
Jesus answered and said to him, Art thou a teacher of Israel, and knowest not these things?
11 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ife tiyankhula zimene tikuzidziwa ndi kuchitira umboni zimene taziona, komabe inu simuvomereza umboni wathu.
Verily, verily, I say to thee, We speak what we know, and testify what we have seen; and ye receive not our testimony.
12 Ine ndikuyankhula kwa iwe zinthu za dziko lapansi ndipo sukukhulupirira. Nanga kodi udzakhulupirira bwanji ngati nditayankhula zinthu zakumwamba?
If I have told you earthly things, and ye believe not, how will ye believe if I tell you heavenly things?
13 Palibe wina aliyense anapita kumwamba, koma yekhayo amene watsika kuchokera kumwamba, Mwana wa Munthu.
And no man hath ascended to heaven, but he that came down from heaven, [even] the Son of man who is in heaven.
14 Tsono monga Mose anapachika njoka mʼchipululu, moteronso Mwana wa Munthu ayenera kupachikidwa,
And as Moses lifted up the serpent in the wilderness, even so must the Son of man be lifted up:
15 kuti aliyense amene akhulupirira Iye akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios )
That whoever believeth in him should not perish, but have eternal life. (aiōnios )
16 “Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios )
For God so loved the world, that he gave his only-begotten Son, that whoever believeth in him, should not perish, but have everlasting life. (aiōnios )
17 Pakuti Mulungu sanatume Mwana wake ku dziko lapansi, kuti akaweruze, koma kuti akapulumutse dziko lapansi.
For God sent not his Son into the world to condemn the world, but that the world through him may be saved.
18 Aliyense wokhulupirira Iye saweruzidwa, koma aliyense wosakhulupirira waweruzidwa kale chifukwa sanakhulupirire dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu.
He that believeth on him, is not condemned: but he that believeth not, is condemned already, because he hath not believed in the name of the only-begotten Son of God.
19 Ndipo chiweruzo ndi ichi: kuwunika kunabwera mʼdziko lapansi, koma anthu anakonda mdima mʼmalo mwa kuwunikako, chifukwa ntchito zawo zinali zoyipa.
And this is the condemnation, that light is come into the world, and men have loved darkness rather than light, because their deeds were evil.
20 Aliyense wochita zoyipa amadana ndi kuwunika, ndipo sabwera poyera chifukwa cha mantha kuti ntchito zake zingaonekere.
For every one that doeth evil hateth the light, neither cometh to the light, lest his deeds should be reproved.
21 Koma aliyense wokhala mu choonadi amabwera ku kuwunika, kuti zionekere poyera zimene iye wachita zachitika kudzera mwa Mulungu.”
But he that doeth truth, cometh to the light, that his deeds may be made manifest, that they are wrought in God.
22 Zitatha izi, Yesu ndi ophunzira ake anapita mʼmadera a ku midzi ya ku Yudeya, kumene Iye anakhala kanthawi akubatiza.
After these things came Jesus and his disciples into the land of Judea; and there he tarried with them, and baptized.
23 Ndipo Yohane amabatizanso ku Ainoni kufupi ndi Salimu, chifukwa kumeneko kunali madzi ambiri ndipo anthu amabwererabwererabe kudzabatizidwa.
And John also was baptizing in Enon, near to Salim, because there was much water there: and they came, and were baptized.
24 (Apa nʼkuti Yohane asanatsekeredwe mʼndende).
For John was not yet cast into prison.
25 Mkangano unabuka pakati pa ophunzira ena a Yohane ndi Ayuda ena pa zamwambo wodziyeretsa wa Ayuda.
Then there arose a question between [some] of John's disciples and the Jews, about purifying.
26 Iwo anabwera kwa Yohane anati, “Rabi, munthu uja munali naye mbali inayo ya mu mtsinje wa Yorodani, amene munamuchitira umboni, taonani naye akubatizanso, ndipo aliyense akupita kwa Iye.”
And they came to John, and said to him, Rabbi, he that was with thee beyond Jordan, to whom thou didst bear testimony, behold, the same baptizeth, and all [men] come to him.
27 Atamva zimenezi, Yohane anayankha kuti, “Munthu amalandira chokhacho chapatsidwa kwa iye kuchokera kumwamba.
John answered and said, A man can receive nothing, except it be given him from heaven.
28 Inuyo ndinu mboni zanga kuti ine ndinati, ‘Ine sindine Khristu koma ndatumidwa patsogolo pa Iye.’
Ye yourselves bear me testimony, that I said I am not the Christ, but that I am sent before him.
29 Mwini wake wa mkwatibwi ndi mkwati. Ndipo bwenzi lamkwati limadikira ndi kumvetsera iye, ndipo amakondwa akamva mawu a mkwatiyo. Ine changa ndi chimwemwe ndipo ndine wosangalala kwambiri.
He that hath the bride, is the bridegroom: but the friend of the bridegroom, who standeth and heareth him, rejoiceth greatly, because of the bridegroom's voice: this my joy therefore is fulfilled.
30 Nʼkoyenera kuti Iyeyo akule, ine ndichepe.
He must increase, but I [must] decrease.
31 “Iye wochokera kumwamba ndi wapamwamba pa onse: iye wochokera mʼdziko lapansi ndi wa dziko lapansi, ndipo amayankhula monga mmodzi wa adziko lapansi. Iye wochokera kumwamba ndi wopambana onse.
He that cometh from above is above all: he that is of the earth is earthly, and speaketh of the earth: he that cometh from heaven is above all.
32 Iye achita umboni pa zimene waziona ndi kuzimva, koma palibe avomereza umboni wake.
And what he hath seen and heard, that he testifieth; and no man receiveth his testimony.
33 Munthu amene amawulandira akutsimikizira kuti Mulungu ndi woona.
He that hath received his testimony, hath set to his seal that God is true.
34 Pakuti amene Mulungu wamutuma amayankhula mawu a Mulungu; Mulungu wamupatsa Mzimu Woyera mopanda malire.
For he whom God hath sent, speaketh the words of God: for [to him] God giveth not the Spirit by measure.
35 Atate amakonda Mwana ndipo apereka zonse mʼmanja mwake.
The Father loveth the Son, and hath given all things into his hand.
36 Aliyense wokhulupirira Mwanayo ali ndi moyo wosatha, koma iye amene samvera Mwanayo sadzawuona moyo, pakuti mkwiyo wa Mulungu umakhala pa iye.” (aiōnios )
He that believeth on the Son, hath everlasting life: and he that believeth not the Son, shall not see life; but the wrath of God abideth on him. (aiōnios )