< Yohane 21 >

1 Zitatha izi Yesu anaonekeranso kwa ophunzira ake, mʼmbali mwa nyanja ya Tiberiya. Anadzionetsera motere:
Emva kwalezizinto uJesu wabuya wazibonakalisa kubafundi elwandle lweTiberiyasi; njalo wazibonakalisa ngalindlela.
2 Simoni Petro, Tomasi (otchedwa Didimo), Natanieli wochokera ku Kana wa ku Galileya, ana a Zebedayo, ndi ophunzira ena awiri anali limodzi.
Babendawonye oSimoni Petro, loTomasi othiwa nguDidimusi, loNathaniyeli oweKana yeGalili, lamadodana kaZebediya, labanye ababili babafundi bakhe.
3 Simoni Petro anawawuza iwo kuti, “Ine ndikupita kukasodza,” ndipo iwo anati, “ife tipita nawe.” Choncho anapita ndi kulowa mʼbwato, koma usiku umenewo sanagwire kanthu.
USimoni Petro wathi kubo: Ngiyagola inhlanzi. Bathi kuye: Lathi sizahamba lawe. Basebephuma bahle bangena emkhunjini, kodwa ngalobobusuku kababambanga lutho.
4 Mmamawa, Yesu anayimirira mʼmbali mwa nyanja, koma ophunzira ake sanazindikire kuti anali Yesu.
Kwathi sekusemadabukakusa uJesu wema ekhunjini; kodwa abafundi babengazi ukuthi nguJesu.
5 Yesu anawafunsa iwo kuti, “Anzanga, kodi muli nsomba?” Iwo anayankha kuti, “Ayi.”
Ngakho uJesu wathi kubo: Bantwana, lilokudla yini? Bamphendula bathi: Hatshi.
6 Iye anati, “Ponyani khoka lanu kudzanja lamanja la bwato lanu ndipo mupha kanthu.” Atatero, iwo analephera kukoka ukonde chifukwa chakuchuluka kwa nsomba.
Wasesithi kubo: Phosani imbule ehlangothini lokunene lomkhumbi, njalo lizathola. Basebephosa, njalo babengaselakho ukulidonsa ngenxa yobunengi benhlanzi.
7 Kenaka ophunzira amene Yesu amamukonda anati kwa Petro, “Ndi Ambuye!” Petro atangomva iye akunena kuti ndi Ambuye, iye anavala chovala chake (pakuti anali atavula) ndipo analumphira mʼnyanja.
Ngakho lowomfundi uJesu ayemthanda wathi kuPetro: YiNkosi. USimoni Petro, esezwile ukuthi yiNkosi, wagqoka isembatho (ngoba wayenqunu), waseziphosela olwandle.
8 Ophunzira enawo analowa mʼbwato akukoka ukonde odzaza ndi nsomba, popeza iwo sanali kutali kuchokera ku mtunda, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi.
Kodwa abanye abafundi beza ngomkolo, bedonsa imbule lenhlanzi, ngoba babengekhatshana lomhlabathi, kodwa kungaba zingalo ezingamakhulu amabili.
9 Atafika pa mtunda, iwo anaona moto wamakala pamenepo ndi nsomba, ndi buledi.
Kwathi sebekhuphukele emhlabathini, babona umlilo wamalahle khona, lenhlanzi zibekwe phezu kwawo, lesinkwa.
10 Yesu anawawuza kuti, “Tabweretsa nsomba zina mwagwirazo.”
UJesu wathi kubo: Lethani ezinye zezinhlanzi elisanda kuzibamba.
11 Simoni Petro anakwera mʼbwato ndi kukokera khoka ku gombe, lodzaza ndi nsomba zikuluzikulu 153, komabe ndi nsomba zochuluka chotero khoka silinangʼambike.
USimoni Petro wasekhwela, wahudulela imbule emhlabathini, ligcwele inhlanzi ezinkulu, ikhulu lamatshumi amahlanu lantathu; njalo lanxa zazinengi kangaka, imbule kalidabukanga.
12 Yesu anawawuza kuti, “Bwerani mudzalandire chakudya chammawa.” Palibe mmodzi wa ophunzira anayesa kumufunsa Iye, “Kodi ndinu ndani?” Iwo anadziwa kuti anali Ambuye.
UJesu wathi kubo: Wozani lidle. Kodwa kakho kubafundi owaba lesibindi sokumbuza ukuthi: Ungubani wena? besazi ukuthi yiNkosi.
13 Yesu anabwera, natenga buledi ndikuwapatsa iwo, ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsomba.
UJesu wasesiza, wathatha isinkwa, wabanika, lenhlanzi ngokufananayo.
14 Aka kanali tsopano kachitatu Yesu akuonekera kwa ophunzira ake Iye ataukitsidwa kwa akufa.
Lokhu sekungokwesithathu uJesu ebonakaliswa kubafundi, esevukile kwabafileyo.
15 Iwo atamaliza kudya chakudya chammawa, Yesu anati kwa Simoni Petro, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikonda Ine kuposa mmene amandikondera awa?” Iye anati, “Inde Ambuye, Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.” Yesu anati, “Samala ana ankhosa anga.”
Sebedlile, uJesu wathi kuSimoni Petro: Simoni kaJona, uyangithanda kulalaba yini? Wathi kuye: Yebo Nkosi; wena uyazi ukuthi ngiyakuthanda. Wathi kuye: Phana amawundlu ami ukudla.
16 Yesu anatinso, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?” Iye anayankha kuti, “Inde, Ambuye, Inu mukudziwa kuti ine ndimakukondani.” Yesu anati, “Weta nkhosa zanga.”
Wabuya wathi kuye ngokwesibili: Simoni kaJona, uyangithanda yini? Wathi kuye: Yebo Nkosi, wena uyazi ukuthi ngiyakuthanda. Wathi kuye: Yelusa izimvu zami.
17 Yesu anati kwa iye kachitatu, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?” Petro anadzimvera chisoni chifukwa Yesu anamufunsa kachitatu kuti, “Kodi umandikonda Ine?” Iye anati, “Ambuye, Inu mudziwa zinthu zonse. Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.” Yesu anati, “Dyetsa nkhosa zanga.
Wathi kuye ngokwesithathu: Simoni kaJona, uyangithanda yini? UPetro wadabuka ngoba wathi kuye ngokwesithathu: Uyangithanda yini? Wasesithi kuye: Nkosi, wena uyakwazi konke; wena uyakwazi ukuthi ngiyakuthanda. UJesu wathi kuye: Phana izimvu zami ukudla.
18 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti uli wamngʼono unkadziveka wekha lamba ndi kupita kumene unkafuna; koma ukadzakalamba udzatambasula manja ako ndipo wina wake adzakuveka ndikukutsogolera kupita kumene sukufuna kupita.”
Ngiqinisile, ngiqinisile, ngithi kuwe: Usemutsha, wawuzibhinca, uhamba lapho othanda khona; kodwa nxa usumdala, uzakwelula izandla zakho, omunye abesekubopha, akuse lapho ongathandi khona.
19 Yesu ananena izi kumuzindikiritsa mtundu wa imfa imene Petro adzalemekezera nayo Mulungu. Kenaka Iye anati kwa Petro, “Nditsate Ine!”
Lalokhu wakutsho, etshengisa indlela yokufa ayezadumisa uNkulunkulu ngayo. Esetshilo lokhu wathi kuye: Ngilandela.
20 Petro anatembenuka ndi kuona kuti ophunzira amene Yesu amamukonda amawatsatira iwo. (Uyu ndi amene anatsamira pachifuwa cha Yesu pa chakudya chamadzulo ndipo iye anati, “Ambuye, kodi ndi ndani amene adzakuperekani Inu?”
UPetro etshibilika wabona umfundi uJesu amthandayo elandela, yena futhi owayeyeme esifubeni sakhe ekudleni kwantambama wathi: Nkosi, ngubani ozakunikela?
21 Petro atamuona iye, anafunsa kuti, “Ambuye, nanga uyu?”
Kwathi uPetro embona wathi kuJesu: Nkosi, lo-ke?
22 Yesu anayankha kuti, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo? Iwe uyenera kunditsata Ine.”
UJesu wathi kuye: Uba ngithanda ukuthi ahlale ngize ngifike, ulani lakho? Ngilandela wena.
23 Chifukwa cha ichi mbiri inafala pakati pa abale kuti wophunzira uyu sadzafa. Koma Yesu sananene kuti iye sadzafa. Iye anati, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo?”
Ngakho lelilizwi laphumela kubazalwane, ukuthi lowomfundi kayikufa; kanti uJesu katshongo kuye ukuthi kayikufa; kodwa wathi: Uba ngithanda ukuthi ahlale ngize ngifike, ulani lakho?
24 Uyu ndi wophunzira amene akuchitira umboni ndipo ndi amene analemba. Ife tidziwa kuti umboni wake ndi woona.
Nguye lowomfundi ofakaza ngalezizinto, lozibhalileyo; njalo siyazi ukuthi ubufakazi bakhe buliqiniso.
25 Koma palinso zina zambiri zimene Yesu anachita. Zikanalembedwa zonsezi, ndikhulupirira dziko lonse lapansi likanasowa malo osungirako mabuku onse amene akanalembedwa.
Njalo zikhona lezinye izinto ezinengi uJesu azenzayo, uba bezilotshiwe zonke ngazinye, ngicabanga ukuthi lomhlaba lawo ubungebe lendawo yezingwalo ezilotshiweyo. Ameni.

< Yohane 21 >