< Yohane 21 >
1 Zitatha izi Yesu anaonekeranso kwa ophunzira ake, mʼmbali mwa nyanja ya Tiberiya. Anadzionetsera motere:
After this, Jesus again showed Himself to the disciples. It was at the Lake of Tiberias. The circumstances were as follows.
2 Simoni Petro, Tomasi (otchedwa Didimo), Natanieli wochokera ku Kana wa ku Galileya, ana a Zebedayo, ndi ophunzira ena awiri anali limodzi.
Simon Peter was with Thomas, called the Twin, Nathanael of Cana in Galilee, the sons of Zabdi, and two others of the Master's disciples.
3 Simoni Petro anawawuza iwo kuti, “Ine ndikupita kukasodza,” ndipo iwo anati, “ife tipita nawe.” Choncho anapita ndi kulowa mʼbwato, koma usiku umenewo sanagwire kanthu.
Simon Peter said to them, "I am going fishing." "We will go too," said they. So they set out and went on board their boat; but they caught nothing that night.
4 Mmamawa, Yesu anayimirira mʼmbali mwa nyanja, koma ophunzira ake sanazindikire kuti anali Yesu.
When, however, day was now dawning, Jesus stood on the beach, though the disciples did not know that it was Jesus.
5 Yesu anawafunsa iwo kuti, “Anzanga, kodi muli nsomba?” Iwo anayankha kuti, “Ayi.”
He called to them. "Children," He said, "have you any food there?" "No," they answered.
6 Iye anati, “Ponyani khoka lanu kudzanja lamanja la bwato lanu ndipo mupha kanthu.” Atatero, iwo analephera kukoka ukonde chifukwa chakuchuluka kwa nsomba.
"Throw the net in on the right hand side," He said, "and you will find fish." So they threw the net in, and now they could scarcely drag it along for the quantity of fish.
7 Kenaka ophunzira amene Yesu amamukonda anati kwa Petro, “Ndi Ambuye!” Petro atangomva iye akunena kuti ndi Ambuye, iye anavala chovala chake (pakuti anali atavula) ndipo analumphira mʼnyanja.
This made the disciple whom Jesus loved say to Peter, "It is the Master." Simon Peter therefore, when he heard the words, "It is the Master," drew on his fisherman's shirt--for he had not been wearing it--put on his girdle, and sprang into the water.
8 Ophunzira enawo analowa mʼbwato akukoka ukonde odzaza ndi nsomba, popeza iwo sanali kutali kuchokera ku mtunda, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi.
But the rest of the disciples came in the small boat (for they were not far from land--only about a hundred yards off), dragging the net full of fish.
9 Atafika pa mtunda, iwo anaona moto wamakala pamenepo ndi nsomba, ndi buledi.
As soon as they landed, they saw a charcoal fire burning there, with fish broiling on it, and bread close by.
10 Yesu anawawuza kuti, “Tabweretsa nsomba zina mwagwirazo.”
Jesus told them to fetch some of the fish which they had just caught.
11 Simoni Petro anakwera mʼbwato ndi kukokera khoka ku gombe, lodzaza ndi nsomba zikuluzikulu 153, komabe ndi nsomba zochuluka chotero khoka silinangʼambike.
So Simon Peter went on board the boat and drew the net ashore full of large fish, 153 in number; and yet, although there were so many, the net had not broken.
12 Yesu anawawuza kuti, “Bwerani mudzalandire chakudya chammawa.” Palibe mmodzi wa ophunzira anayesa kumufunsa Iye, “Kodi ndinu ndani?” Iwo anadziwa kuti anali Ambuye.
"Come this way and have breakfast," said Jesus. But not one of the disciples ventured to question Him as to who He was, for they felt sure that it was the Master.
13 Yesu anabwera, natenga buledi ndikuwapatsa iwo, ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsomba.
Then Jesus came and took the bread and gave them some, and the fish in the same way.
14 Aka kanali tsopano kachitatu Yesu akuonekera kwa ophunzira ake Iye ataukitsidwa kwa akufa.
This was now the third occasion on which Jesus showed Himself to the disciples after He had risen from among the dead.
15 Iwo atamaliza kudya chakudya chammawa, Yesu anati kwa Simoni Petro, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikonda Ine kuposa mmene amandikondera awa?” Iye anati, “Inde Ambuye, Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.” Yesu anati, “Samala ana ankhosa anga.”
When they had finished breakfast, Jesus asked Simon Peter, "Simon, son of John, do you love me more than these others do?" "Yes, Master," was his answer; "you know that you are dear to me." "Then feed my lambs," replied Jesus.
16 Yesu anatinso, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?” Iye anayankha kuti, “Inde, Ambuye, Inu mukudziwa kuti ine ndimakukondani.” Yesu anati, “Weta nkhosa zanga.”
Again a second time He asked him, "Simon, son of John, do you love me?" "Yes, Master," he said, "you know that you are dear to me." "Then be a shepherd to my sheep," He said.
17 Yesu anati kwa iye kachitatu, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?” Petro anadzimvera chisoni chifukwa Yesu anamufunsa kachitatu kuti, “Kodi umandikonda Ine?” Iye anati, “Ambuye, Inu mudziwa zinthu zonse. Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.” Yesu anati, “Dyetsa nkhosa zanga.
A third time Jesus put the question: "Simon, son of John, am I dear to you?" It grieved Peter that Jesus asked him the third time, "Am I dear to you?" "Master," he replied, "you know everything, you can see that you are dear to me." "Then feed my much-loved sheep," said Jesus.
18 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti uli wamngʼono unkadziveka wekha lamba ndi kupita kumene unkafuna; koma ukadzakalamba udzatambasula manja ako ndipo wina wake adzakuveka ndikukutsogolera kupita kumene sukufuna kupita.”
"In most solemn truth I tell you that whereas, when you were young, you used to put on your girdle and walk whichever way you chose, when you have grown old you will stretch out your arms and some one else will put a girdle round you and carry you where you have no wish to go."
19 Yesu ananena izi kumuzindikiritsa mtundu wa imfa imene Petro adzalemekezera nayo Mulungu. Kenaka Iye anati kwa Petro, “Nditsate Ine!”
This He said to indicate the kind of death by which that disciple would bring glory to God; and after speaking thus He said to him, "Follow me."
20 Petro anatembenuka ndi kuona kuti ophunzira amene Yesu amamukonda amawatsatira iwo. (Uyu ndi amene anatsamira pachifuwa cha Yesu pa chakudya chamadzulo ndipo iye anati, “Ambuye, kodi ndi ndani amene adzakuperekani Inu?”
Peter turned round and noticed the disciple whom Jesus loved following--the one who at the supper had leaned back on His breast and had asked, "Master, who is it that is betraying you?"
21 Petro atamuona iye, anafunsa kuti, “Ambuye, nanga uyu?”
On seeing him, Peter asked Jesus, "And, Master, what about him?"
22 Yesu anayankha kuti, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo? Iwe uyenera kunditsata Ine.”
"If I desire him to remain till I come," replied Jesus, "what concern is that of yours? You, yourself, must follow me."
23 Chifukwa cha ichi mbiri inafala pakati pa abale kuti wophunzira uyu sadzafa. Koma Yesu sananene kuti iye sadzafa. Iye anati, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo?”
Hence the report spread among the brethren that that disciple would never die. Yet Jesus did not say, "He is not to die," but, "If I desire him to remain till I come, what concern is that of yours?"
24 Uyu ndi wophunzira amene akuchitira umboni ndipo ndi amene analemba. Ife tidziwa kuti umboni wake ndi woona.
That is the disciple who gives his testimony as to these matters, and has written this history; and we know that his testimony is true.
25 Koma palinso zina zambiri zimene Yesu anachita. Zikanalembedwa zonsezi, ndikhulupirira dziko lonse lapansi likanasowa malo osungirako mabuku onse amene akanalembedwa.
But there are also many other things which Jesus did--so vast a number indeed that if they were all described in detail, I suppose that the world itself could not contain the books that would have to be written.