< Yohane 21 >

1 Zitatha izi Yesu anaonekeranso kwa ophunzira ake, mʼmbali mwa nyanja ya Tiberiya. Anadzionetsera motere:
Siden åbenbarede Jesus sige atter for Disciplene ved Tiberias Søen; men han åbenbarede sig således.
2 Simoni Petro, Tomasi (otchedwa Didimo), Natanieli wochokera ku Kana wa ku Galileya, ana a Zebedayo, ndi ophunzira ena awiri anali limodzi.
Simon Peter og Thomas, hvilket betyder Tvilling, og Nathanael fra Kana i Galilæa og Zebedæus's Sønner og to andre af hans, Disciple vare sammen.
3 Simoni Petro anawawuza iwo kuti, “Ine ndikupita kukasodza,” ndipo iwo anati, “ife tipita nawe.” Choncho anapita ndi kulowa mʼbwato, koma usiku umenewo sanagwire kanthu.
Simon Peter siger til dem: "Jeg går ud at fiske." De sige til ham: "Også vi gå med dig." De gik ud og gik om Bord i Skibet, og den Nat fangede de intet.
4 Mmamawa, Yesu anayimirira mʼmbali mwa nyanja, koma ophunzira ake sanazindikire kuti anali Yesu.
Men da det nu blev Morgen, stod Jesus ved Søbredden; dog vidste Disciplene ikke, at det var Jesus.
5 Yesu anawafunsa iwo kuti, “Anzanga, kodi muli nsomba?” Iwo anayankha kuti, “Ayi.”
Jesus siger da til dem: "Børnlille! have I noget at spise?" De svarede ham: "Nej."
6 Iye anati, “Ponyani khoka lanu kudzanja lamanja la bwato lanu ndipo mupha kanthu.” Atatero, iwo analephera kukoka ukonde chifukwa chakuchuluka kwa nsomba.
Men han sagde til dem: "Kaster Garnet ud på højre Side af Skibet, så skulle I finde." Da kastede de det ud, og de formåede ikke mere at drage det for Fiskenes Mængde.
7 Kenaka ophunzira amene Yesu amamukonda anati kwa Petro, “Ndi Ambuye!” Petro atangomva iye akunena kuti ndi Ambuye, iye anavala chovala chake (pakuti anali atavula) ndipo analumphira mʼnyanja.
Den Discipel, som Jesus elskede, siger da til Peter: "Det er Herren." Da Simon Peter nu hørte, at det var Herren, bandt han sin Fiskerkjortel om sig (thi han var nøgen), og kastede sig i Søen.
8 Ophunzira enawo analowa mʼbwato akukoka ukonde odzaza ndi nsomba, popeza iwo sanali kutali kuchokera ku mtunda, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi.
Men de andre Disciple kom med Skibet, thi de vare ikke langt fra Land, kun omtrent to Hundrede Alen, og de slæbte efter sig Garnet med Fiskene.
9 Atafika pa mtunda, iwo anaona moto wamakala pamenepo ndi nsomba, ndi buledi.
Da de nu kom i Land, se de der en Kulild og Fisk ligge derpå og Brød.
10 Yesu anawawuza kuti, “Tabweretsa nsomba zina mwagwirazo.”
Jesus siger til dem: "Bringer hid af de Fisk, som I nu fangede."
11 Simoni Petro anakwera mʼbwato ndi kukokera khoka ku gombe, lodzaza ndi nsomba zikuluzikulu 153, komabe ndi nsomba zochuluka chotero khoka silinangʼambike.
Simon Peter steg op og trak Garnet på Land, fuldt af store Fisk, et Hundrede og tre og halvtredsindstyve, og skønt de vare så mange, sønderreves Garnet ikke.
12 Yesu anawawuza kuti, “Bwerani mudzalandire chakudya chammawa.” Palibe mmodzi wa ophunzira anayesa kumufunsa Iye, “Kodi ndinu ndani?” Iwo anadziwa kuti anali Ambuye.
Jesus siger til dem: "Kommer og holder Måltid! Men, ingen af Disciplene vovede at spørge ham: "Hvem er du?" thi de vidste, at det var Herren.
13 Yesu anabwera, natenga buledi ndikuwapatsa iwo, ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsomba.
Jesus kommer og tager Brødet og giver dem det, ligeledes også Fiskene.
14 Aka kanali tsopano kachitatu Yesu akuonekera kwa ophunzira ake Iye ataukitsidwa kwa akufa.
Dette var allerede den tredje Gang, at Jesus åbenbarede sig for sine Disciple, efter at han var oprejst fra de døde.
15 Iwo atamaliza kudya chakudya chammawa, Yesu anati kwa Simoni Petro, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikonda Ine kuposa mmene amandikondera awa?” Iye anati, “Inde Ambuye, Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.” Yesu anati, “Samala ana ankhosa anga.”
Da de nu havde holdt Måltid, siger Jesus til Simon Peter: "Simon, Johannes's Søn, elsker du mig mere end disse?" Han siger til ham: "Ja, Herre! du ved, at jeg har dig kær." Han siger til ham: "Vogt mine Lam!"
16 Yesu anatinso, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?” Iye anayankha kuti, “Inde, Ambuye, Inu mukudziwa kuti ine ndimakukondani.” Yesu anati, “Weta nkhosa zanga.”
Han siger atter anden Gang til ham: "Simon, Johannes's Søn, elsker du mig?" Han siger til ham: "Ja, Herre! du ved, at jeg har dig kær." Han siger til ham: "Vær Hyrde for mine Får!"
17 Yesu anati kwa iye kachitatu, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?” Petro anadzimvera chisoni chifukwa Yesu anamufunsa kachitatu kuti, “Kodi umandikonda Ine?” Iye anati, “Ambuye, Inu mudziwa zinthu zonse. Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.” Yesu anati, “Dyetsa nkhosa zanga.
Han siger tredje Gang til ham: "Simon, Johannes's Søn, har du mig kær?" Peter blev bedrøvet, fordi han tredje Gang sagde til ham: "Har du mig kær?" Og han sagde til ham: "Herre! du kender alle Ting, du ved, at jeg har dig kær." Jesus siger til ham: "Vogt mine Får!
18 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti uli wamngʼono unkadziveka wekha lamba ndi kupita kumene unkafuna; koma ukadzakalamba udzatambasula manja ako ndipo wina wake adzakuveka ndikukutsogolera kupita kumene sukufuna kupita.”
Sandelig, sandelig, siger jeg dig, da du var yngre, bandt du selv op om dig og gik, hvorhen du vilde; men når du bliver gammel, skal du udrække dine Hænder, og en anden skal binde op om dig og føre dig derhen, hvor du ikke vil."
19 Yesu ananena izi kumuzindikiritsa mtundu wa imfa imene Petro adzalemekezera nayo Mulungu. Kenaka Iye anati kwa Petro, “Nditsate Ine!”
Men dette sagde han for at betegne, med hvilken Død han skulde herliggøre Gud. Og da han havde sagt dette, siger han til ham: "Følg mig!"
20 Petro anatembenuka ndi kuona kuti ophunzira amene Yesu amamukonda amawatsatira iwo. (Uyu ndi amene anatsamira pachifuwa cha Yesu pa chakudya chamadzulo ndipo iye anati, “Ambuye, kodi ndi ndani amene adzakuperekani Inu?”
Peter vendte sig og så den Discipel følge, som Jesus elskede, og som også lå op til hans Bryst ved Nadveren og sagde: "Herre! hvem er den, som forråder dig?"
21 Petro atamuona iye, anafunsa kuti, “Ambuye, nanga uyu?”
Da nu Peter så ham, siger han til Jesus: "Herre! men hvorledes skal det gå denne?"
22 Yesu anayankha kuti, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo? Iwe uyenera kunditsata Ine.”
Jesus siger til ham: "Dersom jeg vil, at han skal blive, indtil jeg kommer, hvad vedkommer det dig? Følg du mig!"
23 Chifukwa cha ichi mbiri inafala pakati pa abale kuti wophunzira uyu sadzafa. Koma Yesu sananene kuti iye sadzafa. Iye anati, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo?”
Så kom da dette Ord ud iblandt Brødrene: "Denne Discipel dør ikke;" og Jesus havde dog ikke sagt til ham, at han ikke skulde dø, men: "Dersom jeg vil, at han skal blive, indtil jeg kommer, hvad vedkommer det dig?"
24 Uyu ndi wophunzira amene akuchitira umboni ndipo ndi amene analemba. Ife tidziwa kuti umboni wake ndi woona.
Dette er den Discipel, som vidner om disse Ting og har skrevet dette; og vi vide, at hans Vidnesbyrd er sandt.
25 Koma palinso zina zambiri zimene Yesu anachita. Zikanalembedwa zonsezi, ndikhulupirira dziko lonse lapansi likanasowa malo osungirako mabuku onse amene akanalembedwa.
Men der er også mange andre Ting, som Jesus har gjort, og dersom de skulde skrives enkeltvis. mener jeg, at ikke hele Verden kunde rumme de Bøger, som da bleve skrevne.

< Yohane 21 >