< Yohane 20 >
1 Mmamawa tsiku loyamba la sabata, kukanali kamdimabe, Mariya wa ku Magadala anapita ku manda ndipo anaona kuti mwala unali utachotsedwa pa khomo la manda.
Linu kuseni seni he zuba lya matangilo lye viiki, ha ku ba ku sisiha, Maria Magadalana cheza kwi kuumbu mi cha bona ibbwe ni li pindumunwa kuzwa kwi kuumbu.
2 Choncho anabwerera akuthamanga kwa Simoni Petro ndi wophunzira winayo, amene Yesu anamukonda, ndipo anati, “Iwo amuchotsa Ambuye mʼmanda, ndipo ife sitikudziwa kumene iwo amuyika Iye!”
Mi cha tiiya ni kwiza kwa Simone Pitolosi ni ku ba lutwana bamwi abo Jesu ba ba kusuna, mi nati kubali, “Ba ba hindi Simwine kumu zwisa mwi ikuumbu, mi ka twizi uko ku baba ka mulaziki.”
3 Choncho Petro ndi wophunzira winayo ananyamuka kupita ku manda.
Mi kuzwa aho Pitolosi ni zumwi mulutwana chi ba zwa kuyenda, mi chi ba yenda kwi ikuumbu.
4 Onse awiri anathamanga pamodzi koma wophunzira winayo anamupitirira Petro, nafika ku manda moyambirira.
Bonse chi ba tiya hamwina, mi zumwi mulutwana cha tiyaa ha busu kuhitilila Pitolosi mi ni ku sika wentanzi kwi ikuumbu.
5 Ndipo mmene anawerama nasuzumira mʼkati mwa manda anaona nsalu zili potero koma sanalowemo.
Mi cha zunza mo cha bona majila a zi zwato na dansi hateni, kono kana abe njili mukati.
6 Kenaka Simoni Petro, amene anali pambuyo pake, anafika ndi kulowa mʼmanda. Iye anaona nsaluzo zili pamenepo,
Simone Pitolosi ya ba shalile kwali cha sika mi cha yenda mwi ikuumbu. Cha bona majira a zizwato na dansi hateni,
7 pamodzinso ndi nsalu imene anakulungira nayo mutu wa Yesu. Nsaluyi inali yopindidwa pa yokha yosiyanitsidwa ndi inayo.
mi ni jira li bena ku mutwi wa kwe. ka hena li ba dansi hamwina ni majira a zizwato kono liba bungeletwe ha ngi lyolyona.
8 Pomaliza wophunzira winayo, amene anafika ku manda moyambirira, analowanso mʼkati, iye anaona ndi kukhulupirira.
Linu zumwi mu lutwana, iye ya ba tangi kusika kwi ikuumbu, naye che njila mukati, mi cha bona ni ku zumina.
9 (Iwo sanazindikire kuchokera mʼmalemba kuti Yesu anayanera kuuka kuchokera kwa akufa).
Mi ku sikila ina i nako kana ba beni kwi ziba iñolo kuti mbwabuke ku zwa ku ba fwile.
10 Kenaka ophunzira anabwerera ku nyumba zawo,
Mi balutwana chi ba boola ku inzubo hape.
11 koma Mariya anayima kunja kwa manda akulira. Pamene akulira, anawerama ndi kusuzumira mʼmanda
Kono Maria aba zimene hanze lye ikuumbu na silisa. Ha ba ku silisa bulyo, cha kotama ni ku zunza mwi ikuumbu.
12 ndipo anaona angelo awiri atavala zoyera, atakhala pamene panali mtembo wa Yesu, mmodzi kumutu ndi wina kumapazi.
Cha bona ma ngeloi obele muzituba ne keele, limwi ku mutwi, limwi ku matende uko mubiliwa Jesu uba lele.
13 Iwo anamufunsa iye kuti, “Amayi, nʼchifukwa chiyani mukulira?” Iye anati, “Amuchotsa Mbuye wanga, ndipo ine sindikudziwa kumene iwo amuyika.”
Chi bati kwali, “mwanakazi, cinzi ha usilisa?” cha wamba kubali, “Ka kuti ba hinda Simwine wangu, mi kanizi uko kuba mubika.”
14 Atanena izi, iye anatembenuka ndipo anaona Yesu atayima potero koma iye sanazindikire kuti anali Yesu.
Ha wamba ichi, cha chebuka mi cha bona Jesu na zimene hana, kono kana abezi kuti nji Jesu.
15 Iye anati, “Amayi, mukulira chifukwa chiyani? Ndani amene mukumufunafuna?” Poganiza kuti anali mwini munda, iye anati, “Bwana, ngati inu mwamuchotsa, ndiwuzeni kumene mwamuyika, ndipo ine ndikamutenga.”
Jesu chati kwali, “Mwanakazi, chinzi ha u silisa? ukwete ku lola ni?” abali ku seza kuti mu loli we iwa, mi nati kwali, “Mutompehi, heba wa mu zwisa kunze, ni wa mbile ku wa mubika, mi munika mu zwise kwateni.”
16 Yesu anati kwa iye, “Mariya.” Anatembenukira kwa Iye nafuwula mu Chiaramaiki kuti, “Raboni!” (kutanthauza Mphunzitsi).
Jesu nati kwali, “Maria.” Cha che buka, cha wamba kwali mu chi Aramaiki, “Rabboni,” (italusa: “Muluti.”)
17 Yesu anati, “Usandigwire Ine, pakuti sindinapite kwa Atate. Mʼmalo mwake pita kwa abale anga ndikukawawuza kuti, ndikupita kwa Atate ndi kwa Atate anunso, kwa Mulungu wanga ndi Mulungu wanunso.”
Jesu nati kwali, “kanji uni kwati, ka kuti ka nini ku bola kwi wulu kwa Itayo, kono u yende ku ba mwangu mi ukate ku bali kuti muni ye kwi wulu kwa Tayo ni Itayo wako, kwe reeza wangu ni Ireeza wako.”
18 Mariya wa ku Magadala anapita kwa ophunzira ndi uthenga wakuti, “Ndamuona Ambuye!” Iye anawawuza iwo kuti Yesu ananena zinthu izi kwa iye.
Maria Magadalena che za ni ku wambila ba lutwana, “Ni ba boni Simwine” mi ni kuti aba wambi izi ziintu kwali.
19 Madzulo a tsiku limenelo limene linali loyamba la Sabata ophunzira ake ali pamodzi, atatseka ndi kukhoma zitseko chifukwa choopa Ayuda, Yesu anabwera ndi kuyima pakati pawo nati, “Mtendere ukhale nanu!”
Ha chiibali citengu, ho luna lu zuba, izuba lye ntanzi lwe viiki, mi mi lyango ya mu babena ba lutwana, ibe ya litwe cha ku tiya Majuda, Jesu che za mi cha zimana mukati kabo mi chati ku bali, “i nkozo kwenu.”
20 Iye atatha kunena izi, anawaonetsa manja ake ndi mʼnthiti mwake. Ophunzira anasangalala kwambiri pamene anaona Ambuye.
Ha mana ku te chi, cha ba tondeza mayanza akwe ni mpaati yakwe. Mi ba lutwana haba bona Simwine, ba ba sangite.
21 Yesu anatinso, “Mtendere ukhale nanu! Monga Atate anandituma Ine, Inenso ndikukutumani.”
Jesu kuzwaho cha wamba kubali hape, “i nkozo kwenu. Sina Itayo habani tumi, linu mu ni mi tumina.”
22 Ndi mawu amenewo Iye anawapumira ndipo anati, “Landirani Mzimu Woyera.
Jesu hamana ku ta ichi, na huzikiza ha bali mi nati kubali, “Mu tambule lu Huho lu Jolola.
23 Ngati mukhululukira aliyense machimo ake, iwo akhululukidwa; ngati simuwakhululukira, iwo sanakhululukidwe.”
Bonse ba mu wo ndola zibe, ba zi wo ndelwa; bonse ba zibe zi mukwete, zi si kwetwe.”
24 Koma Tomasi (otchedwa Didimo), mmodzi wa khumi ndi awiriwo, sanali ndi ophunzira pamene Yesu anabwera.
Tomasi, zumwi wabe kumi ni bobele, ya ba ku sumpwa Didimasi, kana bena nabo Jesu heza.
25 Ophunzira enawo atamuwuza Tomasi kuti iwo anaona Ambuye, iye ananenetsa kuti, “Pokhapokha nditaona zizindikiro za misomali mʼmanja ake ndi kuyikamo chala changa mʼmene munali misomali ndi kukhudza dzanja langa mʼnthiti mwake, ine sindidzakhulupirira.”
Bamwi ba lutwana ha ku mana chi ba mu cho, “Twa bona Simwine” Cha ba cho, “kwanda chi na bona mu mayanza akwe i bbata lya zi pikili, mi niku bika munwe mwi bbata lya zi pikili, ni ku bika i yanza lyangu mwi mpaati ya kwe, ke te ni zumine.”
26 Patapita sabata, ophunzira ake analinso mʼnyumbamo ndipo Tomasi anali nawo. Ngakhale makomo anali otsekedwa, Yesu anabwera nayima pakati pawo, ndipo anati, “Mtendere ukhale nanu!”
Ha kumana mazuba akwana iyanza ni to tatwe ba lutwana bakwe ba bena mukati hape, Mi Tomasi a bena nabo. Jesu cheza milyango ni basi yalitwe, mi cha ziima mukati ka bo, mi chati, “inkozo kwenu.”
27 Kenaka anati kwa Tomasi, “Ika chala chako apa; ona manja anga. Tambasula dzanja lako ndi kukhudza mʼnthiti mwanga. Leka kukayika, khulupirira.”
Mi cha ti kwa Tomasi, “u chune kunu ni munwe wako, u bone ma yanza angu, u chune kunu ni yanza lya ko, mi uli bike mwi mpaati yangu, kanji ubi yasa zumini, kono u zumine.”
28 Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye wanga ndi Mulungu wanga!”
Tomasi che taaba mi nati kwali, “Simwine wangu ni Ireeza wangu.”
29 Kenaka Yesu anamuwuza kuti, “Kodi wakhulupirira chifukwa wandiona Ine? Ndi odala amene amakhulupirira ngakhale asanaone.”
Jesu na cho kwali, “kakuti wani bona, wa zumina. Ba fuyoletwe nja bo ba seni ku bona, mi ni bazumina.”
30 Yesu anachita zodabwitsa zambiri pamaso pa ophunzira ake zimene sizinalembedwe mʼbuku lino.
Linu Jesu cha tenda zi supo zimwi zingi mu ku bako kwa ba lutwana, zi supo zi seni kuñolwa mwe yi imbuka,
31 Koma izi zalembedwa kuti mukhulupirire kuti Yesu ndi Khristu, Mwana wa Mulungu, ndi kuti mukakhulupirira mukhale nawo moyo mʼdzina lake.
kono izi zi ba ñolwa mukuti mu zumine kuti Jesu nji Kerisite, mwana wa Ireeza, mi nji kuti ku zumina, ni mwaba ni buhalo mwi zina lya kwe.