< Yohane 20 >

1 Mmamawa tsiku loyamba la sabata, kukanali kamdimabe, Mariya wa ku Magadala anapita ku manda ndipo anaona kuti mwala unali utachotsedwa pa khomo la manda.
And in o dai of the wouke Marie Maudeleyn cam eerli to the graue, whanne it was yit derk. And sche say the stoon moued awei fro the graue.
2 Choncho anabwerera akuthamanga kwa Simoni Petro ndi wophunzira winayo, amene Yesu anamukonda, ndipo anati, “Iwo amuchotsa Ambuye mʼmanda, ndipo ife sitikudziwa kumene iwo amuyika Iye!”
Therfor sche ran, and cam to Symount Petre, and to another disciple, whom Jhesus louede, and seith to hem, Thei han takun the Lord fro the graue, and we witen not, where thei han leid hym.
3 Choncho Petro ndi wophunzira winayo ananyamuka kupita ku manda.
Therfor Petre wente out, and thilke other disciple, and thei camen to the graue.
4 Onse awiri anathamanga pamodzi koma wophunzira winayo anamupitirira Petro, nafika ku manda moyambirira.
And thei tweyne runnen togidre, and thilke othere disciple ran bifor Petre, and cam first to the graue.
5 Ndipo mmene anawerama nasuzumira mʼkati mwa manda anaona nsalu zili potero koma sanalowemo.
And whanne he stoupide, he sai the schetis liynge, netheles he entride not.
6 Kenaka Simoni Petro, amene anali pambuyo pake, anafika ndi kulowa mʼmanda. Iye anaona nsaluzo zili pamenepo,
Therfor Symount Petre cam suynge hym, and he entride in to the graue, and he say the schetis leid,
7 pamodzinso ndi nsalu imene anakulungira nayo mutu wa Yesu. Nsaluyi inali yopindidwa pa yokha yosiyanitsidwa ndi inayo.
and the sudarie that was on his heed, not leid with the schetis, but bi it silf wlappid in to a place.
8 Pomaliza wophunzira winayo, amene anafika ku manda moyambirira, analowanso mʼkati, iye anaona ndi kukhulupirira.
Therfor thanne thilke disciple that cam first to the graue, entride, and sai, and bileuede.
9 (Iwo sanazindikire kuchokera mʼmalemba kuti Yesu anayanera kuuka kuchokera kwa akufa).
For thei knewen not yit the scripture, that it behofte him to rise ayen fro deth.
10 Kenaka ophunzira anabwerera ku nyumba zawo,
Therfor the disciplis wenten eftsoone to hem silf.
11 koma Mariya anayima kunja kwa manda akulira. Pamene akulira, anawerama ndi kusuzumira mʼmanda
But Marie stood at the graue with outforth wepynge. And the while sche wepte, sche bowide hir, and bihelde forth in to the graue.
12 ndipo anaona angelo awiri atavala zoyera, atakhala pamene panali mtembo wa Yesu, mmodzi kumutu ndi wina kumapazi.
And sche sai twei aungels sittinge in white, oon at the heed and oon at the feet, where the bodi of Jhesu was leid.
13 Iwo anamufunsa iye kuti, “Amayi, nʼchifukwa chiyani mukulira?” Iye anati, “Amuchotsa Mbuye wanga, ndipo ine sindikudziwa kumene iwo amuyika.”
And thei seien to hir, Womman, what wepist thou? Sche seide to hem, For thei han take awei my lord, and Y woot not, where thei han leid him.
14 Atanena izi, iye anatembenuka ndipo anaona Yesu atayima potero koma iye sanazindikire kuti anali Yesu.
Whanne sche hadde seid these thingis, sche turnede bacward, and sai Jhesu stondinge, and wiste not that it was Jhesu.
15 Iye anati, “Amayi, mukulira chifukwa chiyani? Ndani amene mukumufunafuna?” Poganiza kuti anali mwini munda, iye anati, “Bwana, ngati inu mwamuchotsa, ndiwuzeni kumene mwamuyika, ndipo ine ndikamutenga.”
Jhesus seith to hir, Womman, what wepist thou? whom sekist thou? She gessynge that he was a gardynere, seith to him, Sire, if thou hast takun him vp, seie to me, where thou hast leid him, and Y schal take hym awei.
16 Yesu anati kwa iye, “Mariya.” Anatembenukira kwa Iye nafuwula mu Chiaramaiki kuti, “Raboni!” (kutanthauza Mphunzitsi).
Jhesus seith to hir, Marie. Sche `turnede, and seith to hym, Rabony, that is to seie, Maister.
17 Yesu anati, “Usandigwire Ine, pakuti sindinapite kwa Atate. Mʼmalo mwake pita kwa abale anga ndikukawawuza kuti, ndikupita kwa Atate ndi kwa Atate anunso, kwa Mulungu wanga ndi Mulungu wanunso.”
Jhesus seith to hir, Nyle thou touche me, for Y haue not yit stied to my fadir; but go to my britheren, and seie to hem, Y stie to my fadir and to youre fadir, to my God and to youre God.
18 Mariya wa ku Magadala anapita kwa ophunzira ndi uthenga wakuti, “Ndamuona Ambuye!” Iye anawawuza iwo kuti Yesu ananena zinthu izi kwa iye.
Marie Maudeleyne cam, tellinge to the disciplis, That Y sai the Lord, and these thingis he seide to me.
19 Madzulo a tsiku limenelo limene linali loyamba la Sabata ophunzira ake ali pamodzi, atatseka ndi kukhoma zitseko chifukwa choopa Ayuda, Yesu anabwera ndi kuyima pakati pawo nati, “Mtendere ukhale nanu!”
Therfor whanne it was eue in that dai, oon of the sabatis, and the yatis weren schit, where the disciplis weren gaderid, for drede of the Jewis, Jhesus cam, and stood in the myddil of the disciplis, and he seith to hem, Pees to you.
20 Iye atatha kunena izi, anawaonetsa manja ake ndi mʼnthiti mwake. Ophunzira anasangalala kwambiri pamene anaona Ambuye.
And whanne he hadde seid this, he schewide to hem hondis and side; therfor the disciplis ioieden, for the Lord was seyn.
21 Yesu anatinso, “Mtendere ukhale nanu! Monga Atate anandituma Ine, Inenso ndikukutumani.”
And he seith to hem eft, Pees to you; as the fadir sente me, Y sende you.
22 Ndi mawu amenewo Iye anawapumira ndipo anati, “Landirani Mzimu Woyera.
Whanne he had seid this, he blewe on hem, and seide, Take ye the Hooli Goost;
23 Ngati mukhululukira aliyense machimo ake, iwo akhululukidwa; ngati simuwakhululukira, iwo sanakhululukidwe.”
whos synnes ye foryyuen, tho ben foryouun to hem; and whos ye withholden, tho ben withholdun.
24 Koma Tomasi (otchedwa Didimo), mmodzi wa khumi ndi awiriwo, sanali ndi ophunzira pamene Yesu anabwera.
But Thomas, oon of the twelue, that is seid Didimus, was not with hem, whanne Jhesus cam.
25 Ophunzira enawo atamuwuza Tomasi kuti iwo anaona Ambuye, iye ananenetsa kuti, “Pokhapokha nditaona zizindikiro za misomali mʼmanja ake ndi kuyikamo chala changa mʼmene munali misomali ndi kukhudza dzanja langa mʼnthiti mwake, ine sindidzakhulupirira.”
Therfor the othere disciplis seiden, We han seyn the Lord. And he seide to hem, But Y se in hise hondis the fitchinge of the nailis, and putte my fyngur in to the places of the nailis, and putte myn hond in to his side, Y schal not bileue.
26 Patapita sabata, ophunzira ake analinso mʼnyumbamo ndipo Tomasi anali nawo. Ngakhale makomo anali otsekedwa, Yesu anabwera nayima pakati pawo, ndipo anati, “Mtendere ukhale nanu!”
And after eiyte daies eftsoone hise disciplis weren with ynne, and Thomas with hem. Jhesus cam, while the yatis weren schit, and stood in the myddil, and seide, Pees to you.
27 Kenaka anati kwa Tomasi, “Ika chala chako apa; ona manja anga. Tambasula dzanja lako ndi kukhudza mʼnthiti mwanga. Leka kukayika, khulupirira.”
Afterward he seith to Thomas, Putte in here thi fyngur, and se myn hondis, and putte hidur thin hond, and putte in to my side, and nyle thou be vnbileueful, but feithful.
28 Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye wanga ndi Mulungu wanga!”
Thomas answeride, and seide to him, My Lord and my God.
29 Kenaka Yesu anamuwuza kuti, “Kodi wakhulupirira chifukwa wandiona Ine? Ndi odala amene amakhulupirira ngakhale asanaone.”
Jhesus seith to him, Thomas, for thou hast seyn me, thou bileuedist; blessid ben thei, that seyn not, and han bileued.
30 Yesu anachita zodabwitsa zambiri pamaso pa ophunzira ake zimene sizinalembedwe mʼbuku lino.
And Jhesus dide many othere signes in the siyt of hise disciplis, whiche ben not writun in this book.
31 Koma izi zalembedwa kuti mukhulupirire kuti Yesu ndi Khristu, Mwana wa Mulungu, ndi kuti mukakhulupirira mukhale nawo moyo mʼdzina lake.
But these ben writun, that ye bileue, that Jhesus `is Crist, the sone of God, and that ye bileuynge haue lijf in his name.

< Yohane 20 >