< Yohane 20 >

1 Mmamawa tsiku loyamba la sabata, kukanali kamdimabe, Mariya wa ku Magadala anapita ku manda ndipo anaona kuti mwala unali utachotsedwa pa khomo la manda.
Men paa den første Dag i Ugen kommer Maria Magdalene aarle, medens det endnu er mørkt, til Graven og ser Stenen borttagen fra Graven.
2 Choncho anabwerera akuthamanga kwa Simoni Petro ndi wophunzira winayo, amene Yesu anamukonda, ndipo anati, “Iwo amuchotsa Ambuye mʼmanda, ndipo ife sitikudziwa kumene iwo amuyika Iye!”
Da løber hun og kommer til Simon Peter og til den anden Discipel, ham, hvem Jesus elskede, og siger til dem: „De have borttaget Herren af Graven, og vi vide ikke, hvor de have lagt ham.‟
3 Choncho Petro ndi wophunzira winayo ananyamuka kupita ku manda.
Da gik Peter og den anden Discipel ud, og de kom til Graven.
4 Onse awiri anathamanga pamodzi koma wophunzira winayo anamupitirira Petro, nafika ku manda moyambirira.
Men de to løb sammen, og den anden Discipel løb foran, hurtigere end Peter, og kom først til Graven.
5 Ndipo mmene anawerama nasuzumira mʼkati mwa manda anaona nsalu zili potero koma sanalowemo.
Og da han kiggede ind, ser han Linklæderne ligge der, men gik dog ikke ind.
6 Kenaka Simoni Petro, amene anali pambuyo pake, anafika ndi kulowa mʼmanda. Iye anaona nsaluzo zili pamenepo,
Da kommer Simon Peter, som fulgte ham, og han gik ind i Graven og saa Linklæderne ligge der
7 pamodzinso ndi nsalu imene anakulungira nayo mutu wa Yesu. Nsaluyi inali yopindidwa pa yokha yosiyanitsidwa ndi inayo.
og Tørklædet, som han havde haft paa sit Hoved, ikke liggende ved Linklæderne, men sammenrullet paa et Sted for sig selv.
8 Pomaliza wophunzira winayo, amene anafika ku manda moyambirira, analowanso mʼkati, iye anaona ndi kukhulupirira.
Nu gik da ogsaa den anden Discipel, som var kommen først til Graven, ind, og han saa og troede.
9 (Iwo sanazindikire kuchokera mʼmalemba kuti Yesu anayanera kuuka kuchokera kwa akufa).
Thi de forstode endnu ikke Skriften, at han skulde opstaa fra de døde.
10 Kenaka ophunzira anabwerera ku nyumba zawo,
Da gik Disciplene atter bort til deres Hjem.
11 koma Mariya anayima kunja kwa manda akulira. Pamene akulira, anawerama ndi kusuzumira mʼmanda
Men Maria stod udenfor ved Graven og græd. Som hun nu græd, kiggede hun ind i Graven,
12 ndipo anaona angelo awiri atavala zoyera, atakhala pamene panali mtembo wa Yesu, mmodzi kumutu ndi wina kumapazi.
og hun ser to Engle sidde i hvide Klæder, en ved Hovedet og en ved Fødderne, hvor Jesu Legeme havde ligget.
13 Iwo anamufunsa iye kuti, “Amayi, nʼchifukwa chiyani mukulira?” Iye anati, “Amuchotsa Mbuye wanga, ndipo ine sindikudziwa kumene iwo amuyika.”
Og de sige til hende: „Kvinde! hvorfor græder du?‟ Hun siger til dem: „Fordi de have taget min Herre bort, og jeg ved ikke, hvor de have lagt ham.‟
14 Atanena izi, iye anatembenuka ndipo anaona Yesu atayima potero koma iye sanazindikire kuti anali Yesu.
Da hun havde sagt dette, vendte hun sig om, og hun ser Jesus staa der, og hun vidste ikke, at det var Jesus.
15 Iye anati, “Amayi, mukulira chifukwa chiyani? Ndani amene mukumufunafuna?” Poganiza kuti anali mwini munda, iye anati, “Bwana, ngati inu mwamuchotsa, ndiwuzeni kumene mwamuyika, ndipo ine ndikamutenga.”
Jesus siger til hende: „Kvinde! hvorfor græder du? hvem leder du efter?‟ Hun mente, det var Havemanden, og siger til ham: „Herre! dersom du har baaret ham bort, da sig mig, hvor du har lagt ham, saa vil jeg tage ham.‟
16 Yesu anati kwa iye, “Mariya.” Anatembenukira kwa Iye nafuwula mu Chiaramaiki kuti, “Raboni!” (kutanthauza Mphunzitsi).
Jesus siger til hende: „Maria!‟ Hun vender sig om og siger til ham paa Hebraisk: „Rabbuni!‟ hvilket betyder Mester.
17 Yesu anati, “Usandigwire Ine, pakuti sindinapite kwa Atate. Mʼmalo mwake pita kwa abale anga ndikukawawuza kuti, ndikupita kwa Atate ndi kwa Atate anunso, kwa Mulungu wanga ndi Mulungu wanunso.”
Jesus siger til hende: „Rør ikke ved mig, thi jeg er endnu ikke opfaren til min Fader; men gaa til mine Brødre og sig dem: Jeg farer op til min Fader og eders Fader og til min Gud og eders Gud.‟
18 Mariya wa ku Magadala anapita kwa ophunzira ndi uthenga wakuti, “Ndamuona Ambuye!” Iye anawawuza iwo kuti Yesu ananena zinthu izi kwa iye.
Maria Magdalene kommer og forkynder Disciplene: „Jeg har set Herren, ‟ og at han havde sagt hende dette.
19 Madzulo a tsiku limenelo limene linali loyamba la Sabata ophunzira ake ali pamodzi, atatseka ndi kukhoma zitseko chifukwa choopa Ayuda, Yesu anabwera ndi kuyima pakati pawo nati, “Mtendere ukhale nanu!”
Da det nu var Aften paa den samme Dag, den første Dag i Ugen, og Dørene der, hvor Disciplene opholdt sig, vare lukkede af Frygt for Jøderne, kom Jesus og stod midt iblandt dem, og han siger til dem: „Fred være med eder!‟
20 Iye atatha kunena izi, anawaonetsa manja ake ndi mʼnthiti mwake. Ophunzira anasangalala kwambiri pamene anaona Ambuye.
Og som han sagde dette, viste han dem sine Hænder og sin Side. Saa bleve Disciplene glade, da de saa Herren.
21 Yesu anatinso, “Mtendere ukhale nanu! Monga Atate anandituma Ine, Inenso ndikukutumani.”
Jesus sagde da atter til dem: „Fred være med eder! Ligesom Faderen har udsendt mig, saaledes sender ogsaa jeg eder.‟
22 Ndi mawu amenewo Iye anawapumira ndipo anati, “Landirani Mzimu Woyera.
Og da han havde sagt dette, aandede han paa dem, og han siger til dem: „Modtager den Helligaand!
23 Ngati mukhululukira aliyense machimo ake, iwo akhululukidwa; ngati simuwakhululukira, iwo sanakhululukidwe.”
Hvem I forlade Synderne, dem ere de forladte, og hvem I nægte Forladelse, dem er den nægtet.‟
24 Koma Tomasi (otchedwa Didimo), mmodzi wa khumi ndi awiriwo, sanali ndi ophunzira pamene Yesu anabwera.
Men Thomas, hvilket betyder Tvilling, en af de tolv, var ikke hos dem, da Jesus kom.
25 Ophunzira enawo atamuwuza Tomasi kuti iwo anaona Ambuye, iye ananenetsa kuti, “Pokhapokha nditaona zizindikiro za misomali mʼmanja ake ndi kuyikamo chala changa mʼmene munali misomali ndi kukhudza dzanja langa mʼnthiti mwake, ine sindidzakhulupirira.”
De andre Disciple sagde da til ham: „Vi have set Herren.‟ Men han sagde til dem: „Uden jeg faar set Naglegabet i hans Hænder og stikker min Finger i Naglegabet og stikker min Haand i hans Side, vil jeg ingenlunde tro.‟
26 Patapita sabata, ophunzira ake analinso mʼnyumbamo ndipo Tomasi anali nawo. Ngakhale makomo anali otsekedwa, Yesu anabwera nayima pakati pawo, ndipo anati, “Mtendere ukhale nanu!”
Og otte Dage efter vare hans Disciple atter inde, og Thomas med dem. Jesus kommer, da Dørene vare lukkede, og han stod midt iblandt dem og sagde: „Fred være med eder!‟
27 Kenaka anati kwa Tomasi, “Ika chala chako apa; ona manja anga. Tambasula dzanja lako ndi kukhudza mʼnthiti mwanga. Leka kukayika, khulupirira.”
Derefter siger han til Thomas: „Ræk din Finger hid, og se mine Hænder, og ræk din Haand hid, og stik den i min Side, og vær ikke vantro, men troende!‟
28 Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye wanga ndi Mulungu wanga!”
Thomas svarede og sagde til ham: „Min Herre og min Gud!‟
29 Kenaka Yesu anamuwuza kuti, “Kodi wakhulupirira chifukwa wandiona Ine? Ndi odala amene amakhulupirira ngakhale asanaone.”
Jesus siger til ham: „Fordi du har set mig, har du troet; salige ere de, som ikke have set og dog troet.‟ —
30 Yesu anachita zodabwitsa zambiri pamaso pa ophunzira ake zimene sizinalembedwe mʼbuku lino.
Desuden gjorde Jesus mange andre Tegn for sine Disciples Aasyn, som ikke ere skrevne i denne Bog.
31 Koma izi zalembedwa kuti mukhulupirire kuti Yesu ndi Khristu, Mwana wa Mulungu, ndi kuti mukakhulupirira mukhale nawo moyo mʼdzina lake.
Men dette er skrevet, for at I skulle tro, at Jesus er Kristus, Guds Søn, og for at I, naar I tro, skulle have Livet i hans Navn.

< Yohane 20 >