< Yohane 2 >
1 Pa tsiku lachitatu munali ukwati mu Kana wa ku Galileya. Amayi ake a Yesu anali komweko,
Und am dritten Tage war [Eig. ward] eine Hochzeit zu Kana in Galiläa; und die Mutter Jesu war daselbst.
2 ndipo Yesu ndi ophunzira ake anayitanidwanso ku ukwatiwo.
Es war aber auch Jesus mit seinen Jüngern zu der Hochzeit geladen.
3 Vinyo atatha, amayi a Yesu anati kwa Iye, “Wawathera vinyo.”
Und als es an Wein gebrach, spricht die Mutter Jesu zu ihm: Sie haben keinen Wein.
4 Yesu anayankha kuti, “Amayi, chifukwa chiyani mukundiwuza Ine? Nthawi yanga sinakwane.”
Jesus spricht zu ihr: Was habe ich mit dir zu schaffen, Weib? Meine Stunde ist noch nicht gekommen.
5 Amayi ake anati kwa antchito, “Inu muchite chilichonse chimene akuwuzeni.”
Seine Mutter spricht zu den Dienern: Was irgend er euch sagen mag, tut.
6 Pamenepo panali mitsuko yamiyala yothiramo madzi isanu ndi umodzi, imene Ayuda amagwiritsa ntchito pa mwambo wodziyeretsa. Uliwonse unali ndi malita 100 kapena kupitirirapo.
Es waren aber daselbst sechs steinerne Wasserkrüge aufgestellt, nach der Reinigungssitte der Juden, wovon jeder zwei oder drei Maß [Griech.: Metreten, ein Hohlmaß von etwa 39 Liter] faßte.
7 Yesu anati kwa antchitowo, “Dzazani madzi mʼmitsukoyi,” ndipo iwo anadzaza ndendende.
Jesus spricht zu ihnen: Füllet die Wasserkrüge mit Wasser. Und sie füllten sie bis oben an.
8 Ndipo Iye anatinso kwa iwo, “Tsopano tungani ndipo kaperekeni kwa mkulu waphwando.” Iwo anachita momwemo.
Und er spricht zu ihnen: Schöpfet nun und bringet es dem Speisemeister. Und sie brachten es.
9 Mkulu waphwando analawa madziwo amene anasandulika vinyo, ndipo sanazindikire kumene vinyoyo anachokera, ngakhale kuti antchito amene anatunga madziwo amadziwa. Kenaka anayitanira mkwati pambali
Als aber der Speisemeister das Wasser gekostet hatte, welches Wein geworden war [und er wußte nicht, woher er war, [W. ist] die Diener aber, welche das Wasser geschöpft hatten, wußten es], ruft der Speisemeister den Bräutigam
10 ndipo anati, “Aliyense amatulutsa vinyo wokoma kwambiri poyambirira ndipo kenaka vinyo wosakoma pamene oyitanidwa atamwa kale wambiri; koma iwe wasunga wokoma mpaka tsopano.”
und spricht zu ihm: Jeder Mensch setzt zuerst den guten Wein vor, und wenn sie trunken geworden sind, alsdann den geringeren; du hast den guten Wein bis jetzt aufbewahrt.
11 Ichi chinali chizindikiro chodabwitsa choyamba chimene Yesu anachita ku Kana wa ku Galileya. Potero Iye anawulula ulemerero wake, ndipo ophunzira ake anamukhulupirira Iye.
Diesen Anfang der Zeichen machte Jesus zu Kana in Galiläa und offenbarte seine Herrlichkeit; und seine Jünger glaubten an ihn.
12 Zitatha izi Iye anatsikira ku Kaperenawo pamodzi ndi amayi ake, abale ake ndi ophunzira ake. Iwo anakhala kumeneko masiku owerengeka.
Nach diesem ging er hinab nach Kapernaum, er und seine Mutter und seine Brüder und seine Jünger; und daselbst blieben sie nicht viele Tage.
13 Nthawi ya Paska ya Ayuda itayandikira, Yesu anapita ku Yerusalemu.
Und das Passah der Juden war nahe, und Jesus ging hinauf nach Jerusalem.
14 Mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu Iye anapeza anthu akugulitsa ngʼombe, nkhosa ndi nkhunda ndipo ena akusintha ndalama pa matebulo.
Und er fand im Tempel [die Gebäude; s. die Anm. zu Mat. 4,5] die Ochsen- und Schafe- und Taubenverkäufer, und die Wechsler dasitzen.
15 Chifukwa cha zimenezi Iye anapanga chikwapu cha zingwe ndipo anatulutsa onse mʼbwalo la Nyumbayo, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe; Iye anamwaza ndalama zawo ndi kugudubuza matebulo.
Und er machte eine Geißel aus Stricken und trieb sie alle zum Tempel [die Gebäude; s. die Anm. zu Mat. 4,5] hinaus, sowohl die Schafe als auch die Ochsen; [O. auch die Schafe und die Ochsen] und die Münze der Wechsler schüttete er aus, und die Tische warf er um;
16 Kwa amene amagulitsa nkhunda, Iye anati, “Tulutsani izi muno! Osasandutsa Nyumba ya Atate anga msika!”
und zu den Taubenverkäufern sprach er: Nehmet dies weg von hier, machet nicht das Haus meines Vaters zu einem Kaufhause.
17 Ophunzira ake anakumbukira kuti zinalembedwa kuti, “Kudzipereka kwanga ku nyumba yanu kudzandiphetsa.”
Seine Jünger aber gedachten daran, daß geschrieben steht: "Der Eifer um dein Haus verzehrt mich". [Ps. 69,9]
18 Kenaka Ayuda anamufunsa Yesu kuti, “Kodi mungationetse chizindikiro chodabwitsa chotani chotsimikizira ulamuliro wanu wochitira izi?”
Die Juden nun antworteten und sprachen zu ihm: Was für ein Zeichen zeigst du uns, daß du diese Dinge tust?
19 Yesu anawayankha kuti, “Gwetsani Nyumba ya Mulunguyi ndipo Ine ndidzayimanganso mʼmasiku atatu.”
Jesus antwortete und sprach zu ihnen: Brechet diesen Tempel [das Heiligtum; s. die Anm. zu Mat. 4,5] ab, und in drei Tagen werde ich ihn aufrichten.
20 Ayuda anayankha kuti, “Zinatenga zaka makumi anayi kumanga Nyumbayi, kodi Inu mungayimange masiku atatu?”
Da sprachen die Juden: Sechsundvierzig Jahre ist an diesem Tempel [das Heiligtum; s. die Anm. zu Mat. 4,5] gebaut worden, und du willst ihn in drei Tagen aufrichten?
21 Koma Nyumba ya Mulungu imene amanena linali thupi lake.
Er aber sprach von dem Tempel [das Heiligtum; s. die Anm. zu Mat. 4,5] seines Leibes.
22 Iye ataukitsidwa kwa akufa, ophunzira ake anakumbukira zimene Iye ananena ndipo anakhulupirira Malemba ndi mawu amene Yesu anayankhula.
Als er nun aus den Toten auferweckt war, gedachten seine Jünger daran, daß er dies gesagt hatte, und sie glaubten der Schrift und dem Worte, welches Jesus gesprochen hatte.
23 Tsopano Iye ali mu Yerusalemu pa phwando la Paska, anthu ambiri anaona zizindikiro zodabwitsa zimene amachita ndipo anakhulupirira dzina lake.
Als er aber zu Jerusalem war, am Passah, auf dem Feste, glaubten viele an seinen Namen, als sie seine Zeichen sahen, die er tat.
24 Koma Yesu sanawakhulupirire iwo, pakuti amadziwa anthu onse.
Jesus selbst aber vertraute sich ihnen nicht an, weil er alle kannte
25 Iye sanafune umboni wa wina aliyense popeza amadziwa zomwe zinali mʼmitima mwa anthu.
und nicht bedurfte, daß jemand Zeugnis gebe von dem Menschen; denn er selbst wußte, was in dem Menschen war.