< Yohane 2 >
1 Pa tsiku lachitatu munali ukwati mu Kana wa ku Galileya. Amayi ake a Yesu anali komweko,
Two days later there was a wedding [celebration] in Cana [town], in Galilee [district]. Jesus’ mother was there.
2 ndipo Yesu ndi ophunzira ake anayitanidwanso ku ukwatiwo.
Jesus and [we] his disciples [were also there, because] we had been invited {someone had invited us} also.
3 Vinyo atatha, amayi a Yesu anati kwa Iye, “Wawathera vinyo.”
When the guests had drunk all the wine [that was there], Jesus’ mother said to him, “The wine is all gone; [can you do something about that]?”
4 Yesu anayankha kuti, “Amayi, chifukwa chiyani mukundiwuza Ine? Nthawi yanga sinakwane.”
Jesus said to her, “Ma’am/Woman, (do not [tell] me [what to do]!/why do you [tell] me [what to do]?) [RHQ] It is not yet time [MTY] [to show] that I am [the Messiah by working miracles].”
5 Amayi ake anati kwa antchito, “Inu muchite chilichonse chimene akuwuzeni.”
Then Jesus’ mother said to the servants, “Do whatever he tells you!”
6 Pamenepo panali mitsuko yamiyala yothiramo madzi isanu ndi umodzi, imene Ayuda amagwiritsa ntchito pa mwambo wodziyeretsa. Uliwonse unali ndi malita 100 kapena kupitirirapo.
There were six [empty] stone jars there. The Jews [habitually put water in them] to use for washing things [to make them acceptable to God]. Each jar held (20 to 30 gallons/80 to 120 liters).
7 Yesu anati kwa antchitowo, “Dzazani madzi mʼmitsukoyi,” ndipo iwo anadzaza ndendende.
Jesus said to the servants, “Fill the jars with water!” So they filled the jars to the brim.
8 Ndipo Iye anatinso kwa iwo, “Tsopano tungani ndipo kaperekeni kwa mkulu waphwando.” Iwo anachita momwemo.
Then he told them, “Now, ladle out some [of it] and take it (to the head waiter/to the master of ceremonies).” So the servants did that.
9 Mkulu waphwando analawa madziwo amene anasandulika vinyo, ndipo sanazindikire kumene vinyoyo anachokera, ngakhale kuti antchito amene anatunga madziwo amadziwa. Kenaka anayitanira mkwati pambali
(The head waiter/The master of ceremonies) tasted the water, which had now become wine. He did not know where the wine had come from, but the servants who had ladled out the wine knew. [The wine was delicious]! So he called the bridegroom over,
10 ndipo anati, “Aliyense amatulutsa vinyo wokoma kwambiri poyambirira ndipo kenaka vinyo wosakoma pamene oyitanidwa atamwa kale wambiri; koma iwe wasunga wokoma mpaka tsopano.”
and said to him, “Everyone [else] serves the best wine first. Then when the guests have drunk so much [that they cannot tell the difference], [they serve] the cheap wine. But you [have not done what others do]. You have kept the best wine until now!”
11 Ichi chinali chizindikiro chodabwitsa choyamba chimene Yesu anachita ku Kana wa ku Galileya. Potero Iye anawulula ulemerero wake, ndipo ophunzira ake anamukhulupirira Iye.
That was the first miracle that Jesus did. He did it in Cana [town], in Galilee [district]. By doing it he showed how awesome he is, and as a result, [we] his disciples believed that he [truly was the Messiah].
12 Zitatha izi Iye anatsikira ku Kaperenawo pamodzi ndi amayi ake, abale ake ndi ophunzira ake. Iwo anakhala kumeneko masiku owerengeka.
Jesus then went down to Capernaum [city] with his mother and [younger] brothers and [us] his disciples. We stayed there several days.
13 Nthawi ya Paska ya Ayuda itayandikira, Yesu anapita ku Yerusalemu.
Later, when it was almost time for the Jewish Passover [celebration], Jesus [and we his disciples] went up to Jerusalem.
14 Mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu Iye anapeza anthu akugulitsa ngʼombe, nkhosa ndi nkhunda ndipo ena akusintha ndalama pa matebulo.
There, in the Temple [courtyard], he saw some men who were selling cattle, sheep, and pigeons [for sacrifices]. He also saw men who were sitting at tables, [making a big profit as they] gave people [Temple tax] coins in exchange for [their Roman] coins.
15 Chifukwa cha zimenezi Iye anapanga chikwapu cha zingwe ndipo anatulutsa onse mʼbwalo la Nyumbayo, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe; Iye anamwaza ndalama zawo ndi kugudubuza matebulo.
Then Jesus made a whip from some cords and [used it to] chase out the sheep and cattle from the Temple [courtyard]. By overturning their tables he scattered the coins of the men who were exchanging them.
16 Kwa amene amagulitsa nkhunda, Iye anati, “Tulutsani izi muno! Osasandutsa Nyumba ya Atate anga msika!”
He said to those who were selling doves, “Take these doves away [from here]! Stop [defiling] my Father’s Temple [by] making it a market!”
17 Ophunzira ake anakumbukira kuti zinalembedwa kuti, “Kudzipereka kwanga ku nyumba yanu kudzandiphetsa.”
Then [we] disciples remembered that these words had been written {that [someone/David] had written [these words]} [in the Scriptures prophesying what the Messiah would say]: “Others [PRS] will strongly oppose me because I greatly desire that [people respect] your Sacred Tent.”
18 Kenaka Ayuda anamufunsa Yesu kuti, “Kodi mungationetse chizindikiro chodabwitsa chotani chotsimikizira ulamuliro wanu wochitira izi?”
So [one of] the Jewish [leaders] [SYN] replied to him, “What miracle will you perform to show us that [you have authority from God] to do these things?”
19 Yesu anawayankha kuti, “Gwetsani Nyumba ya Mulunguyi ndipo Ine ndidzayimanganso mʼmasiku atatu.”
Jesus replied to them, “If/When you destroy this temple, I will build it again within three days.”
20 Ayuda anayankha kuti, “Zinatenga zaka makumi anayi kumanga Nyumbayi, kodi Inu mungayimange masiku atatu?”
So the Jewish [leaders] [SYN] said, “We have been building this Temple for 46 years [and it is not finished yet]! So (there is no way you will build it within three days!/how will you build it within three days?) [RHQ]”
21 Koma Nyumba ya Mulungu imene amanena linali thupi lake.
But when Jesus said that about the temple, [he was really talking about] his own body.
22 Iye ataukitsidwa kwa akufa, ophunzira ake anakumbukira zimene Iye ananena ndipo anakhulupirira Malemba ndi mawu amene Yesu anayankhula.
[Later], after Jesus had [died and had] become alive again, [we] his disciples remembered the words he had said. As a result, we believed [what had been prophesied in] the Scriptures [about the Messiah becoming alive again], and we believed that what Jesus said [was true].
23 Tsopano Iye ali mu Yerusalemu pa phwando la Paska, anthu ambiri anaona zizindikiro zodabwitsa zimene amachita ndipo anakhulupirira dzina lake.
While Jesus was in Jerusalem at the Passover celebration, many people came to believe [that he was the Messiah] because they saw the miracles he was performing.
24 Koma Yesu sanawakhulupirire iwo, pakuti amadziwa anthu onse.
But he did not let them tell him what he should do [as the Messiah], because he knew within himself what they were all [thinking].
25 Iye sanafune umboni wa wina aliyense popeza amadziwa zomwe zinali mʼmitima mwa anthu.
He did not need anyone to tell him what others were thinking, because he already knew what they were [thinking and wanting].