< Yohane 2 >

1 Pa tsiku lachitatu munali ukwati mu Kana wa ku Galileya. Amayi ake a Yesu anali komweko,
Amhnüp nghngih käna Kalile hne, Kana mlüha cambumnak veki. Acuia Jesuha nu pi veki.
2 ndipo Yesu ndi ophunzira ake anayitanidwanso ku ukwatiwo.
Jesuh ja axüisaw he pi acuia ami jah khüei hnga.
3 Vinyo atatha, amayi a Yesu anati kwa Iye, “Wawathera vinyo.”
Capyitui päih se Jesuha nu naw, “Capyitui päih ve,” ti lü Jesuh üng a mtheh.
4 Yesu anayankha kuti, “Amayi, chifukwa chiyani mukundiwuza Ine? Nthawi yanga sinakwane.”
Jesuh naw, “I pawh vai ti cun, nanga na mtheh vai am hlü. Ka kcün am pha ham,” a ti.
5 Amayi ake anati kwa antchito, “Inu muchite chilichonse chimene akuwuzeni.”
A nu naw mpyae üng, “A ning jah mtheh naküt pawh ua,” a ti.
6 Pamenepo panali mitsuko yamiyala yothiramo madzi isanu ndi umodzi, imene Ayuda amagwiritsa ntchito pa mwambo wodziyeretsa. Uliwonse unali ndi malita 100 kapena kupitirirapo.
Judahea thuma ngcimcaihnak vaia, kalan mku ja thumkipa keh vangkia mcü khyuk veki.
7 Yesu anati kwa antchitowo, “Dzazani madzi mʼmitsukoyi,” ndipo iwo anadzaza ndendende.
Jesuh naw mpyae üng, “Mcüe tui am jah kbe päih ua,” a ti. Be lü pyep khaia tui ami jah than.
8 Ndipo Iye anatinso kwa iwo, “Tsopano tungani ndipo kaperekeni kwa mkulu waphwando.” Iwo anachita momwemo.
Jesuh naw, “Tukbäih tui avang lo u lü pawi tuiktänga veia cehpüi ua,” a ti. Mpyae naw tuiktänga veia ami cehpüi.
9 Mkulu waphwando analawa madziwo amene anasandulika vinyo, ndipo sanazindikire kumene vinyoyo anachokera, ngakhale kuti antchito amene anatunga madziwo amadziwa. Kenaka anayitanira mkwati pambali
Pawi tuiktäng naw tui cun Capyittuia ngläüh lawki cun mdep lü, angtüi lawnak am ksing, (Tui thanki mpyae naw ta ksingki he). Acunüng cambumki khü lü,
10 ndipo anati, “Aliyense amatulutsa vinyo wokoma kwambiri poyambirira ndipo kenaka vinyo wosakoma pamene oyitanidwa atamwa kale wambiri; koma iwe wasunga wokoma mpaka tsopano.”
“Khyang naküt naw akcüka Capyittui asü am jah khin na ma lü, ami awk phü käna va akpaih am jah khin na khawikie. Nang naw ta tuh vei cäpa asü am jah khin na veki,” a ti.
11 Ichi chinali chizindikiro chodabwitsa choyamba chimene Yesu anachita ku Kana wa ku Galileya. Potero Iye anawulula ulemerero wake, ndipo ophunzira ake anamukhulupirira Iye.
Jesuh naw hina müncankse akcük säih Kalile hne, Kana mlüha mdang lü a hlüngtainak mdangki. Acunüng, axüisaw he naw Jesuh jumkie.
12 Zitatha izi Iye anatsikira ku Kaperenawo pamodzi ndi amayi ake, abale ake ndi ophunzira ake. Iwo anakhala kumeneko masiku owerengeka.
Acunkäna a nu, a nae ja axüisaw he am, Kapenawm mlüha cit u lü acuia khawmhnüp asäng awmkie.
13 Nthawi ya Paska ya Ayuda itayandikira, Yesu anapita ku Yerusalemu.
Judahea Lätnak Pawi kcün pha law se, Jesuh Jerusalema jeng citki.
14 Mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu Iye anapeza anthu akugulitsa ngʼombe, nkhosa ndi nkhunda ndipo ena akusintha ndalama pa matebulo.
Temple k'uma, se mna, to, müme jah jawikie ja, ngui mhlaikia khyange a jah hmuh.
15 Chifukwa cha zimenezi Iye anapanga chikwapu cha zingwe ndipo anatulutsa onse mʼbwalo la Nyumbayo, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe; Iye anamwaza ndalama zawo ndi kugudubuza matebulo.
Kpaihnak vaia yüipawk pawh lü, Temple üngka naw se mna ja toe a jah sät. Ngui mhlaikiea ami ngawhnake jah ktukhawngin lü nguikcange a jah hukxänin pet.
16 Kwa amene amagulitsa nkhunda, Iye anati, “Tulutsani izi muno! Osasandutsa Nyumba ya Atate anga msika!”
Müm jawikiea üng, “Hine akcea jah cehpüi ua, ka Paa im jawihtuknaka käh pyang ua,” a ti.
17 Ophunzira ake anakumbukira kuti zinalembedwa kuti, “Kudzipereka kwanga ku nyumba yanu kudzandiphetsa.”
Axüisawe naw, “Na ima phäha ka ngaihngtühnak naw ka mlung k'uma na uiawng ve,” ti lü, ng’yuki ami süm law be.
18 Kenaka Ayuda anamufunsa Yesu kuti, “Kodi mungationetse chizindikiro chodabwitsa chotani chotsimikizira ulamuliro wanu wochitira izi?”
Judah ngvaie naw ngthäh u lü, “Ahikba na jah pawhki. Na cangki tia a ngsingnak vaia, ia müncankse na jah mhnuh khai ni?” ami ti.
19 Yesu anawayankha kuti, “Gwetsani Nyumba ya Mulunguyi ndipo Ine ndidzayimanganso mʼmasiku atatu.”
Jesuh naw jah msang lü, “Hina Temple kpye uki se, mhnüp kthum üng ka mdüih be khai,” a ti.
20 Ayuda anayankha kuti, “Zinatenga zaka makumi anayi kumanga Nyumbayi, kodi Inu mungayimange masiku atatu?”
Judahe naw, “Hina Temple kum kphyükip ja khyuk so khaia sak ni. Ihawkba nang naw mhnüp kthum üng na mdüih be khawh khai ni?” ami ti.
21 Koma Nyumba ya Mulungu imene amanena linali thupi lake.
Cunüngpi Jesuh naw Temple a ti cun amäta pumsa a pyenaka kyaki.
22 Iye ataukitsidwa kwa akufa, ophunzira ake anakumbukira zimene Iye ananena ndipo anakhulupirira Malemba ndi mawu amene Yesu anayankhula.
Acunakyase, Jesuh thihnak üngka naw a thawh law käna, axüisaw he naw ami veia a pyen khawi süm law bekie. Acunüng cangcim ja ngthu Jesuh naw a pyen cun jumkie.
23 Tsopano Iye ali mu Yerusalemu pa phwando la Paska, anthu ambiri anaona zizindikiro zodabwitsa zimene amachita ndipo anakhulupirira dzina lake.
Jesuh Jerusalem mlüh Lätnak Pawi buh pawhnaka ve se, müncanksee a jah pawh hmuh u lü, khyang khawhah naw ani jumkie.
24 Koma Yesu sanawakhulupirire iwo, pakuti amadziwa anthu onse.
Acunsepi, Jesuh naw khyang naküt jah ksingkia kyase, khyangea veia amät naw amät am ng’apei.
25 Iye sanafune umboni wa wina aliyense popeza amadziwa zomwe zinali mʼmitima mwa anthu.
Khyanga mlung k'uma i veki ti cun ksingkia kyase, khyangea mawng ani üng u naw i a mtheh vai am hlü.

< Yohane 2 >