< Yohane 19 >
1 Kenaka Pilato anatenga Yesu namukwapula mwankhanza.
པཱིལཱཏོ ཡཱིཤུམ྄ ཨཱནཱིཡ ཀཤཡཱ པྲཱཧཱརཡཏ྄།
2 Asilikali analuka nkhata yaminga ndi kumuveka pamutu pake. Kenaka anamuveka mkanjo wapepo
པཤྩཱཏ྄ སེནཱགཎཿ ཀཎྚཀནིརྨྨིཏཾ མུཀུཊཾ ཏསྱ མསྟཀེ སམརྤྱ ཝཱརྟྟཱཀཱིཝརྞཾ རཱཛཔརིཙྪདཾ པརིདྷཱཔྱ,
3 ndipo ankapita kwa Iye mobwerezabwereza ndi kumanena kuti, “Moni mfumu ya Ayuda?” Ndipo amamumenya makofi.
ཧེ ཡིཧཱུདཱིཡཱནཱཾ རཱཛན྄ ནམསྐཱར ཨིཏྱུཀྟྭཱ ཏཾ ཙཔེཊེནཱཧནྟུམ྄ ཨཱརབྷཏ།
4 Pilato anatulukanso ndipo anati kwa Ayuda, “Taonani, ine ndikumubweretsa kuti inu mudziwe kuti ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu.”
ཏདཱ པཱིལཱཏཿ པུནརཔི བཧིརྒཏྭཱ ལོཀཱན྄ ཨཝདཏ྄, ཨསྱ ཀམཔྱཔརཱདྷཾ ན ལབྷེ྅ཧཾ, པཤྱཏ ཏད྄ ཡུཥྨཱན྄ ཛྙཱཔཡིཏུཾ ཡུཥྨཱཀཾ སནྣིདྷཽ བཧིརེནམ྄ ཨཱནཡཱམི།
5 Pamenepo Yesu anatuluka atavala nkhata yaminga ndi mkanjo wapepo ndipo Pilato anawawuza kuti, “Nayu munthu uja!”
ཏཏཿ པརཾ ཡཱིཤུཿ ཀཎྚཀམུཀུཊཝཱན྄ ཝཱརྟྟཱཀཱིཝརྞཝསནཝཱཾཤྩ བཧིརཱགཙྪཏ྄། ཏཏཿ པཱིལཱཏ ཨུཀྟཝཱན྄ ཨེནཾ མནུཥྱཾ པཤྱཏ།
6 Atangomuona Iye akulu a ansembe ndi akuluakulu ena anafuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!” Koma Pilato anayankha kuti, “Inu mutengeni ndi kumupachika. Koma ine sindikupeza chifukwa chomuyimbira mlandu.”
ཏདཱ པྲདྷཱནཡཱཛཀཱཿ པདཱཏཡཤྩ ཏཾ དྲྀཥྚྭཱ, ཨེནཾ ཀྲུཤེ ཝིདྷ, ཨེནཾ ཀྲུཤེ ཝིདྷ, ཨིཏྱུཀྟྭཱ རཝིཏུཾ ཨཱརབྷནྟ། ཏཏཿ པཱིལཱཏཿ ཀཐིཏཝཱན྄ ཡཱུཡཾ སྭཡམ྄ ཨེནཾ ནཱིཏྭཱ ཀྲུཤེ ཝིདྷཏ, ཨཧམ྄ ཨེཏསྱ ཀམཔྱཔརཱདྷཾ ན པྲཱཔྟཝཱན྄།
7 Ayuda anayimirira nati, “Ife tili ndi lamulo, ndipo molingana ndi lamulolo, Iyeyu ayenera kuphedwa chifukwa akudzitcha kuti ndi Mwana wa Mulungu.”
ཡིཧཱུདཱིཡཱཿ པྲཏྱཝདན྄ ཨསྨཱཀཾ ཡཱ ཝྱཝསྠཱསྟེ ཏདནུསཱརེཎཱསྱ པྲཱཎཧནནམ྄ ཨུཙིཏཾ ཡཏོཡཾ སྭམ྄ ཨཱིཤྭརསྱ པུཏྲམཝདཏ྄།
8 Pilato atamva zimenezi, anachita mantha kwambiri,
པཱིལཱཏ ཨིམཱཾ ཀཐཱཾ ཤྲུཏྭཱ མཧཱཏྲཱསཡུཀྟཿ
9 ndipo anabwereranso mʼnyumba yaufumu. Iye anafunsa Yesu kuti, “Kodi umachokera kuti?” Koma Yesu sanayankhe.
སན྄ པུནརཔི རཱཛགྲྀཧ ཨཱགཏྱ ཡཱིཤུཾ པྲྀཥྚཝཱན྄ ཏྭཾ ཀུཏྲཏྱོ ལོཀཿ? ཀིནྟུ ཡཱིཤསྟསྱ ཀིམཔི པྲཏྱུཏྟརཾ ནཱཝདཏ྄།
10 Pilato anati, “Kodi ukukana kundiyankhula ine? Kodi sukuzindikira kuti ine ndili ndi mphamvu yokumasula ndiponso mphamvu yokupachika?”
༡ ཏཏཿ པཱིལཱཏ྄ ཀཐིཏཝཱན ཏྭཾ ཀིཾ མཡཱ སཱརྡྡྷཾ ན སཾལཔིཥྱསི? ཏྭཱཾ ཀྲུཤེ ཝེདྷིཏུཾ ཝཱ མོཙཡིཏུཾ ཤཀྟི རྨམཱསྟེ ཨིཏི ཀིཾ ཏྭཾ ན ཛཱནཱསི? ཏདཱ ཡཱིཤུཿ པྲཏྱཝདད྄ ཨཱིཤྭརེཎཱདཾ མམོཔརི ཏཝ ཀིམཔྱདྷིཔཏིཏྭཾ ན ཝིདྱཏེ, ཏཐཱཔི ཡོ ཛནོ མཱཾ ཏཝ ཧསྟེ སམཱརྤཡཏ྄ ཏསྱ མཧཱཔཱཏཀཾ ཛཱཏམ྄།
11 Yesu anayankha kuti, “Inu simukanakhala ndi mphamvu pa Ine akanapanda kukupatsani kumwamba. Nʼchifukwa chake amene wandipereka Ine kwa inu ndiye wochimwa kwambiri.”
ཏདཱ ཡཱིཤུཿ པྲཏྱཝདད྄ ཨཱིཤྭརེཎཱདཏྟཾ མམོཔརི ཏཝ ཀིམཔྱདྷིཔཏིཏྭཾ ན ཝིདྱཏེ, ཏཐཱཔི ཡོ ཛནོ མཱཾ ཏཝ ཧསྟེ སམཱརྤཡཏ྄ ཏསྱ མཧཱཔཱཏཀཾ ཛཱཏམ྄།
12 Kuyambira pamenepo Pilato anayesa kuti amumasule Yesu, koma Ayuda anapitirira kufuwula kuti, “Ngati mumumasula munthuyu kuti apite, inu si bwenzi la Kaisara.”
ཏདཱརབྷྱ པཱིལཱཏསྟཾ མོཙཡིཏུཾ ཙེཥྚིཏཝཱན྄ ཀིནྟུ ཡིཧཱུདཱིཡཱ རུཝནྟོ ཝྱཱཧརན྄ ཡདཱིམཾ མཱནཝཾ ཏྱཛསི ཏརྷི ཏྭཾ ཀཻསརསྱ མིཏྲཾ ན བྷཝསི, ཡོ ཛནཿ སྭཾ རཱཛཱནཾ ཝཀྟི སཨེཝ ཀཻམརསྱ ཝིརུདྡྷཱཾ ཀཐཱཾ ཀཐཡཏི།
13 Pilato atamva zimenezi, iye anamutulutsa Yesu kunja ndi kukhala pansi pa mpando wa woweruza pamalo otchedwa Mwala Wowaka (umene pa Chiaramaiki ndi Gabata).
ཨེཏཱཾ ཀཐཱཾ ཤྲུཏྭཱ པཱིལཱཏོ ཡཱིཤུཾ བཧིརཱནཱིཡ ནིསྟཱརོཏྶཝསྱ ཨཱསཱདནདིནསྱ དྭིཏཱིཡཔྲཧརཱཏ྄ པཱུཪྻྭཾ པྲསྟརབནྡྷནནཱམྣི སྠཱནེ ྅རྠཱཏ྄ ཨིབྲཱིཡབྷཱཥཡཱ ཡད྄ གབྦིཐཱ ཀཐྱཏེ ཏསྨིན྄ སྠཱནེ ཝིཙཱརཱསན ཨུཔཱཝིཤཏ྄།
14 Linali tsiku lokonzekera Sabata la Paska ndipo nthawi inali ora lachisanu ndi chimodzi masana. Pilato anati kwa Ayuda, “Nayi mfumu yanu.”
ཨནནྟརཾ པཱིལཱཏོ ཡིཧཱུདཱིཡཱན྄ ཨཝདཏ྄, ཡུཥྨཱཀཾ རཱཛཱནཾ པཤྱཏ།
15 Koma iwo anafuwula kuti, “Choka nayeni! Choka nayeni! Mpachikeni!” Pilato anafunsa kuti, “Kodi ine ndipachike mfumu yanuyi?” Akulu a ansembe anayankha kuti, “Ife tilibe mfumu ina koma Kaisara.”
ཀིནྟུ ཨེནཾ དཱུརཱིཀུརུ, ཨེནཾ དཱུརཱིཀུརུ, ཨེནཾ ཀྲུཤེ ཝིདྷ, ཨིཏི ཀཐཱཾ ཀཐཡིཏྭཱ ཏེ རཝིཏུམ྄ ཨཱརབྷནྟ; ཏདཱ པཱིལཱཏཿ ཀཐིཏཝཱན྄ ཡུཥྨཱཀཾ རཱཛཱནཾ ཀིཾ ཀྲུཤེ ཝེདྷིཥྱཱམི? པྲདྷཱནཡཱཛཀཱ ཨུཏྟརམ྄ ཨཝདན྄ ཀཻསརཾ ཝིནཱ ཀོཔི རཱཛཱསྨཱཀཾ ནཱསྟི།
16 Pomaliza Pilato anamupereka kwa iwo kuti akapachikidwe. Choncho asilikali anamutenga Yesu.
ཏཏཿ པཱིལཱཏོ ཡཱིཤུཾ ཀྲུཤེ ཝེདྷིཏུཾ ཏེཥཱཾ ཧསྟེཥུ སམཱརྤཡཏ྄, ཏཏསྟེ ཏཾ དྷྲྀཏྭཱ ནཱིཏཝནྟཿ།
17 Atanyamula mtanda wake, anapita kumalo otchedwa “Malo a Bade” (mʼChiaramaiki amatchedwa Gologota).
ཏཏཿ པརཾ ཡཱིཤུཿ ཀྲུཤཾ ཝཧན྄ ཤིརཿཀཔཱལམ྄ ཨརྠཱད྄ ཡད྄ ཨིབྲཱིཡབྷཱཥཡཱ གུལྒལྟཱཾ ཝདནྟི ཏསྨིན྄ སྠཱན ཨུཔསྠིཏཿ།
18 Pamenepo iwo anamupachika Iye pamodzi ndi anthu ena awiri, mmodzi mbali ina ndi wina mbali inanso ndipo Yesu pakati.
ཏཏསྟེ མདྷྱསྠཱནེ ཏཾ ཏསྱོབྷཡཔཱརྴྭེ དྭཱཝཔརཽ ཀྲུཤེ྅ཝིདྷན྄།
19 Pilato analemba chikwangwani chomwe anachikhoma pa mtandapo. Panalembedwa mawu akuti, yesu wa ku nazareti, mfumu ya ayuda.
ཨཔརམ྄ ཨེཥ ཡིཧཱུདཱིཡཱནཱཾ རཱཛཱ ནཱསརཏཱིཡཡཱིཤུཿ, ཨིཏི ཝིཛྙཱཔནཾ ལིཁིཏྭཱ པཱིལཱཏསྟསྱ ཀྲུཤོཔརི སམཡོཛཡཏ྄།
20 Ayuda ambiri anawerenga chikwangwanichi, pakuti pamalo pamene Yesu anapachikidwapo panali pafupi ndi mzinda ndipo chikwangwanicho chinalembedwa mu Chiaramaiki, Chilatini ndi Chigriki.
སཱ ལིཔིཿ ཨིབྲཱིཡཡཱུནཱནཱིཡརོམཱིཡབྷཱཥཱབྷི རླིཁིཏཱ; ཡཱིཤོཿ ཀྲུཤཝེདྷནསྠཱནཾ ནགརསྱ སམཱིཔཾ, ཏསྨཱད྄ བཧཝོ ཡིཧཱུདཱིཡཱསྟཱཾ པཋིཏུམ྄ ཨཱརབྷནྟ།
21 Kenaka mkulu wa ansembe wa Ayuda anakadandaula kwa Pilato nati, “Musalembe kuti ‘Mfumu ya Ayuda,’ koma kuti munthuyu amadzitcha kuti ndi mfumu ya Ayuda.”
ཡིཧཱུདཱིཡཱནཱཾ པྲདྷཱནཡཱཛཀཱཿ པཱིལཱཏམིཏི ནྱཝེདཡན྄ ཡིཧཱུདཱིཡཱནཱཾ རཱཛེཏི ཝཱཀྱཾ ན ཀིནྟུ ཨེཥ སྭཾ ཡིཧཱུདཱིཡཱནཱཾ རཱཛཱནམ྄ ཨཝདད྄ ཨིཏྠཾ ལིཁཏུ།
22 Pilato anayankha kuti, “Chimene ine ndalemba, ndalemba.”
ཏཏཿ པཱིལཱཏ ཨུཏྟརཾ དཏྟཝཱན྄ ཡལླེཁནཱིཡཾ ཏལླིཁིཏཝཱན྄།
23 Asilikali atamupachika Yesu, anatenga zovala zake ndi kuzigawa zigawo zinayi, gawo limodzi la aliyense wa iwo, ndi kutsala mwinjiro wamʼkati wokha. Chovala ichi chinawombedwa kuyambira pamwamba mpaka pansi wopanda msoko.
ཨིཏྠཾ སེནཱགཎོ ཡཱིཤུཾ ཀྲུཤེ ཝིདྷིཏྭཱ ཏསྱ པརིདྷེཡཝསྟྲཾ ཙཏུརོ བྷཱགཱན྄ ཀྲྀཏྭཱ ཨེཀཻཀསེནཱ ཨེཀཻཀབྷཱགམ྄ ཨགྲྀཧླཏ྄ ཏསྱོཏྟརཱིཡཝསྟྲཉྩཱགྲྀཧླཏ྄། ཀིནྟཱུཏྟརཱིཡཝསྟྲཾ སཱུཙིསེཝནཾ ཝིནཱ སཪྻྭམ྄ ཨཱུཏཾ།
24 Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni tisachingʼambe koma tichite maere kuti tione amene achitenge.” Izi zinachitika kuti malemba akwaniritsidwe amene anati, “Iwo anagawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.” Choncho izi ndi zimene asilikali anachita.
ཏསྨཱཏྟེ ཝྱཱཧརན྄ ཨེཏཏ྄ ཀཿ པྲཱཔྶྱཏི? ཏནྣ ཁཎྜཡིཏྭཱ ཏཏྲ གུཊིཀཱཔཱཏཾ ཀརཝཱམ། ཝིབྷཛནྟེ྅དྷརཱིཡཾ མེ ཝསནཾ ཏེ པརསྤརཾ། མམོཏྟརཱིཡཝསྟྲཱརྠཾ གུཊིཀཱཾ པཱཏཡནྟི ཙ། ཨིཏི ཡདྭཱཀྱཾ དྷརྨྨཔུསྟཀེ ལིཁིཏམཱསྟེ ཏཏ྄ སེནཱགཎེནེཏྠཾ ཝྱཝཧརཎཱཏ྄ སིདྡྷམབྷཝཏ྄།
25 Pafupi ndi mtanda wa Yesu panayima amayi ake, mngʼono wa amayi ake, Mariya mkazi wa Kaliyopa ndi Mariya wa ku Magadala.
ཏདཱནཱིཾ ཡཱིཤོ རྨཱཏཱ མཱཏུ རྦྷགིནཱི ཙ ཡཱ ཀླིཡཔཱ བྷཱཪྻྱཱ མརིཡམ྄ མགྡལཱིནཱི མརིཡམ྄ ཙ ཨེཏཱསྟསྱ ཀྲུཤསྱ སནྣིདྷཽ སམཏིཥྛན྄།
26 Yesu ataona amayi ake pamenepo ndi wophunzira amene Iye anamukonda atayima pafupipo, Iye anati kwa amayi ake, “Amayi nayu mwana wanu.”
ཏཏོ ཡཱིཤུཿ སྭམཱཏརཾ པྲིཡཏམཤིཥྱཉྩ སམཱིཔེ དཎྜཱཡམཱནཽ ཝིལོཀྱ མཱཏརམ྄ ཨཝདཏ྄, ཧེ ཡོཥིད྄ ཨེནཾ ཏཝ པུཏྲཾ པཤྱ,
27 Anawuzanso wophunzirayo kuti, “Nawa amayi ako.” Kuyambira nthawi imeneyo, wophunzirayo anatenga amayiwo kupita nawo kwawo.
ཤིཥྱནྟྭཝདཏ྄, ཨེནཱཾ ཏཝ མཱཏརཾ པཤྱ། ཏཏཿ ས ཤིཥྱསྟདྒྷཊིཀཱཡཱཾ ཏཱཾ ནིཛགྲྀཧཾ ནཱིཏཝཱན྄།
28 Atadziwa kuti zonse zatha tsopano komanso kuti malemba akwaniritsidwe, Yesu anati, “Ine ndili ndi ludzu.”
ཨནནྟརཾ སཪྻྭཾ ཀརྨྨཱདྷུནཱ སམྤནྣམབྷཱུཏ྄ ཡཱིཤུརིཏི ཛྙཱཏྭཱ དྷརྨྨཔུསྟཀསྱ ཝཙནཾ ཡཐཱ སིདྡྷཾ བྷཝཏི ཏདརྠམ྄ ཨཀཐཡཏ྄ མམ པིཔཱསཱ ཛཱཏཱ།
29 Pomwepo panali mtsuko wodzaza ndi vinyo wosasa, choncho iwo ananyika chinkhupule ndi kuchisomeka ku mtengo wa hisope nachifikitsa kukamwa kwa Yesu.
ཏཏསྟསྨིན྄ སྠཱནེ ཨམླརསེན པཱུརྞཔཱཏྲསྠིཏྱཱ ཏེ སྤཉྫམེཀཾ ཏདམླརསེནཱརྡྲཱིཀྲྀཏྱ ཨེསོབྣལེ ཏད྄ ཡོཛཡིཏྭཱ ཏསྱ མུཁསྱ སནྣིདྷཱཝསྠཱཔཡན྄།
30 Yesu atalandira chakumwachi anati, “Kwatha.” Ndipo Iye anaweramitsa mutu wake napereka mzimu wake.
ཏདཱ ཡཱིཤུརམླརསཾ གྲྀཧཱིཏྭཱ སཪྻྭཾ སིདྡྷམ྄ ཨིཏི ཀཐཱཾ ཀཐཡིཏྭཱ མསྟཀཾ ནམཡན྄ པྲཱཎཱན྄ པཪྻྱཏྱཛཏ྄།
31 Popeza linali Tsiku Lokonzekera ndipo tsiku linalo linali Sabata lapadera; Ayuda sanafune kuti mitembo ikhale pa mtanda pa Sabata, iwo anapempha Pilato kuti akathyole miyendo ndi kutsitsa mitemboyo.
ཏདྭིནམ྄ ཨཱསཱདནདིནཾ ཏསྨཱཏ྄ པརེ྅ཧནི ཝིཤྲཱམཝཱརེ དེཧཱ ཡཐཱ ཀྲུཤོཔརི ན ཏིཥྛནྟི, ཡཏཿ ས ཝིཤྲཱམཝཱརོ མཧཱདིནམཱསཱིཏ྄, ཏསྨཱད྄ ཡིཧཱུདཱིཡཱཿ པཱིལཱཏནིཀཊཾ གཏྭཱ ཏེཥཱཾ པཱདབྷཉྫནསྱ སྠཱནཱནྟརནཡནསྱ ཙཱནུམཏིཾ པྲཱརྠཡནྟ།
32 Chifukwa chake asilikali anabwera ndi kuthyola miyendo ya munthu oyamba amene anapachikidwa ndi Yesu ndipo kenaka ya winayo.
ཨཏཿ སེནཱ ཨཱགཏྱ ཡཱིཤུནཱ སཧ ཀྲུཤེ ཧཏཡོཿ པྲཐམདྭིཏཱིཡཙོརཡོཿ པཱདཱན྄ ཨབྷཉྫན྄;
33 Koma atafika pa Yesu ndi kupeza kuti anali atamwalira kale, iwo sanathyole miyendo yake.
ཀིནྟུ ཡཱིཤོཿ སནྣིདྷིཾ གཏྭཱ ས མྲྀཏ ཨིཏི དྲྀཥྚྭཱ ཏསྱ པཱདཽ ནཱབྷཉྫན྄།
34 Mʼmalo mwake, mmodzi wa asilikaliwo anamubaya Yesu ndi mkondo mʼnthiti, ndipo nthawi yomweyo munatuluka magazi ndi madzi.
པཤྩཱད྄ ཨེཀོ ཡོདྡྷཱ ཤཱུལཱགྷཱཏེན ཏསྱ ཀུཀྵིམ྄ ཨཝིདྷཏ྄ ཏཏྐྵཎཱཏ྄ ཏསྨཱད྄ རཀྟཾ ཛལཉྩ ནིརགཙྪཏ྄།
35 Munthu amene anaona izi wapereka umboni ndipo umboni wake ndi woona. Iye akudziwa kuti akunena choonadi kuti inunso mukhulupirire.
ཡོ ཛནོ྅སྱ སཱཀྵྱཾ དདཱཏི ས སྭཡཾ དྲྀཥྚཝཱན྄ ཏསྱེདཾ སཱཀྵྱཾ སཏྱཾ ཏསྱ ཀཐཱ ཡུཥྨཱཀཾ ཝིཤྭཱསཾ ཛནཡིཏུཾ ཡོགྱཱ ཏཏ྄ ས ཛཱནཱཏི།
36 Zinthu izi zinachitika kuti malemba akwaniritsidwe: “Palibe limodzi la mafupa limene lidzathyoledwa,”
ཏསྱཻཀམ྄ ཨསྡྷྱཔི ན བྷཾཀྵྱཏེ,
37 ndi monga lemba linanso linena, “Iwo adzayangʼana Iye amene iwo anamubaya.”
ཏདྭད྄ ཨནྱཤཱསྟྲེཔི ལིཁྱཏེ, ཡཐཱ, "དྲྀཥྚིཔཱཏཾ ཀརིཥྱནྟི ཏེ྅ཝིདྷན྄ ཡནྟུ ཏམྤྲཏི། "
38 Kenaka, Yosefe wa ku Arimateyu anakapempha mtembo wa Yesu kwa Pilato. Tsono Yosefe anali wophunzira wa Yesu koma mobisa chifukwa iye ankaopa Ayuda. Atalandira chilolezo kwa Pilato, anakatsitsa mtembo wa Yesu.
ཨརིམཐཱིཡནགརསྱ ཡཱུཥཕྣཱམཱ ཤིཥྱ ཨེཀ ཨཱསཱིཏ྄ ཀིནྟུ ཡིཧཱུདཱིཡེབྷྱོ བྷཡཱཏ྄ པྲཀཱཤིཏོ ན བྷཝཏི; ས ཡཱིཤོ རྡེཧཾ ནེཏུཾ པཱིལཱཏསྱཱནུམཏིཾ པྲཱརྠཡཏ, ཏཏཿ པཱིལཱཏེནཱནུམཏེ སཏི ས གཏྭཱ ཡཱིཤོ རྡེཧམ྄ ཨནཡཏ྄།
39 Nekodimo, munthu amene poyamba pake anabwera kwa Yesu usiku, anatenga mafuta osakaniza ndi mure ndi aloe wolemera pafupifupi makilogalamu 32.
ཨཔརཾ ཡོ ནིཀདཱིམོ རཱཏྲཽ ཡཱིཤོཿ སམཱིཔམ྄ ཨགཙྪཏ྄ སོཔི གནྡྷརསེན མིཤྲིཏཾ པྲཱཡེཎ པཉྩཱཤཏྶེཊཀམགུརུཾ གྲྀཧཱིཏྭཱགཙྪཏ྄།
40 Pamenepo anatenga mtembo wa Yesu nawukulunga pamodzi ndi zonunkhiritsa mu nsalu za mtundu woyera monga mwa mwambo wa maliro wa Ayuda.
ཏཏསྟེ ཡིཧཱུདཱིཡཱནཱཾ ཤྨཤཱནེ སྠཱཔནརཱིཏྱནུསཱརེཎ ཏཏྶུགནྡྷིདྲཝྱེཎ སཧིཏཾ ཏསྱ དེཧཾ ཝསྟྲེཎཱཝེཥྚཡན྄།
41 Pamalo pamene anapachikidwa Yesu panali munda ndipo mʼmundamo munali manda atsopano mʼmene munali simunayikidwemo aliyense.
ཨཔརཉྩ ཡཏྲ སྠཱནེ ཏཾ ཀྲུཤེ྅ཝིདྷན྄ ཏསྱ ནིཀཊསྠོདྱཱནེ ཡཏྲ ཀིམཔི མྲྀཏདེཧཾ ཀདཱཔི ནཱསྠཱཔྱཏ ཏཱདྲྀཤམ྄ ཨེཀཾ ནཱུཏནཾ ཤྨཤཱནམ྄ ཨཱསཱིཏ྄།
42 Chifukwa linali Tsiku la Ayuda Lokonzekera ndi kuti mandawo anali pafupipo, iwo anayika Yesu mʼmenemo.
ཡིཧཱུདཱིཡཱནཱམ྄ ཨཱསཱདནདིནཱགམནཱཏ྄ ཏེ ཏསྨིན྄ སམཱིཔསྠཤྨཤཱནེ ཡཱིཤུམ྄ ཨཤཱཡཡན྄།