< Yohane 18 >
1 Yesu atamaliza kupemphera, Iye anachoka ndi ophunzira ake ndi kuwoloka chigwa cha Kidroni. Kumbali inayo kunali munda wa Olivi, ndipo Iye ndi ophunzira ake analowamo.
UJesu esekhulumile lezizinto waphuma kanye labafundi bakhewaya ngaphetsheya kwesifudlana iKidroni, lapho okwakukhona isivande, angena kuso yena labafundi bakhe.
2 Tsopano Yudasi, amene anamupereka amadziwa malowo chifukwa Yesu ankakumana ndi ophunzira ake kumeneko.
Njalo uJudasi laye, owamnikelayo, wayeyazi lindawo; ngoba uJesu wayebuthana khona labafundi bakhe kanengi.
3 Choncho Yudasi anabwera ku munda, akutsogolera gulu la asilikali ndi akuluakulu ena ochokera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi. Iwo anali atanyamula miyuni, nyale ndi zida.
Ngakho uJudasi, esethethe isigaba samabutho, labancedisi abavela kubapristi abakhulu labaFarisi, waya khona belezibane lamalambi lezikhali.
4 Yesu, podziwa zonse zimene zimati zichitike kwa Iye, anatuluka ndi kuwafunsa kuti, “Kodi mukufuna ndani?”
Kwathi uJesu, ekwazi konke okwakuzamehlela, waphuma wathi kubo: Lidinga bani?
5 Iwo anayankha kuti, “Yesu wa ku Nazareti.” Yesu anati, “Ndine.” (Ndipo Yudasi womuperekayo anali atayima nawo pamenepo).
Bamphendula bathi: UJesu weNazaretha. UJesu wathi kubo: Mina nginguye. LoJudasi owamnikelayo laye wayemi labo.
6 Pamene Yesu anati, “Ndine,” iwo anabwerera mʼmbuyo ndi kugwa pansi.
Ngakho kuthe esithi kubo: Mina nginguye; bahlehla nyovane, bawela phansi.
7 Iye anawafunsanso kuti, “Kodi mukumufuna ndani?” Ndipo iwo anati, “Yesu wa ku Nazareti.”
Wasephinda wababuza wathi: Lidinga bani? Basebesithi: UJesu weNazaretha.
8 Yesu anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kuti Ndine. Ngati inu mukufuna Ine, asiyeni anthu awa apite.”
UJesu waphendula wathi: Ngilitshelile ukuthi mina nginguye; ngakho uba lidinga mina, yekelani laba bahambe;
9 Izi zinachitika kuti mawu amene Iye anayankhula akwaniritsidwe: “Ine sindinataye ndi mmodzi yemwe mwa iwo amene mwandipatsa.”
ukuze ligcwaliseke ilizwi ayelikhulumile elokuthi: Kulabo owanginika bona, angilahlekelwanga lamunye wabo.
10 Kenaka Simoni amene anali ndi lupanga analitulutsa ndi kutema nalo wantchito wa wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake la kudzanja lamanja. (Dzina la wantchitoyo ndi Makusi).
Kwathi uSimoni Petro elenkemba wayihwatsha, wagadla inceku yompristi omkhulu, waquma indlebe yayo yokunene. Lebizo lenceku lalinguMalikusi.
11 Yesu analamula Petro kuti, “Bwezera lupanga mʼchimake! Kodi Ine ndisamwere chikho chimene Atate andipatsa?”
UJesu wasesithi kuPetro: Faka inkemba yakho esikhwameni; inkezo uBaba anginike yona, kangiyikuyinatha yini?
12 Kenaka gulu la asilikali ndi olamulira wawo ndi akuluakulu a Ayuda anamugwira Yesu. Iwo anamumanga.
Ngakho isigaba samabutho lenduna labancedisi bamaJuda bambamba uJesu, bambopha,
13 Poyamba anapita naye kwa Anasi amene anali mkamwini wa Kayafa, mkulu wa ansembe chaka chimenecho.
basebemusa kuqala kuAnasi; ngoba wayenguyisezala kaKayafasi, owayengumpristi omkhulu ngalowomnyaka.
14 Kayafa anali amene analangiza Ayuda kuti kukanakhala kwabwino ngati munthu mmodzi akanafera anthu.
Kwakunguye uKayafasi owayecebise amaJuda, ukuthi kwakulungile ukuthi umuntu oyedwa afele isizwe.
15 Simoni Petro ndi ophunzira wina ankamutsatira Yesu chifukwa ophunzira uyu amadziwika kwa mkulu wa ansembe. Iye analowa ndi Yesu mʼbwalo la mkulu wa ansembe
USimoni Petro wasemlandela uJesu, lomunye umfundi. Lalowomfundi wayesaziwa ngumpristi omkhulu, wangena loJesu egumeni lompristi omkhulu;
16 koma Petro anadikira kunja pa khomo. Ophunzira winayo amene amadziwika kwa mkulu wa ansembe, anatuluka ndi kuyankhula ndi mtsikana amene anali mlonda wa pa khomo ndi kumulowetsa Petro.
kodwa uPetro wayemi ngaphandle emnyango. Wasephuma lowomfundi omunye owayesaziwa ngumpristi omkhulu, wasekhuluma lomlindisangokazi, wamngenisa uPetro.
17 Mtsikanayo anafunsa Petro kuti, “Kodi iwe sindiwe mmodzi wa ophunzira a Munthu uyu?” Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”
Incekukazi encane engumlindisango yasisithi kuPetro: Kawusuye lawe omunye wabafundi balumuntu yini? Yena wathi: Kangisuye.
18 Popeza kunkazizira, anyamata antchito ndi akuluakulu ena anasonkha moto wamakala namawotha atayimirira mozungulira. Petro nayenso anayimirira pamodzi ndi iwo namawotha nawo motowo.
Njalo izinceku labancedisi babemi bebase umlilo wamalahle, ngoba kwakumakhaza, njalo besotha; uPetro laye wayemi labo esotha.
19 Pa nthawi imeneyi, mkulu wa ansembe anamufunsa Yesu za ophunzira ake ndi chiphunzitso chake.
Umpristi omkhulu wasembuza uJesu ngabafundi bakhe, langemfundiso yakhe.
20 Yesu anayankha kuti, “Ine ndinayankhula poyera ku dziko lapansi. Nthawi zonse ndimaphunzitsa mʼsunagoge kapena mʼNyumba ya Mulungu kumene Ayuda onse amasonkhana pamodzi. Ine sindimanena kanthu mseri.
UJesu wamphendula wathi: Mina ngikhulume obala emhlabeni; ngezikhathi zonke mina bengifundisa esinagogeni lethempelini, lapho amaJuda abuthana khona ngesikhathi sonke, njalo kangikhulumanga lutho ensitha.
21 Nʼchifukwa chiyani mukundifunsa Ine? Afunseni amene amamva. Zoonadi akudziwa zimene Ine ndinanena.”
Ubuzelani kimi? Buza labo abakuzwayo lokho engakukhuluma labo; khangela, bona bayazazi izinto mina engazitshoyo.
22 Yesu atanena izi, mmodzi wa akuluakulu amene anali pafupi anamumenya kumaso. Iye anafunsa kuti, “Mayankhidwe awa ndi woti ndi kuyankha mkulu wa ansembe?”
Kwathi esetshilo lezizinto, omunye wabancedisi owayemi khona wamwakala uJesu, esithi: Kanti uphendula njalo umpristi omkhulu?
23 Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndanena kanthu kolakwika, chitirani umboni chimene ndalakwa. Koma ngati ndanena zoona, nʼchifukwa chiyani mwandimenya?”
UJesu wamphendula wathi: Uba ngikhulume kubi, fakaza ngobubi; kodwa uba kuhle, ungitshayelani?
24 Kenaka Anasi anamutumiza Iye, ali womangidwabe, kwa Kayafa, mkulu wa ansembe.
UAnasi wasemthuma ebotshiwe kuKayafasi umpristi omkhulu.
25 Pamene Simoni Petro anali chiyimirire kuwotha moto, anafunsidwa kuti, “Kodi iwe si mmodzi wa ophunzira ake?” Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”
Kodwa uSimoni Petro wayemi esotha; basebesithi kuye: Kawusuye lawe omunye wabafundi bakhe yini? Waphika yena, wathi: Kangisuye.
26 Mmodzi wa antchito a mkulu wa ansembe, mʼbale wa munthu amene anadulidwa khutu ndi Petro anamutsutsa iye kuti, “Kodi sindinakuone iwe pamodzi ndi Iye mʼmunda muja?”
Omunye wezinceku zompristi omkhulu, oyisinini somuntu uPetro aquma indlebe yakhe, wathi: Mina kangikubonanga yini esivandeni ulaye?
27 Petro anakananso, ndipo pa nthawi yomweyo tambala analira.
UPetro wasebuya ephika; njalo lahle lakhala iqhude.
28 Kenaka Ayuda anamutenga Yesu kuchoka kwa Kayafa ndi kupita ku nyumba yaufumu ya bwanamkubwa wa Chiroma. Tsopano kunali mmamawa, ndipo polewa kudetsedwa monga mwa mwambo Ayuda sanalowe mʼnyumba yaufumuyo; iwo anafuna kuti adye Paska.
Basebemkhupha uJesu kuKayafasi bamusa endlini yombusi; njalo kwakusekuseni, kodwa kabangenanga bona endlini yombusi, ukuze bangangcoli, kodwa ukuze badle iphasika.
29 Choncho Pilato anatuluka napita kwa iwo ndipo anati, “Kodi ndi milandu yanji imene mukumuzenga munthu uyu?”
Ngakho uPilatu waphumela kubo, wathi: Limbeka cala bani lumuntu?
30 Iwo anayankha kuti, “Ngati Iye akanakhala kuti si wolakwa, ife sitikanamupereka kwa inu.”
Basebephendula bathi kuye: Uba lo ubengesuye owenza okubi, ngabe kasimnikelanga kuwe.
31 Pilato anati, “Mutengeni inu eni ake ndi kumuweruza Iye monga mwa malamulo anu.” Ayuda anatsutsa nati, “Koma tilibe ulamuliro wakupha aliyense.”
UPilatu wasesithi kubo: Mthatheni lina, limahlulele njengomlayo wakini. Ngakho amaJuda athi kuye: Kakuvunyelwa kithi ukubulala umuntu;
32 Izi zinachitika kuti mawu a Yesu amene anayankhula kusonyeza mtundu wa imfa imene Iye anati adzafe nayo akwaniritsidwe.
ukuze kugcwaliseke ilizwi uJesu alikhulumayo, ukutshengisa uhlobo lokufa ayezakufa ngalo.
33 Kenaka Pilato anapita mʼkati mwa nyumba yaufumu nayitanitsa Yesu, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi iwe ndi mfumu ya Ayuda?”
Ngakho uPilatu wabuye wangena endlini yombusi, wambiza uJesu, wathi kuye: Wena uyiNkosi yamaJuda yini?
34 Yesu anafunsa kuti, “Kodi amenewo ndi maganizo anu wokha? Kapena kuti ena anakuwuzani za Ine?”
UJesu wamphendula wathi: Uyazitsholo lokhu wena yini, kumbe abanye bakutshelile ngami?
35 Pilato anayankha kuti, “Kodi iwe ukuganiza kuti ine ndine Myuda? Ndi anthu ako ndi akulu a ansembe ako amene akupereka iwe kwa ine. Kodi walakwanji?”
UPilatu waphendula wathi: Kanti ngingumJuda mina? Isizwe sakini labapristi abakhulu bakunikele kimi; wenzeni?
36 Yesu anati, “Ufumu wanga si wa dziko lapansi lino. Ukanakhala wa pansi pano, antchito anga akanachita nkhondo kulepheretsa Ayuda kundigwira. Koma tsopano ufumu wanga ndi wochokera kumalo ena.”
UJesu waphendula wathi: Umbuso wami kawusiwo walumhlaba; uba umbuso wami ubungowalumhlaba, inceku zami bezizakulwa, ukuze nginganikelwa kumaJuda; kodwa khathesi umbuso wami kawusiwo owalapha.
37 Pilato anati, “Kani ndiwe mfumu!” Yesu anayankha kuti, “Inu mwalondola ponena kuti, Ine ndine mfumu. Kunena zoona, Ine ndinabadwa chifukwa cha chimenechi, ndipo nʼchifukwa chake ndinabwera mʼdziko lapansi, kudzachitira umboni choonadi. Aliyense amene ali mbali yachoonadi amamvera mawu anga.”
UPilatu wasesithi kuye: Ngakho uyinkosi yini? UJesu waphendula wathi: Uyatsho wena, ukuthi mina ngiyinkosi. Mina ngazalelwa lokhu, njalo ngizele lokhu emhlabeni, ukuze ngifakazele iqiniso. Wonke oweqiniso uyalizwa ilizwi lami.
38 Pilato anafunsa kuti, “Kodi choonadi nʼchiyani?” Ndi mawu awa iye anapitanso kwa Ayuda ndipo anati, “Ine sindikupeza mlandu mwa Iye.
UPilatu wathi kuye: Liyini iqiniso? Kwathi esetshilo lokhu, wabuya waphumela kumaJuda, wathi kuwo: Mina kangitholi lacala kuye.
39 Koma ndi mwambo wanu kuti pa nthawi ya Paska, ine ndikumasulireni wamʼndende mmodzi. Kodi mufuna ndikumasulireni ‘Mfumu ya Ayuda?’”
Kodwa lilomkhuba, wokuthi ngilikhululele omunye ngephasika; ngakho liyathanda ukuthi ngilikhululele iNkosi yamaJuda yini?
40 Iwo anafuwula nati, “Ameneyu ayi! Mutipatse ife Baraba!” Barabayo anali wachifwamba.
Wonke asememeza futhi, athi: Hatshi lo, kodwa uBarabasi; kodwa uBarabasi wayengumphangi.