< Yohane 18 >
1 Yesu atamaliza kupemphera, Iye anachoka ndi ophunzira ake ndi kuwoloka chigwa cha Kidroni. Kumbali inayo kunali munda wa Olivi, ndipo Iye ndi ophunzira ake analowamo.
Après avoir prononcé ces paroles, Jésus sortit avec ses disciples de l'autre côté du torrent de Cédron, où il y avait un jardin, dans lequel il entra avec ses disciples.
2 Tsopano Yudasi, amene anamupereka amadziwa malowo chifukwa Yesu ankakumana ndi ophunzira ake kumeneko.
Judas, qui le trahissait, connaissait aussi ce lieu, car Jésus s'y réunissait souvent avec ses disciples.
3 Choncho Yudasi anabwera ku munda, akutsogolera gulu la asilikali ndi akuluakulu ena ochokera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi. Iwo anali atanyamula miyuni, nyale ndi zida.
Judas donc, ayant pris un détachement de soldats et d'officiers des principaux sacrificateurs et des pharisiens, y vint avec des lanternes, des torches et des armes.
4 Yesu, podziwa zonse zimene zimati zichitike kwa Iye, anatuluka ndi kuwafunsa kuti, “Kodi mukufuna ndani?”
Jésus donc, sachant tout ce qui lui arrivait, sortit et leur dit: « Qui cherchez-vous? »
5 Iwo anayankha kuti, “Yesu wa ku Nazareti.” Yesu anati, “Ndine.” (Ndipo Yudasi womuperekayo anali atayima nawo pamenepo).
Ils lui répondirent: « Jésus de Nazareth. » Jésus leur dit: « Je suis lui. » Judas, qui le livrait, se tenait aussi avec eux.
6 Pamene Yesu anati, “Ndine,” iwo anabwerera mʼmbuyo ndi kugwa pansi.
Lorsqu'il leur dit: « C'est moi », ils reculèrent et tombèrent à terre.
7 Iye anawafunsanso kuti, “Kodi mukumufuna ndani?” Ndipo iwo anati, “Yesu wa ku Nazareti.”
Il leur demanda donc à nouveau: « Qui cherchez-vous? » Ils ont dit: « Jésus de Nazareth. »
8 Yesu anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kuti Ndine. Ngati inu mukufuna Ine, asiyeni anthu awa apite.”
Jésus répondit: « Je vous ai dit que c'était moi. Si donc vous me cherchez, laissez ceux-là s'en aller, »
9 Izi zinachitika kuti mawu amene Iye anayankhula akwaniritsidwe: “Ine sindinataye ndi mmodzi yemwe mwa iwo amene mwandipatsa.”
afin que s'accomplisse la parole qu'il a dite: « De ceux que tu m'as donnés, je n'ai perdu aucun. »
10 Kenaka Simoni amene anali ndi lupanga analitulutsa ndi kutema nalo wantchito wa wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake la kudzanja lamanja. (Dzina la wantchitoyo ndi Makusi).
Simon-Pierre, ayant une épée, la tira, frappa le serviteur du souverain sacrificateur, et lui coupa l'oreille droite. Le nom du serviteur était Malchus.
11 Yesu analamula Petro kuti, “Bwezera lupanga mʼchimake! Kodi Ine ndisamwere chikho chimene Atate andipatsa?”
Jésus dit alors à Pierre: « Remets l'épée dans son fourreau. La coupe que le Père m'a donnée, ne la boirai-je pas? »
12 Kenaka gulu la asilikali ndi olamulira wawo ndi akuluakulu a Ayuda anamugwira Yesu. Iwo anamumanga.
Le détachement, le commandant et les officiers des Juifs se saisirent donc de Jésus, le lièrent,
13 Poyamba anapita naye kwa Anasi amene anali mkamwini wa Kayafa, mkulu wa ansembe chaka chimenecho.
et le conduisirent d'abord chez Anne, car il était beau-père de Caïphe, qui était grand prêtre cette année-là.
14 Kayafa anali amene analangiza Ayuda kuti kukanakhala kwabwino ngati munthu mmodzi akanafera anthu.
Or, c'est Caïphe qui avait conseillé aux Juifs qu'il convenait qu'un seul homme périsse pour le peuple.
15 Simoni Petro ndi ophunzira wina ankamutsatira Yesu chifukwa ophunzira uyu amadziwika kwa mkulu wa ansembe. Iye analowa ndi Yesu mʼbwalo la mkulu wa ansembe
Simon Pierre suivait Jésus, ainsi qu'un autre disciple. Or ce disciple était connu du grand prêtre, et il entra avec Jésus dans la cour du grand prêtre;
16 koma Petro anadikira kunja pa khomo. Ophunzira winayo amene amadziwika kwa mkulu wa ansembe, anatuluka ndi kuyankhula ndi mtsikana amene anali mlonda wa pa khomo ndi kumulowetsa Petro.
mais Pierre se tenait à la porte, dehors. L'autre disciple, qui était connu du grand prêtre, sortit donc, parla à la servante qui gardait la porte, et fit entrer Pierre.
17 Mtsikanayo anafunsa Petro kuti, “Kodi iwe sindiwe mmodzi wa ophunzira a Munthu uyu?” Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”
Alors la servante qui gardait la porte dit à Pierre: « Es-tu aussi un des disciples de cet homme? » Il a dit: « Je ne le suis pas. »
18 Popeza kunkazizira, anyamata antchito ndi akuluakulu ena anasonkha moto wamakala namawotha atayimirira mozungulira. Petro nayenso anayimirira pamodzi ndi iwo namawotha nawo motowo.
Or les serviteurs et les officiers se tenaient là, ayant fait un feu de charbons, car il faisait froid. Ils se chauffaient. Pierre était avec eux, debout et se réchauffant.
19 Pa nthawi imeneyi, mkulu wa ansembe anamufunsa Yesu za ophunzira ake ndi chiphunzitso chake.
Le grand prêtre interrogea donc Jésus sur ses disciples et sur son enseignement.
20 Yesu anayankha kuti, “Ine ndinayankhula poyera ku dziko lapansi. Nthawi zonse ndimaphunzitsa mʼsunagoge kapena mʼNyumba ya Mulungu kumene Ayuda onse amasonkhana pamodzi. Ine sindimanena kanthu mseri.
Jésus lui répondit: « J'ai parlé ouvertement au monde. J'ai toujours enseigné dans les synagogues et dans le temple, là où les Juifs se réunissent toujours. Je n'ai rien dit en secret.
21 Nʼchifukwa chiyani mukundifunsa Ine? Afunseni amene amamva. Zoonadi akudziwa zimene Ine ndinanena.”
Pourquoi m'interroges-tu? Demandez à ceux qui m'ont entendu ce que je leur ai dit. Voici, ils savent les choses que j'ai dites. »
22 Yesu atanena izi, mmodzi wa akuluakulu amene anali pafupi anamumenya kumaso. Iye anafunsa kuti, “Mayankhidwe awa ndi woti ndi kuyankha mkulu wa ansembe?”
Lorsqu'il eut dit cela, l'un des officiers qui se tenait là frappa Jésus de la main, en disant: « C'est ainsi que tu réponds au grand prêtre? »
23 Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndanena kanthu kolakwika, chitirani umboni chimene ndalakwa. Koma ngati ndanena zoona, nʼchifukwa chiyani mwandimenya?”
Jésus lui répondit: « Si j'ai mal parlé, témoigne du mal; mais si j'ai bien parlé, pourquoi me frappes-tu? »
24 Kenaka Anasi anamutumiza Iye, ali womangidwabe, kwa Kayafa, mkulu wa ansembe.
Annas l'envoya lié à Caïphe, le grand prêtre.
25 Pamene Simoni Petro anali chiyimirire kuwotha moto, anafunsidwa kuti, “Kodi iwe si mmodzi wa ophunzira ake?” Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”
Or Simon-Pierre était debout et se chauffait. Ils lui dirent donc: « Tu n'es pas aussi un de ses disciples, n'est-ce pas? » Il l'a nié et a dit: « Je ne le suis pas. »
26 Mmodzi wa antchito a mkulu wa ansembe, mʼbale wa munthu amene anadulidwa khutu ndi Petro anamutsutsa iye kuti, “Kodi sindinakuone iwe pamodzi ndi Iye mʼmunda muja?”
Un des serviteurs du grand prêtre, parent de celui à qui Pierre avait coupé l'oreille, dit: « Ne t'ai-je pas vu avec lui dans le jardin? »
27 Petro anakananso, ndipo pa nthawi yomweyo tambala analira.
Pierre le renia donc de nouveau, et aussitôt le coq chanta.
28 Kenaka Ayuda anamutenga Yesu kuchoka kwa Kayafa ndi kupita ku nyumba yaufumu ya bwanamkubwa wa Chiroma. Tsopano kunali mmamawa, ndipo polewa kudetsedwa monga mwa mwambo Ayuda sanalowe mʼnyumba yaufumuyo; iwo anafuna kuti adye Paska.
Ils conduisirent donc Jésus de chez Caïphe au prétoire. C'était de bonne heure, et eux-mêmes n'entraient pas dans le prétoire, afin de ne pas se souiller, mais de pouvoir manger la Pâque.
29 Choncho Pilato anatuluka napita kwa iwo ndipo anati, “Kodi ndi milandu yanji imene mukumuzenga munthu uyu?”
Pilate sortit donc vers eux et dit: « Quelle accusation portez-vous contre cet homme? »
30 Iwo anayankha kuti, “Ngati Iye akanakhala kuti si wolakwa, ife sitikanamupereka kwa inu.”
Ils lui répondirent: « Si cet homme n'était pas un malfaiteur, nous ne te l'aurions pas livré. »
31 Pilato anati, “Mutengeni inu eni ake ndi kumuweruza Iye monga mwa malamulo anu.” Ayuda anatsutsa nati, “Koma tilibe ulamuliro wakupha aliyense.”
Pilate leur dit donc: « Prenez-le vous-mêmes, et jugez-le selon votre loi. » C'est pourquoi les Juifs lui dirent: « Il nous est interdit de mettre quelqu'un à mort »,
32 Izi zinachitika kuti mawu a Yesu amene anayankhula kusonyeza mtundu wa imfa imene Iye anati adzafe nayo akwaniritsidwe.
afin que s'accomplisse la parole de Jésus, qu'il avait prononcée, en indiquant par quel genre de mort il devait mourir.
33 Kenaka Pilato anapita mʼkati mwa nyumba yaufumu nayitanitsa Yesu, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi iwe ndi mfumu ya Ayuda?”
Pilate entra donc de nouveau dans le prétoire, appela Jésus, et lui dit: « Es-tu le roi des Juifs? »
34 Yesu anafunsa kuti, “Kodi amenewo ndi maganizo anu wokha? Kapena kuti ena anakuwuzani za Ine?”
Jésus lui répondit: « Tu dis cela tout seul, ou bien d'autres t'ont-ils parlé de moi? »
35 Pilato anayankha kuti, “Kodi iwe ukuganiza kuti ine ndine Myuda? Ndi anthu ako ndi akulu a ansembe ako amene akupereka iwe kwa ine. Kodi walakwanji?”
Pilate répondit: « Je ne suis pas Juif, n'est-ce pas? Ta propre nation et les chefs des prêtres t'ont livré à moi. Qu'as-tu fait? »
36 Yesu anati, “Ufumu wanga si wa dziko lapansi lino. Ukanakhala wa pansi pano, antchito anga akanachita nkhondo kulepheretsa Ayuda kundigwira. Koma tsopano ufumu wanga ndi wochokera kumalo ena.”
Jésus répondit: « Mon Royaume n'est pas de ce monde. Si mon Royaume était de ce monde, alors mes serviteurs combattraient, pour que je ne sois pas livré aux Juifs. Mais maintenant, mon Royaume n'est pas d'ici-bas. »
37 Pilato anati, “Kani ndiwe mfumu!” Yesu anayankha kuti, “Inu mwalondola ponena kuti, Ine ndine mfumu. Kunena zoona, Ine ndinabadwa chifukwa cha chimenechi, ndipo nʼchifukwa chake ndinabwera mʼdziko lapansi, kudzachitira umboni choonadi. Aliyense amene ali mbali yachoonadi amamvera mawu anga.”
Pilate lui dit donc: « Es-tu donc un roi? » Jésus répondit: « Vous dites que je suis un roi. C'est pour cela que je suis né, et c'est pour cela que je suis venu dans le monde, afin de rendre témoignage à la vérité. Tous ceux qui sont de la vérité écoutent ma voix. »
38 Pilato anafunsa kuti, “Kodi choonadi nʼchiyani?” Ndi mawu awa iye anapitanso kwa Ayuda ndipo anati, “Ine sindikupeza mlandu mwa Iye.
Pilate lui dit: « Qu'est-ce que la vérité? » Après avoir dit cela, il sortit de nouveau vers les Juifs, et leur dit: « Je ne trouve aucun motif d'accusation contre lui.
39 Koma ndi mwambo wanu kuti pa nthawi ya Paska, ine ndikumasulireni wamʼndende mmodzi. Kodi mufuna ndikumasulireni ‘Mfumu ya Ayuda?’”
Mais vous avez pour coutume que je vous livre quelqu'un à la Pâque. Voulez-vous donc que je vous relâche le roi des Juifs? »
40 Iwo anafuwula nati, “Ameneyu ayi! Mutipatse ife Baraba!” Barabayo anali wachifwamba.
Alors ils crièrent tous à nouveau, disant: « Pas cet homme, mais Barabbas! » Or Barabbas était un brigand.