< Yohane 17 >
1 Yesu atatha kunena izi, anayangʼana kumwamba ndipo anapemphera: “Atate, nthawi yafika. Lemekezani Mwana wanu, kuti Mwana wanuyo akulemekezeni Inu.
Ie nitsarae’ Iesoà, le niandrandra mb’andikerañe ey, nanao ty hoe: O Aba, fa tondroke ty ora; rengeo t’i Ana’o, handrengea’e Azo.
2 Pakuti Inu munamupatsa Iye ulamuliro pa anthu onse kuti apereke moyo wosatha kwa onse amene mwamupatsa. (aiōnios )
Fa nimea’o lily re hifehe ze kila nofotse, soa te ho tolora’e haveloñe nainai’e ze hene natolo’o aze. (aiōnios )
3 Tsono moyo wosathawo ndi uwu: Iwo akudziweni Inu, Mulungu yekhayo woona, ndi Yesu Khristu, amene Inu mwamutuma. (aiōnios )
Zao o haveloñe nainai’eo, t’ie ho fohi’ iereo ry Andrianañahare tokañe to, naho Iesoà Norizañe nahitri’oy. (aiōnios )
4 Ine ndabweretsa ulemerero wanu pa dziko pamene ndamaliza ntchito imene munandipatsa kuti ndi igwire.
Fa nandrengeako an-tane atoy vaho nihenefako i nampitoloñe’o Ahiy.
5 Ndipo tsopano, Atate, ndilemekezeni Ine pamaso panu ndi ulemerero uja umene ndinali nawo kwa Inu dziko lapansi lisanayambe.
O Aba itoloro engeñe añila’o eo henaneo amy engeñe nindrezan-tika taolo’ ty fifotora’ ty voatse toiy.
6 “Ine ndawadziwitsa za Inu anthu amene munandipatsa mʼdziko lapansi. Iwo anali anu. Inu munawapereka kwa Ine ndipo amvera mawu anu.
Fa nampahafohineko ondaty natolo’o ahy boak’ ami’ty voatse toio ty tahina’o, ie nifanaña’o, naho natolo’o ahiko vaho nambena’ iereo o tsara’oo.
7 Tsopano akudziwa kuti zonse zimene munandipatsa nʼzochokera kwa Inu.
Fa rendre’ iereo henaneo te boak’ ama’o ze hene natolo’o ahy,
8 Pakuti Ine ndiwapatsa mawu amene Inu munandipatsa ndipo awalandira. Iwo akudziwa ndithu kuti Ine ndinachokera kwa Inu, ndipo akukhulupirira kuti Inu ndiye amene munandituma Ine.
ie natoloko o saontsy nimea’o ahikoo, naho rinambe’ iereo, naho rendre’ iereo to te boak’ ama’o iraho vaho antofa’ iereo te Ihe ro nañitrik’ ahy.
9 Ine ndikuwapempherera. Ine sindikupempherera dziko lapansi, koma anthu amene Inu mwandipatsa, pakuti ndi anu.
Ihalaliako; tsy ho ami’ty voatse toy ty ihalaliako, fa ho amo natolo’o ahikoo amy t’ie azo.
10 Zonse zimene Ine ndili nazo ndi zanu, ndipo zonse zimene Inu muli nazo ndi zanga. Choncho Ine ndalemekezedwa mwa iwowo.
Kila azo o ahikoo, naho ahiko o azoo; vaho nahazoako engeñe.
11 Ine sindikukhalanso mʼdziko lapansi nthawi yayitali, koma iwo akanali mʼdziko lapansi. Ine ndikubwera kwa Inu. Atate Woyera, atetezeni ndi mphamvu za dzina lanu. Dzina limene munandipatsa Ine, kuti iwo akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
Tsy ami’ty voatse toy ka iraho, fe ami’ty voatse toy o retoañe, vaho homb’ ama’o mb’eo iraho. Ry Aba masiñe, tambozoro an-tahina’o o natolo’o ahikoo, soa t’ie ho raike manahake itikañe.
12 Pamene ndinali nawo, ndinawateteza ndi kuwasunga mosamala mʼdzina limene munandipatsa. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatayika kupatula yekhayo amene anayenera kuwonongeka kuti malemba akwaniritsidwe.
Izaho nimpiam’ iereo, le nambenako an-tahina’o o natolo’o ahikoo; nitambozoreko o natolo’o ahikoo, tsy ia ty nipoke naho tsy i anan-kamomohañey hampañeneke o Sokitse Masiñeo.
13 “Tsopano ndikubwera kwa Inu. Ndikunena izi ndikanali mʼdziko lapansi, kuti iwo akhale ndi muyeso wodzaza wachimwemwe changa mʼkati mwawo.
Mb’ama’o mb’eo iraho henaneo; naho taroñeko ami’ty voatse toy o entañe zao, handiforañe am’iereo o haehakoo.
14 Ine ndawapatsa mawu anu ndipo dziko lapansi likudana nawo, pakuti sali a dziko lapansi monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
Fa natoloko iareo o tsara’oo le niheje’ ty voatse toy, amy t’ie tsy mpiami’ ty voatse toy, hambañe amy te izaho tsy mpiami’ ty voatse toy.
15 Sindikupempha kuti muwachotse mʼdziko lapansi koma kuti muwateteze kwa woyipayo.
Tsy ihalaliako te hakareñe ami’ty voatse toy iereo, fa t’ie ho kalañeñe ami’ty raty.
16 Iwo si a dziko lapansi, monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
Tsy mpiama’ ty voatse toy iereo, hambañe amy te izaho tsy mpiami’ ty voatse toy.
17 Ayeretseni ndi choonadi chanu. Mawu anu ndiye choonadi.
Ampiavaho an-katò iereo; o tsara’oo ro to.
18 Monga Inu munandituma Ine mʼdziko lapansi, Inenso ndikuwatuma mʼdziko lapansi.
Hambañe ami’ty nañiraha’o ahy mb’ami’ty voatse toy, ty nañitrifako iareo mb’ami’ty voatse toy.
19 Chifukwa cha iwowa Ine ndikudziyeretsa, kuti iwo ayeretsedwenso kwenikweni.
Ie ro añamasiñako vatañe, hañavaheko iareo añami’ty hatò.
20 “Ine sindikupempherera iwo okhawa, komanso amene adzandikhulupirira chifukwa cha uthenga wawo.
Tsy ho a iretoañe avao o ihalaliakoo, fa ho amo mbe hiato amako ami’ ty tsara’ iareoo;
21 Ndikuwapempherera kuti onsewa akhale amodzi. Monga Inu Atate muli mwa Ine ndi Ine mwa Inu, iwonso akhale mwa Ife kuti dziko lapansi likhulupirire kuti Inu munandituma Ine.
soa te ho raike iaby iereo, hambañe amy te amako irehe Aba, naho ama’o iraho, vaho ho raik’ aman-tikañe iereo, hatokisa’ ty voatse toy te nañitrik’ ahy irehe.
22 Ine ndawapatsa ulemerero umene munandipatsa Ine, kuti akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
Fa natoloko iareo i engeñe natolo’o ahikoy, soa t’ie ho raike, hambañe amy te itika ro raike:
23 Ine ndikhale mwa iwo ndipo Inu mwa Ine kuti umodzi wawo ukhale wangwiro. Choncho dziko lapansi lidzadziwa kuti Inu munandituma Ine ndipo Inu mwawakonda iwowa monga momwe Inu munandikondera Ine.
Izaho am’iereo, naho Ihe amako, hamonirañe iareo ho raike; soa te ho fohi’ ty voatse toy te nañitrik’ ahy irehe vaho nikoko iareo, manahake ty fikokoa’o ahy.
24 “Atate, Ine ndikufuna kuti anthu amene mwandipatsa Ine adzakhale ndi Ine kumene kuli Ine, ndi kuona ulemerero wanga, ulemerero umene munandipatsa chifukwa Inu munandikonda dziko lapansi lisanalengedwe.
O Aba, salalaeko te hindre amako ami’ty hitoerako o natolo’o ahikoo, hahaoniñe i engeñe natolo’o ahiy, amy t’ie nikokoa’o taolo’ ty nañoreña’o ty voatse toy.
25 “Atate wolungama, ngakhale kuti dziko lapansi silikudziwani Inu, Ine ndimakudziwani, ndipo iwo amadziwa kuti Inu munandituma Ine.
Ry Aba vantañe, ihe tsy nifohi’ ty voatse toy, fe fohiko, naho fohi’ iretoañe te Ihe ro nañitrik’ ahy,
26 Ine ndawadziwitsa dzina lanu, ndipo ndidzapitiriza kuwadziwitsa dzina lanulo, kuti chikondi chomwe munandikonda nacho chikhale mwa iwo, ndipo Ine mwa iwo.”
naho nampahafohineko iareo i tahina’oy, mbore hampandrendreheko, soa te ho am’ iareo i fikokoañe nikokoa’o ahiy vaho izaho am’ iareo.