< Yohane 16 >

1 “Ine ndakuwuzani zonsezi kuti musadzakhumudwe.
N waani yi lani, ke lan da ti tua yipo tungbali bonla.
2 Iwo adzakuchotsani mʼsunagoge mwawo. Kunena zoona, nthawi ikubwera imene aliyense amene adzakuphani adzaganiza kuti akutumikira Mulungu.
Bi baa ñani yi li balimaama diena nni. U yogunu kpendi ke yua n baa kpa yi, baa nua ke o kpiagidi U Tiene.
3 Iwo adzachita zoterozo chifukwa sanadziwe Atate kapena Inenso.
Bi baa tiendi yi lani kuli, kelima baa bani Baa, baa bani mini moko.
4 Ine ndakuwuzani izi kuti nthawi ikadzafika mudzakumbukire kuti Ine ndinakuchenjezani kale. Ine sindinakuwuzeni izi poyamba paja chifukwa ndinali nanu.”
N waani yi lani ke li yogunu yaa ti pundi yin tiadi ke n den waani yi la. Mii den waani la hali mi cilima. Kelima n den ye leni yi.
5 “Tsopano Ine ndikupita kwa Iye amene anandituma koma palibe wina mwa inu akundifunsa kuti, ‘Kodi mukupita kuti?’
Moala n caa yua n soani nni kani, ama yi siiga o bakuli naa buali nni, a caa le yo?
6 Muli ndi chisoni kwambiri chifukwa ndakuwuzani zimene.
Li paboanli cuo yi boncianla, kelima n waani lani.
7 Komatu ndakuwuzani zoona. Ine ndikuti kuli bwino kwa inu kuti ndichoke. Ngati sindichoka, Nkhosweyo sidzabwera kwa inu, koma ngati Ine ndipita, ndidzamutumiza kwa inu.
Li baa hani yipo min gedi, kelima n yaa gedi o todikoa kan cua, ama n ya gedi n baa soani yipo o todikoa.
8 Iye akabwera, adzatsutsa dziko lapansi za uchimo, zachilungamo ndi zachiweruzo.
O ya cua o baa paadi handuna ti tuonbiadi po, mi tegima leni li bujiali.
9 Za uchimo, chifukwa anthu sakhulupirira Ine.
Ti tuonbiadi po kelima baa daani nni.
10 Za chilungamo, chifukwa Ine ndi kupita kwa Atate, kumene simudzandionanso.
Mi teginma po kelima n caa Baa po ke yi kan go le nni.
11 Za chiweruzo, chifukwa wolamulira dziko lino lapansi waweruzidwa tsopano.
Li bujiali po kelima handuna bado buudi jia no.
12 “Ine ndili ndi zambiri zoti ndiyankhule nanu, koma simungathe kuzilandira tsopano.
N pia mi maama boncianla, ki baa waani yi, ama yi kan fidi ki gama moala. O baagikoa, imoamoani fuoma yua,
13 Koma pamene Iye, Mzimu wachoonadi, abwera, adzakutsogolerani mʼchoonadi chonse. Iye sadzayankhula mwa Iye yekha, adzayankhula zokhazo zimene wamva ndipo Iye adzakuwuzani zimene zikubwera.
o ya cua o baa gobidi yi, yin bandi imoamoani kuli, kelima o kan maadi o yuceli maama, ama o baa taa wan gbadi yaale ki waani, yaa bonla n baa cua.
14 Iye adzalemekeza Ine chifukwa adzatenga za Ine nadzakudziwitsani.
O baa kpiagidi nni, kelima o baa taa min pia yaale ki yaa wangi yi.
15 Zonse za Atate ndi zanga. Ichi nʼchifukwa chake Ine ndanena kuti Mzimu Woyera adzatenga kwa Ine zanga kuti muzidziwe.”
Baa n pia yaala kuli ye n ya niinne, lanyaapo n teni ke n yedi: O baa taa min pia yaala ki yaa wangi yi.
16 Yesu anapitiriza kuyankhula kuti, “Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso, ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso.”
Li ya pugini waamu, yi kan go le nni, ama li yaa yanwaamu yi go baa le nni. Kelima n caa Baa po.
17 Ena a ophunzira ake anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi Iye akutanthauza chiyani ponena kuti, ‘Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso,’ ndi ‘ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso,’ ndiponso ‘chifukwa ndikupita kwa Atate?’”
Lanyaapo ohoadikaaba siiga bi tianba den tua bi yaba: Wan tua li yaa pugini waamu yi kan go le nni, ama li ya go yanwaamu, yi go baa le nni, kelima n caa Baa po yeni mo bua ki yedi be yo?
18 Iwo anapitiriza kufunsana kuti, “Kodi akutanthauza chiyani, ‘kanthawi kochepa?’ Ife sitikumvetsetsa chimene Iye akuyankhula.”
Bi den tua: Lanwani be n bua ki yedi: Yogunu waamu yeni. Tii bani wan maadi yaa yaala.
19 Yesu anadziwa kuti ankafuna kuti amufunse za zimenezi, choncho anawafunsa kuti, “Kodi mukufunsana wina ndi mnzake chimene Ine ndimatanthauza pamene ndinati, ‘Mwa kanthawi kochepa simudzandionanso,’ ndi ‘patatha nthawi pangʼono mudzandionanso?’
Jesu den bani ke bi bua ki buali o, lane o den yedi ba: Yi buali yi yaba yaala n bua ki yedi: Li ya pugini waamu, yi kan go le nni ama li yaa yanwaamu yi go baa le nni.
20 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti inu mudzalira ndi kubuma pomwe dziko lapansi lidzakhale likukondwera. Inu mudzamva chisoni, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe.
N waani yi, imoamoani yi baa buudi ki go mua, ama handuna yaaba baa mangi bi pala, yi pabiidili baa lebidi ki tua pamanli.
21 Mayi akamabereka mwana amamva ululu chifukwa nthawi yake yafika; koma mwana wake akabadwa amayiwala ululu wake chifukwa cha chimwemwe chake chakuti mwana wabadwa mʼdziko lapansi.
O pua yaa baa maa yaa yogunu o yen le ti yanyagidi kelima o maa yogunu pundi, ama o ya mala waa go tiadi ofala po. Kelima o mala nisaalo handuna nni.
22 Chimodzimodzinso ndi inu. Tsopano ino ndi nthawi yanu yomva chisoni, koma Ine ndidzakuonaninso ndipo inu mudzasangalala, ndipo palibe amene adzachotsa chimwemwe chanu.
Li tie yene leni yinba moko, li pabiidili cuo yi, ama n go baa le yi ke yi pala baa mangi, o bakuli kan fie yi kani laa pamanli.
23 Tsiku limenelo inu simudzandipemphanso kalikonse. Ine ndikukuwuzani zoona kuti Atate anga adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
Laa daali ya pundi yi kan go buali nni li bakuli, n yedi yi imoamoani, yin baa mia Baa yaala n yeli nni kuli o baa payi la.
24 Mpaka tsopano simunapemphe kalikonse mʼdzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
Hali moala yi daa mia li bakuli n yeli nni. Mia mani yi baa ba, ke yi pamanli n dagidi cian.
25 “Ngakhale ndakhala ndikuyankhula mʼmafanizo, nthawi ikubwera imene Ine sindidzagwiritsanso ntchito mafanizo otere koma ndidzakuwuzani momveka za Atate anga.
N maadi yi lankuli leni mi kpanjama. Yogunu kpendi ke n kan go maadi yi leni kpanjama, ama n baa yaa maadi yi n Baa maama ke li doagidi cain.
26 Tsiku limenelo inu mudzapempha mʼdzina langa. Ine sindikunena kuti ndidzapempha Atate mʼmalo mwanu ayi.
Laa daali ya pundi, yi baa miadi o n yenli nni. Mii yedi yi ke n baa mia Baa yipo,
27 Atate mwini anakukondani chifukwa inu mwandikonda Ine ndipo mwakhulupirira kuti Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate.
kelima Baa wani o ba bua yi, kelima yi den bua nni, ki daani ke ñani U Tienu kani.
28 Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate ndi kulowa mʼdziko lapansi. Tsopano ndikulisiya dziko lapansi kubwerera kwa Atate.”
N ñani Baa kani ki cua handuna nni, moala n ña handuna nni ki caa Baa po.
29 Kenaka ophunzira ake anati, “Tsopano mukuyankhula momveka bwino ndi mopanda mafanizo.
O hoadikaaba den yedi o: Moa a maadi ke li doagidi cain, haa taani leni kpanjama.
30 Tsopano ife tikuona kuti Inu mumadziwa zinthu zonse ndi kuti sipafunika wina aliyense kukufunsani. Mwa ichi ife takhulupirira kuti Inu munachokera kwa Mulungu.”
Moala ti bandi ke a bani li bonla kuli, laa tiladi han guudi ke nilo ba n buali a, bonla bakuli, lanyaapo yo ke ti daani, ke ha ñani U Tienu kani ki cua.
31 Yesu anawafunsa kuti, “Kodi tsopano mwakhulupirira?”
Jesu den yedi ba: Yi daani moala.
32 Koma nthawi ikubwera ndipo yafika, pamene inu mudzabalalitsidwa, aliyense ku nyumba yake. Inu mudzandisiya ndekhandekha. Koma Ine sindili ndekha, pakuti Atate anga ali nane.
Diidi u yogunu kpendi ke yi baa yadi ki ha nni, yua kuli n gedi o kaanu, ama n kan yaa ye n bebe, kelima Baa ye leni nni.
33 “Ine ndakuwuzani izi kuti mwa Ine mukhale nawo mtendere. Mʼdziko lapansi mudzakhala nawo mavuto. Koma limbikani mtima! Ine ndaligonjetsa dziko lapansi.”
N waani yi lani ke yin baa mi yanduanma n niini. Yi baa le ofalabiado handuna nni. Ama yin paagi yi pala kelima mini paadi handuna.

< Yohane 16 >