< Yohane 16 >
1 “Ine ndakuwuzani zonsezi kuti musadzakhumudwe.
ESTESIJA jusangane jamyo para chamiyo, fanmatotompo.
2 Iwo adzakuchotsani mʼsunagoge mwawo. Kunena zoona, nthawi ikubwera imene aliyense amene adzakuphani adzaganiza kuti akutumikira Mulungu.
Infanmayute juyong gui sinagoga sija; junggan, y tiempo ufato nae jayeja y pumuno jamyo, jinasoña na jafatinas y checho Yuus.
3 Iwo adzachita zoterozo chifukwa sanadziwe Atate kapena Inenso.
Ya estesija infanfinatinas, sa ti jatungo y Tata, ni guajo.
4 Ine ndakuwuzani izi kuti nthawi ikadzafika mudzakumbukire kuti Ine ndinakuchenjezani kale. Ine sindinakuwuzeni izi poyamba paja chifukwa ndinali nanu.”
Ya estesija guinin jusangane jamyo, na yaguin ufato ayo na ora, injaso estesija, jaftaemanoja y jusangane jamyo.
5 “Tsopano Ine ndikupita kwa Iye amene anandituma koma palibe wina mwa inu akundifunsa kuti, ‘Kodi mukupita kuti?’
Lao pago bae jujanao para ayo y tumago yo; ya taya uno guiya jamyo ufaesen yo: Para mano jao?
6 Muli ndi chisoni kwambiri chifukwa ndakuwuzani zimene.
Lao pot y jusangane jamyo nu estesija y pinite esta bula y corasonmiyo.
7 Komatu ndakuwuzani zoona. Ine ndikuti kuli bwino kwa inu kuti ndichoke. Ngati sindichoka, Nkhosweyo sidzabwera kwa inu, koma ngati Ine ndipita, ndidzamutumiza kwa inu.
Lao jusangane jamyo ni minagajet, na maulegñaja para jamyo na jujanao; sa yaguin ti jumanao yo, y Consoladot ti umamaela guiya jamyo; lao yaguin jumanao yo, junamamaela güe guiya jamyo.
8 Iye akabwera, adzatsutsa dziko lapansi za uchimo, zachilungamo ndi zachiweruzo.
Sa yaguin ufato güe, ujusga y tano ni isao yan y tininas yan y juisio:
9 Za uchimo, chifukwa anthu sakhulupirira Ine.
Y isao sa sija ti majonggue yo;
10 Za chilungamo, chifukwa Ine ndi kupita kwa Atate, kumene simudzandionanso.
Y tininas sa bae jujanao para y Tata, ya jocog nae inliiyo;
11 Za chiweruzo, chifukwa wolamulira dziko lino lapansi waweruzidwa tsopano.
Y juisio sa y magas este y tano esta jajusga.
12 “Ine ndili ndi zambiri zoti ndiyankhule nanu, koma simungathe kuzilandira tsopano.
Guaja yo megae na güinaja trabia para jusangane jamyo; lao ti siña jamyo insingon pago.
13 Koma pamene Iye, Mzimu wachoonadi, abwera, adzakutsogolerani mʼchoonadi chonse. Iye sadzayankhula mwa Iye yekha, adzayankhula zokhazo zimene wamva ndipo Iye adzakuwuzani zimene zikubwera.
Lao yaguin ufato ayo y Espiritun minagajet, güiya infanfinanue jamyo todo y minagajet; sa ti usangan pot güiyaja, lao todosija, jiningogña, ayosija usangan: yan ayosija y umasusede despues, inninafanmanatungo jamyo.
14 Iye adzalemekeza Ine chifukwa adzatenga za Ine nadzakudziwitsani.
Güiya ufannae yo minalag sa mañuñule y güinaja na guiya guajo ya ujasangane jamyo.
15 Zonse za Atate ndi zanga. Ichi nʼchifukwa chake Ine ndanena kuti Mzimu Woyera adzatenga kwa Ine zanga kuti muzidziwe.”
Todosija y güinajan Tata, iyoco; ayo mina, jusangan na mañuñule y güinaja na guiya guajo ya ujasangane jamyo.
16 Yesu anapitiriza kuyankhula kuti, “Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso, ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso.”
Trabia dididija na tiempo, ti inlie yo talo; ya y otro biaje dididija na tiempo inlie yo.
17 Ena a ophunzira ake anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi Iye akutanthauza chiyani ponena kuti, ‘Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso,’ ndi ‘ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso,’ ndiponso ‘chifukwa ndikupita kwa Atate?’”
Ya y palo disipulo ilegñija entre sija uno yan otro: Jafa muna ilegña este nu jita? Dididija na tiempo ti inlie yo; ya y otro biaje, dididija na tiempo inlie yo: sa bae jujanao para as Tata?
18 Iwo anapitiriza kufunsana kuti, “Kodi akutanthauza chiyani, ‘kanthawi kochepa?’ Ife sitikumvetsetsa chimene Iye akuyankhula.”
Ayo nae ilegñija: Jafa este muna ilegña? Dididija na tiempo? Ti tatungo jafa ilegña.
19 Yesu anadziwa kuti ankafuna kuti amufunse za zimenezi, choncho anawafunsa kuti, “Kodi mukufunsana wina ndi mnzake chimene Ine ndimatanthauza pamene ndinati, ‘Mwa kanthawi kochepa simudzandionanso,’ ndi ‘patatha nthawi pangʼono mudzandionanso?’
Lao jatungoja si Jesus na manmalago na umafaesen güe, ya ilegña nu sija: Manafaesen entre jamyo jafa y ilelegco: Dididija na tiempo ya ti inlie yo; ya otro biaje, dididija na tiempo inlie yo?
20 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti inu mudzalira ndi kubuma pomwe dziko lapansi lidzakhale likukondwera. Inu mudzamva chisoni, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe.
Magajet ya magajet y jusangane jamyo: infananges yan infanugungñaejon, lao y tano umagof; ya jamyo infantriste, lao y tristenmiyo umabira para minagof.
21 Mayi akamabereka mwana amamva ululu chifukwa nthawi yake yafika; koma mwana wake akabadwa amayiwala ululu wake chifukwa cha chimwemwe chake chakuti mwana wabadwa mʼdziko lapansi.
Y palaoan yaguin para ufañago guaja pinitiña, sa mato y oraña; lao yaguin munjayan jafañago y patgon, mafeta nu y pinitiña, pot y minagofña na esta mañago un taotao gui tano.
22 Chimodzimodzinso ndi inu. Tsopano ino ndi nthawi yanu yomva chisoni, koma Ine ndidzakuonaninso ndipo inu mudzasangalala, ndipo palibe amene adzachotsa chimwemwe chanu.
Pago jamyo locue magajet na infantriste; lao yaguin manaliijit talo, ufanmagof corasonmiyo, ya taya siña munajanao y minagofmiyo guiya jamyo.
23 Tsiku limenelo inu simudzandipemphanso kalikonse. Ine ndikukuwuzani zoona kuti Atate anga adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
Ayo na jaane ti infaesen yo ni jafa. Magajet y magajet y jusangane jamyo, todosija y ingagao y Tata, infanninae pot y naanjo.
24 Mpaka tsopano simunapemphe kalikonse mʼdzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
Asta pago taya ingagagao pot y naanjo: gagao ya inresibi, ya ubula y minagofmiyo.
25 “Ngakhale ndakhala ndikuyankhula mʼmafanizo, nthawi ikubwera imene Ine sindidzagwiritsanso ntchito mafanizo otere koma ndidzakuwuzani momveka za Atate anga.
Estesija guinin jusangane jamyo gui acomparasion sija; lao ufato y ora na ti jusangane jamyo gui acomparasion sija, lao jusangane jamyo claro y güinajan Tata.
26 Tsiku limenelo inu mudzapempha mʼdzina langa. Ine sindikunena kuti ndidzapempha Atate mʼmalo mwanu ayi.
Ayo na jaane infanmangagao pot y naanjo: lao ada ti jusangane jamyo na guajo jutayuyute jamyo gui Tata;
27 Atate mwini anakukondani chifukwa inu mwandikonda Ine ndipo mwakhulupirira kuti Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate.
Sa y Tata mangüinaeya jamyo, sa esta inguaeya yo, ya injenggue na mamaela yo guinin as Yuus.
28 Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate ndi kulowa mʼdziko lapansi. Tsopano ndikulisiya dziko lapansi kubwerera kwa Atate.”
Mamaela yo guinin as Tata, ya matoyo gui tano: lao judingo talo y tano, sa bae janao para as Tata.
29 Kenaka ophunzira ake anati, “Tsopano mukuyankhula momveka bwino ndi mopanda mafanizo.
Y disipuluña ilegñija: Estagüe, pago na unsangan claro, ya taya acomparasion unsangan.
30 Tsopano ife tikuona kuti Inu mumadziwa zinthu zonse ndi kuti sipafunika wina aliyense kukufunsani. Mwa ichi ife takhulupirira kuti Inu munachokera kwa Mulungu.”
Pago intingo na jago untungo todosija; ya ti unnesesita ni jaye unfinaesenjao: pot este injenggue na jago mamaela guinin as Yuus.
31 Yesu anawafunsa kuti, “Kodi tsopano mwakhulupirira?”
Maninepe sija as Jesus: Injenggue pago?
32 Koma nthawi ikubwera ndipo yafika, pamene inu mudzabalalitsidwa, aliyense ku nyumba yake. Inu mudzandisiya ndekhandekha. Koma Ine sindili ndekha, pakuti Atate anga ali nane.
Estagüe na ufato y ora, ya esta mato pago, na cada uno ujanao para y iyoña, ya indingo yo namaesaja; lao trabia ti guajoja namaesaja sa jumajame an Tata.
33 “Ine ndakuwuzani izi kuti mwa Ine mukhale nawo mtendere. Mʼdziko lapansi mudzakhala nawo mavuto. Koma limbikani mtima! Ine ndaligonjetsa dziko lapansi.”
Estesija jusangane jamyo, para infangaepas guiya guajo. Infangaemasâpet gui tano; lao mantiene y minatatnganmiyo, sa guajo esta jugana y tano.