< Yohane 15 >

1 “Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate anga ndiye mwini munda.
«من تاک حقیقی هستم و پدر من باغبان است.۱
2 Iye amadula nthambi iliyonse ya mwa Ine imene sibala chipatso, koma nthambi iliyonse imene imabala chipatso amayisadzira bwino kuti ibale zipatso zambiri.
هر شاخه‌ای در من که میوه نیاورد، آن را دور می‌سازد و هر‌چه میوه آرد آن راپاک می‌کند تا بیشتر میوه آورد.۲
3 Inu ndinu oyera kale chifukwa cha mawu amene ndayankhula inu.
الحال شما به‌سبب کلامی که به شما گفته‌ام پاک هستید.۳
4 Khalani mwa Ine, monga Ine ndili mwa inu. Palibe nthambi imene ingabereke chipatso pa yokha ngati sinalumikizike ku mpesa. Chomwechonso inu simungathe kubereka chipatso pokhapokha mutakhala mwa Ine.
در من بمانید و من در شما. همچنانکه شاخه از خودنمی تواند میوه آورد اگر در تاک نماند، همچنین شما نیز اگر در من نمانید.۴
5 “Ine ndine mpesa; inu ndinu nthambi zake. Ngati munthu akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye, adzabereka zipatso zambiri; popanda Ine simungathe kuchita kanthu.
من تاک هستم و شماشاخه‌ها. آنکه در من می‌ماند و من در او، میوه بسیار می‌آورد زیرا که جدا از من هیچ نمی توانیدکرد.۵
6 Ngati wina aliyense sakhala mwa Ine, iyeyo ali ngati nthambi imene yatayidwa ndi kufota. Nthambi zotero zimatoledwa, kuponyedwa pa moto ndi kupsa.
اگر کسی در من نماند، مثل شاخه بیرون انداخته می‌شود و می‌خشکد و آنها را جمع کرده، در آتش می‌اندازند و سوخته می‌شود.۶
7 Ngati inu mukhala mwa Ine ndipo mawu anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene mukufuna ndipo mudzapatsidwa.
اگر در من بمانید و کلام من در شما بماند، آنچه خواهیدبطلبید که برای شما خواهد شد.۷
8 Atate anga amalemekezedwa mukamabereka zipatso zochuluka, ndipo potero mudzionetsa kuti ndinu ophunzira anga.
جلال پدر من آشکارا می‌شود به اینکه میوه بسیار بیاورید وشاگرد من بشوید.۸
9 “Monga momwe Atate amandikondera Ine, Inenso ndakukondani. Tsopano khalani mʼchikondi changa.
همچنان‌که پدر مرا محبت نمود، من نیز شما را محبت نمودم؛ در محبت من بمانید.۹
10 Ngati mumvera malamulo anga, mudzakhala mʼchikondi changa, monga Ine ndimamvera malamulo a Atate anga, ndipo ndimakhala mʼchikondi chawo.
اگر احکام مرا نگاه دارید، در محبت من خواهید ماند، چنانکه من احکام پدر خود را نگاه داشته‌ام و در محبت او می‌مانم.۱۰
11 Ine ndakuwuzani izi kuti chimwemwe changa chikhale mwa Inu, kuti chimwemwe chanu chikhale chokwanira.
این را به شماگفتم تا خوشی من در شما باشد و شادی شماکامل گردد.۱۱
12 Lamulo langa ndi ili: ‘Kondanani wina ndi mnzake monga Ine ndakonda inu.’
«این است حکم من که یکدیگر را محبت نمایید، همچنان‌که شما را محبت نمودم.۱۲
13 Palibe munthu ali ndi chikondi choposa ichi, choti munthu nʼkutaya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.
کسی محبت بزرگتر از این ندارد که جان خودرا بجهت دوستان خود بدهد.۱۳
14 Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene Ine ndikulamulani.
شما دوست من هستید اگر آنچه به شما حکم می‌کنم به‌جا آرید.۱۴
15 Ine sindikutchulaninso antchito, chifukwa wantchito sadziwa zimene bwana wake akuchita. Mʼmalo mwake Ine ndakutchani abwenzi pakuti zilizonse zimene ndinaphunzira kwa Atate, Ine ndakudziwitsani.
دیگر شما را بنده نمی خوانم زیرا که بنده آنچه آقایش می‌کند نمی داند؛ لکن شما را دوست خوانده‌ام زیرا که هرچه از پدر شنیده‌ام به شمابیان کردم.۱۵
16 Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani kuti mupite ndi kukabereka zipatso, zipatso zake za nthawi yayitali. Choncho Atate adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
شما مرا برنگزیدید، بلکه من شما رابرگزیدم و شما را مقرر کردم تا شما بروید و میوه آورید و میوه شما بماند تا هر‌چه از پدر به اسم من طلب کنید به شما عطا کند.۱۶
17 Lamulo langa ndi ili: ‘Muzikondana.’
به این چیزها شما را حکم می‌کنم تایکدیگر را محبت نمایید.۱۷
18 “Ngati dziko lapansi lidana nanu, dziwani kuti linayamba kudana ndi Ine.
«اگر جهان شما رادشمن دارد، بدانید که پیشتر از شما مرا دشمن داشته است.۱۸
19 Inu mukanakhala anthu a dziko lapansi, dziko lapansi likanakukondani ngati anthu ake omwe. Koma mmene zilili, inu si anthu a dziko lapansi. Ine ndakusankhani kuchokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake dziko lapansi limakudani.
اگر از جهان می‌بودید، جهان خاصان خود را دوست می‌داشت. لکن چونکه ازجهان نیستید بلکه من شما را از جهان برگزیده‌ام، از این سبب جهان با شما دشمنی می‌کند.۱۹
20 Kumbukirani mawu amene ndinayankhula nanu akuti, ‘Palibe wantchito amene amaposa bwana wake.’ Ngati anandizunza Ine, iwo adzakuzunzaninso inu. Ngati anamvera chiphunzitso changa, iwo adzamvera chanunso.
به‌خاطر آرید کلامی را که به شما گفتم: غلام بزرگتراز آقای خود نیست. اگر مرا زحمت دادند، شما رانیز زحمت خواهند داد، اگر کلام مرا نگاه داشتند، کلام شما را هم نگاه خواهند داشت.۲۰
21 Iwo adzakuchitani zimenezi chifukwa cha dzina langa, popeza sakudziwa amene anandituma Ine.
لکن بجهت اسم من جمیع این کارها را به شما خواهندکرد زیرا که فرستنده مرا نمی شناسند.۲۱
22 Ine ndikanapanda kubwera ndi kuyankhula nawo, sakanakhala ndi mlandu. Koma tsopano alibe choti nʼkukanira mlandu wawo.
اگرنیامده بودم و به ایشان تکلم نکرده، گناه نمی داشتند؛ و اما الان عذری برای گناه خودندارند.۲۲
23 Iye amene amadana ndi Ine amadananso Atate anga.
هر‌که مرا دشمن دارد پدر مرا نیز دشمن دارد.۲۳
24 Ine ndikanapanda kuchita pakati pawo zinthu zimene wina aliyense sanachitepo, iwo sakanakhala ochimwa. Koma tsopano aona zodabwitsa izi, komabe akundida Ine pamodzi ndi Atate anga.
و اگر در میان ایشان کارهایی نکرده بودم که غیر از من کسی هرگز نکرده بود، گناه نمی داشتند. ولیکن اکنون دیدند و دشمن داشتند مرا و پدر مرا نیز.۲۴
25 Koma zatere kuti zikwaniritse zimene zinalembedwa mʼmalamulo awo: ‘Iwo anandida Ine popanda chifukwa.’
بلکه تا تمام شودکلامی که در شریعت ایشان مکتوب است که “مرابی سبب دشمن داشتند.”۲۵
26 “Nkhoswe ikadzabwera imene Ine ndidzakutumizireni kuchokera kwa Atate, ndiye Mzimu Woyera wachoonadi amene achokera kwa Atate, Iyeyo adzandichitira umboni Ine.
لیکن چون تسلی دهنده که او را از جانب پدر نزد شما می‌فرستم آید، یعنی روح راستی که از پدر صادر می‌گردد، او بر من شهادت خواهد داد.۲۶
27 Inunso mudzandichitira umboni Ine, popeza mwakhala nane kuchokera pachiyambi.”
و شما نیزشهادت خواهید داد زیرا که از ابتدا با من بوده‌اید.۲۷

< Yohane 15 >