< Yohane 15 >

1 “Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate anga ndiye mwini munda.
Jeg er det sanne vintre, og min Fader er vingårdsmannen.
2 Iye amadula nthambi iliyonse ya mwa Ine imene sibala chipatso, koma nthambi iliyonse imene imabala chipatso amayisadzira bwino kuti ibale zipatso zambiri.
Hver gren på mig som ikke bærer frukt, den tar han bort, og hver den som bærer frukt, den renser han, forat den skal bære mere frukt.
3 Inu ndinu oyera kale chifukwa cha mawu amene ndayankhula inu.
I er alt rene på grunn av det ord som jeg har talt til eder;
4 Khalani mwa Ine, monga Ine ndili mwa inu. Palibe nthambi imene ingabereke chipatso pa yokha ngati sinalumikizike ku mpesa. Chomwechonso inu simungathe kubereka chipatso pokhapokha mutakhala mwa Ine.
bli i mig, så blir jeg i eder! Likesom grenen ikke kan bære frukt av sig selv, men bare når den blir i vintreet, således heller ikke I uten at I blir i mig.
5 “Ine ndine mpesa; inu ndinu nthambi zake. Ngati munthu akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye, adzabereka zipatso zambiri; popanda Ine simungathe kuchita kanthu.
Jeg er vintreet, I er grenene; den som blir i mig, og jeg i ham, han bærer megen frukt; for uten mig kan I intet gjøre.
6 Ngati wina aliyense sakhala mwa Ine, iyeyo ali ngati nthambi imene yatayidwa ndi kufota. Nthambi zotero zimatoledwa, kuponyedwa pa moto ndi kupsa.
Om nogen ikke blir i mig, da kastes han ut som en gren og visner, og de sankes sammen og kastes på ilden, og de brenner.
7 Ngati inu mukhala mwa Ine ndipo mawu anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene mukufuna ndipo mudzapatsidwa.
Dersom I blir i mig, og mine ord blir i eder, da bed om hvad I vil, og I skal få det.
8 Atate anga amalemekezedwa mukamabereka zipatso zochuluka, ndipo potero mudzionetsa kuti ndinu ophunzira anga.
Derved er min Fader herliggjort at I bærer megen frukt, og I skal bli mine disipler.
9 “Monga momwe Atate amandikondera Ine, Inenso ndakukondani. Tsopano khalani mʼchikondi changa.
Likesom Faderen har elsket mig, så har jeg elsket eder; bli i min kjærlighet!
10 Ngati mumvera malamulo anga, mudzakhala mʼchikondi changa, monga Ine ndimamvera malamulo a Atate anga, ndipo ndimakhala mʼchikondi chawo.
Dersom I holder mine bud, da blir I i min kjærlighet, likesom jeg har holdt min Faders bud og blir i hans kjærlighet.
11 Ine ndakuwuzani izi kuti chimwemwe changa chikhale mwa Inu, kuti chimwemwe chanu chikhale chokwanira.
Dette har jeg talt til eder forat min glede kan være i eder, og eders glede kan bli fullkommen.
12 Lamulo langa ndi ili: ‘Kondanani wina ndi mnzake monga Ine ndakonda inu.’
Dette er mitt bud at I skal elske hverandre, likesom jeg har elsket eder.
13 Palibe munthu ali ndi chikondi choposa ichi, choti munthu nʼkutaya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.
Ingen har større kjærlighet enn denne at han setter sitt liv til for sine venner;
14 Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene Ine ndikulamulani.
I er mine venner dersom I gjør det jeg byder eder.
15 Ine sindikutchulaninso antchito, chifukwa wantchito sadziwa zimene bwana wake akuchita. Mʼmalo mwake Ine ndakutchani abwenzi pakuti zilizonse zimene ndinaphunzira kwa Atate, Ine ndakudziwitsani.
Jeg kaller eder ikke lenger tjenere; for tjeneren vet ikke hvad hans herre gjør; men eder har jeg kalt venner, for alt det jeg har hørt av min Fader, har jeg kunngjort eder.
16 Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani kuti mupite ndi kukabereka zipatso, zipatso zake za nthawi yayitali. Choncho Atate adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
I har ikke utvalgt mig, men jeg har utvalgt eder, og jeg har satt eder til å gå ut og bære frukt, frukt som varer, forat Faderen skal gi eder alt det I beder ham om i mitt navn.
17 Lamulo langa ndi ili: ‘Muzikondana.’
Dette byder jeg eder at I skal elske hverandre.
18 “Ngati dziko lapansi lidana nanu, dziwani kuti linayamba kudana ndi Ine.
Når verden hater eder, da skal I vite at den har hatet mig før eder.
19 Inu mukanakhala anthu a dziko lapansi, dziko lapansi likanakukondani ngati anthu ake omwe. Koma mmene zilili, inu si anthu a dziko lapansi. Ine ndakusankhani kuchokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake dziko lapansi limakudani.
Var I av verden, da vilde verden elske sitt eget; men fordi I ikke er av verden, men jeg har utvalgt eder av verden, derfor hater verden eder.
20 Kumbukirani mawu amene ndinayankhula nanu akuti, ‘Palibe wantchito amene amaposa bwana wake.’ Ngati anandizunza Ine, iwo adzakuzunzaninso inu. Ngati anamvera chiphunzitso changa, iwo adzamvera chanunso.
Kom det ord i hu som jeg sa eder: En tjener er ikke større enn sin herre! Har de forfulgt mig, så skal de også forfølge eder; har de holdt mitt ord, så skal de også holde eders.
21 Iwo adzakuchitani zimenezi chifukwa cha dzina langa, popeza sakudziwa amene anandituma Ine.
Men alt dette skal de gjøre mot eder for mitt navns skyld, fordi de ikke kjenner ham som har sendt mig.
22 Ine ndikanapanda kubwera ndi kuyankhula nawo, sakanakhala ndi mlandu. Koma tsopano alibe choti nʼkukanira mlandu wawo.
Var jeg ikke kommet og hadde talt til dem, da hadde de ikke synd; men nu har de ingen undskyldning for sin synd.
23 Iye amene amadana ndi Ine amadananso Atate anga.
Den som hater mig, han hater også min Fader.
24 Ine ndikanapanda kuchita pakati pawo zinthu zimene wina aliyense sanachitepo, iwo sakanakhala ochimwa. Koma tsopano aona zodabwitsa izi, komabe akundida Ine pamodzi ndi Atate anga.
Hadde jeg ikke gjort de gjerninger blandt dem som ingen annen har gjort, da hadde de ikke synd; men nu har de sett dem og allikevel hatet både mig og min Fader.
25 Koma zatere kuti zikwaniritse zimene zinalembedwa mʼmalamulo awo: ‘Iwo anandida Ine popanda chifukwa.’
Men dette er skjedd forat det ord skal opfylles som er skrevet i deres lov: De hatet mig uten årsak.
26 “Nkhoswe ikadzabwera imene Ine ndidzakutumizireni kuchokera kwa Atate, ndiye Mzimu Woyera wachoonadi amene achokera kwa Atate, Iyeyo adzandichitira umboni Ine.
Når talsmannen kommer, som jeg skal sende eder fra Faderen, sannhetens Ånd, som utgår fra Faderen, han skal vidne om mig.
27 Inunso mudzandichitira umboni Ine, popeza mwakhala nane kuchokera pachiyambi.”
Men også I skal vidne; for I har vært med mig fra begynnelsen av.

< Yohane 15 >