< Yohane 15 >
1 “Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate anga ndiye mwini munda.
"I am the Vine--the True Vine, and my Father is the vine-dresser.
2 Iye amadula nthambi iliyonse ya mwa Ine imene sibala chipatso, koma nthambi iliyonse imene imabala chipatso amayisadzira bwino kuti ibale zipatso zambiri.
Every branch in me--if it bears no fruit, He takes away; and every branch that bears fruit He prunes, that it may bear more fruit.
3 Inu ndinu oyera kale chifukwa cha mawu amene ndayankhula inu.
Already you are cleansed--through the teaching which I have given you.
4 Khalani mwa Ine, monga Ine ndili mwa inu. Palibe nthambi imene ingabereke chipatso pa yokha ngati sinalumikizike ku mpesa. Chomwechonso inu simungathe kubereka chipatso pokhapokha mutakhala mwa Ine.
Continue in me, and let me continue in you. Just as the branch cannot bear fruit of itself--that is, if it does not continue in the vine--so neither can you if you do not continue in me.
5 “Ine ndine mpesa; inu ndinu nthambi zake. Ngati munthu akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye, adzabereka zipatso zambiri; popanda Ine simungathe kuchita kanthu.
I am the Vine, you are the branches. He who continues in me and in whom I continue bears abundant fruit, for apart from me you can do nothing.
6 Ngati wina aliyense sakhala mwa Ine, iyeyo ali ngati nthambi imene yatayidwa ndi kufota. Nthambi zotero zimatoledwa, kuponyedwa pa moto ndi kupsa.
If any one does not continue in me, he is like the unfruitful branch which is at once thrown away and then withers up. Such branches they gather up and throw into the fire and they are burned.
7 Ngati inu mukhala mwa Ine ndipo mawu anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene mukufuna ndipo mudzapatsidwa.
"If you continue in me and my sayings continue in you, ask what you will and it shall be done for you.
8 Atate anga amalemekezedwa mukamabereka zipatso zochuluka, ndipo potero mudzionetsa kuti ndinu ophunzira anga.
By this is God glorified--by your bearing abundant fruit and thus being true disciples of mine.
9 “Monga momwe Atate amandikondera Ine, Inenso ndakukondani. Tsopano khalani mʼchikondi changa.
As the Father has loved me, I have also loved you: continue in my love.
10 Ngati mumvera malamulo anga, mudzakhala mʼchikondi changa, monga Ine ndimamvera malamulo a Atate anga, ndipo ndimakhala mʼchikondi chawo.
If you obey my commands, you will continue in my love, as I have obeyed my Father's commands and continue in His love.
11 Ine ndakuwuzani izi kuti chimwemwe changa chikhale mwa Inu, kuti chimwemwe chanu chikhale chokwanira.
"These things I have spoken to you in order that I may have joy in you, and that your joy may become perfect.
12 Lamulo langa ndi ili: ‘Kondanani wina ndi mnzake monga Ine ndakonda inu.’
This is my commandment to you, to love one another as I have loved you.
13 Palibe munthu ali ndi chikondi choposa ichi, choti munthu nʼkutaya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.
No one has greater love than this--a man laying down his life for his friends.
14 Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene Ine ndikulamulani.
You are my friends, if you do what I command you.
15 Ine sindikutchulaninso antchito, chifukwa wantchito sadziwa zimene bwana wake akuchita. Mʼmalo mwake Ine ndakutchani abwenzi pakuti zilizonse zimene ndinaphunzira kwa Atate, Ine ndakudziwitsani.
No longer do I call you servants, because a servant does not know what his master is doing; but I have called you friends, because all that I have heard from the Father I have made known to you.
16 Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani kuti mupite ndi kukabereka zipatso, zipatso zake za nthawi yayitali. Choncho Atate adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
It is not you who chose me, but it is I who chose you and appointed you that you might go and be fruitful and that your fruit might remain; so that whatever petition you present to the Father in my name He may give you.
17 Lamulo langa ndi ili: ‘Muzikondana.’
"Thus I command you to love one another.
18 “Ngati dziko lapansi lidana nanu, dziwani kuti linayamba kudana ndi Ine.
If the world hates you, remember that it has first had me as the fixed object of its hatred.
19 Inu mukanakhala anthu a dziko lapansi, dziko lapansi likanakukondani ngati anthu ake omwe. Koma mmene zilili, inu si anthu a dziko lapansi. Ine ndakusankhani kuchokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake dziko lapansi limakudani.
If you belonged to the world, the world would love its own property. But because you do not belong to the world, and I have chosen you out of the world--for that reason the world hates you.
20 Kumbukirani mawu amene ndinayankhula nanu akuti, ‘Palibe wantchito amene amaposa bwana wake.’ Ngati anandizunza Ine, iwo adzakuzunzaninso inu. Ngati anamvera chiphunzitso changa, iwo adzamvera chanunso.
Bear in mind what I said to you, 'A servant is not superior to his master.' If they have persecuted me, they will also persecute you: if they have obeyed my teaching, they will obey yours also.
21 Iwo adzakuchitani zimenezi chifukwa cha dzina langa, popeza sakudziwa amene anandituma Ine.
But they will inflict all this suffering upon you on account of your bearing my name--because they do not know Him who sent me.
22 Ine ndikanapanda kubwera ndi kuyankhula nawo, sakanakhala ndi mlandu. Koma tsopano alibe choti nʼkukanira mlandu wawo.
"If I had not come and spoken to them, they would have had no sin; but as the case stands they are without excuse for their sin.
23 Iye amene amadana ndi Ine amadananso Atate anga.
He who hates me hates my Father also.
24 Ine ndikanapanda kuchita pakati pawo zinthu zimene wina aliyense sanachitepo, iwo sakanakhala ochimwa. Koma tsopano aona zodabwitsa izi, komabe akundida Ine pamodzi ndi Atate anga.
If I had not done among them, as I have, such miracles as no one else ever did, they would have had no sin; but they have in fact seen and also hated both me and my Father.
25 Koma zatere kuti zikwaniritse zimene zinalembedwa mʼmalamulo awo: ‘Iwo anandida Ine popanda chifukwa.’
But this has been so, in order that the saying may be fulfilled which stands written in their Law, 'They have hated me without any reason.'
26 “Nkhoswe ikadzabwera imene Ine ndidzakutumizireni kuchokera kwa Atate, ndiye Mzimu Woyera wachoonadi amene achokera kwa Atate, Iyeyo adzandichitira umboni Ine.
"When the Advocate is come whom I will send to you from the Father's presence--the Spirit of Truth who comes forth from the Father's presence--He will be a witness concerning me.
27 Inunso mudzandichitira umboni Ine, popeza mwakhala nane kuchokera pachiyambi.”
And you also are witnesses, because you have been with me from the first.