< Yohane 15 >

1 “Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate anga ndiye mwini munda.
"Jeg er det sande Vintræ, og min Fader er Vingårdsmanden.
2 Iye amadula nthambi iliyonse ya mwa Ine imene sibala chipatso, koma nthambi iliyonse imene imabala chipatso amayisadzira bwino kuti ibale zipatso zambiri.
Hver Gren på mig, som ikke bærer Frugt, den borttager han, og hver den, som bærer Frugt, renser han, for at den skal bære mere Frugt.
3 Inu ndinu oyera kale chifukwa cha mawu amene ndayankhula inu.
I ere allerede rene på Grund af det Ord, som jeg har talt til eder.
4 Khalani mwa Ine, monga Ine ndili mwa inu. Palibe nthambi imene ingabereke chipatso pa yokha ngati sinalumikizike ku mpesa. Chomwechonso inu simungathe kubereka chipatso pokhapokha mutakhala mwa Ine.
Bliver i mig, da bliver også jeg i eder. Ligesom Grenen ikke kan bære Frugt af sig selv, uden den bliver på Vintræet, således kunne I ikke heller, uden I blive i mig.
5 “Ine ndine mpesa; inu ndinu nthambi zake. Ngati munthu akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye, adzabereka zipatso zambiri; popanda Ine simungathe kuchita kanthu.
Jeg er Vintræet, I ere Grenene. Den, som bliver i mig, og jeg i ham, han bærer megen Frugt; thi uden mig kunne I slet intet gøre.
6 Ngati wina aliyense sakhala mwa Ine, iyeyo ali ngati nthambi imene yatayidwa ndi kufota. Nthambi zotero zimatoledwa, kuponyedwa pa moto ndi kupsa.
Om nogen ikke bliver i mig, han bliver udkastet som en Gren og visner; man sanker dem og kaster dem i Ilden, og de brændes.
7 Ngati inu mukhala mwa Ine ndipo mawu anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene mukufuna ndipo mudzapatsidwa.
Dersom I blive i mig, og mine Ord blive i eder, da beder, om hvad som helst I ville, og det skal blive eder til Del.
8 Atate anga amalemekezedwa mukamabereka zipatso zochuluka, ndipo potero mudzionetsa kuti ndinu ophunzira anga.
Derved er min Fader herliggjort, at I bære megen Frugt, og I skulle blive mine Disciple.
9 “Monga momwe Atate amandikondera Ine, Inenso ndakukondani. Tsopano khalani mʼchikondi changa.
Ligesom Faderen har elsket mig, så har også jeg elsket eder; bliver i min Kærlighed!
10 Ngati mumvera malamulo anga, mudzakhala mʼchikondi changa, monga Ine ndimamvera malamulo a Atate anga, ndipo ndimakhala mʼchikondi chawo.
Dersom I holde mine Befalinger, skulle I blive i min Kærlighed, ligesom jeg har holdt min Faders Befalinger og bliver i hans Kærlighed.
11 Ine ndakuwuzani izi kuti chimwemwe changa chikhale mwa Inu, kuti chimwemwe chanu chikhale chokwanira.
Dette har jeg talt til eder, for at min Glæde kan være i eder, og eders Glæde kan blive fuldkommen.
12 Lamulo langa ndi ili: ‘Kondanani wina ndi mnzake monga Ine ndakonda inu.’
Dette er min Befaling, at I skulle elske hverandre, ligesom jeg har elsket eder.
13 Palibe munthu ali ndi chikondi choposa ichi, choti munthu nʼkutaya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.
Større Kærlighed har ingen end denne, at han sætter sit Liv til for sine Venner.
14 Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene Ine ndikulamulani.
I ere mine Venner, dersom I gøre, hvad jeg befaler eder.
15 Ine sindikutchulaninso antchito, chifukwa wantchito sadziwa zimene bwana wake akuchita. Mʼmalo mwake Ine ndakutchani abwenzi pakuti zilizonse zimene ndinaphunzira kwa Atate, Ine ndakudziwitsani.
Jeg kalder eder ikke længere Tjenere; thi Tjeneren ved ikke, hvad hans Herre gør; men eder har jeg kaldt Venner; thi alt det, som jeg har hørt af min Fader, har jeg kundgjort eder.
16 Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani kuti mupite ndi kukabereka zipatso, zipatso zake za nthawi yayitali. Choncho Atate adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
I have ikke udvalgt mig, men jeg har udvalgt eder og sat eder til, at I skulle gå hen og bære Frugt, og eders Frugt skal blive ved, for at Faderen skal give eder, hvad som helst I bede ham om i mit Navn.
17 Lamulo langa ndi ili: ‘Muzikondana.’
Dette befaler jeg eder, at I skulle elske hverandre.
18 “Ngati dziko lapansi lidana nanu, dziwani kuti linayamba kudana ndi Ine.
Når Verden hader eder, da vid, at den har hadet mig førend eder.
19 Inu mukanakhala anthu a dziko lapansi, dziko lapansi likanakukondani ngati anthu ake omwe. Koma mmene zilili, inu si anthu a dziko lapansi. Ine ndakusankhani kuchokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake dziko lapansi limakudani.
Vare I af Verden, da vilde Verden elske sit eget; men fordi I ikke ere af Verden, men jeg har valgt eder ud af Verden, derfor hader Verden eder.
20 Kumbukirani mawu amene ndinayankhula nanu akuti, ‘Palibe wantchito amene amaposa bwana wake.’ Ngati anandizunza Ine, iwo adzakuzunzaninso inu. Ngati anamvera chiphunzitso changa, iwo adzamvera chanunso.
Kommer det Ord i Hu, som jeg har sagt eder: En Tjener er ikke større end sin Herre. Have de forfulgt mig, ville de også forfølge eder; have de holdt mit Ord, ville de også holde eders.
21 Iwo adzakuchitani zimenezi chifukwa cha dzina langa, popeza sakudziwa amene anandituma Ine.
Men alt dette ville de gøre imod eder for mit Navns Skyld, fordi de ikke kende den, som sendte mig.
22 Ine ndikanapanda kubwera ndi kuyankhula nawo, sakanakhala ndi mlandu. Koma tsopano alibe choti nʼkukanira mlandu wawo.
Dersom jeg ikke var kommen og havde talt til dem, havde de ikke Synd; men nu have de ingen Undskyldning for deres Synd.
23 Iye amene amadana ndi Ine amadananso Atate anga.
Den, som hader mig, hader også min Fader.
24 Ine ndikanapanda kuchita pakati pawo zinthu zimene wina aliyense sanachitepo, iwo sakanakhala ochimwa. Koma tsopano aona zodabwitsa izi, komabe akundida Ine pamodzi ndi Atate anga.
Havde jeg ikke gjort de Gerninger iblandt dem, som ingen anden har gjort, havde de ikke Synd; men nu have de set dem og dog hadet både mig og min Fader.
25 Koma zatere kuti zikwaniritse zimene zinalembedwa mʼmalamulo awo: ‘Iwo anandida Ine popanda chifukwa.’
Dog, det Ord, som er skrevet i deres Lov, må opfyldes: De hadede mig uforskyldt.
26 “Nkhoswe ikadzabwera imene Ine ndidzakutumizireni kuchokera kwa Atate, ndiye Mzimu Woyera wachoonadi amene achokera kwa Atate, Iyeyo adzandichitira umboni Ine.
Men når Talsmanden kommer, som jeg skal sende eder fra Faderen, Sandhedens Ånd, som udgår fra Faderen, da skal han vidne om mig.
27 Inunso mudzandichitira umboni Ine, popeza mwakhala nane kuchokera pachiyambi.”
Men også I skulle vidne; thi I vare med mig fra Begyndelsen."

< Yohane 15 >