< Yohane 15 >
1 “Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate anga ndiye mwini munda.
„Jsem kmen vinné révy a můj Otec je vinařem.
2 Iye amadula nthambi iliyonse ya mwa Ine imene sibala chipatso, koma nthambi iliyonse imene imabala chipatso amayisadzira bwino kuti ibale zipatso zambiri.
Odřezává plané výhonky a plodné očišťuje, aby nesly větší úrodu.
3 Inu ndinu oyera kale chifukwa cha mawu amene ndayankhula inu.
I vás očistil, a to mým poselstvím.
4 Khalani mwa Ine, monga Ine ndili mwa inu. Palibe nthambi imene ingabereke chipatso pa yokha ngati sinalumikizike ku mpesa. Chomwechonso inu simungathe kubereka chipatso pokhapokha mutakhala mwa Ine.
Zůstaňte ve spojení se mnou. Vždyť výhonek oddělený od kmene nemůže nést žádné ovoce; právě tak je to i s vámi.
5 “Ine ndine mpesa; inu ndinu nthambi zake. Ngati munthu akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye, adzabereka zipatso zambiri; popanda Ine simungathe kuchita kanthu.
Já jsem vinný kmen a vy jste výhonky. Proto jen v těsném spojení se mnou prožijete plodný život. Beze mne to nedokážete.
6 Ngati wina aliyense sakhala mwa Ine, iyeyo ali ngati nthambi imene yatayidwa ndi kufota. Nthambi zotero zimatoledwa, kuponyedwa pa moto ndi kupsa.
Kdo žije beze mne, bude jako planý výhonek odříznut, uschne a bude spálen.
7 Ngati inu mukhala mwa Ine ndipo mawu anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene mukufuna ndipo mudzapatsidwa.
Zůstanete-li se mnou spojeni a nepřestane-li na vás působit mé poselství, pak dostanete všechno, o co v modlitbě požádáte.
8 Atate anga amalemekezedwa mukamabereka zipatso zochuluka, ndipo potero mudzionetsa kuti ndinu ophunzira anga.
Když povedete plodný život jako moji učedníci, vzdáte tím čest Bohu.
9 “Monga momwe Atate amandikondera Ine, Inenso ndakukondani. Tsopano khalani mʼchikondi changa.
Miluji vás tak, jako mne miluje Otec.
10 Ngati mumvera malamulo anga, mudzakhala mʼchikondi changa, monga Ine ndimamvera malamulo a Atate anga, ndipo ndimakhala mʼchikondi chawo.
Jste-li se mnou spojeni poslušností mých příkazů, proudí do vás Boží láska jako životodárná míza. Právě tak jsem já spojen poslušností s Otcem a naplněn jeho láskou.
11 Ine ndakuwuzani izi kuti chimwemwe changa chikhale mwa Inu, kuti chimwemwe chanu chikhale chokwanira.
Raduji se z toho a chci, abyste se i vy mohli vždycky plně radovat.
12 Lamulo langa ndi ili: ‘Kondanani wina ndi mnzake monga Ine ndakonda inu.’
Přikazuji vám, abyste se vzájemně milovali tak, jako jsem já miloval vás.
13 Palibe munthu ali ndi chikondi choposa ichi, choti munthu nʼkutaya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.
Největší lásku přátelům prokáže ten, kdo za ně položí vlastní život.
14 Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene Ine ndikulamulani.
Zůstanete mými přáteli, budete-li jednat v souladu se mnou.
15 Ine sindikutchulaninso antchito, chifukwa wantchito sadziwa zimene bwana wake akuchita. Mʼmalo mwake Ine ndakutchani abwenzi pakuti zilizonse zimene ndinaphunzira kwa Atate, Ine ndakudziwitsani.
Nejste už mými sluhy, protože sluha se nevyzná v úmyslu svého pána. Řekl jsem vám s důvěrou vše, co vím od Otce, a proto jste se stali mými přáteli.
16 Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani kuti mupite ndi kukabereka zipatso, zipatso zake za nthawi yayitali. Choncho Atate adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
Já jsem si vybral vás, ne vy mne. Vybavil jsem vás k tomu, abyste žili plodný život, který by před Bohem obstál. Proste a Otec vám to dá.
17 Lamulo langa ndi ili: ‘Muzikondana.’
Usilujte především o vzájemnou lásku.
18 “Ngati dziko lapansi lidana nanu, dziwani kuti linayamba kudana ndi Ine.
Lidé vás budou nenávidět, ale vzpomeňte si, že mne nenáviděli dříve než vás.
19 Inu mukanakhala anthu a dziko lapansi, dziko lapansi likanakukondani ngati anthu ake omwe. Koma mmene zilili, inu si anthu a dziko lapansi. Ine ndakusankhani kuchokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake dziko lapansi limakudani.
Milovali by vás, kdybyste se přizpůsobili. Vy mezi ně ale nepatříte, protože já jsem si vás vyvolil. Vyvedl jsem vás ze světa a oni vás za to nenávidí.
20 Kumbukirani mawu amene ndinayankhula nanu akuti, ‘Palibe wantchito amene amaposa bwana wake.’ Ngati anandizunza Ine, iwo adzakuzunzaninso inu. Ngati anamvera chiphunzitso changa, iwo adzamvera chanunso.
Připomeňte si slova, která jsem vám už jednou řekl: sluha není větší než jeho pán. Jestliže pronásledují mne, jak by nepronásledovali vás! Když chytali za slovo mne, budou číhat i na vás.
21 Iwo adzakuchitani zimenezi chifukwa cha dzina langa, popeza sakudziwa amene anandituma Ine.
To všechno vám budou dělat proto, že nevěří, že za mnou i za vámi stojí Bůh.
22 Ine ndikanapanda kubwera ndi kuyankhula nawo, sakanakhala ndi mlandu. Koma tsopano alibe choti nʼkukanira mlandu wawo.
Kdybych byl nepřišel a nemluvil k nim, byli by bez viny. Teď jsou však bez výmluvy.
23 Iye amene amadana ndi Ine amadananso Atate anga.
Ti, kdo mnou pohrdají, pohrdají Bohem.
24 Ine ndikanapanda kuchita pakati pawo zinthu zimene wina aliyense sanachitepo, iwo sakanakhala ochimwa. Koma tsopano aona zodabwitsa izi, komabe akundida Ine pamodzi ndi Atate anga.
Usvědčuje je moje dílo, které nemá obdoby. Mají je před očima, a přece se zatvrdili proti mně i Otci. Však je o nich psáno v Písmu: ‚Nenáviděli mne bez důvodu.‘
25 Koma zatere kuti zikwaniritse zimene zinalembedwa mʼmalamulo awo: ‘Iwo anandida Ine popanda chifukwa.’
26 “Nkhoswe ikadzabwera imene Ine ndidzakutumizireni kuchokera kwa Atate, ndiye Mzimu Woyera wachoonadi amene achokera kwa Atate, Iyeyo adzandichitira umboni Ine.
Pošlu vám zastánce od Otce – Ducha pravdy, který pochází z Otce. Ten dosvědčí, co vám říkám.
27 Inunso mudzandichitira umboni Ine, popeza mwakhala nane kuchokera pachiyambi.”
Ale i vy budete mými svědky, protože mne všude provázíte.