< Yohane 14 >
1 “Mtima wanu usavutike. Khulupirirani Mulungu; khulupirirani Inenso.
Let not your heart be troubled. Have faith in God, and have faith in me.
2 Mʼnyumba mwa Atate anga muli zipinda zambiri. Kukanakhala kuti mulibemo ndikanakuwuzani. Ine ndikupita kumeneko kukakukonzerani malo.
In my Father's house are many mansions; if it were not so, I would have told you. For I go away to prepare a place for you;
3 Ndipo ndikapita kukakukonzerani malo, ndidzabweranso kudzakutengani, kuti kumene kuli Ineko, inunso mukakhale komweko.
and when I have gone away and prepared a place for you, I will come again, and will take you to myself; that where I am, ye also may be.
4 Inu mukudziwa njira ya kumene Ine ndikupita.”
And ye know the way whither I go.
5 Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye ife sitikudziwa kumene Inu mukupita, nanga tingadziwe bwanji njirayo?”
Thomas saith to him, Lord, we know not whither thou goest; how then do we know the way?
6 Yesu anayankha kuti, “Ine ndine njira, choonadi ndi moyo. Palibe munthu angafike kwa Atate popanda kudzera mwa Ine.
Jesus saith to him, I am the way, and the truth, and the life; no one cometh to the Father but through me.
7 Mukanandidziwadi Ine, mukanadziwanso Atate anga. Kuyambira tsopano, mukuwadziwa ndipo mwawaona.”
If ye knew me, ye would know my Father also; and from this time ye know him, and have seen him.
8 Filipo anati, “Ambuye, tionetseni Atatewo ndipo ife tikhutitsidwa.”
Philip saith to him, Lord, show us the Father, and we shall be satisfied.
9 Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe Filipo, ndakhala pakati panu nthawi yonseyi ndipo iwe sukundidziwabe? Aliyense amene waona Ine, waonanso Atate. Tsono ukunena bwanji kuti, ‘Tionetseni Atate?’
Jesus saith to him, Have I been so long time with you, and dost thou not know me, Philip? He that hath seen me hath seen the Father; how is it that thou sayest, Show us the Father?
10 Kodi sukukhulupirira kuti Ine ndili mwa Atate, ndipo Atate ali mwa Ine? Mawu amene Ine ndiyankhula kwa inu si mawu anga okha koma ndi mawu Atate wokhala mwa Ine, amene akugwira ntchito yake.
Dost thou not believe that I am in the Father, and the Father in me? The words that I speak to you, I speak not from myself; but the Father, who dwelleth in me, doeth his works.
11 Khulupirirani Ine pamene ndi kuti Ine ndili mwa Atate ndipo Atate ali mwa Ine. Koma ngati si chomwecho, khulupiriranitu Ine chifukwa cha ntchito zanga zodabwitsa.
Believe me, that I am in the Father, and the Father in me; but if not, believe for the very works' sake.
12 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene akhulupirira Ine adzachita zimene Ine ndakhala ndikuchita. Iye adzachita ngakhale zinthu zazikulu kuposa zimenezi, chifukwa ndikupita kwa Atate.
Truly, truly do I say to you, He that believeth in me, the works that I do shall he do also, and greater than these shall he do; because I am going to the Father,
13 Ndipo Ine ndidzachita chilichonse chimene inu mudzapempha mʼdzina langa kuti Atate alemekezedwe mwa Mwana.
and whatever ye shall ask in my name, that will I do; that the Father may be glorified in the Son.
14 Ngati mudzapempha kanthu kalikonse mʼdzina langa, Ine ndidzachita.
If ye shall ask any thing in my name, I will do it.
15 “Ngati mundikonda Ine, sungani malamulo anga.
If ye love me, ye will keep my commandments;
16 Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina kuti izikhala nanu nthawi zonse. (aiōn )
and I will pray the Father, and he will give you another Comforter, that he may be with you for ever; (aiōn )
17 Nkhosweyo ndiye Mzimu wachoonadi. Dziko lapansi silingalandire Nkhosweyi chifukwa samuona kapena kumudziwa. Koma inu mumamudziwa pakuti amakhala nanu ndipo adzakhala mwa inu.
the Spirit of truth, which the world cannot receive, because it doth not behold it, nor know it; ye know it, because it abideth with you, and will be in you.
18 Ine sindikusiyani nokha kuti mukhale ana amasiye. Ine ndidzabweranso kwa inu.
I will not leave you bereaved; I am coming to you.
19 Patsala nthawi yochepa dziko lapansi silidzandionanso koma inu mudzandiona. Popeza kuti Ine ndili ndi moyo, inunso mudzakhala ndi moyo.
Yet a little while, and the world beholdeth me no more; but ye will behold me, because I live, and ye will live.
20 Tsiku limenelo inu mudzazindikira kuti Ine ndili mwa Atate, ndipo inu muli mwa Ine, ndipo Ine ndili mwa inu.
In that day ye will know that I am in my Father, and ye in me, and I in you.
21 Iye amene amadziwa malamulo anga ndi kuwasunga ndiye amene amandikonda. Wokonda Ine adzakondedwa ndi Atate wanga ndipo Inenso ndidzamukonda ndikudzionetsa ndekha kwa iye.”
He that hath my commandments and keepeth them, he it is that loveth me; and he that loveth me will be loved by my Father; and I will love him, and will manifest myself to him.
22 Kenaka Yudasi (osati Yudasi Isikarioti) anati, “Koma Ambuye, nʼchifukwa chiyani mukufuna kudzionetsa nokha kwa ife, osati ku dziko lapansi?”
Judas, not Iscariot, saith to him, And how is it, Lord, that thou art going to manifest thyself to us, and not to the world?
23 Yesu anamuyankha kuti, “Ngati wina aliyense andikonda Ine, adzasunga mawu anga. Atate wanga adzamukonda, ndipo Ife tidzabwera ndi kukhala naye.
Jesus answered and said to him, If any one loveth me, he will keep my word; and my Father will love him, and we will come to him, and make our abode with him.
24 Iye amene sandikonda Ine sasunga mawu anga. Mawu awa amene mukumva si anga ndi a Atate amene anandituma Ine.
He that loveth me not, keepeth not my words; and the word which ye hear is not mine, but the Father's who sent me.
25 “Ndayankhula zonsezi ndikanali nanu.
These things have I spoken to you, while abiding with you;
26 Koma Nkhosweyo, Mzimu Woyera, amene Atate adzamutumiza mʼdzina langa adzakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo adzakukumbutsani zonse zimene ndinakuwuzani.
but the Comforter, the Holy Spirit which the Father will send in my name, he will teach you all things, and bring to your remembrance all things which I have said to you.
27 Ine ndikukusiyirani mtendere. Ndikukupatsani mtendere wanga. Ine sindikukupatsani monga dziko lapansi limaperekera. Mtima wanu usavutike ndipo musachite mantha.
Peace I leave with you; my peace I give to you; not as the world giveth, do I give to you. Let not your heart be troubled, nor let it be afraid.
28 “Inu munamva Ine ndikunena kuti, ‘Ine ndikupita ndipo ndidzabweranso kwa inu.’ Mukanandikonda, mukanasangalala kuti Ine ndikupita kwa Atate, pakuti Atate ndi wamkulu kuposa Ine.
Ye heard me say to you, I am going away, and am coming again to you. If ye loved me, ye would have rejoiced that I go to the Father; for the Father is greater than I.
29 Ine ndakuwuzani tsopano zisanachitike, kuti zikadzachitika mudzakhulupirire.
And now I have told you before it hath come to pass, that when it hath come to pass ye may believe.
30 Ine sindiyankhulanso nanu zambiri nthawi yayitali popeza wolamulira dziko lapansi akubwera. Iye alibe mphamvu pa Ine,
I shall not talk much more with you. For the prince of the world cometh, and hath nothing in me.
31 koma kuti dziko lapansi lizindikire kuti Ine ndimakonda Atate ndi kuti ndimachita zokhazokha zimene Atate wandilamulira Ine. “Nyamukani; tizipita.”
But [[this must be]] that the world may know that I love the Father, and that as the Father gave me commandment so I do. Arise, let us go hence.