< Yohane 13 >

1 Inali pafupifupi nthawi ya phwando la Paska. Yesu anadziwa kuti nthawi yafika yoti achoke mʼdziko lapansi ndi kupita kwa Atate. Atawakonda ake amene anali mʼdziko lapansi, Iye anawaonetsa chikondi chake chonse.
before then the/this/who festival the/this/who Passover lamb to know the/this/who Jesus that/since: that (to come/go *N(k)O*) it/s/he the/this/who hour in order that/to to depart out from the/this/who world this/he/she/it to/with the/this/who father to love the/this/who one's own/private the/this/who in/on/among the/this/who world toward goal/tax to love it/s/he
2 Atayamba kudya mgonero, mdierekezi anali atalowa kale mu mtima wa Yudasi Isikarioti mwana wa Simoni, kuti amupereke Yesu.
and dinner (to be *N(k)O*) the/this/who devilish/the Devil already to throw: put toward the/this/who heart in order that/to to deliver it/s/he (Judas *N(k)O*) Simon (Iscariot *NK(o)*)
3 Yesu podziwa kuti Atate anamupatsa Iye zonse mʼmanja mwake, ndi kuti Iye anachokera kwa Mulungu ndipo amabwerera kwa Mulunguyo;
to know (the/this/who *k*) (Jesus *K*) that/since: that all (to give *N(k)O*) it/s/he the/this/who father toward the/this/who hand and that/since: that away from God to go out and to/with the/this/who God to go
4 anayimirira kuchoka pa chakudya navula zovala zake natenga nsalu yopukutira nadzimanga mʼchiwuno mwake.
to arise out from the/this/who dinner and to place the/this/who clothing and to take towel to tie around themself
5 Atachita izi, anathira madzi mʼbeseni ndi kuyamba kusambitsa mapazi a ophunzira ake, ndi kuwapukuta ndi chopukutira chimene anachimanga mʼchiwuno mwake.
then to throw: pour water toward the/this/who wash basin and be first to wash the/this/who foot the/this/who disciple and to wipe off the/this/who towel which to be to tie around
6 Atafika pa Petro, Petroyo anati kwa Iye, “Ambuye, kodi mudzandisambitsa mapazi anga?”
to come/go therefore/then to/with Simon Peter (and *k*) to say it/s/he (that *ko*) lord: God you me to wash the/this/who foot
7 Yesu anayankha kuti, “Iwe sukuzindikira tsopano chimene ndikuchita, koma udzazindikira mʼtsogolo.”
to answer Jesus and to say it/s/he which I/we to do/make: do you no to know now to know then with/after this/he/she/it
8 Petro anati, “Ayi, Inu simudzandisambitsa konse mapazi anga.” Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine sindisambitsa mapazi ako, ulibe gawo mwa Ine.” (aiōn g165)
to say it/s/he Peter no not to wash me the/this/who foot toward the/this/who an age: eternity to answer (the/this/who *k*) Jesus it/s/he if not to wash you no to have/be part with/after I/we (aiōn g165)
9 Simoni Petro anayankha kuti, “Ambuye, osati mapazi okha komanso manja anga ndi mutu wanga womwe!”
to say it/s/he Simon Peter lord: God not the/this/who foot me alone but and the/this/who hand and the/this/who head
10 Yesu anayankha kuti, “Munthu amene wasamba amangofunika kusamba mapazi ake okha chifukwa thupi lake lonse ndi loyera. Ndipo inu ndinu oyera, ngakhale kuti si aliyense mwa inu.”
to say it/s/he the/this/who Jesus the/this/who to wash no to have/be need (if: not *no*) (not *N(K)O*) the/this/who foot to wash but to be clean all and you clean to be but not! all
11 Pakuti Iye anadziwa amene adzamupereka, ndipo nʼchifukwa chake anati saliyense wa inu ali woyera.
to perceive: know for the/this/who to deliver it/s/he through/because of this/he/she/it to say (that/since: that *no*) not! all clean to be
12 Iye atamaliza kusambitsa mapazi awo anavala zovala zake ndi kubwerera pamalo pake. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuzindikira zimene ndakuchitirani inu?
when therefore/then to wash the/this/who foot it/s/he and to take the/this/who clothing it/s/he and (to recline *N(k)O*) again to say it/s/he to know which? to do/make: do you
13 Inu mumanditcha Ine, ‘Mphunzitsi’ ndi ‘Mbuye,’ ndipo mumakhoza mukamatero, pakuti ichi ndi chimene Ine ndili.
you to call me the/this/who teacher and the/this/who lord: God and well to say to be for
14 Tsono ngati Ine, Mbuye wanu ndi Mphunzitsi wanu, ndasambitsa mapazi anu, inunso muyenera kusambitsana mapazi anu.
if therefore/then I/we to wash you the/this/who foot the/this/who lord: God and the/this/who teacher and you to owe one another to wash the/this/who foot
15 Ine ndakupatsani chitsanzo kuti muzichita monga Ine ndachitira.
example for to give you in order that/to as/just as I/we to do/make: do you and you to do/make: do
16 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti wantchito saposa mbuye wake, kapena wotumidwa kuposa amene wamutuma.
amen amen to say you no to be slave great the/this/who lord: master it/s/he nor apostle great the/this/who to send it/s/he
17 Ngati inu mudziwa zinthu zimenezi, mudzakhala odala mukamazichita.
if this/he/she/it to know blessed to be if to do/make: do it/s/he
18 “Ine sindikunena za inu nonse. Ine ndikudziwa amene ndinawasankha. Koma izi zikukwaniritsa malemba: ‘Iye amene akudya nawo chakudya changa, ndiye amene anandiwukira.’
no about all you to say I/we to know (which? *N(k)O*) to select but in order that/to the/this/who a writing to fulfill the/this/who to eat (with/after *k*) (me *N(k)O*) the/this/who bread to lift up upon/to/against I/we the/this/who heel it/s/he
19 “Ine ndikukuwuzani tsopano zisanachitike zimenezi, kuti pamene zachitika, mudzakhulupirire kuti Ine Ndine.
away from now to say you before the/this/who to be in order that/to (to trust (in) *NK(o)*) when(-ever) to be that/since: that I/we to be
20 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene alandira amene Ine ndamutuma, alandiranso Ine. Aliyense amene alandira Ine, alandiranso amene anandituma.”
amen amen to say you the/this/who to take (if *N(k)O*) one to send I/we to take the/this/who then I/we to take to take the/this/who to send me
21 Yesu atanena izi, anavutika kwambiri mu mzimu ndipo anachitira umboni kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mmodzi mwa inu adzandipereka.”
this/he/she/it to say the/this/who Jesus to trouble the/this/who spirit/breath: spirit and to testify and to say amen amen to say you that/since: that one out from you to deliver me
22 Ophunzira ake anapenyetsetsana wina ndi mnzake, posadziwa kuti amanena za yani.
to see (therefore/then *KO*) toward one another the/this/who disciple be perplexed about which? to say
23 Mmodzi wa ophunzira ake amene Yesu anamukonda, anali atatsamira pachifuwa chake.
to be (then *k*) to recline one (out from *no*) the/this/who disciple it/s/he in/on/among the/this/who bosom the/this/who Jesus which to love the/this/who Jesus
24 Simoni Petro anamukodola wophunzirayo ndi kuti, “Mufunseni akunena za yani.”
to motion therefore/then this/he/she/it Simon Peter (and to say it/s/he *o*) (to inquire *NK(o)*) which? if (to be *NK(o)*) about which to say
25 Atamutsamiranso Yesuyo, anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndani?”
(to recline therefore/then *N(k)O*) that (thus(-ly) *NO*) upon/to/against the/this/who chest the/this/who Jesus to say it/s/he lord: God which? to be
26 Yesu anayankha kuti, “Iye amene ndidzamupatsa buledi amene ndanyema ndikususa ndi ameneyo.” Kenaka, atasunsa gawo la buledi, Iye anapereka kwa Yudasi Isikarioti, mwana wa Simoni.
to answer (therefore/then *O*) the/this/who Jesus that to be which I/we (to dip *N(k)O*) the/this/who piece (and *no*) (to give *N(k)O*) (it/s/he *no*) (and *k*) (to dip *N(k)O*) (therefore/then *NO*) the/this/who piece (to take and *NO*) to give Judas Simon (Iscariot *N(k)O*)
27 Nthawi yomweyo Yudasi atangodya bulediyo, Satana analowa mwa Iye. Yesu anamuwuza Iye kuti, “Chomwe ukufuna kuchita, chita msanga.”
and with/after the/this/who piece then to enter toward that the/this/who Satan to say therefore/then it/s/he the/this/who Jesus which to do/make: do to do/make: do quicker
28 Koma panalibe ndi mmodzi yemwe pa chakudyapo amene anamvetsa chifukwa chimene Yesu ananenera izi kwa iye.
this/he/she/it then none to know the/this/who to recline to/with which? to say it/s/he
29 Popeza Yudasi amasunga ndalama, ena amaganiza kuti Yesu amamuwuza iye kuti akagule zomwe zimafunika pa phwando, kapena kukapereka kanthu kena kake kwa osauka.
one for to think since the/this/who moneybag to have/be (the/this/who *k*) Judas that/since: since to say it/s/he the/this/who Jesus to buy which need to have/be toward the/this/who festival or the/this/who poor in order that/to one to give
30 Nthawi yomweyo Yudasi atangodya buledi, anatuluka, ndipo unali usiku.
to take therefore/then the/this/who piece that to go out immediately to be then night
31 Yudasi atatuluka, Yesu anati, “Tsopano Mwana wa Munthu walemekezedwa, ndipo mwa Iyeyu Mulungu walemekezedwanso.
when therefore/then to go out to say (the/this/who *k*) Jesus now to glorify the/this/who son the/this/who a human and the/this/who God to glorify in/on/among it/s/he
32 Ngati Mulungu walemekezedwa mwa Iye, Mulungu mwini adzalemekezanso Mwana, ndipo amulemekeza nthawi yomweyo.
if the/this/who God to glorify in/on/among it/s/he and the/this/who God to glorify it/s/he in/on/among (it/s/he *N(k)O*) and immediately to glorify it/s/he
33 “Ana anga, Ine ndikhala nanu kwa nthawi yochepa chabe. Inu mudzandifunafuna Ine, ndipo monga momwe ndinawawuzira Ayuda, choncho Ine ndikukuwuzani tsopano kuti, kumene Ine ndikupita, inu simungabwereko.
children still small with/after you to be to seek me and as/just as to say the/this/who Jew that/since: that where(-ever) I/we to go you no be able to come/go and you to say now
34 “Lamulo latsopano limene ndikukupatsani ndi lakuti: Kondanani wina ndi mnzake, monga momwe Ine ndinakonda inu. Nanunso mukondane wina ndi mnzake.
commandment new to give you in order that/to to love one another as/just as to love you in order that/to and you to love one another
35 Mukamakondana aliyense adzadziwa kuti ndinu ophunzira anga.”
in/on/among this/he/she/it to know all that/since: that I/we disciple to be if love to have/be in/on/among one another
36 Simoni Petro anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukupita kuti?” Yesu anayankha kuti, “Kumene Ine ndikupita iwe sunganditsatire tsopano, koma udzanditsatira mʼtsogolo.”
to say it/s/he Simon Peter lord: God where? to go to answer it/s/he (the/this/who *k*) Jesus where(-ever) to go no be able me now to follow to follow then later (me *k*)
37 Petro anafunsa kuti, “Ambuye, nʼchifukwa chiyani ine sindingakutsatireni tsopano? Ine ndidzapereka moyo wanga chifukwa cha Inu.”
to say it/s/he the/this/who Peter lord: God through/because of which? no be able you (to follow *NK(o)*) now the/this/who soul: life me above/for you to place
38 Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe udzalolera kutaya moyo chifukwa cha Ine? Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti tambala asanalire, iwe udzandikana katatu!”
(to answer *N(k)O*) (it/s/he the/this/who *k*) Jesus the/this/who soul: life you above/for I/we to place amen amen to say you no not rooster (to call *N(k)O*) until which (to deny *N(k)O*) me three times

< Yohane 13 >