< Yohane 13 >

1 Inali pafupifupi nthawi ya phwando la Paska. Yesu anadziwa kuti nthawi yafika yoti achoke mʼdziko lapansi ndi kupita kwa Atate. Atawakonda ake amene anali mʼdziko lapansi, Iye anawaonetsa chikondi chake chonse.
Men før Påskehøjtiden, da Jesus vidste, at hans Time var kommen, til at han skulde gå bort fra denne Verden til Faderen, da, ligesom han havde elsket sine egne, som vare i Verden, så elskede han dem indtil Enden.
2 Atayamba kudya mgonero, mdierekezi anali atalowa kale mu mtima wa Yudasi Isikarioti mwana wa Simoni, kuti amupereke Yesu.
Og medens der holdtes Aftensmåltid, da Djævelen allerede havde indskudt i Judas's, Simons Søns, Iskariots Hjerte, at han skulde forråde ham;
3 Yesu podziwa kuti Atate anamupatsa Iye zonse mʼmanja mwake, ndi kuti Iye anachokera kwa Mulungu ndipo amabwerera kwa Mulunguyo;
da Jesus vidste, at Faderen havde givet ham alle Ting i Hænde, og at han var udgået fra Gud og gik hen til Gud:
4 anayimirira kuchoka pa chakudya navula zovala zake natenga nsalu yopukutira nadzimanga mʼchiwuno mwake.
så rejser han sig fra Måltidet og lægger sine Klæder fra sig, og han tog et Linklæde og bandt det om sig.
5 Atachita izi, anathira madzi mʼbeseni ndi kuyamba kusambitsa mapazi a ophunzira ake, ndi kuwapukuta ndi chopukutira chimene anachimanga mʼchiwuno mwake.
Derefter hælder han Vand i Vaskefadet og begyndte at to Disciplenes Fødder og at tørre dem med Linklædet, som han var ombunden med.
6 Atafika pa Petro, Petroyo anati kwa Iye, “Ambuye, kodi mudzandisambitsa mapazi anga?”
Han kommer da til Simon Peter; og denne siger til ham: "Herre! tor du mine Fødder?"
7 Yesu anayankha kuti, “Iwe sukuzindikira tsopano chimene ndikuchita, koma udzazindikira mʼtsogolo.”
Jesus svarede og sagde til ham: "Hvad jeg gør, ved du ikke nu, men du skal forstå det siden efter."
8 Petro anati, “Ayi, Inu simudzandisambitsa konse mapazi anga.” Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine sindisambitsa mapazi ako, ulibe gawo mwa Ine.” (aiōn g165)
Peter siger til ham: "Du skal i al Evighed ikke to mine Fødder." Jesus svarede ham: "Dersom jeg ikke tor dig, har du ikke Lod sammen med mig." (aiōn g165)
9 Simoni Petro anayankha kuti, “Ambuye, osati mapazi okha komanso manja anga ndi mutu wanga womwe!”
Simon Peter siger til ham: "Herre! ikke mine Fødder alene, men også Hænderne og Hovedet."
10 Yesu anayankha kuti, “Munthu amene wasamba amangofunika kusamba mapazi ake okha chifukwa thupi lake lonse ndi loyera. Ndipo inu ndinu oyera, ngakhale kuti si aliyense mwa inu.”
Jesus siger til ham: "Den, som er tvættet, har ikke nødig at to andet end Fødderne, men er ren over det hele; og I ere rene, men ikke alle."
11 Pakuti Iye anadziwa amene adzamupereka, ndipo nʼchifukwa chake anati saliyense wa inu ali woyera.
Thi han kendte den, som forrådte ham; derfor sagde han: "I ere ikke alle rene."
12 Iye atamaliza kusambitsa mapazi awo anavala zovala zake ndi kubwerera pamalo pake. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuzindikira zimene ndakuchitirani inu?
Da han nu havde toet deres Fødder og havde taget sine Klæder og atter sat sig til Bords, sagde han til dem: "Vide I, hvad jeg har gjort ved eder?
13 Inu mumanditcha Ine, ‘Mphunzitsi’ ndi ‘Mbuye,’ ndipo mumakhoza mukamatero, pakuti ichi ndi chimene Ine ndili.
I kalde mig Mester og Herre, og I tale ret, thi jeg er det.
14 Tsono ngati Ine, Mbuye wanu ndi Mphunzitsi wanu, ndasambitsa mapazi anu, inunso muyenera kusambitsana mapazi anu.
Når da jeg, Herren og Mesteren, har toet eders Fødder, så ere også I skyldige at to hverandres Fødder.
15 Ine ndakupatsani chitsanzo kuti muzichita monga Ine ndachitira.
Thi jeg har givet eder et Eksempel, for at, ligesom jeg gjorde ved eder, skulle også I gøre.
16 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti wantchito saposa mbuye wake, kapena wotumidwa kuposa amene wamutuma.
Sandelig, sandelig, siger jeg eder, en Tjener er ikke større end sin Herre, ikke heller et Sendebud større end den, som har sendt ham.
17 Ngati inu mudziwa zinthu zimenezi, mudzakhala odala mukamazichita.
Når I vide dette, ere I salige, om I gøre det.
18 “Ine sindikunena za inu nonse. Ine ndikudziwa amene ndinawasankha. Koma izi zikukwaniritsa malemba: ‘Iye amene akudya nawo chakudya changa, ndiye amene anandiwukira.’
Jeg taler ikke om eder alle; jeg ved, hvilke jeg har udvalgt; men Skriften måtte opfyldes: Den, som æder Brødet med mig, har opløftet sin Hæl imod mig.
19 “Ine ndikukuwuzani tsopano zisanachitike zimenezi, kuti pamene zachitika, mudzakhulupirire kuti Ine Ndine.
Fra nu af siger jeg eder det, førend det sker, for at I, når det er sket, skulle tro, at det er mig.
20 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene alandira amene Ine ndamutuma, alandiranso Ine. Aliyense amene alandira Ine, alandiranso amene anandituma.”
Sandelig, sandelig, siger jeg eder, den, som modtager, hvem jeg sender, modtager mig; men den, som modtager mig, modtager ham, som har sendt mig."
21 Yesu atanena izi, anavutika kwambiri mu mzimu ndipo anachitira umboni kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mmodzi mwa inu adzandipereka.”
Da Jesus havde sagt dette, blev han heftigt bevæget i Ånden og vidnede og sagde: "Sandelig, sandelig, siger jeg eder, en af eder vil forråde mig."
22 Ophunzira ake anapenyetsetsana wina ndi mnzake, posadziwa kuti amanena za yani.
Da så Disciplene på hverandre, tvivlrådige om, hvem han talte om.
23 Mmodzi wa ophunzira ake amene Yesu anamukonda, anali atatsamira pachifuwa chake.
Men der var en iblandt hans Disciple, som sad til Bords ved Jesu Side, han, hvem Jesus elskede.
24 Simoni Petro anamukodola wophunzirayo ndi kuti, “Mufunseni akunena za yani.”
Til denne nikker da Simon Peter og siger til ham: "Sig, hvem det er, han taler om?"
25 Atamutsamiranso Yesuyo, anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndani?”
Men denne bøjer sig op til Jesu Bryst og siger til ham: "Herre! hvem er det?"
26 Yesu anayankha kuti, “Iye amene ndidzamupatsa buledi amene ndanyema ndikususa ndi ameneyo.” Kenaka, atasunsa gawo la buledi, Iye anapereka kwa Yudasi Isikarioti, mwana wa Simoni.
Jesus svarer: "Det er den, hvem jeg giver det Stykke Brød, som jeg dypper." Så dypper han Stykket og tager og giver det til Judas, Simons Søn, Iskariot.
27 Nthawi yomweyo Yudasi atangodya bulediyo, Satana analowa mwa Iye. Yesu anamuwuza Iye kuti, “Chomwe ukufuna kuchita, chita msanga.”
Og efter at han havde fået Stykket, da gik Satan ind i ham. Så siger Jesus til ham: "Hvad du gør, gør det snart!"
28 Koma panalibe ndi mmodzi yemwe pa chakudyapo amene anamvetsa chifukwa chimene Yesu ananenera izi kwa iye.
Men ingen af dem, som sade til Bords, forstod, hvorfor han sagde ham dette.
29 Popeza Yudasi amasunga ndalama, ena amaganiza kuti Yesu amamuwuza iye kuti akagule zomwe zimafunika pa phwando, kapena kukapereka kanthu kena kake kwa osauka.
Thi nogle mente, efterdi Judas havde Pungen, at Jesus sagde til ham: "Køb, hvad vi have nødig til Højtiden;" eller at han skulde give noget til de fattige.
30 Nthawi yomweyo Yudasi atangodya buledi, anatuluka, ndipo unali usiku.
Da han nu havde fået Stykket, gik han straks ud. Men det var Nat.
31 Yudasi atatuluka, Yesu anati, “Tsopano Mwana wa Munthu walemekezedwa, ndipo mwa Iyeyu Mulungu walemekezedwanso.
Da han nu var gået ud, siger Jesus: "Nu er Menneskesønnen herliggjort, og Gud er herliggjort i ham.
32 Ngati Mulungu walemekezedwa mwa Iye, Mulungu mwini adzalemekezanso Mwana, ndipo amulemekeza nthawi yomweyo.
Dersom Gud er herliggjort i ham, skal Gud også herliggøre ham i sig, og han skal snart herliggøre ham.
33 “Ana anga, Ine ndikhala nanu kwa nthawi yochepa chabe. Inu mudzandifunafuna Ine, ndipo monga momwe ndinawawuzira Ayuda, choncho Ine ndikukuwuzani tsopano kuti, kumene Ine ndikupita, inu simungabwereko.
Børnlille! endnu en liden Stund er jeg hos eder. I skulle lede efter mig, og ligesom jeg sagde til Jøderne: "Hvor jeg går hen, kunne I ikke komme," siger jeg nu også til eder.
34 “Lamulo latsopano limene ndikukupatsani ndi lakuti: Kondanani wina ndi mnzake, monga momwe Ine ndinakonda inu. Nanunso mukondane wina ndi mnzake.
Jeg giver eder en ny Befaling, at I skulle elske hverandre, at ligesom jeg elskede eder, skulle også I elske hverandre.
35 Mukamakondana aliyense adzadziwa kuti ndinu ophunzira anga.”
Derpå skulle alle kende, at I ere mine Disciple, om I have indbyrdes Kærlighed."
36 Simoni Petro anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukupita kuti?” Yesu anayankha kuti, “Kumene Ine ndikupita iwe sunganditsatire tsopano, koma udzanditsatira mʼtsogolo.”
Simon Peter siger til ham: "Herre! hvor går du hen?" Jesus svarede ham: "Hvor jeg går hen, kan du ikke nu følge mig, men siden skal du følge mig."
37 Petro anafunsa kuti, “Ambuye, nʼchifukwa chiyani ine sindingakutsatireni tsopano? Ine ndidzapereka moyo wanga chifukwa cha Inu.”
Peter siger til ham: "Herre! hvorfor kan jeg ikke følge dig nu? Jeg vil sætte mit Liv til for dig?
38 Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe udzalolera kutaya moyo chifukwa cha Ine? Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti tambala asanalire, iwe udzandikana katatu!”
Jesus svarer: "Vil du sætte dit Liv til for mig? Sandelig, sandelig, siger jeg dig, Hanen skal ikke gale, førend du har fornægtet mig tre Gange."

< Yohane 13 >